Check out the new design

Prijevod značenja časnog Kur'ana - Prijevod na čeva jezik - Halid Ibrahim Betala * - Sadržaj prijevodā


Prijevod značenja Sura: El-En'am   Ajet:
فَقُطِعَ دَابِرُ ٱلۡقَوۡمِ ٱلَّذِينَ ظَلَمُواْۚ وَٱلۡحَمۡدُ لِلَّهِ رَبِّ ٱلۡعَٰلَمِينَ
Choncho mizu ya anthu oipa idadulidwa. Ndipo kuyamikidwa konse kwabwino nkwa Allah, Mbuye wa zolengedwa.
Tefsiri na arapskom jeziku:
قُلۡ أَرَءَيۡتُمۡ إِنۡ أَخَذَ ٱللَّهُ سَمۡعَكُمۡ وَأَبۡصَٰرَكُمۡ وَخَتَمَ عَلَىٰ قُلُوبِكُم مَّنۡ إِلَٰهٌ غَيۡرُ ٱللَّهِ يَأۡتِيكُم بِهِۗ ٱنظُرۡ كَيۡفَ نُصَرِّفُ ٱلۡأٓيَٰتِ ثُمَّ هُمۡ يَصۡدِفُونَ
Nena: “Tandiuzani, ngati Allah atakuchotserani kumva kwanu ndi kupenya kwanu, nadinda chidindo m’mitima yanu (kuti asalowemo mawu amalangizo a mtundu uliwonse), kodi ndi mulungu uti, kupatula Allah, amene angakubwezereninso (zimenezi)?” Taona momwe tikufotokozera mwatsatanetsatane zizindikiro kenako iwo akunyozera.
Tefsiri na arapskom jeziku:
قُلۡ أَرَءَيۡتَكُمۡ إِنۡ أَتَىٰكُمۡ عَذَابُ ٱللَّهِ بَغۡتَةً أَوۡ جَهۡرَةً هَلۡ يُهۡلَكُ إِلَّا ٱلۡقَوۡمُ ٱلظَّٰلِمُونَ
Nena: “Tandiuzani, ngati masautso a Allah atakufikani mwadzidzidzi kapena moonekera, kodi angaonongeke ndi ena osati anthu ochita zoipa?”
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَمَا نُرۡسِلُ ٱلۡمُرۡسَلِينَ إِلَّا مُبَشِّرِينَ وَمُنذِرِينَۖ فَمَنۡ ءَامَنَ وَأَصۡلَحَ فَلَا خَوۡفٌ عَلَيۡهِمۡ وَلَا هُمۡ يَحۡزَنُونَ
Ndipo sititumiza atumiki koma kuti akhale ouza nkhani zabwino ndi ochenjeza. Choncho amene akhulupirira nakonza zinthu, pa iwo sipadzakhala mantha ndiponso sadzadandaula.
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَٱلَّذِينَ كَذَّبُواْ بِـَٔايَٰتِنَا يَمَسُّهُمُ ٱلۡعَذَابُ بِمَا كَانُواْ يَفۡسُقُونَ
Ndipo amene atsutsa zizindikiro zathu, chilango chidzawakhudza chifukwa chakupandukira kwawo chilamulo.
Tefsiri na arapskom jeziku:
قُل لَّآ أَقُولُ لَكُمۡ عِندِي خَزَآئِنُ ٱللَّهِ وَلَآ أَعۡلَمُ ٱلۡغَيۡبَ وَلَآ أَقُولُ لَكُمۡ إِنِّي مَلَكٌۖ إِنۡ أَتَّبِعُ إِلَّا مَا يُوحَىٰٓ إِلَيَّۚ قُلۡ هَلۡ يَسۡتَوِي ٱلۡأَعۡمَىٰ وَٱلۡبَصِيرُۚ أَفَلَا تَتَفَكَّرُونَ
Nena: “Ine sindikukuuzani kuti ndili nazo nkhokwe za Allah kapena kuti ndikudziwa zamseri, ndiponso sindikukuuzani kuti ine ndine mngelo. Ine sinditsata china koma zomwe zikuvumbulutsidwa kwa ine.” Nena: “Kodi wakhungu ndi wopenya angafanane? Bwanji simukuganizira?”
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَأَنذِرۡ بِهِ ٱلَّذِينَ يَخَافُونَ أَن يُحۡشَرُوٓاْ إِلَىٰ رَبِّهِمۡ لَيۡسَ لَهُم مِّن دُونِهِۦ وَلِيّٞ وَلَا شَفِيعٞ لَّعَلَّهُمۡ يَتَّقُونَ
Achenjeze ndi Qur’an iyi omwe akuopa kuti adzasonkhanitsidwa kwa Mbuye wawo pomwe ali opanda mtetezi ngakhale muomboli aliyense kupatula Iye, kuti iwo aope (Allah).
Tefsiri na arapskom jeziku:
وَلَا تَطۡرُدِ ٱلَّذِينَ يَدۡعُونَ رَبَّهُم بِٱلۡغَدَوٰةِ وَٱلۡعَشِيِّ يُرِيدُونَ وَجۡهَهُۥۖ مَا عَلَيۡكَ مِنۡ حِسَابِهِم مِّن شَيۡءٖ وَمَا مِنۡ حِسَابِكَ عَلَيۡهِم مِّن شَيۡءٖ فَتَطۡرُدَهُمۡ فَتَكُونَ مِنَ ٱلظَّٰلِمِينَ
Ndipo usawathamangitse omwe akupembedza Mbuye wawo m’mawa ndi madzulo pofuna chiyanjo Chake. Chiwerengero chawo sichili pa iwe ngakhale pang’ono, ndipo chiwerengero chako sichili pa iwo ngakhale pang’ono kotero kuti nkwathamangitsa. (Ngati uwapirikitsa) ukhala m’gulu la anthu ochita zoipa.
Tefsiri na arapskom jeziku:
 
Prijevod značenja Sura: El-En'am
Indeks sura Broj stranice
 
Prijevod značenja časnog Kur'ana - Prijevod na čeva jezik - Halid Ibrahim Betala - Sadržaj prijevodā

Halid Ibrahim Bejtala je preveo.

Zatvaranje