Traducción de los significados del Sagrado Corán - Traducción al Chewa * - Índice de traducciones


Traducción de significados Capítulo: Sura Al-Alaq   Versículo:

Sura Al-Alaq

ٱقۡرَأۡ بِٱسۡمِ رَبِّكَ ٱلَّذِي خَلَقَ
Werenga! (Iwe Mneneri (s.a.w), zomwe zikuvumbulutsidwa) mdzina la Mbuye wako Yemwe adalenga (zolengedwa zonse).[460]
[460] Tanena kale mndemanga 7 yamu surat - Dhuha kuti Mneneri Muhammad (s.a.w) asadapatsidwe uneneri wake ndi Allah adali kudandaula kwambiri poona anthu ake ali osokera ndiponso poona kuti iye sadali kudziwa momwe angawaongolere. Pambuyo pake adali kumapita ku mapiri amene adali pafupi ndi Mzinda wa Makka. Kumeneko adali kupemphera ndi kumalingalira ndi kupempha Allah kuti amusonyeze njira ya chiongoko. Choncho tsiku lina pamene adali ku phanga la Hiraa, pafupi ndi Makka ali mkati mopemphera, Mngelo adamuonekera mwadzidzidzi nati: “Iwe Muhammad! Ine ndine Jiburil (Gabrie!) ndipo iwe ndiwe Mtumiki wa Allah kwa zolengedwa zonse!” Pambuyo pake adamuuza kuti: “werenga!” Mneneri adayankha: “Ine sindidziwa kuwerenga.” Jiburil uja adamgwira ndi kumpana mwamphamvu mpaka adavutika kwambiri. Adamsiyanso ndi kumuuza: “werenga!” Mneneri adayankha monga adamuyankhira poyamba mpaka kadakwana katatu akumuchita zokhazokhazo. Kenaka adamuwerengera ma Ayah kuchokera 1 mpaka 5. Ma Ayah amenewa ndiwo oyamba kuvumbulutsidwa m’Qur’an.
Las Exégesis Árabes:
خَلَقَ ٱلۡإِنسَٰنَ مِنۡ عَلَقٍ
Adalenga munthu kuchokera ku magazi owundana.[461]
[461] Madzi ambewu ya munthu, pambuyo pokhazikika mchiberekero kwa masiku makumi anayi, amatembenuka ndikukhala magazi. Ili ndilo tanthauzo la Ayah imeneyi.
Las Exégesis Árabes:
ٱقۡرَأۡ وَرَبُّكَ ٱلۡأَكۡرَمُ
Werenga! Ndipo Mbuye wako ndi Wopereka kwambiri.[462]
[462] Ayah 3 ndi 5 Mtumiki (s.a.w) akuyankhidwa pa kunena kwake kwa kuti: “Ine sindidziwa kuwerenga.” Choncho Allah akumuuza kuti Iye ndi Mfulu weniweni, ndi Yemwe adawaphunzitsa anthu kulemba ndi cholembera ndi zonse zomwe sadali kuzidziwa. Kwa ufulu Wake wochuluka ndi mphamvu Zake pa chilichonse, sichovuta kwa Iye (Allah) kumphunzitsa Mtumiki Wake kuwerenga molakatula.
Las Exégesis Árabes:
ٱلَّذِي عَلَّمَ بِٱلۡقَلَمِ
Yemwe waphunzitsa (munthu kulemba) ndi cholembera.
Las Exégesis Árabes:
عَلَّمَ ٱلۡإِنسَٰنَ مَا لَمۡ يَعۡلَمۡ
Waphunzitsa munthu zinthu (zambiri) zomwe (iye) sadali kuzidziwa.
Las Exégesis Árabes:
كَلَّآ إِنَّ ٱلۡإِنسَٰنَ لَيَطۡغَىٰٓ
Zoona ndithu koma munthu akupyola malire (podzikweza).
Las Exégesis Árabes:
أَن رَّءَاهُ ٱسۡتَغۡنَىٰٓ
Chifukwa chodziona kuti walemera.
Las Exégesis Árabes:
إِنَّ إِلَىٰ رَبِّكَ ٱلرُّجۡعَىٰٓ
Palibe chikaiko, (iwe Mneneri (s.a.w) kobwerera (onse) nkwa Mbuye wako basi; (adzawaukitsa).[463]
[463] Tanthauzo lake nkuti musanyengedwe ndi chumacho chifukwa chakuti, popanda chikaiko, mubwerera kwa Mbuye wanu ndipo chumacho sichidzakuthandizani chilichonse pa maso Pake.
Las Exégesis Árabes:
أَرَءَيۡتَ ٱلَّذِي يَنۡهَىٰ
Kodi wamuona yemwe akuletsa,
Las Exégesis Árabes:
عَبۡدًا إِذَا صَلَّىٰٓ
Kapolo (wa Allah) akamapemphera?
Las Exégesis Árabes:
أَرَءَيۡتَ إِن كَانَ عَلَى ٱلۡهُدَىٰٓ
Tandiuza ngati ali pachiongoko?
Las Exégesis Árabes:
أَوۡ أَمَرَ بِٱلتَّقۡوَىٰٓ
Kapena kuti akulamulira zoopa Allah?
Las Exégesis Árabes:
أَرَءَيۡتَ إِن كَذَّبَ وَتَوَلَّىٰٓ
Tandiuza (za woletsayo) ngati akutsutsa (zimene wadza nazo Mneneri) ndikunyoza (chikhulupiliro ndi ntchito yabwino)?
Las Exégesis Árabes:
أَلَمۡ يَعۡلَم بِأَنَّ ٱللَّهَ يَرَىٰ
Kodi sakudziwa kuti Allah akuona (machitidwe ake. Ndipo adzamlipira)?
Las Exégesis Árabes:
كَلَّا لَئِن لَّمۡ يَنتَهِ لَنَسۡفَعَۢا بِٱلنَّاصِيَةِ
Ayi ndithu ngati sasiya timukoka tsitsi lapatsumba (tiligwira mwamphamvu tsumba lake ndikukamponya ku Moto).
Las Exégesis Árabes:
نَاصِيَةٖ كَٰذِبَةٍ خَاطِئَةٖ
Tsumba labodza (ndiponso) lamachimo.
Las Exégesis Árabes:
فَلۡيَدۡعُ نَادِيَهُۥ
Basi aliitane gulu lakelo, (la amene amakhala nawo pabwalo kuti amthandize pano pa dziko kapena tsiku lachimaliziro),
Las Exégesis Árabes:
سَنَدۡعُ ٱلزَّبَانِيَةَ
Nafe tiitana azabaniya (angelo a ku Moto).
Las Exégesis Árabes:
كَلَّا لَا تُطِعۡهُ وَٱسۡجُدۡۤ وَٱقۡتَرِب۩
Ayi ndithu usamumvere (pa zimene akukuletsazo); koma gwetsa nkhope yako pansi, ndipo dziyandikitse kwa Mbuye wako.
Las Exégesis Árabes:
 
Traducción de significados Capítulo: Sura Al-Alaq
Índice de Capítulos Número de página
 
Traducción de los significados del Sagrado Corán - Traducción al Chewa - Índice de traducciones

Traducción del significado del Corán al chewa por Khaled Ibrahim Betala (ed.2020)

Cerrar