Firo maanaaji al-quraan tedduɗo oo - Firo siisiiwo * - Tippudi firooji ɗii


Firo maanaaji Aaya: (1) Simoore: Simoore rewɓe

Simoore rewɓe

يَٰٓأَيُّهَا ٱلنَّاسُ ٱتَّقُواْ رَبَّكُمُ ٱلَّذِي خَلَقَكُم مِّن نَّفۡسٖ وَٰحِدَةٖ وَخَلَقَ مِنۡهَا زَوۡجَهَا وَبَثَّ مِنۡهُمَا رِجَالٗا كَثِيرٗا وَنِسَآءٗۚ وَٱتَّقُواْ ٱللَّهَ ٱلَّذِي تَسَآءَلُونَ بِهِۦ وَٱلۡأَرۡحَامَۚ إِنَّ ٱللَّهَ كَانَ عَلَيۡكُمۡ رَقِيبٗا
E inu anthu! Opani Mbuye wanu yemwe adakulengani kuchokera mwa munthu mmodzi (Adam) ndipo adalenga mmenemo mkazi wake (Hawa), ndipo adafalitsa amuna ndi akazi ambiri kuchokera mwa awiriwo. Ndipo opani Allah yemwe kupyolera mwa Iye mumapemphana. Ndipo (sungani) chibale. Ndithudi Allah Ndimyang’aniri pa inu (akuona chilichonse chimene muchita).[105]
[105] Ndime iyi ikulimbikitsa za kuopa Allah ndi kumulemekeza potsatira malamulo ake ndi kupewa zomwe Iye waletsa. Iye ndi amene adakulenga. Ndiyemwenso adalenga zonse zimene iwe adakulengera. Ngakhale iwe amene utafuna chithandizo kwa anzako umampempha ponena kuti: ‘‘Ndikukupempha m’dzina la Allah kuti undichitire chakuti.” Izi umachita poona kuti iye adzalemekeza dzina la Allah, ndipo adzakwaniritsa chomwe ukufunacho. Koma nanga bwanji ukuchita zimene Allah waletsa? Bwanji sukulemekeza lamulo lake pomwe iwe ukufuna kuti anthu achite zomwe sukuchita. Apa akutiuzanso kuti Allah akuona chilichonse chimene anthu ake akuchita, ngakhale chikhale chochepa chotani.
Faccirooji aarabeeji:
 
Firo maanaaji Aaya: (1) Simoore: Simoore rewɓe
Tippudi cimooje Tonngoode hello ngoo
 
Firo maanaaji al-quraan tedduɗo oo - Firo siisiiwo - Tippudi firooji ɗii

Firo maanaaji al-quraan tedduɗo oo fayde e ɗemngal siisii, fari ɗum ko Kaaliid piitalaa. Tummbutere hitaande 2020

Uddude