Bản dịch ý nghĩa nội dung Qur'an - Dịch thuật tiếng Chichio * - Mục lục các bản dịch


Ý nghĩa nội dung Chương: Chương Al-Shu-'ara'   Câu:

Chương Al-Shu-'ara'

طسٓمٓ
Tâ-Sîn-Mîm.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
تِلۡكَ ءَايَٰتُ ٱلۡكِتَٰبِ ٱلۡمُبِينِ
Izi ndi Ayah (ndime) za buku (la Qur’an) lofotokoza chilichonse (chofunika m’chipembedzo).
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
لَعَلَّكَ بَٰخِعٞ نَّفۡسَكَ أَلَّا يَكُونُواْ مُؤۡمِنِينَ
Mwina iwe (Mtumiki Muhammad {s.a.w}) udziononga wekha (ndi madandaulo) chifukwa chakuti (iwo) sadakhale okhulupirira.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
إِن نَّشَأۡ نُنَزِّلۡ عَلَيۡهِم مِّنَ ٱلسَّمَآءِ ءَايَةٗ فَظَلَّتۡ أَعۡنَٰقُهُمۡ لَهَا خَٰضِعِينَ
Tikadafuna, tikadawatsitsira chizizwa kuchokera kumwamba; kotero kuti makosi awo akadadzichepetsa ndi chizizwacho, (sakadatha kucheukira kwina koma sitifuna kukakamiza anthu kuti akhale Asilamu).[295]
[295] Mtumiki Muhammad (s.a.w) adali kuwawidwa mtima kwambiri poona kuti anthu sakuvomereza uthenga wachoonadi umene iye adadza nawo, ndipo adali kuwamvera chisoni kwambiri. Choncho Allah adamtonthoza pomuuza kuti: “Usadziphe wekha chifukwa chokhala ndi maganizo owamvera chisoni.” Allah akadafuna kuwaongola mowakakamiza akadatha kutero; koma sadafune.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَمَا يَأۡتِيهِم مِّن ذِكۡرٖ مِّنَ ٱلرَّحۡمَٰنِ مُحۡدَثٍ إِلَّا كَانُواْ عَنۡهُ مُعۡرِضِينَ
Ndipo palibe pamene chikuwadzera chivumbulutso chatsopano chochokera kwa (Allah) Wachifundo chambiri koma amazipatula ku icho (chivumbulutso).
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
فَقَدۡ كَذَّبُواْ فَسَيَأۡتِيهِمۡ أَنۢبَٰٓؤُاْ مَا كَانُواْ بِهِۦ يَسۡتَهۡزِءُونَ
Ndithu atsutsa; choncho posachedwapa ziwadzera nkhani zomwe adali kuzichitira chipongwe.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
أَوَلَمۡ يَرَوۡاْ إِلَى ٱلۡأَرۡضِ كَمۡ أَنۢبَتۡنَا فِيهَا مِن كُلِّ زَوۡجٖ كَرِيمٍ
Kodi sadaone nthaka? Ndimmera ungati taumeretsa m’menemo kuchokera mu mtundu ulionse, wokongola?
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
إِنَّ فِي ذَٰلِكَ لَأٓيَةٗۖ وَمَا كَانَ أَكۡثَرُهُم مُّؤۡمِنِينَ
Ndithu m’zimenezo muli zizindikiro (zosonyeza mphamvu za Allah). Koma ambiri a iwo sali okhulupirira.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَإِنَّ رَبَّكَ لَهُوَ ٱلۡعَزِيزُ ٱلرَّحِيمُ
Ndipo, ndithu Mbuye wako ndi Mwini mphamvu zoposa; Wachisoni chosatha.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَإِذۡ نَادَىٰ رَبُّكَ مُوسَىٰٓ أَنِ ٱئۡتِ ٱلۡقَوۡمَ ٱلظَّٰلِمِينَ
Ndipo (akumbutse) pamene Mbuye wako adaitana (m’neneri) Mûsa; adamuuza: “Pita kwa anthu ochita zoipa.”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
قَوۡمَ فِرۡعَوۡنَۚ أَلَا يَتَّقُونَ
Anthu a Farawo; (auze): “Kodi sawopa (Allah)?”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
قَالَ رَبِّ إِنِّيٓ أَخَافُ أَن يُكَذِّبُونِ
(Mûsa) adati: “Mbuye wanga! Ine ndikuopa kuti anganditsutse.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَيَضِيقُ صَدۡرِي وَلَا يَنطَلِقُ لِسَانِي فَأَرۡسِلۡ إِلَىٰ هَٰرُونَ
Ndipo chingabanike chifuwa changa (ndi maganizo, chifukwa chakunditsutsa kwawo); ndiponso lirime langa siliyankhula momveka bwino. Choncho tumizaninso uthengawu kwa Harun (kuti tikhale awiri ndipo azikandithangata pantchito yangayi).
