クルアーンの対訳 - チェワ語対訳 * - 対訳の目次


対訳 節: (108) 章: ユースフ章
قُلۡ هَٰذِهِۦ سَبِيلِيٓ أَدۡعُوٓاْ إِلَى ٱللَّهِۚ عَلَىٰ بَصِيرَةٍ أَنَا۠ وَمَنِ ٱتَّبَعَنِيۖ وَسُبۡحَٰنَ ٱللَّهِ وَمَآ أَنَا۠ مِنَ ٱلۡمُشۡرِكِينَ
Nena: “Iyi ndi njira yanga. Ndikuitanira kwa Allah mwa nzeru zokwanira, ine ndi omwe akunditsata. Ndithu Allah wapatukana (ndi mbiri zopunguka). Ndipo ine sindili mwa ophatikiza (Allah ndi zinthu zina).”[235]
[235] Apa Mtumiki (s.a.w) akuuzidwa kuti awauze anthu kuti iye pamodzi ndi amene akumutsata kuti amalalikira Chisilamu kwa anthu popereka kwa anthuwo mitsutso yanzeru, ndikuperekanso zisonyezo ndi maumboni amphamvu. Sibwino Msilamu kutsatira chinthu popanda kuchidziwa bwinobwino. Qur’an ikunenetsa kuti osatsatira chinthu popanda kuchidziwa bwinobwino pokhapokha chinthucho chitanenedwa ndi Allah kapena Mtumiki Wake.
アラビア語 クルアーン注釈:
 
対訳 節: (108) 章: ユースフ章
章名の目次 ページ番号
 
クルアーンの対訳 - チェワ語対訳 - 対訳の目次

クルアーン・チェワ語対訳 - Khalid Ibrahim

閉じる