《古兰经》译解 - 契瓦语翻译 * - 译解目录


含义的翻译 段: (7) 章: 尼萨仪
لِّلرِّجَالِ نَصِيبٞ مِّمَّا تَرَكَ ٱلۡوَٰلِدَانِ وَٱلۡأَقۡرَبُونَ وَلِلنِّسَآءِ نَصِيبٞ مِّمَّا تَرَكَ ٱلۡوَٰلِدَانِ وَٱلۡأَقۡرَبُونَ مِمَّا قَلَّ مِنۡهُ أَوۡ كَثُرَۚ نَصِيبٗا مَّفۡرُوضٗا
Amuna m’chuma chimene makolo ndi achibale asiya ali ndi gawo. Naonso akazi ali ndigawo m’chuma chimene asiya makolo ndi achibale (chapafupi), ngakhale chitakhala chochepa kapena chochuluka ndigawo logawidwa (ndi Allah)[110]
[110] Apa tsopano akufotokoza mmene chuma chamasiye angachigawire ponena kuti m’Chisilamu akazi akuwalola kuwagawirako chuma cha abale awo, osati kuti amuna okha ndiwo, owagawira. Koma gawo lomwe mkazi amapatsidwa limacheperapo poyerekeza ndi gawo lomwe mwamuna amalandira. Chifukwa chakuti mwamuna ndiye ali ndi udindo waukulu poyerekeza ndi mkazi. Mwamuna ali ndi udindo woyang’anira mkazi wake, ana ake ndi makolo ake. Koma mkazi alibe udindo woyang’anira mwamuna wake. Ndiponso alibe udindo woyang’anira mwana kapena makolo ake, pokhapokha ngati tate wa anawo ali wochepa nzeru. Zikatero mpomwe mkaziyo amakhala ndi udindo woyang’anira ana ake.
阿拉伯语经注:
 
含义的翻译 段: (7) 章: 尼萨仪
章节目录 页码
 
《古兰经》译解 - 契瓦语翻译 - 译解目录

古兰经契瓦文译解,哈利德·伊布拉欣·比德拉翻译,2020年版

关闭