د قرآن کریم د معناګانو ژباړه - چیچوایي ژباړه * - د ژباړو فهرست (لړلیک)


د معناګانو ژباړه سورت: الشعراء   آیت:

الشعراء

طسٓمٓ
Tâ-Sîn-Mîm.
عربي تفسیرونه:
تِلۡكَ ءَايَٰتُ ٱلۡكِتَٰبِ ٱلۡمُبِينِ
Izi ndi Ayah (ndime) za buku (la Qur’an) lofotokoza chilichonse (chofunika m’chipembedzo).
عربي تفسیرونه:
لَعَلَّكَ بَٰخِعٞ نَّفۡسَكَ أَلَّا يَكُونُواْ مُؤۡمِنِينَ
Mwina iwe (Mtumiki Muhammad {s.a.w}) udziononga wekha (ndi madandaulo) chifukwa chakuti (iwo) sadakhale okhulupirira.
عربي تفسیرونه:
إِن نَّشَأۡ نُنَزِّلۡ عَلَيۡهِم مِّنَ ٱلسَّمَآءِ ءَايَةٗ فَظَلَّتۡ أَعۡنَٰقُهُمۡ لَهَا خَٰضِعِينَ
Tikadafuna, tikadawatsitsira chizizwa kuchokera kumwamba; kotero kuti makosi awo akadadzichepetsa ndi chizizwacho, (sakadatha kucheukira kwina koma sitifuna kukakamiza anthu kuti akhale Asilamu).[295]
[295] Mtumiki Muhammad (s.a.w) adali kuwawidwa mtima kwambiri poona kuti anthu sakuvomereza uthenga wachoonadi umene iye adadza nawo, ndipo adali kuwamvera chisoni kwambiri. Choncho Allah adamtonthoza pomuuza kuti: “Usadziphe wekha chifukwa chokhala ndi maganizo owamvera chisoni.” Allah akadafuna kuwaongola mowakakamiza akadatha kutero; koma sadafune.
عربي تفسیرونه:
وَمَا يَأۡتِيهِم مِّن ذِكۡرٖ مِّنَ ٱلرَّحۡمَٰنِ مُحۡدَثٍ إِلَّا كَانُواْ عَنۡهُ مُعۡرِضِينَ
Ndipo palibe pamene chikuwadzera chivumbulutso chatsopano chochokera kwa (Allah) Wachifundo chambiri koma amazipatula ku icho (chivumbulutso).
عربي تفسیرونه:
فَقَدۡ كَذَّبُواْ فَسَيَأۡتِيهِمۡ أَنۢبَٰٓؤُاْ مَا كَانُواْ بِهِۦ يَسۡتَهۡزِءُونَ
Ndithu atsutsa; choncho posachedwapa ziwadzera nkhani zomwe adali kuzichitira chipongwe.
عربي تفسیرونه:
أَوَلَمۡ يَرَوۡاْ إِلَى ٱلۡأَرۡضِ كَمۡ أَنۢبَتۡنَا فِيهَا مِن كُلِّ زَوۡجٖ كَرِيمٍ
Kodi sadaone nthaka? Ndimmera ungati taumeretsa m’menemo kuchokera mu mtundu ulionse, wokongola?
عربي تفسیرونه:
إِنَّ فِي ذَٰلِكَ لَأٓيَةٗۖ وَمَا كَانَ أَكۡثَرُهُم مُّؤۡمِنِينَ
Ndithu m’zimenezo muli zizindikiro (zosonyeza mphamvu za Allah). Koma ambiri a iwo sali okhulupirira.
عربي تفسیرونه:
وَإِنَّ رَبَّكَ لَهُوَ ٱلۡعَزِيزُ ٱلرَّحِيمُ
Ndipo, ndithu Mbuye wako ndi Mwini mphamvu zoposa; Wachisoni chosatha.
عربي تفسیرونه:
وَإِذۡ نَادَىٰ رَبُّكَ مُوسَىٰٓ أَنِ ٱئۡتِ ٱلۡقَوۡمَ ٱلظَّٰلِمِينَ
Ndipo (akumbutse) pamene Mbuye wako adaitana (m’neneri) Mûsa; adamuuza: “Pita kwa anthu ochita zoipa.”
عربي تفسیرونه:
قَوۡمَ فِرۡعَوۡنَۚ أَلَا يَتَّقُونَ
Anthu a Farawo; (auze): “Kodi sawopa (Allah)?”
عربي تفسیرونه:
قَالَ رَبِّ إِنِّيٓ أَخَافُ أَن يُكَذِّبُونِ
(Mûsa) adati: “Mbuye wanga! Ine ndikuopa kuti anganditsutse.
عربي تفسیرونه:
وَيَضِيقُ صَدۡرِي وَلَا يَنطَلِقُ لِسَانِي فَأَرۡسِلۡ إِلَىٰ هَٰرُونَ
Ndipo chingabanike chifuwa changa (ndi maganizo, chifukwa chakunditsutsa kwawo); ndiponso lirime langa siliyankhula momveka bwino. Choncho tumizaninso uthengawu kwa Harun (kuti tikhale awiri ndipo azikandithangata pantchito yangayi).
عربي تفسیرونه:
وَلَهُمۡ عَلَيَّ ذَنۢبٞ فَأَخَافُ أَن يَقۡتُلُونِ
Ndipo iwowo ndili nawo mlandu ndipo ndikuopa kuti angandiphe (pobwezera chimene ndidawalakwira powaphera munthu wawo).
عربي تفسیرونه:
قَالَ كَلَّاۖ فَٱذۡهَبَا بِـَٔايَٰتِنَآۖ إِنَّا مَعَكُم مُّسۡتَمِعُونَ
(Allah) adati: “Iyayi! Pitani pamodzi ndi zozizwa Zathu; ndithu Ife tikakhala nanu limodzi (pokuthangatani) uku tikumvetsera (zimene azikanena).”
عربي تفسیرونه:
فَأۡتِيَا فِرۡعَوۡنَ فَقُولَآ إِنَّا رَسُولُ رَبِّ ٱلۡعَٰلَمِينَ
“Choncho mpitireni Farawo, ndipo kamuuzeni kuti: “Ife ndi atumiki a Mbuye wa zolengedwa zonse.”
عربي تفسیرونه:
أَنۡ أَرۡسِلۡ مَعَنَا بَنِيٓ إِسۡرَٰٓءِيلَ
“(Tatumidwa) kuti uwapereke kwa ife ana a Israyeli (kuti tinke nawo ku Sham).”
عربي تفسیرونه:
قَالَ أَلَمۡ نُرَبِّكَ فِينَا وَلِيدٗا وَلَبِثۡتَ فِينَا مِنۡ عُمُرِكَ سِنِينَ
(Farawo) adati (kwa Mûsa): “Kodi sitidakulere kwathu uli mwana, ndi kukhala nafe pa moyo wako zaka zambiri?”
عربي تفسیرونه:
وَفَعَلۡتَ فَعۡلَتَكَ ٱلَّتِي فَعَلۡتَ وَأَنتَ مِنَ ٱلۡكَٰفِرِينَ
“Ndipo udachita chochita chako chimene udachichita, ndipo iwe ndiwe mmodzi wa osathokoza!”
عربي تفسیرونه:
قَالَ فَعَلۡتُهَآ إِذٗا وَأَنَا۠ مِنَ ٱلضَّآلِّينَ
(Mûsa) adati: “Ndidachita zimenezo pomwe ine ndidali mmodzi wa osazindikira zinthu.”
عربي تفسیرونه:
فَفَرَرۡتُ مِنكُمۡ لَمَّا خِفۡتُكُمۡ فَوَهَبَ لِي رَبِّي حُكۡمٗا وَجَعَلَنِي مِنَ ٱلۡمُرۡسَلِينَ
“Choncho ndidakuthawani pomwe ndidakuopani; tsono Mbuye wanga wandipatsa nzeru zoweruzira (zinthu), ndi kundisankha kukhala mmodzi wa atumiki.”
عربي تفسیرونه:
وَتِلۡكَ نِعۡمَةٞ تَمُنُّهَا عَلَيَّ أَنۡ عَبَّدتَّ بَنِيٓ إِسۡرَٰٓءِيلَ
“Ndipo kodi umenewu ndimtendere wonditonzera pomwe mudawaika muukapolo ana a Israyeli!”
