Übersetzung der Bedeutungen von dem heiligen Quran - الترجمة الشيشيوا * - Übersetzungen


Übersetzung der Bedeutungen Surah / Kapitel: Al-Humazah   Vers:

Al-Humazah

وَيۡلٞ لِّكُلِّ هُمَزَةٖ لُّمَزَةٍ
Kuonongeka koopsa kudzampeza aliyense wojeda ndi wonyoza anthu polozera (ndi maso kapena kuyankhula ndi lirime).[482]
[482] Kujeda kwa mtundu uliwonse ndi koipa. Anthu ambiri amaganiza kuti kujeda ndi chinthu chochepa, saona kuti ndi chinthu choipa, pomwe Qur’an ikuletsa kwatunthu mpaka mwakuti imamufanizira munthu wojeda ngati munthu yemwe amadya minofu ya mnzake wakufa. Mu Ayah imeneyi, Allah wanena kuti “Wayilun” lomwe tanthauzo lake ndi “Kuonongeka koopsa.” Choncho nkofunika kwa munthu aliyense kupewa khalidwe lojeda.
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
ٱلَّذِي جَمَعَ مَالٗا وَعَدَّدَهُۥ
Yemwe wasonkhanitsa chuma ndikumachiwerengera.[483]
[483] Mmenemo ndi momwe alili munthu wa umbombo, kukoma kwa chuma kwa iye, ndikuchisonkhanitsa ndikumachiwerengera akakhala ndi danga; sikuti akufuna kudziwa kuchuluka kwake koma kungokondweretsedwa ndikuchiwerengako. Saganizira zimene zingamuthandize iye mwini kapena kuthandiza anzake.
Chuma ntchito yake ndikuti chimthandize mwini chumacho pa zinthu zabwino zosiyanasiyana pamodzi ndi anzake, osati kungochikhazika ndikumangochiwerengera mokhumbiza ena.
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
يَحۡسَبُ أَنَّ مَالَهُۥٓ أَخۡلَدَهُۥ
Akuganiza kuti chuma chakecho chimkhazika (pa dziko) nthawi yaitali (ndikumteteza ku zimene sakuzifuna).
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
كَلَّاۖ لَيُنۢبَذَنَّ فِي ٱلۡحُطَمَةِ
Sichoncho! (Asiye maganizo amenewo) ndithudi, akaponyedwa ku Moto woononga (chifukwa cha kuipa kwa zochita zake).
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
وَمَآ أَدۡرَىٰكَ مَا ٱلۡحُطَمَةُ
Ndi chiyani chingakudziwitse za Moto woonongawu?
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
نَارُ ٱللَّهِ ٱلۡمُوقَدَةُ
Umenewu ndi Moto wa Allah woyaka (nthawi zonse, woononga chilichonse choponyedwa mmenemo).
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
ٱلَّتِي تَطَّلِعُ عَلَى ٱلۡأَفۡـِٔدَةِ
Umene umakwera mpaka ku mtima.[484]
[484] Moto umenewu, sukapsereza kunja kokha, ukapsereza mpaka ndi mu mtima momwe.
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
إِنَّهَا عَلَيۡهِم مُّؤۡصَدَةٞ
Ndithu motowo ukawazinga (ndi kuwatsekera makomo).
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
فِي عَمَدٖ مُّمَدَّدَةِۭ
Munsanamira za zitalizitali (kotero kuti sakatha kugwedezeka mmenemo kapena kupulumuka).
Arabische Interpretationen von dem heiligen Quran:
 
Übersetzung der Bedeutungen Surah / Kapitel: Al-Humazah
Suren/ Kapiteln Liste Nummer der Seite
 
Übersetzung der Bedeutungen von dem heiligen Quran - الترجمة الشيشيوا - Übersetzungen

ترجمة معاني القرآن الكريم إلى اللغة الشيشيوا، ترجمها خالد إبراهيم بيتالا. نسخة عام 2020م.

Schließen