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَلَهُمۡ عَلَيَّ ذَنۢبٞ فَأَخَافُ أَن يَقۡتُلُونِ
Ndipo iwowo ndili nawo mlandu ndipo ndikuopa kuti angandiphe (pobwezera chimene ndidawalakwira powaphera munthu wawo).
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
قَالَ كَلَّاۖ فَٱذۡهَبَا بِـَٔايَٰتِنَآۖ إِنَّا مَعَكُم مُّسۡتَمِعُونَ
(Allah) adati: “Iyayi! Pitani pamodzi ndi zozizwa Zathu; ndithu Ife tikakhala nanu limodzi (pokuthangatani) uku tikumvetsera (zimene azikanena).”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
فَأۡتِيَا فِرۡعَوۡنَ فَقُولَآ إِنَّا رَسُولُ رَبِّ ٱلۡعَٰلَمِينَ
“Choncho mpitireni Farawo, ndipo kamuuzeni kuti: “Ife ndi atumiki a Mbuye wa zolengedwa zonse.”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
أَنۡ أَرۡسِلۡ مَعَنَا بَنِيٓ إِسۡرَٰٓءِيلَ
“(Tatumidwa) kuti uwapereke kwa ife ana a Israyeli (kuti tinke nawo ku Sham).”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
قَالَ أَلَمۡ نُرَبِّكَ فِينَا وَلِيدٗا وَلَبِثۡتَ فِينَا مِنۡ عُمُرِكَ سِنِينَ
(Farawo) adati (kwa Mûsa): “Kodi sitidakulere kwathu uli mwana, ndi kukhala nafe pa moyo wako zaka zambiri?”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَفَعَلۡتَ فَعۡلَتَكَ ٱلَّتِي فَعَلۡتَ وَأَنتَ مِنَ ٱلۡكَٰفِرِينَ
“Ndipo udachita chochita chako chimene udachichita, ndipo iwe ndiwe mmodzi wa osathokoza!”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
قَالَ فَعَلۡتُهَآ إِذٗا وَأَنَا۠ مِنَ ٱلضَّآلِّينَ
(Mûsa) adati: “Ndidachita zimenezo pomwe ine ndidali mmodzi wa osazindikira zinthu.”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
فَفَرَرۡتُ مِنكُمۡ لَمَّا خِفۡتُكُمۡ فَوَهَبَ لِي رَبِّي حُكۡمٗا وَجَعَلَنِي مِنَ ٱلۡمُرۡسَلِينَ
“Choncho ndidakuthawani pomwe ndidakuopani; tsono Mbuye wanga wandipatsa nzeru zoweruzira (zinthu), ndi kundisankha kukhala mmodzi wa atumiki.”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَتِلۡكَ نِعۡمَةٞ تَمُنُّهَا عَلَيَّ أَنۡ عَبَّدتَّ بَنِيٓ إِسۡرَٰٓءِيلَ
“Ndipo kodi umenewu ndimtendere wonditonzera pomwe mudawaika muukapolo ana a Israyeli!”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
قَالَ فِرۡعَوۡنُ وَمَا رَبُّ ٱلۡعَٰلَمِينَ
Farawo adati: “Kodi ndani Mbuye wa zolengedwayo?”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
قَالَ رَبُّ ٱلسَّمَٰوَٰتِ وَٱلۡأَرۡضِ وَمَا بَيۡنَهُمَآۖ إِن كُنتُم مُّوقِنِينَ
(Mûsa) adati: “Mbuye wa thambo ndi nthaka ndi zapakati pake, ngati muli ndi chitsimikizo. (Amachita chilichonse m’menemo mmene wafunira; kupereka moyo ndi imfa).”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
قَالَ لِمَنۡ حَوۡلَهُۥٓ أَلَا تَسۡتَمِعُونَ
(Farawo) adauza omwe adali m’mphepete mwake (mwachipongwe): “Kodi simukumva (mawu achibwanawa)?”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