عربي تفسیرونه:
قَالَ فِرۡعَوۡنُ وَمَا رَبُّ ٱلۡعَٰلَمِينَ
Farawo adati: “Kodi ndani Mbuye wa zolengedwayo?”
عربي تفسیرونه:
قَالَ رَبُّ ٱلسَّمَٰوَٰتِ وَٱلۡأَرۡضِ وَمَا بَيۡنَهُمَآۖ إِن كُنتُم مُّوقِنِينَ
(Mûsa) adati: “Mbuye wa thambo ndi nthaka ndi zapakati pake, ngati muli ndi chitsimikizo. (Amachita chilichonse m’menemo mmene wafunira; kupereka moyo ndi imfa).”
عربي تفسیرونه:
قَالَ لِمَنۡ حَوۡلَهُۥٓ أَلَا تَسۡتَمِعُونَ
(Farawo) adauza omwe adali m’mphepete mwake (mwachipongwe): “Kodi simukumva (mawu achibwanawa)?”
عربي تفسیرونه:
قَالَ رَبُّكُمۡ وَرَبُّ ءَابَآئِكُمُ ٱلۡأَوَّلِينَ
(Mûsa adapitiriza kunena) adati: “Allah ndi Mbuye wanu komanso Mbuye wamakolo anu oyamba.”
عربي تفسیرونه:
قَالَ إِنَّ رَسُولَكُمُ ٱلَّذِيٓ أُرۡسِلَ إِلَيۡكُمۡ لَمَجۡنُونٞ
(Farawo) adati (kwa anthu ake pofuna kuwakwiitsa): “Ndithu Mtumiki wanu amene watumidwa kwa inu, ngwamisala.”
عربي تفسیرونه:
قَالَ رَبُّ ٱلۡمَشۡرِقِ وَٱلۡمَغۡرِبِ وَمَا بَيۡنَهُمَآۖ إِن كُنتُمۡ تَعۡقِلُونَ
(Mûsa) adati: “Mbuye wakuvuma ndi kuzambwe, ndi zomwe ziri pakati pake ngati mumazindikira (zinthu, muzindikira izi).”
عربي تفسیرونه:
قَالَ لَئِنِ ٱتَّخَذۡتَ إِلَٰهًا غَيۡرِي لَأَجۡعَلَنَّكَ مِنَ ٱلۡمَسۡجُونِينَ
(Farawo) adati: “Ngati udzipangira mulungu wina kusiya ine, ndikuchita kukhala mmodzi wa omangidwa kundende.”
عربي تفسیرونه:
قَالَ أَوَلَوۡ جِئۡتُكَ بِشَيۡءٖ مُّبِينٖ
(Mûsa) adati: “Kodi ngakhale nditakubweretsera chinthu choonekera poyera (chosonyeza kuti zimene ndikunenazi ndizoona ndatumidwa ndi Allah)?”
عربي تفسیرونه:
قَالَ فَأۡتِ بِهِۦٓ إِن كُنتَ مِنَ ٱلصَّٰدِقِينَ
(Farawo) adati: “Chibweretse, ngati uli mwa onena zoona.”
عربي تفسیرونه:
فَأَلۡقَىٰ عَصَاهُ فَإِذَا هِيَ ثُعۡبَانٞ مُّبِينٞ
Ndipo (Mûsa) adaponya (pansi) ndodo yake, mwadzidzidzi idasanduka njoka yopenyeka.
عربي تفسیرونه:
وَنَزَعَ يَدَهُۥ فَإِذَا هِيَ بَيۡضَآءُ لِلنَّٰظِرِينَ
Ndipo adatulutsa dzanja lake; pompo lidali loyera (kwambiri) kwa (onse) openya.
عربي تفسیرونه:
قَالَ لِلۡمَلَإِ حَوۡلَهُۥٓ إِنَّ هَٰذَا لَسَٰحِرٌ عَلِيمٞ
(Farawo) adauza akuluakulu omwe adali m’mphepete mwake: “Ndithu uyu ndi wamatsenga wodziwa kwambiri.”
عربي تفسیرونه:
يُرِيدُ أَن يُخۡرِجَكُم مِّنۡ أَرۡضِكُم بِسِحۡرِهِۦ فَمَاذَا تَأۡمُرُونَ
“Akufuna kukutulutsani m’dziko lanu ndi matsenga ake; kodi nanga mukuti chiyani?”[296]
[296] Farawo adasimidwa, adatha nzeru zedi ndi mawu amene adali kutuluka m’kamwa mwa Musa kotero kuti adangoti kakasi, kusowa chonena, nayamba kuwafunsa nzeru ndi malangizo anthu ake pomwe iye ankadzitcha kuti ndi mulungu wodziwa zonse, wamphamvu zoposa.
عربي تفسیرونه:
قَالُوٓاْ أَرۡجِهۡ وَأَخَاهُ وَٱبۡعَثۡ فِي ٱلۡمَدَآئِنِ حَٰشِرِينَ
(Anthu) adati (kwa Farawo): “Mpatse nthawi ndi m’bale wakeyo, ndipo tumiza (amithenga) m’mizinda yonse osonkhanitsa anthu.”
عربي تفسیرونه:
يَأۡتُوكَ بِكُلِّ سَحَّارٍ عَلِيمٖ
“Ndipo akubweretsera amatsenga onse odziwa kwabasi (kotero kuti adzampambana Mûsa).”
عربي تفسیرونه:
فَجُمِعَ ٱلسَّحَرَةُ لِمِيقَٰتِ يَوۡمٖ مَّعۡلُومٖ
Choncho amatsenga adasonkhanitsidwa mu nthawi ya tsiku lodziwika.
عربي تفسیرونه:
وَقِيلَ لِلنَّاسِ هَلۡ أَنتُم مُّجۡتَمِعُونَ
Ndipo anthu adauzidwa: “Kodi inu musonkhana? (Choncho, sonkhanani).”
عربي تفسیرونه:
لَعَلَّنَا نَتَّبِعُ ٱلسَّحَرَةَ إِن كَانُواْ هُمُ ٱلۡغَٰلِبِينَ
“Mwina tingawatsatire amatsenga ngati iwo ndiamene apambane.”
عربي تفسیرونه:
فَلَمَّا جَآءَ ٱلسَّحَرَةُ قَالُواْ لِفِرۡعَوۡنَ أَئِنَّ لَنَا لَأَجۡرًا إِن كُنَّا نَحۡنُ ٱلۡغَٰلِبِينَ
Ndipo pamene amatsenga adadza, adati kwa Farawo: “Kodi tidzakhala ndi mphoto ngati ife ndife tipambane?”
عربي تفسیرونه:
قَالَ نَعَمۡ وَإِنَّكُمۡ إِذٗا لَّمِنَ ٱلۡمُقَرَّبِينَ
(Farawo) adati: “Inde, (ndipo kuonjezera apo) ndithu inu mudzakhala mwa amene amakhala pafupi (ndi ine, monga nduna zanga).”
عربي تفسیرونه:
قَالَ لَهُم مُّوسَىٰٓ أَلۡقُواْ مَآ أَنتُم مُّلۡقُونَ
Mûsa adati kwa iwo: “Ponyani zimene mufuna kuponya (zosonyeza kuya kwa matsenga anu).”
عربي تفسیرونه:
فَأَلۡقَوۡاْ حِبَالَهُمۡ وَعِصِيَّهُمۡ وَقَالُواْ بِعِزَّةِ فِرۡعَوۡنَ إِنَّا لَنَحۡنُ ٱلۡغَٰلِبُونَ
Choncho adaponya zingwe zawo ndi ndodo zawo, ndipo adati: “Kupyolera mu mphamvu za Farawo, ndithu ife ndife opambana.”
عربي تفسیرونه:
فَأَلۡقَىٰ مُوسَىٰ عَصَاهُ فَإِذَا هِيَ تَلۡقَفُ مَا يَأۡفِكُونَ
Kenako Mûsa adaponya ndodo yake; mwadzidzidzi iyo idameza zabodza zomwe iwo adakonza.
عربي تفسیرونه:
فَأُلۡقِيَ ٱلسَّحَرَةُ سَٰجِدِينَ
Pamenepo amatsenga adadzigwetsa pansi molambira.
