Bản dịch ý nghĩa nội dung Qur'an - Dịch thuật tiếng Chichio * - Mục lục các bản dịch


Ý nghĩa nội dung Câu: (51) Chương: Chương Al-Anfal
ذَٰلِكَ بِمَا قَدَّمَتۡ أَيۡدِيكُمۡ وَأَنَّ ٱللَّهَ لَيۡسَ بِظَلَّٰمٖ لِّلۡعَبِيدِ
“Izo ndi chifukwa cha (machimo) amene manja anu anawatsogoza, ndipo Allah sali opondereza akapolo (Ake).”[203]
[203] Mizimu ya osakhulupilira ikamachotsedwa, imachotsedwa mwamasautso kwambiri. Koma amene ali pafupi ndi wakufayo saona zimenezi pakuti ife sititha kuiona mizimu ndi zonse zokhudzana ndi mizimu. Ife timangoona thupi lawakufayo poliona thupilo likuzunzika. Kuzunzika kwa mzimu sindiko kuzunzika kwa thupi. Choncho kuzunzika komwe kukunenedwa apa nkuzunzika kwa mzimu komwe kumaapeza anthu osakhulupilira. Komatu masautso athupi amene amawapeza anthu ena panthawi ya imfa pophuphaphupha, sasonyeza kusalungama kwa munthuyo. Koma amasonyeza mphamvu zomwe zidali m’thupi mwa munthuyo. Sizikhudzana ndi kulungama kwake ndi kusalungama kwake. Mungawaone anthu oipa akufa ndi imfa yodekha pomwe amene adali abwino akufa ndi imfa yophuphaphupha ndikudzimenyamenya. Choncho kuphuphaphupha kumeneko nkwathupi chifukwa chokhala ndi mphamvu. Choncho tisadodome pomwe tiona munthu wabwino akuphuphaphupha.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
 
Ý nghĩa nội dung Câu: (51) Chương: Chương Al-Anfal
Mục lục các chương Kinh Số trang
 
Bản dịch ý nghĩa nội dung Qur'an - Dịch thuật tiếng Chichio - Mục lục các bản dịch

Bản dịch ý nghĩa nội dung Kinh Qur'an bằng tiếng Chichio, do Khalid Ibrahim Petala dịch thuật, bản dịch năm 2020.

Đóng lại