Firo maanaaji al-quraan tedduɗo oo - Firo siisiiwo * - Tippudi firooji ɗii


Firo maanaaji Aaya: (181) Simoore: Simoore nagge
فَمَنۢ بَدَّلَهُۥ بَعۡدَ مَا سَمِعَهُۥ فَإِنَّمَآ إِثۡمُهُۥ عَلَى ٱلَّذِينَ يُبَدِّلُونَهُۥٓۚ إِنَّ ٱللَّهَ سَمِيعٌ عَلِيمٞ
Ndipo amene asinthe malangizowo pambuyo pakuwamva; uchimo wake uli pa amene akusinthawo. Ndithudi, Allah Ngwakumva; Ngodziwa.[18]
[18] Apa akuwachenjeza amene auzidwa wasiyawo kuti asasinthepo kanthu. Ndipo akunenetsa kuti ngati wasiyawo uwonongedwa ndiye kuti anthu omwe adalandira wasiyawo akhala ndi uchimo chifukwa chosintha wasiyawo. Koma ngati wasiyawo udalembedwa mopanda chilungamo, monga kuti iye adati: “Chuma changa m’dzawapatse ana anga aamuna okha basi,” nkusiya kutchulapo aakazi, apo Allah akuloleza olandira wasiyawo kuti aukonze ndi kuwagawira ana onsewo mwachilungamo.
Faccirooji aarabeeji:
 
Firo maanaaji Aaya: (181) Simoore: Simoore nagge
Tippudi cimooje Tonngoode hello ngoo
 
Firo maanaaji al-quraan tedduɗo oo - Firo siisiiwo - Tippudi firooji ɗii

Firo maanaaji al-quraan tedduɗo oo fayde e ɗemngal siisii, fari ɗum ko Kaaliid piitalaa. Tummbutere hitaande 2020

Uddude