عربي تفسیرونه:
قَالُوٓاْ ءَامَنَّا بِرَبِّ ٱلۡعَٰلَمِينَ
Adati: “Tamkhulupirira Mbuye wa zolengedwa.”
عربي تفسیرونه:
رَبِّ مُوسَىٰ وَهَٰرُونَ
“Mbuye wa Mûsa ndi Harun.”
عربي تفسیرونه:
قَالَ ءَامَنتُمۡ لَهُۥ قَبۡلَ أَنۡ ءَاذَنَ لَكُمۡۖ إِنَّهُۥ لَكَبِيرُكُمُ ٱلَّذِي عَلَّمَكُمُ ٱلسِّحۡرَ فَلَسَوۡفَ تَعۡلَمُونَۚ لَأُقَطِّعَنَّ أَيۡدِيَكُمۡ وَأَرۡجُلَكُم مِّنۡ خِلَٰفٖ وَلَأُصَلِّبَنَّكُمۡ أَجۡمَعِينَ
(Farawo) adati: “Ha! Mwamkhulupirira chotani ndisanakulolezeni? Ndithu iyeyu ndimkulu wanu amene adakuphunzitsani matsenga. Choncho posachedwa mudziwa (chimene ndikuchiteni) ndithu ndidula manja anu ndi miyendo yanu mosinthanitsa (podula mkono wakumanja ndi mwendo wakumanzere; kapena kudula mkono wakumanzere ndi mwendo wakumanja), ndipo kenako ndikupachikani nonsenu.”
عربي تفسیرونه:
قَالُواْ لَا ضَيۡرَۖ إِنَّآ إِلَىٰ رَبِّنَا مُنقَلِبُونَ
(Amatsenga) adati: “Palibe vuto, ndithu ife (tonse) tibwerera kwa Mbuye wathu.”
عربي تفسیرونه:
إِنَّا نَطۡمَعُ أَن يَغۡفِرَ لَنَا رَبُّنَا خَطَٰيَٰنَآ أَن كُنَّآ أَوَّلَ ٱلۡمُؤۡمِنِينَ
“Ndithu ife tikuyembekezera kuti Mbuye wathu atikhululukire zolakwa zathu; pokhala oyamba mwa okhulupirira.”
عربي تفسیرونه:
۞ وَأَوۡحَيۡنَآ إِلَىٰ مُوسَىٰٓ أَنۡ أَسۡرِ بِعِبَادِيٓ إِنَّكُم مُّتَّبَعُونَ
Ndipo tidamvumbulutsira Mûsa (kuti): “Pita ndi anthu anga m’nthawi yausiku (musamuke m’dziko la Iguputo); ndithu inu mutsatidwa.”
عربي تفسیرونه:
فَأَرۡسَلَ فِرۡعَوۡنُ فِي ٱلۡمَدَآئِنِ حَٰشِرِينَ
Choncho Farawo adatuma (owatuma) kuti asonkhanitse anthu m’mizinda (kuti aletse ana a Israyeli kutuluka).
عربي تفسیرونه:
إِنَّ هَٰٓؤُلَآءِ لَشِرۡذِمَةٞ قَلِيلُونَ
(Adawauza otumidwa aja kuti auze anthu kuti): “Ndithu awa (ana a Israyeli) ndikagulu kochepa.
عربي تفسیرونه:
وَإِنَّهُمۡ لَنَا لَغَآئِظُونَ
Ndipo ndithu iwo akutikwiitsa.
عربي تفسیرونه:
وَإِنَّا لَجَمِيعٌ حَٰذِرُونَ
Koma ndithu ife tonse (ndife ochuluka komabe ngakhale zili choncho) tikuwaopa.”
عربي تفسیرونه:
فَأَخۡرَجۡنَٰهُم مِّن جَنَّٰتٖ وَعُيُونٖ
Choncho tidawatulutsa m’minda ndi mwa akasupe.
عربي تفسیرونه:
وَكُنُوزٖ وَمَقَامٖ كَرِيمٖ
Ndi m’nkhokwe za chuma ndi m’malo okongola.
عربي تفسیرونه:
كَذَٰلِكَۖ وَأَوۡرَثۡنَٰهَا بَنِيٓ إِسۡرَٰٓءِيلَ
Momwemo ndi mmene tidawachitira ndipo tidawalowetsera chokolo zinthu zawo zonse kwa ana a Israyeli.
عربي تفسیرونه:
فَأَتۡبَعُوهُم مُّشۡرِقِينَ
Choncho (anthu a Farawo ndi iye mwini) adawatsatira (ana a Israyeli) dzuwa litatuluka.
عربي تفسیرونه:
فَلَمَّا تَرَٰٓءَا ٱلۡجَمۡعَانِ قَالَ أَصۡحَٰبُ مُوسَىٰٓ إِنَّا لَمُدۡرَكُونَ
Ndipo pamene magulu awiri adaonana (anthu a Farawo ndi anthu a Mûsa), anthu a Mûsa adati: “Ndithu ife tigwidwa.”
عربي تفسیرونه:
قَالَ كَلَّآۖ إِنَّ مَعِيَ رَبِّي سَيَهۡدِينِ
(Mûsa) adati: “Iyayi! Ndithu Mbuye wanga ali nane pamodzi. Andiongolera (kuti ife tonse tipulumuke).”
عربي تفسیرونه:
فَأَوۡحَيۡنَآ إِلَىٰ مُوسَىٰٓ أَنِ ٱضۡرِب بِّعَصَاكَ ٱلۡبَحۡرَۖ فَٱنفَلَقَ فَكَانَ كُلُّ فِرۡقٖ كَٱلطَّوۡدِ ٱلۡعَظِيمِ
Ndipo tidam’vumbulutsira mawu Mûsa (akuti): “Menya nyanja ndi ndodo yako.” Ndipo idagawikana, mbali iliyonse idali ngati phiri lalikulu.
عربي تفسیرونه:
وَأَزۡلَفۡنَا ثَمَّ ٱلۡأٓخَرِينَ
Ndipo tidawayandikitsa pamenepo anthu enawo, (Farawo ndi anthu ake nalowa pa njira yomweyo pambuyo pa Mûsa ndi anthu ake).
عربي تفسیرونه:
وَأَنجَيۡنَا مُوسَىٰ وَمَن مَّعَهُۥٓ أَجۡمَعِينَ
Ndipo tidapulumutsa Mûsa ndi onse amene adali nawo (mpaka adaoloka nyanjayo, madzi ali chiimire mbali iyi ndi iyi).
عربي تفسیرونه:
ثُمَّ أَغۡرَقۡنَا ٱلۡأٓخَرِينَ
Kenako tidawamiza enawo, (Farawo ndi anthu ake).
عربي تفسیرونه:
إِنَّ فِي ذَٰلِكَ لَأٓيَةٗۖ وَمَا كَانَ أَكۡثَرُهُم مُّؤۡمِنِينَ
Ndithu pa zimenezi pali lingaliro. Koma ambiri a iwo sali okhulupirira.
عربي تفسیرونه:
وَإِنَّ رَبَّكَ لَهُوَ ٱلۡعَزِيزُ ٱلرَّحِيمُ
Ndipo, ndithu Mbuye wako ndi Mwini mphamvu zoposa (amalanga ndi chilango choopsa omwe amunyoza); Wachisoni (kwa omkhulupirira ndi kumumvera).
عربي تفسیرونه:
وَٱتۡلُ عَلَيۡهِمۡ نَبَأَ إِبۡرَٰهِيمَ
Ndipo awerengere (osakhulupirira) nkhani ya (M’neneri) Ibrahim.
عربي تفسیرونه:
إِذۡ قَالَ لِأَبِيهِ وَقَوۡمِهِۦ مَا تَعۡبُدُونَ
Pamene adafunsa bambo wake ndi anthu ake (kuti); “Kodi mukupembedza chiyani?”
عربي تفسیرونه:
قَالُواْ نَعۡبُدُ أَصۡنَامٗا فَنَظَلُّ لَهَا عَٰكِفِينَ
Adati: “Tikupembedza mafano; ndipo tipitiriza kuwapembedza.”
عربي تفسیرونه:
قَالَ هَلۡ يَسۡمَعُونَكُمۡ إِذۡ تَدۡعُونَ
(Ibrahim) adati: “Kodi amakumvani mukawaitana?”
