Traducción de los significados del Sagrado Corán - Traducción al Chewa * - Índice de traducciones


Traducción de significados Capítulo: Sura Al-Humaza   Versículo:

Sura Al-Humaza

وَيۡلٞ لِّكُلِّ هُمَزَةٖ لُّمَزَةٍ
Kuonongeka koopsa kudzampeza aliyense wojeda ndi wonyoza anthu polozera (ndi maso kapena kuyankhula ndi lirime).[482]
[482] Kujeda kwa mtundu uliwonse ndi koipa. Anthu ambiri amaganiza kuti kujeda ndi chinthu chochepa, saona kuti ndi chinthu choipa, pomwe Qur’an ikuletsa kwatunthu mpaka mwakuti imamufanizira munthu wojeda ngati munthu yemwe amadya minofu ya mnzake wakufa. Mu Ayah imeneyi, Allah wanena kuti “Wayilun” lomwe tanthauzo lake ndi “Kuonongeka koopsa.” Choncho nkofunika kwa munthu aliyense kupewa khalidwe lojeda.
Las Exégesis Árabes:
ٱلَّذِي جَمَعَ مَالٗا وَعَدَّدَهُۥ
Yemwe wasonkhanitsa chuma ndikumachiwerengera.[483]
[483] Mmenemo ndi momwe alili munthu wa umbombo, kukoma kwa chuma kwa iye, ndikuchisonkhanitsa ndikumachiwerengera akakhala ndi danga; sikuti akufuna kudziwa kuchuluka kwake koma kungokondweretsedwa ndikuchiwerengako. Saganizira zimene zingamuthandize iye mwini kapena kuthandiza anzake.
Chuma ntchito yake ndikuti chimthandize mwini chumacho pa zinthu zabwino zosiyanasiyana pamodzi ndi anzake, osati kungochikhazika ndikumangochiwerengera mokhumbiza ena.
Las Exégesis Árabes:
يَحۡسَبُ أَنَّ مَالَهُۥٓ أَخۡلَدَهُۥ
Akuganiza kuti chuma chakecho chimkhazika (pa dziko) nthawi yaitali (ndikumteteza ku zimene sakuzifuna).
Las Exégesis Árabes:
كَلَّاۖ لَيُنۢبَذَنَّ فِي ٱلۡحُطَمَةِ
Sichoncho! (Asiye maganizo amenewo) ndithudi, akaponyedwa ku Moto woononga (chifukwa cha kuipa kwa zochita zake).
Las Exégesis Árabes:
وَمَآ أَدۡرَىٰكَ مَا ٱلۡحُطَمَةُ
Ndi chiyani chingakudziwitse za Moto woonongawu?
Las Exégesis Árabes:
نَارُ ٱللَّهِ ٱلۡمُوقَدَةُ
Umenewu ndi Moto wa Allah woyaka (nthawi zonse, woononga chilichonse choponyedwa mmenemo).
Las Exégesis Árabes:
ٱلَّتِي تَطَّلِعُ عَلَى ٱلۡأَفۡـِٔدَةِ
Umene umakwera mpaka ku mtima.[484]
[484] Moto umenewu, sukapsereza kunja kokha, ukapsereza mpaka ndi mu mtima momwe.
Las Exégesis Árabes:
إِنَّهَا عَلَيۡهِم مُّؤۡصَدَةٞ
Ndithu motowo ukawazinga (ndi kuwatsekera makomo).
Las Exégesis Árabes:
فِي عَمَدٖ مُّمَدَّدَةِۭ
Munsanamira za zitalizitali (kotero kuti sakatha kugwedezeka mmenemo kapena kupulumuka).
Las Exégesis Árabes:
 
Traducción de significados Capítulo: Sura Al-Humaza
Índice de Capítulos Número de página
 
Traducción de los significados del Sagrado Corán - Traducción al Chewa - Índice de traducciones

Traducción del significado del Corán al chewa por Khaled Ibrahim Betala (ed.2020)

Cerrar