クルアーンの対訳 - チェワ語対訳 * - 対訳の目次


対訳 節: (19) 章: ユースフ章
وَجَآءَتۡ سَيَّارَةٞ فَأَرۡسَلُواْ وَارِدَهُمۡ فَأَدۡلَىٰ دَلۡوَهُۥۖ قَالَ يَٰبُشۡرَىٰ هَٰذَا غُلَٰمٞۚ وَأَسَرُّوهُ بِضَٰعَةٗۚ وَٱللَّهُ عَلِيمُۢ بِمَا يَعۡمَلُونَ
Ndipo aulendo adadza (pafupi ndi chitsimecho) ndipo adatuma wotunga madzi wawo, choncho iye adaponya ndowa yake (m’chitsime, ndipo akukoka ndowa ija adaona mwana) nati: “Eee, chisangalalo changa! Aka kamwana kakamuna!” Pomwepo iwo (amene adalipo pa chitsimepo) adam’bisa (kwa a paulendo anzawo) monga katundu wamalonda (yemwe adamgula). Koma Allah ankadziwa zimene adali kuchita (ndipo adanka naye ku Iguputo).[230]
[230] 19-20. Apa tikuona kuti kugulitsana anthu kudayambika kalekale zedi kuyambira zaka 4,000 zapitazo mu nthawi ya umbuli. Koma adani achipembedzo cha Chisilamu akuchinamizira Chisilamu kuti ndicho chidadza ndi ukapolo wogulitsa anthu. Chikhalirecho Chisilamu ndicho chidadza kuzalimbikitsa zopereka ufulu kwa kapolo.
アラビア語 クルアーン注釈:
 
対訳 節: (19) 章: ユースフ章
章名の目次 ページ番号
 
クルアーンの対訳 - チェワ語対訳 - 対訳の目次

クルアーン・チェワ語対訳 - Khalid Ibrahim

閉じる