عربي تفسیرونه:
أَوۡ يَنفَعُونَكُمۡ أَوۡ يَضُرُّونَ
“Kapena amakuthandizani (mukawapembedza) kapena amapereka masautso kwa inu (mukasiya kuwapembedza)?”
عربي تفسیرونه:
قَالُواْ بَلۡ وَجَدۡنَآ ءَابَآءَنَا كَذَٰلِكَ يَفۡعَلُونَ
(Iwo) adati: “Koma tidapeza makolo athu akuchita zimenezi.”
عربي تفسیرونه:
قَالَ أَفَرَءَيۡتُم مَّا كُنتُمۡ تَعۡبُدُونَ
(Ibrahim) adati: “Kodi mukuwaona awa amene mwakhala mukuwapembedza,”
عربي تفسیرونه:
أَنتُمۡ وَءَابَآؤُكُمُ ٱلۡأَقۡدَمُونَ
“Inu ndi makolo anu amene adatsogola?”
عربي تفسیرونه:
فَإِنَّهُمۡ عَدُوّٞ لِّيٓ إِلَّا رَبَّ ٱلۡعَٰلَمِينَ
“Ndithu iwo ndiadani anga, kupatula Mbuye wa zolengedwa zonse;”
عربي تفسیرونه:
ٱلَّذِي خَلَقَنِي فَهُوَ يَهۡدِينِ
“Yemwe adandilenga, ndiponso Yemwe akundiongolera (kunjira yolungama);”
عربي تفسیرونه:
وَٱلَّذِي هُوَ يُطۡعِمُنِي وَيَسۡقِينِ
“Ndiyemwe akundidyetsa ndi kundimwetsa.”
عربي تفسیرونه:
وَإِذَا مَرِضۡتُ فَهُوَ يَشۡفِينِ
“Ndipo ndikadwala ndiyemwe amandichiritsa.”
عربي تفسیرونه:
وَٱلَّذِي يُمِيتُنِي ثُمَّ يُحۡيِينِ
“Ndi Amene adzandipatsa imfa, ndipo (tsiku la Qiyâma) adzandidzutsa;”
عربي تفسیرونه:
وَٱلَّذِيٓ أَطۡمَعُ أَن يَغۡفِرَ لِي خَطِيٓـَٔتِي يَوۡمَ ٱلدِّينِ
“Ndi Yemwe ndikuyembekezera kuti adzandikhululukira zolakwa zanga tsiku la malipiro.”
عربي تفسیرونه:
رَبِّ هَبۡ لِي حُكۡمٗا وَأَلۡحِقۡنِي بِٱلصَّٰلِحِينَ
“E Mbuye wanga! Ndipatseni nzeru zoweruzira (zinthu), ndikundilumikiza ndi anthu abwino;”
عربي تفسیرونه:
وَٱجۡعَل لِّي لِسَانَ صِدۡقٖ فِي ٱلۡأٓخِرِينَ
“Ndipatseni kutchulidwa kwabwino kwa anthu ena odza pambuyo;”
عربي تفسیرونه:
وَٱجۡعَلۡنِي مِن وَرَثَةِ جَنَّةِ ٱلنَّعِيمِ
“Ndichiteni kukhala mmodzi mwa olandira Munda wamtendere;”
عربي تفسیرونه:
وَٱغۡفِرۡ لِأَبِيٓ إِنَّهُۥ كَانَ مِنَ ٱلضَّآلِّينَ
“Ndipo khululukirani bambo wanga; ndithu iye adali mmodzi wa osokera;”
عربي تفسیرونه:
وَلَا تُخۡزِنِي يَوۡمَ يُبۡعَثُونَ
“Ndipo musadzandiyalutse pa tsiku loukitsidwa anthu (ku imfa);”
عربي تفسیرونه:
يَوۡمَ لَا يَنفَعُ مَالٞ وَلَا بَنُونَ
“Tsiku lomwe chuma ndi ana sizidzathandiza (aliyense).”
عربي تفسیرونه:
إِلَّا مَنۡ أَتَى ٱللَّهَ بِقَلۡبٖ سَلِيمٖ
“Kupatula yemwe adzadza kwa Allah ndi mtima woyera (iye ndiamene adzathandizidwa patsikulo).”
عربي تفسیرونه:
وَأُزۡلِفَتِ ٱلۡجَنَّةُ لِلۡمُتَّقِينَ
Ndipo Munda wamtendere udzayandikitsidwa kwa oopa (Allah),
عربي تفسیرونه:
وَبُرِّزَتِ ٱلۡجَحِيمُ لِلۡغَاوِينَ
Ndipo Jahannam idzaonetsedwa kwa opotoka;
عربي تفسیرونه:
وَقِيلَ لَهُمۡ أَيۡنَ مَا كُنتُمۡ تَعۡبُدُونَ
Ndipo kudzanenedwa kwa iwo: “Ali kuti amene mudali kuwapembedza aja,
عربي تفسیرونه:
مِن دُونِ ٱللَّهِ هَلۡ يَنصُرُونَكُمۡ أَوۡ يَنتَصِرُونَ
M’malo mwa Allah? Kodi angathe kukuthandizani kapena kudzithandiza okha?”
عربي تفسیرونه:
فَكُبۡكِبُواْ فِيهَا هُمۡ وَٱلۡغَاوُۥنَ
Ndipo iwo ndi opotoka ena adzaponyedwa ndi nkhope zawo m’menemo (mu Jahannam).
عربي تفسیرونه:
وَجُنُودُ إِبۡلِيسَ أَجۡمَعُونَ
Ndi magulu onse ankhondo a Iblis (omwe adali kukometsa kwa anthu zoipa ndi machimo).
عربي تفسیرونه:
قَالُواْ وَهُمۡ فِيهَا يَخۡتَصِمُونَ
Adzanena (movomereza kulakwa kwawo) uku naonso ali m’menemo, akukangana (ndi anzawo omwe adawasokeretsa):
عربي تفسیرونه:
تَٱللَّهِ إِن كُنَّا لَفِي ضَلَٰلٖ مُّبِينٍ
“Ndikulumbira Allah, ndithu tidali m’kusokera kowonekera.
عربي تفسیرونه:
إِذۡ نُسَوِّيكُم بِرَبِّ ٱلۡعَٰلَمِينَ
Pamene timakufananitsani ndi Mbuye wa zolengedwa.
عربي تفسیرونه:
وَمَآ أَضَلَّنَآ إِلَّا ٱلۡمُجۡرِمُونَ
Ndipo sadatisokeretse, koma oipa okha basi.
عربي تفسیرونه:
فَمَا لَنَا مِن شَٰفِعِينَ
Choncho ife tilibe aomboli (otiombola),
عربي تفسیرونه:
وَلَا صَدِيقٍ حَمِيمٖ
Ngakhalenso bwenzi wapamtima (woti angatipulumutse kumasautsowa).
عربي تفسیرونه:
فَلَوۡ أَنَّ لَنَا كَرَّةٗ فَنَكُونَ مِنَ ٱلۡمُؤۡمِنِينَ
Tikadapeza mwayi wobwerera (ku moyo wa padziko), tikadakhala mwa okhulupirira.”
عربي تفسیرونه:
إِنَّ فِي ذَٰلِكَ لَأٓيَةٗۖ وَمَا كَانَ أَكۡثَرُهُم مُّؤۡمِنِينَ
Ndithu m’zimenezi, muli malingaliro akulu, koma ambiri a iwo sali okhulupirira.
عربي تفسیرونه:
وَإِنَّ رَبَّكَ لَهُوَ ٱلۡعَزِيزُ ٱلرَّحِيمُ
Ndipo ndithu Mbuye wako, ndiye Mwini mphamvu zoposa; Wachisoni chosatha.
عربي تفسیرونه:
كَذَّبَتۡ قَوۡمُ نُوحٍ ٱلۡمُرۡسَلِينَ
Anthu a Nuh adatsutsa atumiki.
عربي تفسیرونه:
إِذۡ قَالَ لَهُمۡ أَخُوهُمۡ نُوحٌ أَلَا تَتَّقُونَ
Pamene adawauza Nuh m’bale wawo kuti: “Kodi simukuopa (Allah ngakhale nditakuuzani zoopsa zimene zikukudikirani)?”
