કુરઆન મજીદના શબ્દોનું ભાષાંતર - ચેવા ભાષાતર * - ભાષાંતરોની અનુક્રમણિકા


શબ્દોનું ભાષાંતર સૂરહ: અલ્ મુતફ્ફીન   આયત:

અલ્ મુતફ્ફીન

وَيۡلٞ لِّلۡمُطَفِّفِينَ
Kuonongeka koopsa kukawapeza opunguza miyeso ya malonda.
અરબી તફસીરો:
ٱلَّذِينَ إِذَا ٱكۡتَالُواْ عَلَى ٱلنَّاسِ يَسۡتَوۡفُونَ
Amene amati akamadziyezera zinthu kwa anthu amafuna kulandira miyeso yodzadza.
અરબી તફસીરો:
وَإِذَا كَالُوهُمۡ أَو وَّزَنُوهُمۡ يُخۡسِرُونَ
Koma pamene iwo akamawayesera pa muyeso wa mbale kapena wa sikelo amapungula (choyenera kulandira ogulawo).
અરબી તફસીરો:
أَلَا يَظُنُّ أُوْلَٰٓئِكَ أَنَّهُم مَّبۡعُوثُونَ
Kodi amenewa (akupungula miyeso pamalondawo) sakuganiza kuti adzaukitsidwa;
અરબી તફસીરો:
لِيَوۡمٍ عَظِيمٖ
Pa tsiku lalikulu (ndiponso loopsa)?
અરબી તફસીરો:
يَوۡمَ يَقُومُ ٱلنَّاسُ لِرَبِّ ٱلۡعَٰلَمِينَ
Tsiku limene adzaimilira anthu pamaso pa Mbuye wa zolengedwa.
અરબી તફસીરો:
كَلَّآ إِنَّ كِتَٰبَ ٱلۡفُجَّارِ لَفِي سِجِّينٖ
Ayi! Ndithu (siyani chinyengo pamalonda ndi kusalabadira kuuka mmanda); zolembedwa za ntchito ya oipa zili mu Sijjin.
અરબી તફસીરો:
وَمَآ أَدۡرَىٰكَ مَا سِجِّينٞ
Nanga nchiyani chitakudziwitse za Sijjin?
અરબી તફસીરો:
كِتَٰبٞ مَّرۡقُومٞ
Ameneyu ndi kaundula wamkulu yemwe walembedwa (mkati mwake ntchito za anthu oipa).
અરબી તફસીરો:
وَيۡلٞ يَوۡمَئِذٖ لِّلۡمُكَذِّبِينَ
Chilango chaukali tsiku limenelo chili pa otsutsa,[401]
[401] Kutsutsa kulipo kwa mitundu itatu:
(a) Kutsutsa kwa mawu ndi zochita;
(b) Kutsutsa kwa zochita zokha, monga ukauzidwa kuti chinthu ichi nchoipa, munthu nkudziwa kuti zoona nchoipadi koma nkudzachichita chimenecho mosalabadira;
(c) Kutsutsa ndi zolankhula zokha. Kumeneko ndiko monga munthu akudziwa kuti chakutichakuti ncholetsedwa (haramu) koma m’malo mwake iye nkumati chimenecho nchovomerezeka (halali)
અરબી તફસીરો:
ٱلَّذِينَ يُكَذِّبُونَ بِيَوۡمِ ٱلدِّينِ
Amene akutsutsa za tsiku la malipiro.
અરબી તફસીરો:
وَمَا يُكَذِّبُ بِهِۦٓ إِلَّا كُلُّ مُعۡتَدٍ أَثِيمٍ
Ndipo palibe angalitsutse koma yekhayo wopyola malire (pochita zoipa), wa machimo ambiri;
અરબી તફસીરો:
إِذَا تُتۡلَىٰ عَلَيۡهِ ءَايَٰتُنَا قَالَ أَسَٰطِيرُ ٱلۡأَوَّلِينَ
