Prijevod značenja časnog Kur'ana - الترجمة الشيشيوا * - Sadržaj prijevodā


Prijevod značenja Ajet: (51) Sura: Sura el-Enfal
ذَٰلِكَ بِمَا قَدَّمَتۡ أَيۡدِيكُمۡ وَأَنَّ ٱللَّهَ لَيۡسَ بِظَلَّٰمٖ لِّلۡعَبِيدِ
“Izo ndi chifukwa cha (machimo) amene manja anu anawatsogoza, ndipo Allah sali opondereza akapolo (Ake).”[203]
[203] Mizimu ya osakhulupilira ikamachotsedwa, imachotsedwa mwamasautso kwambiri. Koma amene ali pafupi ndi wakufayo saona zimenezi pakuti ife sititha kuiona mizimu ndi zonse zokhudzana ndi mizimu. Ife timangoona thupi lawakufayo poliona thupilo likuzunzika. Kuzunzika kwa mzimu sindiko kuzunzika kwa thupi. Choncho kuzunzika komwe kukunenedwa apa nkuzunzika kwa mzimu komwe kumaapeza anthu osakhulupilira. Komatu masautso athupi amene amawapeza anthu ena panthawi ya imfa pophuphaphupha, sasonyeza kusalungama kwa munthuyo. Koma amasonyeza mphamvu zomwe zidali m’thupi mwa munthuyo. Sizikhudzana ndi kulungama kwake ndi kusalungama kwake. Mungawaone anthu oipa akufa ndi imfa yodekha pomwe amene adali abwino akufa ndi imfa yophuphaphupha ndikudzimenyamenya. Choncho kuphuphaphupha kumeneko nkwathupi chifukwa chokhala ndi mphamvu. Choncho tisadodome pomwe tiona munthu wabwino akuphuphaphupha.
Tefsiri na arapskom jeziku:
 
Prijevod značenja Ajet: (51) Sura: Sura el-Enfal
Indeks sura Broj stranice
 
Prijevod značenja časnog Kur'ana - الترجمة الشيشيوا - Sadržaj prijevodā

ترجمة معاني القرآن الكريم إلى اللغة الشيشيوا، ترجمها خالد إبراهيم بيتالا. نسخة عام 2020م.

Zatvaranje