عربي تفسیرونه:
إِنِّي لَكُمۡ رَسُولٌ أَمِينٞ
“Ndithu ine kwa inu ndine Mtumiki wokhulupirika;”
عربي تفسیرونه:
فَٱتَّقُواْ ٱللَّهَ وَأَطِيعُونِ
“Choncho muopeni Allah ndipo ndimvereni.”
عربي تفسیرونه:
وَمَآ أَسۡـَٔلُكُمۡ عَلَيۡهِ مِنۡ أَجۡرٍۖ إِنۡ أَجۡرِيَ إِلَّا عَلَىٰ رَبِّ ٱلۡعَٰلَمِينَ
“Ndipo sindikupemphani malipiro pa zimenezi; malipiro anga ali kwa (Allah) Mbuye wa zolengedwa.”
عربي تفسیرونه:
فَٱتَّقُواْ ٱللَّهَ وَأَطِيعُونِ
“Choncho muopeni Allah ndipo ndimvereni.”
عربي تفسیرونه:
۞ قَالُوٓاْ أَنُؤۡمِنُ لَكَ وَٱتَّبَعَكَ ٱلۡأَرۡذَلُونَ
(Iwo) adati: “Nchotani kuti tikukhulupirire iwe chikhalirecho anthu wamba ndi amene akukutsatira?”
عربي تفسیرونه:
قَالَ وَمَا عِلۡمِي بِمَا كَانُواْ يَعۡمَلُونَ
(Nuh) adati: “Sindikudziwa zimene adali kuchita (zomwe zachititsa kuti Allah awaongolere kunjira yoongoka).”
عربي تفسیرونه:
إِنۡ حِسَابُهُمۡ إِلَّا عَلَىٰ رَبِّيۖ لَوۡ تَشۡعُرُونَ
“Chiwerengero chawo sichili kwina koma kwa Mbuye wanga, mukadakhala mukuzindikira.”
عربي تفسیرونه:
وَمَآ أَنَا۠ بِطَارِدِ ٱلۡمُؤۡمِنِينَ
“Ndipo sindine wopirikitsa okhulupirira (ku chipembedzo cha Allah kuti inu olemekezeka muchikhulupirire).”
عربي تفسیرونه:
إِنۡ أَنَا۠ إِلَّا نَذِيرٞ مُّبِينٞ
“Ine sikanthu , koma ndine mchenjezi woonekera.”
عربي تفسیرونه:
قَالُواْ لَئِن لَّمۡ تَنتَهِ يَٰنُوحُ لَتَكُونَنَّ مِنَ ٱلۡمَرۡجُومِينَ
(Iwo) adati: “Ngati susiya, iwe Nuh, (zonena zakozi) ndithu ukhala mmodzi mwa ogendedwa (miyala mpaka ufe).”
عربي تفسیرونه:
قَالَ رَبِّ إِنَّ قَوۡمِي كَذَّبُونِ
(Nuh) adati (kwa Allah): “Mbuye wanga! Ndithu anthu anga anditsutsa.”
عربي تفسیرونه:
فَٱفۡتَحۡ بَيۡنِي وَبَيۡنَهُمۡ فَتۡحٗا وَنَجِّنِي وَمَن مَّعِيَ مِنَ ٱلۡمُؤۡمِنِينَ
Choncho weruzani pakati panga ndi pakati pa iwo (chiweruzo chabwino), ndipo ndipulumutseni pamodzi ndi amene alinane mwa okhulupirira.”
عربي تفسیرونه:
فَأَنجَيۡنَٰهُ وَمَن مَّعَهُۥ فِي ٱلۡفُلۡكِ ٱلۡمَشۡحُونِ
Choncho, tidampulumutsa pamodzi ndi omwe adali naye m’chombo chodzadza (ndi chilichonse chamoyo chomwe chidalipo m’dziko, chachimuna ndi chachikazi chidaikidwa m’menemo).
عربي تفسیرونه:
ثُمَّ أَغۡرَقۡنَا بَعۡدُ ٱلۡبَاقِينَ
Pambuyo pake tidawamiza otsalawo.
عربي تفسیرونه:
إِنَّ فِي ذَٰلِكَ لَأٓيَةٗۖ وَمَا كَانَ أَكۡثَرُهُم مُّؤۡمِنِينَ
Ndithu m’zimenezi muli malingaliro; koma ambiri a iwo sadali okhulupirira.
عربي تفسیرونه:
وَإِنَّ رَبَّكَ لَهُوَ ٱلۡعَزِيزُ ٱلرَّحِيمُ
Ndipo ndithu Mbuye wako, Iye Ngwamphamvu zoposa; Ngwachisoni chosatha.
عربي تفسیرونه:
كَذَّبَتۡ عَادٌ ٱلۡمُرۡسَلِينَ
Naonso Âdi adatsutsa atumiki.
عربي تفسیرونه:
إِذۡ قَالَ لَهُمۡ أَخُوهُمۡ هُودٌ أَلَا تَتَّقُونَ
Pamene m’bale wawo (Mneneri) Hûd adawafunsa kuti: “Kodi simuopa (Allah)?”
عربي تفسیرونه:
إِنِّي لَكُمۡ رَسُولٌ أَمِينٞ
“Ndithu ine ndine Mtumiki wokhulupirika kwa inu;”
عربي تفسیرونه:
فَٱتَّقُواْ ٱللَّهَ وَأَطِيعُونِ
“Choncho, muopeni Allah ndipo mverani ine.”
عربي تفسیرونه:
وَمَآ أَسۡـَٔلُكُمۡ عَلَيۡهِ مِنۡ أَجۡرٍۖ إِنۡ أَجۡرِيَ إِلَّا عَلَىٰ رَبِّ ٱلۡعَٰلَمِينَ
“Ndipo pazimenezi sindikukupemphani malipiro; ndithu malipiro anga ali kwa (Allah) Mbuye wa zolengedwa.”
عربي تفسیرونه:
أَتَبۡنُونَ بِكُلِّ رِيعٍ ءَايَةٗ تَعۡبَثُونَ
“Kodi mukudzimangira nyumba pamalo paliponse pachitunda pokongola, moseweretsa?”
عربي تفسیرونه:
وَتَتَّخِذُونَ مَصَانِعَ لَعَلَّكُمۡ تَخۡلُدُونَ
“Ndipo mukudzimangira (nyumba zonga) linga ngati kuti mukuona kuti mudzakhala muyaya?”
عربي تفسیرونه:
وَإِذَا بَطَشۡتُم بَطَشۡتُمۡ جَبَّارِينَ
“Ndipo mukamamenya nkhondo mumamenya modzitukumula.”
عربي تفسیرونه:
فَٱتَّقُواْ ٱللَّهَ وَأَطِيعُونِ
“Choncho muopeni Allah ndipo ndimvereni.”
عربي تفسیرونه:
وَٱتَّقُواْ ٱلَّذِيٓ أَمَدَّكُم بِمَا تَعۡلَمُونَ
“Ndipo muopeni Yemwe adakupatsani zimene mukuzidziwa.”
عربي تفسیرونه:
أَمَدَّكُم بِأَنۡعَٰمٖ وَبَنِينَ
“Adakupatsani ziweto ndi ana.”
عربي تفسیرونه:
وَجَنَّٰتٖ وَعُيُونٍ
“Ndi minda ndi akasupe.”
عربي تفسیرونه:
إِنِّيٓ أَخَافُ عَلَيۡكُمۡ عَذَابَ يَوۡمٍ عَظِيمٖ
“Ndithu ine ndikukuoperani chilango cha tsiku lalikulu.”
عربي تفسیرونه:
قَالُواْ سَوَآءٌ عَلَيۡنَآ أَوَعَظۡتَ أَمۡ لَمۡ تَكُن مِّنَ ٱلۡوَٰعِظِينَ
Iwo adati: “Kwa ife nchimodzimodzi, utichenjeze kapena iwe usakhale mmodzi mwa ochenjeza.”
عربي تفسیرونه:
إِنۡ هَٰذَآ إِلَّا خُلُقُ ٱلۡأَوَّلِينَ
“Ndithu kutero (anthu ena kudzitcha atumiki a Allah), sikanthu koma ndi machitidwe a anthu akale.”
