แปล​ความหมาย​อัลกุรอาน​ - คำแปลภาษาชิเชวา * - สารบัญ​คำแปล


แปลความหมาย​ สูเราะฮ์: Al-‘Alaq   อายะฮ์:

Al-‘Alaq

ٱقۡرَأۡ بِٱسۡمِ رَبِّكَ ٱلَّذِي خَلَقَ
Werenga! (Iwe Mneneri (s.a.w), zomwe zikuvumbulutsidwa) mdzina la Mbuye wako Yemwe adalenga (zolengedwa zonse).[460]
[460] Tanena kale mndemanga 7 yamu surat - Dhuha kuti Mneneri Muhammad (s.a.w) asadapatsidwe uneneri wake ndi Allah adali kudandaula kwambiri poona anthu ake ali osokera ndiponso poona kuti iye sadali kudziwa momwe angawaongolere. Pambuyo pake adali kumapita ku mapiri amene adali pafupi ndi Mzinda wa Makka. Kumeneko adali kupemphera ndi kumalingalira ndi kupempha Allah kuti amusonyeze njira ya chiongoko. Choncho tsiku lina pamene adali ku phanga la Hiraa, pafupi ndi Makka ali mkati mopemphera, Mngelo adamuonekera mwadzidzidzi nati: “Iwe Muhammad! Ine ndine Jiburil (Gabrie!) ndipo iwe ndiwe Mtumiki wa Allah kwa zolengedwa zonse!” Pambuyo pake adamuuza kuti: “werenga!” Mneneri adayankha: “Ine sindidziwa kuwerenga.” Jiburil uja adamgwira ndi kumpana mwamphamvu mpaka adavutika kwambiri. Adamsiyanso ndi kumuuza: “werenga!” Mneneri adayankha monga adamuyankhira poyamba mpaka kadakwana katatu akumuchita zokhazokhazo. Kenaka adamuwerengera ma Ayah kuchokera 1 mpaka 5. Ma Ayah amenewa ndiwo oyamba kuvumbulutsidwa m’Qur’an.
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
خَلَقَ ٱلۡإِنسَٰنَ مِنۡ عَلَقٍ
Adalenga munthu kuchokera ku magazi owundana.[461]
[461] Madzi ambewu ya munthu, pambuyo pokhazikika mchiberekero kwa masiku makumi anayi, amatembenuka ndikukhala magazi. Ili ndilo tanthauzo la Ayah imeneyi.
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
ٱقۡرَأۡ وَرَبُّكَ ٱلۡأَكۡرَمُ
Werenga! Ndipo Mbuye wako ndi Wopereka kwambiri.[462]
[462] Ayah 3 ndi 5 Mtumiki (s.a.w) akuyankhidwa pa kunena kwake kwa kuti: “Ine sindidziwa kuwerenga.” Choncho Allah akumuuza kuti Iye ndi Mfulu weniweni, ndi Yemwe adawaphunzitsa anthu kulemba ndi cholembera ndi zonse zomwe sadali kuzidziwa. Kwa ufulu Wake wochuluka ndi mphamvu Zake pa chilichonse, sichovuta kwa Iye (Allah) kumphunzitsa Mtumiki Wake kuwerenga molakatula.
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
ٱلَّذِي عَلَّمَ بِٱلۡقَلَمِ
Yemwe waphunzitsa (munthu kulemba) ndi cholembera.
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
عَلَّمَ ٱلۡإِنسَٰنَ مَا لَمۡ يَعۡلَمۡ
Waphunzitsa munthu zinthu (zambiri) zomwe (iye) sadali kuzidziwa.
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
كَلَّآ إِنَّ ٱلۡإِنسَٰنَ لَيَطۡغَىٰٓ
Zoona ndithu koma munthu akupyola malire (podzikweza).
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
أَن رَّءَاهُ ٱسۡتَغۡنَىٰٓ
Chifukwa chodziona kuti walemera.
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
إِنَّ إِلَىٰ رَبِّكَ ٱلرُّجۡعَىٰٓ
Palibe chikaiko, (iwe Mneneri (s.a.w) kobwerera (onse) nkwa Mbuye wako basi; (adzawaukitsa).[463]
[463] Tanthauzo lake nkuti musanyengedwe ndi chumacho chifukwa chakuti, popanda chikaiko, mubwerera kwa Mbuye wanu ndipo chumacho sichidzakuthandizani chilichonse pa maso Pake.
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
أَرَءَيۡتَ ٱلَّذِي يَنۡهَىٰ
Kodi wamuona yemwe akuletsa,
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
عَبۡدًا إِذَا صَلَّىٰٓ
Kapolo (wa Allah) akamapemphera?
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
أَرَءَيۡتَ إِن كَانَ عَلَى ٱلۡهُدَىٰٓ
Tandiuza ngati ali pachiongoko?
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
أَوۡ أَمَرَ بِٱلتَّقۡوَىٰٓ
Kapena kuti akulamulira zoopa Allah?
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
أَرَءَيۡتَ إِن كَذَّبَ وَتَوَلَّىٰٓ
Tandiuza (za woletsayo) ngati akutsutsa (zimene wadza nazo Mneneri) ndikunyoza (chikhulupiliro ndi ntchito yabwino)?
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
أَلَمۡ يَعۡلَم بِأَنَّ ٱللَّهَ يَرَىٰ
Kodi sakudziwa kuti Allah akuona (machitidwe ake. Ndipo adzamlipira)?
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
كَلَّا لَئِن لَّمۡ يَنتَهِ لَنَسۡفَعَۢا بِٱلنَّاصِيَةِ
Ayi ndithu ngati sasiya timukoka tsitsi lapatsumba (tiligwira mwamphamvu tsumba lake ndikukamponya ku Moto).
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
نَاصِيَةٖ كَٰذِبَةٍ خَاطِئَةٖ
Tsumba labodza (ndiponso) lamachimo.
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
فَلۡيَدۡعُ نَادِيَهُۥ
Basi aliitane gulu lakelo, (la amene amakhala nawo pabwalo kuti amthandize pano pa dziko kapena tsiku lachimaliziro),
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
سَنَدۡعُ ٱلزَّبَانِيَةَ
Nafe tiitana azabaniya (angelo a ku Moto).
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
كَلَّا لَا تُطِعۡهُ وَٱسۡجُدۡۤ وَٱقۡتَرِب۩
Ayi ndithu usamumvere (pa zimene akukuletsazo); koma gwetsa nkhope yako pansi, ndipo dziyandikitse kwa Mbuye wako.
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
 
แปลความหมาย​ สูเราะฮ์: Al-‘Alaq
สารบัญสูเราะฮ์ หมายเลข​หน้า​
 
แปล​ความหมาย​อัลกุรอาน​ - คำแปลภาษาชิเชวา - สารบัญ​คำแปล

การแปลความหมายอัลกุรอานเป็นภาษาชิเชวา แปลโดย คอลิด อิบรอฮีม เบตาลา (ed. 2020)

ปิด