Kur'an-ı Kerim meal tercümesi - الترجمة الشيشيوا * - Mealler fihristi


Anlam tercümesi Sure: Sûretu'l-Humezeh   Ayet:

Sûretu'l-Humezeh

وَيۡلٞ لِّكُلِّ هُمَزَةٖ لُّمَزَةٍ
Kuonongeka koopsa kudzampeza aliyense wojeda ndi wonyoza anthu polozera (ndi maso kapena kuyankhula ndi lirime).[482]
[482] Kujeda kwa mtundu uliwonse ndi koipa. Anthu ambiri amaganiza kuti kujeda ndi chinthu chochepa, saona kuti ndi chinthu choipa, pomwe Qur’an ikuletsa kwatunthu mpaka mwakuti imamufanizira munthu wojeda ngati munthu yemwe amadya minofu ya mnzake wakufa. Mu Ayah imeneyi, Allah wanena kuti “Wayilun” lomwe tanthauzo lake ndi “Kuonongeka koopsa.” Choncho nkofunika kwa munthu aliyense kupewa khalidwe lojeda.
Arapça tefsirler:
ٱلَّذِي جَمَعَ مَالٗا وَعَدَّدَهُۥ
Yemwe wasonkhanitsa chuma ndikumachiwerengera.[483]
[483] Mmenemo ndi momwe alili munthu wa umbombo, kukoma kwa chuma kwa iye, ndikuchisonkhanitsa ndikumachiwerengera akakhala ndi danga; sikuti akufuna kudziwa kuchuluka kwake koma kungokondweretsedwa ndikuchiwerengako. Saganizira zimene zingamuthandize iye mwini kapena kuthandiza anzake.
Chuma ntchito yake ndikuti chimthandize mwini chumacho pa zinthu zabwino zosiyanasiyana pamodzi ndi anzake, osati kungochikhazika ndikumangochiwerengera mokhumbiza ena.
Arapça tefsirler:
يَحۡسَبُ أَنَّ مَالَهُۥٓ أَخۡلَدَهُۥ
Akuganiza kuti chuma chakecho chimkhazika (pa dziko) nthawi yaitali (ndikumteteza ku zimene sakuzifuna).
Arapça tefsirler:
كَلَّاۖ لَيُنۢبَذَنَّ فِي ٱلۡحُطَمَةِ
Sichoncho! (Asiye maganizo amenewo) ndithudi, akaponyedwa ku Moto woononga (chifukwa cha kuipa kwa zochita zake).
Arapça tefsirler:
وَمَآ أَدۡرَىٰكَ مَا ٱلۡحُطَمَةُ
Ndi chiyani chingakudziwitse za Moto woonongawu?
Arapça tefsirler:
نَارُ ٱللَّهِ ٱلۡمُوقَدَةُ
Umenewu ndi Moto wa Allah woyaka (nthawi zonse, woononga chilichonse choponyedwa mmenemo).
Arapça tefsirler:
ٱلَّتِي تَطَّلِعُ عَلَى ٱلۡأَفۡـِٔدَةِ
Umene umakwera mpaka ku mtima.[484]
[484] Moto umenewu, sukapsereza kunja kokha, ukapsereza mpaka ndi mu mtima momwe.
Arapça tefsirler:
إِنَّهَا عَلَيۡهِم مُّؤۡصَدَةٞ
Ndithu motowo ukawazinga (ndi kuwatsekera makomo).
Arapça tefsirler:
فِي عَمَدٖ مُّمَدَّدَةِۭ
Munsanamira za zitalizitali (kotero kuti sakatha kugwedezeka mmenemo kapena kupulumuka).
Arapça tefsirler:
 
Anlam tercümesi Sure: Sûretu'l-Humezeh
Surelerin fihristi Sayfa numarası
 
Kur'an-ı Kerim meal tercümesi - الترجمة الشيشيوا - Mealler fihristi

ترجمة معاني القرآن الكريم إلى اللغة الشيشيوا، ترجمها خالد إبراهيم بيتالا. نسخة عام 2020م.

Kapat