عربي تفسیرونه:
وَمَا نَحۡنُ بِمُعَذَّبِينَ
“Ndipo ife sitidzalangidwa (monga momwe ukunenera).”
عربي تفسیرونه:
فَكَذَّبُوهُ فَأَهۡلَكۡنَٰهُمۡۚ إِنَّ فِي ذَٰلِكَ لَأٓيَةٗۖ وَمَا كَانَ أَكۡثَرُهُم مُّؤۡمِنِينَ
Choncho adamtsutsa, ndipo tidawaononga. Ndithu m’zimenezi muli malingaliro; koma ambiri a iwo sadali okhulupirira.
عربي تفسیرونه:
وَإِنَّ رَبَّكَ لَهُوَ ٱلۡعَزِيزُ ٱلرَّحِيمُ
Ndipo ndithu Mbuye wako ndiye Wamphamvu zoposa; Wachisoni chosatha.
عربي تفسیرونه:
كَذَّبَتۡ ثَمُودُ ٱلۡمُرۡسَلِينَ
A Samudu (naonso) adatsutsa atumiki.
عربي تفسیرونه:
إِذۡ قَالَ لَهُمۡ أَخُوهُمۡ صَٰلِحٌ أَلَا تَتَّقُونَ
Pamene m’bale wawo Swalih adawauza kuti: “Kodi simuopa (Allah)?”
عربي تفسیرونه:
إِنِّي لَكُمۡ رَسُولٌ أَمِينٞ
“Ndithu ine ndimtumiki wokhulupirika kwa inu.”
عربي تفسیرونه:
فَٱتَّقُواْ ٱللَّهَ وَأَطِيعُونِ
“Choncho muopeni Allah ndipo mverani ine.”
عربي تفسیرونه:
وَمَآ أَسۡـَٔلُكُمۡ عَلَيۡهِ مِنۡ أَجۡرٍۖ إِنۡ أَجۡرِيَ إِلَّا عَلَىٰ رَبِّ ٱلۡعَٰلَمِينَ
“Ndipo sindikupemphani malipiro pa zimenezi. Palibe kumene kuli malipiro anga koma kwa Mbuye wa zolengedwa.”
عربي تفسیرونه:
أَتُتۡرَكُونَ فِي مَا هَٰهُنَآ ءَامِنِينَ
“Kodi (mukuganizira kuti) mudzasiidwa mwamtendere pa izi zili pano (popanda imfa kukudzerani?)”
عربي تفسیرونه:
فِي جَنَّٰتٖ وَعُيُونٖ
“M’minda ndi mu akasupe?”
عربي تفسیرونه:
وَزُرُوعٖ وَنَخۡلٖ طَلۡعُهَا هَضِيمٞ
“Ndi (m’minda) yammera ndi mitengo yakanjedza yamikoko yakupsa yofewa?”
عربي تفسیرونه:
وَتَنۡحِتُونَ مِنَ ٱلۡجِبَالِ بُيُوتٗا فَٰرِهِينَ
“Ndipo mukugoba nyumba m’mapiri mwaluso.”
عربي تفسیرونه:
فَٱتَّقُواْ ٱللَّهَ وَأَطِيعُونِ
“Choncho muopeni Allah ndipo ndimvereni.”
عربي تفسیرونه:
وَلَا تُطِيعُوٓاْ أَمۡرَ ٱلۡمُسۡرِفِينَ
“Ndipo musamvere za awo opyola malire.”
عربي تفسیرونه:
ٱلَّذِينَ يُفۡسِدُونَ فِي ٱلۡأَرۡضِ وَلَا يُصۡلِحُونَ
“Amene akuononga pa dziko, ndipo sakonza.”
عربي تفسیرونه:
قَالُوٓاْ إِنَّمَآ أَنتَ مِنَ ٱلۡمُسَحَّرِينَ
Iwo adati: “Ndithu iwe ndi mmodzi wa olodzedwa.”
عربي تفسیرونه:
مَآ أَنتَ إِلَّا بَشَرٞ مِّثۡلُنَا فَأۡتِ بِـَٔايَةٍ إِن كُنتَ مِنَ ٱلصَّٰدِقِينَ
“Iwe suli kanthu, koma munthu ngati ife; tabwera ndi chozizwitsa, ngati ndiwedi mmodzi wa onena zoona!”
عربي تفسیرونه:
قَالَ هَٰذِهِۦ نَاقَةٞ لَّهَا شِرۡبٞ وَلَكُمۡ شِرۡبُ يَوۡمٖ مَّعۡلُومٖ
Iye adati: “(Ndakubweretserani) ngamira iyi yaikazi; (koma) ili ndi gawo lake lakumwa, ndipo inu muli ndi gawo lanu lakutunga (madzi) patsiku lodziwika. (Tsiku lina lotunga rnadzi anthu).”
عربي تفسیرونه:
وَلَا تَمَسُّوهَا بِسُوٓءٖ فَيَأۡخُذَكُمۡ عَذَابُ يَوۡمٍ عَظِيمٖ
“Ndipo musaikhudze ndi choipa chilichonse kuopera kuti chingakupezeni chilango cha tsiku lalikulu.”
عربي تفسیرونه:
فَعَقَرُوهَا فَأَصۡبَحُواْ نَٰدِمِينَ
Koma iwo adaipha; ndipo adali odzinena (pamene chidadza chilango cha Allah).
عربي تفسیرونه:
فَأَخَذَهُمُ ٱلۡعَذَابُۚ إِنَّ فِي ذَٰلِكَ لَأٓيَةٗۖ وَمَا كَانَ أَكۡثَرُهُم مُّؤۡمِنِينَ
Choncho chilango (cha Allah) chidawaononga, ndithu pa zimenezi pali phunziro; koma ambiri a iwo sadali okhulupirira.
عربي تفسیرونه:
وَإِنَّ رَبَّكَ لَهُوَ ٱلۡعَزِيزُ ٱلرَّحِيمُ
Ndipo, ndithu Mbuye wako, Iye Ngwamphamvu zoposa; wachisoni chosatha.
عربي تفسیرونه:
كَذَّبَتۡ قَوۡمُ لُوطٍ ٱلۡمُرۡسَلِينَ
Anthu a Luti adatsutsa atumiki.
عربي تفسیرونه:
إِذۡ قَالَ لَهُمۡ أَخُوهُمۡ لُوطٌ أَلَا تَتَّقُونَ
Pamene m’bale wawo Luti adanena kwa iwo (kuti): “Kodi simuopa (Allah)?”
عربي تفسیرونه:
إِنِّي لَكُمۡ رَسُولٌ أَمِينٞ
“Ndithu ine ndine Mtumiki wokhulupirika kwa inu.”
عربي تفسیرونه:
فَٱتَّقُواْ ٱللَّهَ وَأَطِيعُونِ
“Choncho muopeni Allah ndipo ndimvereni.”
عربي تفسیرونه:
وَمَآ أَسۡـَٔلُكُمۡ عَلَيۡهِ مِنۡ أَجۡرٍۖ إِنۡ أَجۡرِيَ إِلَّا عَلَىٰ رَبِّ ٱلۡعَٰلَمِينَ
“Ndipo sindikupemphani malipiro pa zimenezi; palibe komwe kuli malipiro anga koma kwa Mbuye wazolengedwa.”
عربي تفسیرونه:
أَتَأۡتُونَ ٱلذُّكۡرَانَ مِنَ ٱلۡعَٰلَمِينَ
“Kodi mukugonana ndi amuna (anzanu) muzolengedwa (za Allah),
عربي تفسیرونه:
وَتَذَرُونَ مَا خَلَقَ لَكُمۡ رَبُّكُم مِّنۡ أَزۡوَٰجِكُمۚ بَلۡ أَنتُمۡ قَوۡمٌ عَادُونَ
“Ndikusiya amene Mbuye wanu adakulengerani kuti akhale akazi anu? Ndithu inu ndinu anthu olumpha malire.”
عربي تفسیرونه:
قَالُواْ لَئِن لَّمۡ تَنتَهِ يَٰلُوطُ لَتَكُونَنَّ مِنَ ٱلۡمُخۡرَجِينَ
Iwo adati: “Ngati susiya (izi), E iwe Luti! ndithu ukhala mmodzi wa opirikitsidwa.”
