Traducción de los significados del Sagrado Corán - Traducción al Chewa * - Índice de traducciones


Traducción de significados Versículo: (1) Capítulo: Sura Al-Alaq

Sura Al-Alaq

ٱقۡرَأۡ بِٱسۡمِ رَبِّكَ ٱلَّذِي خَلَقَ
Werenga! (Iwe Mneneri (s.a.w), zomwe zikuvumbulutsidwa) mdzina la Mbuye wako Yemwe adalenga (zolengedwa zonse).[460]
[460] Tanena kale mndemanga 7 yamu surat - Dhuha kuti Mneneri Muhammad (s.a.w) asadapatsidwe uneneri wake ndi Allah adali kudandaula kwambiri poona anthu ake ali osokera ndiponso poona kuti iye sadali kudziwa momwe angawaongolere. Pambuyo pake adali kumapita ku mapiri amene adali pafupi ndi Mzinda wa Makka. Kumeneko adali kupemphera ndi kumalingalira ndi kupempha Allah kuti amusonyeze njira ya chiongoko. Choncho tsiku lina pamene adali ku phanga la Hiraa, pafupi ndi Makka ali mkati mopemphera, Mngelo adamuonekera mwadzidzidzi nati: “Iwe Muhammad! Ine ndine Jiburil (Gabrie!) ndipo iwe ndiwe Mtumiki wa Allah kwa zolengedwa zonse!” Pambuyo pake adamuuza kuti: “werenga!” Mneneri adayankha: “Ine sindidziwa kuwerenga.” Jiburil uja adamgwira ndi kumpana mwamphamvu mpaka adavutika kwambiri. Adamsiyanso ndi kumuuza: “werenga!” Mneneri adayankha monga adamuyankhira poyamba mpaka kadakwana katatu akumuchita zokhazokhazo. Kenaka adamuwerengera ma Ayah kuchokera 1 mpaka 5. Ma Ayah amenewa ndiwo oyamba kuvumbulutsidwa m’Qur’an.
Las Exégesis Árabes:
 
Traducción de significados Versículo: (1) Capítulo: Sura Al-Alaq
Índice de Capítulos Número de página
 
Traducción de los significados del Sagrado Corán - Traducción al Chewa - Índice de traducciones

Traducción del significado del Corán al chewa por Khaled Ibrahim Betala (ed.2020)

Cerrar