Vertaling van de betekenissen Edele Qur'an - Chewa vertaling * - Index van vertaling


Vertaling van de betekenissen Vers: (153) Surah: Soerat Albaqarah (De Koe)
يَٰٓأَيُّهَا ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ ٱسۡتَعِينُواْ بِٱلصَّبۡرِ وَٱلصَّلَوٰةِۚ إِنَّ ٱللَّهَ مَعَ ٱلصَّٰبِرِينَ
E inu amene mwakhulupirira! Dzithandizeni (pa zinthu zanu) popirira, ndi popemphera Swala. Ndithudi, Allah ali pamodzi ndi opirira. [7]
[7] M’ndimeyi Allah akulangiza Asilamu kuti akhale opilira pa masautso amtundu uliwonse amene akukumana nawo. Kupilira ndi chida chakuthwa chopambanitsa munthu ndi kugonjetsera masautso. Munthu wosapilira ndi zopweteka sangapambane pa zofuna zake. Allah akutilangizanso kuti tifunefune chithandizo pochulukitsa Swala chifukwa chakuti imalimbitsa mtima wa munthu pa masautso. Mtumiki (s.a.w) ankati masautso akamukhudza amachita changu kukapemphera Swala. Ndipo ankayankhula kuti: “Allah waupanga mpumulo wanga kukhala mkati mwa Swala.”
Arabische uitleg van de Qur'an:
 
Vertaling van de betekenissen Vers: (153) Surah: Soerat Albaqarah (De Koe)
Surah's Index Pagina nummer
 
Vertaling van de betekenissen Edele Qur'an - Chewa vertaling - Index van vertaling

De vertaling van de betekenissen van de Heilige Quran in de Chewa-taal, vertaald door Khaled Ibrahim Bitalla. Editie van 2020.

Sluit