عربي تفسیرونه:
قَالَ إِنِّي لِعَمَلِكُم مِّنَ ٱلۡقَالِينَ
Iye adati: “Ndithu ine ndine m’modzi wakuzida izi zochita zanu (choncho Sindisiya kuzidzudzula).”
عربي تفسیرونه:
رَبِّ نَجِّنِي وَأَهۡلِي مِمَّا يَعۡمَلُونَ
“E Mbuye wanga! Ndipulumutseni ine ndi banja langa ku (matsoka a) zimene akuchita.”
عربي تفسیرونه:
فَنَجَّيۡنَٰهُ وَأَهۡلَهُۥٓ أَجۡمَعِينَ
Ndipo tidampulumutsa iye ndi onse a pa banja lake,
عربي تفسیرونه:
إِلَّا عَجُوزٗا فِي ٱلۡغَٰبِرِينَ
Kupatula nkhalamba yaikazi idali mwa otsalira m’mbuyo.
عربي تفسیرونه:
ثُمَّ دَمَّرۡنَا ٱلۡأٓخَرِينَ
Titatero tidawaononga enawo.
عربي تفسیرونه:
وَأَمۡطَرۡنَا عَلَيۡهِم مَّطَرٗاۖ فَسَآءَ مَطَرُ ٱلۡمُنذَرِينَ
Ndipo tidawavumbwitsira mvula (yamiyala); iyipirenji, mvula ya ochenjezedwa!
عربي تفسیرونه:
إِنَّ فِي ذَٰلِكَ لَأٓيَةٗۖ وَمَا كَانَ أَكۡثَرُهُم مُّؤۡمِنِينَ
Ndithu pazimenezi pali malingaliro. Koma ambiri a iwo sadali okhulupirira.
عربي تفسیرونه:
وَإِنَّ رَبَّكَ لَهُوَ ٱلۡعَزِيزُ ٱلرَّحِيمُ
Ndipo, ndithu Mbuye wako, Ngwamphamvu kwambiri; Ngwachisoni chosatha.
عربي تفسیرونه:
كَذَّبَ أَصۡحَٰبُ لۡـَٔيۡكَةِ ٱلۡمُرۡسَلِينَ
Anthu a m’dziko lamitengo yambiri (Madiana) adatsutsa atumiki.
عربي تفسیرونه:
إِذۡ قَالَ لَهُمۡ شُعَيۡبٌ أَلَا تَتَّقُونَ
(Akumbutse) pamene (Mneneri) Shuaib adati kwa iwo: “Kodi simuopa (Allah)?”
عربي تفسیرونه:
إِنِّي لَكُمۡ رَسُولٌ أَمِينٞ
“Ndithu ndine Mtumiki wokhulupirika kwa inu.”
عربي تفسیرونه:
فَٱتَّقُواْ ٱللَّهَ وَأَطِيعُونِ
“Choncho muopeni Allah ndipo ndimvereni.”
عربي تفسیرونه:
وَمَآ أَسۡـَٔلُكُمۡ عَلَيۡهِ مِنۡ أَجۡرٍۖ إِنۡ أَجۡرِيَ إِلَّا عَلَىٰ رَبِّ ٱلۡعَٰلَمِينَ
“Ndipo sindikupemphani malipiro pa zimenezi; kulibe malipiro anga koma kwa (Allah) Mbuye wa zolengedwa.”
عربي تفسیرونه:
۞ أَوۡفُواْ ٱلۡكَيۡلَ وَلَا تَكُونُواْ مِنَ ٱلۡمُخۡسِرِينَ
“Kwaniritsani mulingo (pamalonda pamene mukupima), ndipo musakhale mwaopungula (mulingo).”
عربي تفسیرونه:
وَزِنُواْ بِٱلۡقِسۡطَاسِ ٱلۡمُسۡتَقِيمِ
“Ndipo yesani ndi sikelo yolungama (yolondola).”
عربي تفسیرونه:
وَلَا تَبۡخَسُواْ ٱلنَّاسَ أَشۡيَآءَهُمۡ وَلَا تَعۡثَوۡاْ فِي ٱلۡأَرۡضِ مُفۡسِدِينَ
“Ndipo musawachepetsere anthu zinthu zawo, ndiponso musayende padziko uku mukuononga.”
عربي تفسیرونه:
وَٱتَّقُواْ ٱلَّذِي خَلَقَكُمۡ وَٱلۡجِبِلَّةَ ٱلۡأَوَّلِينَ
“Ndipo muopeni amene adalenga inu ndiponso zolengedwa zoyamba (zimene zidanka kale).”
عربي تفسیرونه:
قَالُوٓاْ إِنَّمَآ أَنتَ مِنَ ٱلۡمُسَحَّرِينَ
Iwo adati: “Ndithu iwe ndi mmodzi wa olodzedwa.”
عربي تفسیرونه:
وَمَآ أَنتَ إِلَّا بَشَرٞ مِّثۡلُنَا وَإِن نَّظُنُّكَ لَمِنَ ٱلۡكَٰذِبِينَ
“Ndipo iwe suli kanthu koma munthu ngati ife, ndipo ndithu tikukutsimikizira kuti ndiwe mmodzi wa abodza.”
عربي تفسیرونه:
فَأَسۡقِطۡ عَلَيۡنَا كِسَفٗا مِّنَ ٱلسَّمَآءِ إِن كُنتَ مِنَ ٱلصَّٰدِقِينَ
“Choncho tigwetsere zidutswa za thambo (kuti zitiononge) ngati uli mmodzi wa onena zoona.”
عربي تفسیرونه:
قَالَ رَبِّيٓ أَعۡلَمُ بِمَا تَعۡمَلُونَ
(Shuaib) adati: “Mbuye wanga Ngodziwa kwambiri zimene mukuchita. (Akadzaona kuti inu ngoyenera kulangidwa ndizidutswa za thambo, adzakulangani).”
عربي تفسیرونه:
فَكَذَّبُوهُ فَأَخَذَهُمۡ عَذَابُ يَوۡمِ ٱلظُّلَّةِۚ إِنَّهُۥ كَانَ عَذَابَ يَوۡمٍ عَظِيمٍ
Koma adamutsutsa. Ndipo chidawagwera chilango chatsiku la mthunzi; ndithu chimenecho chidali chilango cha tsiku lalikulu.
عربي تفسیرونه:
إِنَّ فِي ذَٰلِكَ لَأٓيَةٗۖ وَمَا كَانَ أَكۡثَرُهُم مُّؤۡمِنِينَ
Ndithu pa zimenezi pali lingaliro; koma ambiri a iwo sadali okhulupirira.
عربي تفسیرونه:
وَإِنَّ رَبَّكَ لَهُوَ ٱلۡعَزِيزُ ٱلرَّحِيمُ
Ndipo, ndithu Mbuye wako Ngwamphamvu kwambiri; Ngwachisoni chosatha.
عربي تفسیرونه:
وَإِنَّهُۥ لَتَنزِيلُ رَبِّ ٱلۡعَٰلَمِينَ
Ndipo, ndithu iyi (Qur’an) ndiyo chivumbulutso cha Mbuye wazolengedwa zonse.
عربي تفسیرونه:
نَزَلَ بِهِ ٱلرُّوحُ ٱلۡأَمِينُ
Mzimu Wokhulupirika (Jiburil) udaivumbulutsa.
عربي تفسیرونه:
عَلَىٰ قَلۡبِكَ لِتَكُونَ مِنَ ٱلۡمُنذِرِينَ
Pa mtima wako kuti ukhale mmodzi wa achenjezi,
عربي تفسیرونه:
بِلِسَانٍ عَرَبِيّٖ مُّبِينٖ
M’chiyankhulo cha Chiarabu chomveka bwino.
عربي تفسیرونه:
وَإِنَّهُۥ لَفِي زُبُرِ ٱلۡأَوَّلِينَ
Ndipo ndithu izi (zomwe zili m’Qur’an) zilipo m’mabuku akale.
عربي تفسیرونه:
أَوَلَمۡ يَكُن لَّهُمۡ ءَايَةً أَن يَعۡلَمَهُۥ عُلَمَٰٓؤُاْ بَنِيٓ إِسۡرَٰٓءِيلَ
Kodi sipadapezeke chisonyezo kwa iwo kuti akuidziwa (Qur’an) odziwa mwa ana a Israyeli (kotero kuti ena alowa m’Chisilamu)?