Pamene ma Ayah Athu akuwerengedwa kwa iye (onena za tsiku la malipiro ndikuuka mmanda) amanena kuti: “Izi ndi nthano za anthu akale.”
અરબી તફસીરો:
كَلَّاۖ بَلۡۜ رَانَ عَلَىٰ قُلُوبِهِم مَّا كَانُواْ يَكۡسِبُونَ
Iyayi, sichoncho! Koma yaphimbidwa mitima yawo ndi dzimbiri (la machimo) omwe akhala akukolola.[402]
[402] Munthu akachita choipa koyamba ndipo osalapa, limalowa dontho lakuda mu mtima mwake; nthawi iliyonse pamene akuonjezera machimo, dontho lija limakulirakulira mpaka kuuphimba mtima wonse. Dontho limeneli ndilo likutchedwa “Ran.” Tsono mtima ngati utaphimbidwa chotere sulabadira kuchita zoipa, ngakhale kuti auongole sungaongoke.
અરબી તફસીરો:
كَلَّآ إِنَّهُمۡ عَن رَّبِّهِمۡ يَوۡمَئِذٖ لَّمَحۡجُوبُونَ
Ayi ndithu iwo (okanira) tsiku limenelo) adzatchingidwa kwa Mbuye wawo; (sadzamuona).
અરબી તફસીરો:
ثُمَّ إِنَّهُمۡ لَصَالُواْ ٱلۡجَحِيمِ
Pambuyo pake adzalowa ku Moto; (oyaka)
અરબી તફસીરો:
ثُمَّ يُقَالُ هَٰذَا ٱلَّذِي كُنتُم بِهِۦ تُكَذِّبُونَ
Kenaka adzauzidwa (powaliritsa) “Ichi nchilango chomwe mudali kuchitsutsa (pa dziko lapansi).”
અરબી તફસીરો:
كَلَّآ إِنَّ كِتَٰبَ ٱلۡأَبۡرَارِ لَفِي عِلِّيِّينَ
Zoona, ndithu kaundula wa anthu abwino (ochita ntchito zabwino) ali mu Illiyyun.
અરબી તફસીરો:
وَمَآ أَدۡرَىٰكَ مَا عِلِّيُّونَ
Nanga nchiyani chitakudziwitse za Illiyyun?
અરબી તફસીરો:
كِتَٰبٞ مَّرۡقُومٞ
Ameneyu ndi kaundula (wamkulu) yemwe walembedwa (mkati mwake ntchito za anthu abwino);
અરબી તફસીરો:
يَشۡهَدُهُ ٱلۡمُقَرَّبُونَ
Amamuyikira umboni (angelo) amene ayandikitsidwa (kwa Allah).
અરબી તફસીરો:
إِنَّ ٱلۡأَبۡرَارَ لَفِي نَعِيمٍ
Ndithu ochita zabwino adzakhala mu mtendere,
અરબી તફસીરો:
عَلَى ٱلۡأَرَآئِكِ يَنظُرُونَ
Atakhala pa mipando ya ulemu uku akuyang’ana (zimene Allah wawapatsa monga mtendere ndi ulemelero).
અરબી તફસીરો:
تَعۡرِفُ فِي وُجُوهِهِمۡ نَضۡرَةَ ٱلنَّعِيمِ
Udzaona kuwala kwa mtendere pa nkhope zawo;
અરબી તફસીરો:
يُسۡقَوۡنَ مِن رَّحِيقٖ مَّخۡتُومٍ
Adzamwetsedwa vinyo (woyeretsedwa) wotsekeredwa ndi zitsekerero zolimba;
અરબી તફસીરો:
خِتَٰمُهُۥ مِسۡكٞۚ وَفِي ذَٰلِكَ فَلۡيَتَنَافَسِ ٱلۡمُتَنَٰفِسُونَ
Komalizira kwake (kwa vinyoyo) kuzikatuluka fungo la misk; kuti akapeze zimenezi, apikisane opikisana.[403]
