Përkthimi i kuptimeve të Kuranit Fisnik - الترجمة الشيشيوا * - Përmbajtja e përkthimeve


Përkthimi i kuptimeve Ajeti: (7) Surja: Suretu En Nisa
لِّلرِّجَالِ نَصِيبٞ مِّمَّا تَرَكَ ٱلۡوَٰلِدَانِ وَٱلۡأَقۡرَبُونَ وَلِلنِّسَآءِ نَصِيبٞ مِّمَّا تَرَكَ ٱلۡوَٰلِدَانِ وَٱلۡأَقۡرَبُونَ مِمَّا قَلَّ مِنۡهُ أَوۡ كَثُرَۚ نَصِيبٗا مَّفۡرُوضٗا
Amuna m’chuma chimene makolo ndi achibale asiya ali ndi gawo. Naonso akazi ali ndigawo m’chuma chimene asiya makolo ndi achibale (chapafupi), ngakhale chitakhala chochepa kapena chochuluka ndigawo logawidwa (ndi Allah)[110]
[110] Apa tsopano akufotokoza mmene chuma chamasiye angachigawire ponena kuti m’Chisilamu akazi akuwalola kuwagawirako chuma cha abale awo, osati kuti amuna okha ndiwo, owagawira. Koma gawo lomwe mkazi amapatsidwa limacheperapo poyerekeza ndi gawo lomwe mwamuna amalandira. Chifukwa chakuti mwamuna ndiye ali ndi udindo waukulu poyerekeza ndi mkazi. Mwamuna ali ndi udindo woyang’anira mkazi wake, ana ake ndi makolo ake. Koma mkazi alibe udindo woyang’anira mwamuna wake. Ndiponso alibe udindo woyang’anira mwana kapena makolo ake, pokhapokha ngati tate wa anawo ali wochepa nzeru. Zikatero mpomwe mkaziyo amakhala ndi udindo woyang’anira ana ake.
Tefsiret në gjuhën arabe:
 
Përkthimi i kuptimeve Ajeti: (7) Surja: Suretu En Nisa
Përmbajtja e sureve Numri i faqes
 
Përkthimi i kuptimeve të Kuranit Fisnik - الترجمة الشيشيوا - Përmbajtja e përkthimeve

ترجمة معاني القرآن الكريم إلى اللغة الشيشيوا، ترجمها خالد إبراهيم بيتالا. نسخة عام 2020م.

Mbyll