Bản dịch ý nghĩa nội dung Qur'an - Dịch thuật tiếng Chichio * - Mục lục các bản dịch


Ý nghĩa nội dung Câu: (153) Chương: Chương Al-Baqarah
يَٰٓأَيُّهَا ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ ٱسۡتَعِينُواْ بِٱلصَّبۡرِ وَٱلصَّلَوٰةِۚ إِنَّ ٱللَّهَ مَعَ ٱلصَّٰبِرِينَ
E inu amene mwakhulupirira! Dzithandizeni (pa zinthu zanu) popirira, ndi popemphera Swala. Ndithudi, Allah ali pamodzi ndi opirira. [7]
[7] M’ndimeyi Allah akulangiza Asilamu kuti akhale opilira pa masautso amtundu uliwonse amene akukumana nawo. Kupilira ndi chida chakuthwa chopambanitsa munthu ndi kugonjetsera masautso. Munthu wosapilira ndi zopweteka sangapambane pa zofuna zake. Allah akutilangizanso kuti tifunefune chithandizo pochulukitsa Swala chifukwa chakuti imalimbitsa mtima wa munthu pa masautso. Mtumiki (s.a.w) ankati masautso akamukhudza amachita changu kukapemphera Swala. Ndipo ankayankhula kuti: “Allah waupanga mpumulo wanga kukhala mkati mwa Swala.”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
 
Ý nghĩa nội dung Câu: (153) Chương: Chương Al-Baqarah
Mục lục các chương Kinh Số trang
 
Bản dịch ý nghĩa nội dung Qur'an - Dịch thuật tiếng Chichio - Mục lục các bản dịch

Bản dịch ý nghĩa nội dung Kinh Qur'an bằng tiếng Chichio, do Khalid Ibrahim Petala dịch thuật, bản dịch năm 2020.

Đóng lại