Traduzione dei Significati del Sacro Corano - Traduzione chicheŵa * - Indice Traduzioni


Traduzione dei significati Versetto: (1) Sura: Al-‘Alaq

Al-‘Alaq

ٱقۡرَأۡ بِٱسۡمِ رَبِّكَ ٱلَّذِي خَلَقَ
Werenga! (Iwe Mneneri (s.a.w), zomwe zikuvumbulutsidwa) mdzina la Mbuye wako Yemwe adalenga (zolengedwa zonse).[460]
[460] Tanena kale mndemanga 7 yamu surat - Dhuha kuti Mneneri Muhammad (s.a.w) asadapatsidwe uneneri wake ndi Allah adali kudandaula kwambiri poona anthu ake ali osokera ndiponso poona kuti iye sadali kudziwa momwe angawaongolere. Pambuyo pake adali kumapita ku mapiri amene adali pafupi ndi Mzinda wa Makka. Kumeneko adali kupemphera ndi kumalingalira ndi kupempha Allah kuti amusonyeze njira ya chiongoko. Choncho tsiku lina pamene adali ku phanga la Hiraa, pafupi ndi Makka ali mkati mopemphera, Mngelo adamuonekera mwadzidzidzi nati: “Iwe Muhammad! Ine ndine Jiburil (Gabrie!) ndipo iwe ndiwe Mtumiki wa Allah kwa zolengedwa zonse!” Pambuyo pake adamuuza kuti: “werenga!” Mneneri adayankha: “Ine sindidziwa kuwerenga.” Jiburil uja adamgwira ndi kumpana mwamphamvu mpaka adavutika kwambiri. Adamsiyanso ndi kumuuza: “werenga!” Mneneri adayankha monga adamuyankhira poyamba mpaka kadakwana katatu akumuchita zokhazokhazo. Kenaka adamuwerengera ma Ayah kuchokera 1 mpaka 5. Ma Ayah amenewa ndiwo oyamba kuvumbulutsidwa m’Qur’an.
Esegesi in lingua araba:
 
Traduzione dei significati Versetto: (1) Sura: Al-‘Alaq
Indice delle Sure Numero di pagina
 
Traduzione dei Significati del Sacro Corano - Traduzione chicheŵa - Indice Traduzioni

Traduzione dei significati del Nobile Corano in lingua chicheŵa, a cura di Khaled Ibrahim Beitala، ed. 2020

Chiudi