[403] Apa, akutilamula kupikisana pakuchita zabwino kuti tipeze madalitso amene awakonzera anthu abwino. Kumeneko ndikuti munthu aliyense alimbikire kuchita mapemphero ndi zina zabwino.
અરબી તફસીરો:
وَمِزَاجُهُۥ مِن تَسۡنِيمٍ
Ndipo chosakanizira cha vinyoyo ndi madzi a Tasnim.
અરબી તફસીરો:
عَيۡنٗا يَشۡرَبُ بِهَا ٱلۡمُقَرَّبُونَ
(Tasnim ameneyo) ndi kasupe amene azikamwa amene ayandikitsidwa (kwa Allah.)
અરબી તફસીરો:
إِنَّ ٱلَّذِينَ أَجۡرَمُواْ كَانُواْ مِنَ ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ يَضۡحَكُونَ
Ndithu amene adachita machimo adali kuwaseka (mwachipongwe) okhulupirira (pa dziko lapansi);
અરબી તફસીરો:
وَإِذَا مَرُّواْ بِهِمۡ يَتَغَامَزُونَ
(Okhulupirira) akadutsa pafupi ndi iwo ankakodolerana maso (mwachipongwe);
અરબી તફસીરો:
وَإِذَا ٱنقَلَبُوٓاْ إِلَىٰٓ أَهۡلِهِمُ ٱنقَلَبُواْ فَكِهِينَ
Ndipo akabwerera kwa anzawo amabwerera akusangalala (ndi kunyozedwa kwa okhulupirira);
અરબી તફસીરો:
وَإِذَا رَأَوۡهُمۡ قَالُوٓاْ إِنَّ هَٰٓؤُلَآءِ لَضَآلُّونَ
Ndipo (nthawi zonse) akawaona Asilamu amanena: “Ndithu awa ndi osokera (chifukwa chomkhulupirira Mtumiki).” (s.a.w)
અરબી તફસીરો:
وَمَآ أُرۡسِلُواْ عَلَيۡهِمۡ حَٰفِظِينَ
Sanatumizidwe (Akafiri) kukhala ayang’aniri kwa okhulupirira (ndikuwaweruza zakulungama ndi kusokera).
અરબી તફસીરો:
فَٱلۡيَوۡمَ ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ مِنَ ٱلۡكُفَّارِ يَضۡحَكُونَ
Basi lero okhulupirira awaseka osakhulupirira (powabwezera chipongwe chawo chimene ankachita pa dziko lapansi),[404]
[404] (Ndime 34-36) Tanthauzo lake ndikuti okhulupilira, tsiku lachimaliziro adzakhala m’mipando ya ulemu uku akuwayang’ana ndi kuwaseka anthu osakhulupilira ali m’mavuto monga momwe iwo adali kuseka okhulupilira pa dziko lapansi.
અરબી તફસીરો:
عَلَى ٱلۡأَرَآئِكِ يَنظُرُونَ
Atakhala pa mipando ya ulemu uku akuyang’ana (mtendere umene Allah wawapatsa).
અરબી તફસીરો:
هَلۡ ثُوِّبَ ٱلۡكُفَّارُ مَا كَانُواْ يَفۡعَلُونَ
Kodi alipidwa osakhulupirira pa zomwe ankachita zija (pa dziko lapansi)?
અરબી તફસીરો:
 
શબ્દોનું ભાષાંતર સૂરહ: અલ્ મુતફ્ફીન
સૂરહ માટે અનુક્રમણિકા પેજ નંબર
 
કુરઆન મજીદના શબ્દોનું ભાષાંતર - ચેવા ભાષાતર - ભાષાંતરોની અનુક્રમણિકા

ચેવા ભાષાતરમાં

બંધ કરો