Traduzione dei Significati del Sacro Corano - Traduzione chicheŵa * - Indice Traduzioni


Traduzione dei significati Versetto: (7) Sura: An-Nisâ’
لِّلرِّجَالِ نَصِيبٞ مِّمَّا تَرَكَ ٱلۡوَٰلِدَانِ وَٱلۡأَقۡرَبُونَ وَلِلنِّسَآءِ نَصِيبٞ مِّمَّا تَرَكَ ٱلۡوَٰلِدَانِ وَٱلۡأَقۡرَبُونَ مِمَّا قَلَّ مِنۡهُ أَوۡ كَثُرَۚ نَصِيبٗا مَّفۡرُوضٗا
Amuna m’chuma chimene makolo ndi achibale asiya ali ndi gawo. Naonso akazi ali ndigawo m’chuma chimene asiya makolo ndi achibale (chapafupi), ngakhale chitakhala chochepa kapena chochuluka ndigawo logawidwa (ndi Allah)[110]
[110] Apa tsopano akufotokoza mmene chuma chamasiye angachigawire ponena kuti m’Chisilamu akazi akuwalola kuwagawirako chuma cha abale awo, osati kuti amuna okha ndiwo, owagawira. Koma gawo lomwe mkazi amapatsidwa limacheperapo poyerekeza ndi gawo lomwe mwamuna amalandira. Chifukwa chakuti mwamuna ndiye ali ndi udindo waukulu poyerekeza ndi mkazi. Mwamuna ali ndi udindo woyang’anira mkazi wake, ana ake ndi makolo ake. Koma mkazi alibe udindo woyang’anira mwamuna wake. Ndiponso alibe udindo woyang’anira mwana kapena makolo ake, pokhapokha ngati tate wa anawo ali wochepa nzeru. Zikatero mpomwe mkaziyo amakhala ndi udindo woyang’anira ana ake.
Esegesi in lingua araba:
 
Traduzione dei significati Versetto: (7) Sura: An-Nisâ’
Indice delle Sure Numero di pagina
 
Traduzione dei Significati del Sacro Corano - Traduzione chicheŵa - Indice Traduzioni

Traduzione dei significati del Nobile Corano in lingua chicheŵa, a cura di Khaled Ibrahim Beitala، ed. 2020

Chiudi