عربي تفسیرونه:
وَلَوۡ نَزَّلۡنَٰهُ عَلَىٰ بَعۡضِ ٱلۡأَعۡجَمِينَ
Ndipo tikadaivumbulutsa kwa wina amene sali Muarabu,
عربي تفسیرونه:
فَقَرَأَهُۥ عَلَيۡهِم مَّا كَانُواْ بِهِۦ مُؤۡمِنِينَ
Kotero kuti nkuwawerengera momveka bwino, sakadaikhulupirira.
عربي تفسیرونه:
كَذَٰلِكَ سَلَكۡنَٰهُ فِي قُلُوبِ ٱلۡمُجۡرِمِينَ
Momwemo ndimo tidalowetsera kuitsutsa (Qur’an) m’mitima ya oipa.
عربي تفسیرونه:
لَا يُؤۡمِنُونَ بِهِۦ حَتَّىٰ يَرَوُاْ ٱلۡعَذَابَ ٱلۡأَلِيمَ
Sangaikhulupirire kufikira ataona chilango chowawa.
عربي تفسیرونه:
فَيَأۡتِيَهُم بَغۡتَةٗ وَهُمۡ لَا يَشۡعُرُونَ
Choncho chidzawadzera mwadzidzidzi pomwe iwo sakuzindikira.
عربي تفسیرونه:
فَيَقُولُواْ هَلۡ نَحۡنُ مُنظَرُونَ
Tero adzayamba kunena: “Kodi ife tipatsidwa nthawi (yoti tilape)?”
عربي تفسیرونه:
أَفَبِعَذَابِنَا يَسۡتَعۡجِلُونَ
Kodi akuchifulumizitsa chilango Chathu?
عربي تفسیرونه:
أَفَرَءَيۡتَ إِن مَّتَّعۡنَٰهُمۡ سِنِينَ
Kodi ukuona bwanji, ngati titawasangalatsa zaka (zankhaninkhani).
عربي تفسیرونه:
ثُمَّ جَآءَهُم مَّا كَانُواْ يُوعَدُونَ
Kenako nkuwadzera (chilango) chomwe adalonjezedwa,
عربي تفسیرونه:
مَآ أَغۡنَىٰ عَنۡهُم مَّا كَانُواْ يُمَتَّعُونَ
Sizidawathandize zomwe adali kusangalatsidwa nazozo.
عربي تفسیرونه:
وَمَآ أَهۡلَكۡنَا مِن قَرۡيَةٍ إِلَّا لَهَا مُنذِرُونَ
Ndipo sitidauononge mudzi uliwonse koma udali ndi achenjezi.
عربي تفسیرونه:
ذِكۡرَىٰ وَمَا كُنَّا ظَٰلِمِينَ
(Kuti akhale) chikumbutso. Ndipo sitidali osalungama (powaononga popanda kuwachenjeza).
عربي تفسیرونه:
وَمَا تَنَزَّلَتۡ بِهِ ٱلشَّيَٰطِينُ
Ndipo asatana sadaivumbulutse (iyi Qur’an monga osakhulupirira akunenera monyoza).
عربي تفسیرونه:
وَمَا يَنۢبَغِي لَهُمۡ وَمَا يَسۡتَطِيعُونَ
Ndipo sikoyenera kwa iwo (kuivumbulutsa Qur’an) ndiponso sangathe.
عربي تفسیرونه:
إِنَّهُمۡ عَنِ ٱلسَّمۡعِ لَمَعۡزُولُونَ
Ndithu iwo ngotsekerezedwa kumvetsera (zimene angelo amalankhula kumwamba).
عربي تفسیرونه:
فَلَا تَدۡعُ مَعَ ٱللَّهِ إِلَٰهًا ءَاخَرَ فَتَكُونَ مِنَ ٱلۡمُعَذَّبِينَ
Choncho usapembedze mulungu wina pamodzi ndi Allah, kuti ungakhale mwa olangidwa.
عربي تفسیرونه:
وَأَنذِرۡ عَشِيرَتَكَ ٱلۡأَقۡرَبِينَ
Ndipo achenjeze abale ako a pafupi.
عربي تفسیرونه:
وَٱخۡفِضۡ جَنَاحَكَ لِمَنِ ٱتَّبَعَكَ مِنَ ٱلۡمُؤۡمِنِينَ
Ndipo fungatira ndi phiko lako amene akutsata mwa okhulupirira. (Ukhale wachifundo kwa iwo).
عربي تفسیرونه:
فَإِنۡ عَصَوۡكَ فَقُلۡ إِنِّي بَرِيٓءٞ مِّمَّا تَعۡمَلُونَ
Ngati atakunyoza, nena: “Ine ndili kutali ndi zimene mukuchitazo.”
عربي تفسیرونه:
وَتَوَكَّلۡ عَلَى ٱلۡعَزِيزِ ٱلرَّحِيمِ
Ndipo tsamira kwa (Mbuye wako) Mwini mphamvu zoposa; Wachisoni chosatha.
عربي تفسیرونه:
ٱلَّذِي يَرَىٰكَ حِينَ تَقُومُ
Yemwe akukuona pamene ukuimilira (pamapemphero).
عربي تفسیرونه:
وَتَقَلُّبَكَ فِي ٱلسَّٰجِدِينَ
Ndikutembenukatembenuka kwako (pogwetsa mphumi yako pansi ndi kudzuka ndi kuimilira) pamodzi ndi ogwetsa mphumi pansi (polambira Allah).
عربي تفسیرونه:
إِنَّهُۥ هُوَ ٱلسَّمِيعُ ٱلۡعَلِيمُ
Ndithu Iye Ngwakumva; Ngodziwa chilichonse.
عربي تفسیرونه:
هَلۡ أُنَبِّئُكُمۡ عَلَىٰ مَن تَنَزَّلُ ٱلشَّيَٰطِينُ
Kodi ndikuuzeni amene asatana amawatsikira?
عربي تفسیرونه:
تَنَزَّلُ عَلَىٰ كُلِّ أَفَّاكٍ أَثِيمٖ
Amamtsikira yense wabodza lamkunkhuniza; wamachimo.
عربي تفسیرونه:
يُلۡقُونَ ٱلسَّمۡعَ وَأَكۡثَرُهُمۡ كَٰذِبُونَ
Amawaponyera (asatana anzawo a mu anthu) zimene azimva. Koma ambiri a iwo ngabodza.
عربي تفسیرونه:
وَٱلشُّعَرَآءُ يَتَّبِعُهُمُ ٱلۡغَاوُۥنَ
Ndipo alakatuli (olakatula zopanda phindu) amatsatidwa ndi (anthu) opotoka.
عربي تفسیرونه:
أَلَمۡ تَرَ أَنَّهُمۡ فِي كُلِّ وَادٖ يَهِيمُونَ
Kodi suona kuti iwo akungoyumbayumba m’chigwa chilichonse (chamawu)?
عربي تفسیرونه:
وَأَنَّهُمۡ يَقُولُونَ مَا لَا يَفۡعَلُونَ
Ndithunso iwo akunena zomwe sachita.
عربي تفسیرونه:
إِلَّا ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ وَعَمِلُواْ ٱلصَّٰلِحَٰتِ وَذَكَرُواْ ٱللَّهَ كَثِيرٗا وَٱنتَصَرُواْ مِنۢ بَعۡدِ مَا ظُلِمُواْۗ وَسَيَعۡلَمُ ٱلَّذِينَ ظَلَمُوٓاْ أَيَّ مُنقَلَبٖ يَنقَلِبُونَ
Kupatula amene akhulupirira ndikumachita zabwino, ndikumamtchula Allah mowirikiza, ndikuzipulumutsa okha pambuyo pochitiridwa zoipa. Ndipo posachedwa amene adzichitira okha zoipa adziwa kotembenukira komwe adzatembenukire.
عربي تفسیرونه:
 
د معناګانو ژباړه سورت: الشعراء
د سورتونو فهرست (لړلیک) د مخ نمبر
 
د قرآن کریم د معناګانو ژباړه - چیچوایي ژباړه - د ژباړو فهرست (لړلیک)

چیچوایي ژبې ته د قرآن کریم د معناګانو ژباړه، خالد ابراهیم بیتالا ژباړلې ده، ۲۰۲۰ کال چاپ

بندول