قَالَ رَبُّكُمۡ وَرَبُّ ءَابَآئِكُمُ ٱلۡأَوَّلِينَ
(Mûsa adapitiriza kunena) adati: “Allah ndi Mbuye wanu komanso Mbuye wamakolo anu oyamba.”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
قَالَ إِنَّ رَسُولَكُمُ ٱلَّذِيٓ أُرۡسِلَ إِلَيۡكُمۡ لَمَجۡنُونٞ
(Farawo) adati (kwa anthu ake pofuna kuwakwiitsa): “Ndithu Mtumiki wanu amene watumidwa kwa inu, ngwamisala.”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
قَالَ رَبُّ ٱلۡمَشۡرِقِ وَٱلۡمَغۡرِبِ وَمَا بَيۡنَهُمَآۖ إِن كُنتُمۡ تَعۡقِلُونَ
(Mûsa) adati: “Mbuye wakuvuma ndi kuzambwe, ndi zomwe ziri pakati pake ngati mumazindikira (zinthu, muzindikira izi).”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
قَالَ لَئِنِ ٱتَّخَذۡتَ إِلَٰهًا غَيۡرِي لَأَجۡعَلَنَّكَ مِنَ ٱلۡمَسۡجُونِينَ
(Farawo) adati: “Ngati udzipangira mulungu wina kusiya ine, ndikuchita kukhala mmodzi wa omangidwa kundende.”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
قَالَ أَوَلَوۡ جِئۡتُكَ بِشَيۡءٖ مُّبِينٖ
(Mûsa) adati: “Kodi ngakhale nditakubweretsera chinthu choonekera poyera (chosonyeza kuti zimene ndikunenazi ndizoona ndatumidwa ndi Allah)?”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
قَالَ فَأۡتِ بِهِۦٓ إِن كُنتَ مِنَ ٱلصَّٰدِقِينَ
(Farawo) adati: “Chibweretse, ngati uli mwa onena zoona.”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
فَأَلۡقَىٰ عَصَاهُ فَإِذَا هِيَ ثُعۡبَانٞ مُّبِينٞ
Ndipo (Mûsa) adaponya (pansi) ndodo yake, mwadzidzidzi idasanduka njoka yopenyeka.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَنَزَعَ يَدَهُۥ فَإِذَا هِيَ بَيۡضَآءُ لِلنَّٰظِرِينَ
Ndipo adatulutsa dzanja lake; pompo lidali loyera (kwambiri) kwa (onse) openya.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
قَالَ لِلۡمَلَإِ حَوۡلَهُۥٓ إِنَّ هَٰذَا لَسَٰحِرٌ عَلِيمٞ
(Farawo) adauza akuluakulu omwe adali m’mphepete mwake: “Ndithu uyu ndi wamatsenga wodziwa kwambiri.”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
يُرِيدُ أَن يُخۡرِجَكُم مِّنۡ أَرۡضِكُم بِسِحۡرِهِۦ فَمَاذَا تَأۡمُرُونَ
“Akufuna kukutulutsani m’dziko lanu ndi matsenga ake; kodi nanga mukuti chiyani?”[296]
[296] Farawo adasimidwa, adatha nzeru zedi ndi mawu amene adali kutuluka m’kamwa mwa Musa kotero kuti adangoti kakasi, kusowa chonena, nayamba kuwafunsa nzeru ndi malangizo anthu ake pomwe iye ankadzitcha kuti ndi mulungu wodziwa zonse, wamphamvu zoposa.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
قَالُوٓاْ أَرۡجِهۡ وَأَخَاهُ وَٱبۡعَثۡ فِي ٱلۡمَدَآئِنِ حَٰشِرِينَ
(Anthu) adati (kwa Farawo): “Mpatse nthawi ndi m’bale wakeyo, ndipo tumiza (amithenga) m’mizinda yonse osonkhanitsa anthu.”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
يَأۡتُوكَ بِكُلِّ سَحَّارٍ عَلِيمٖ
“Ndipo akubweretsera amatsenga onse odziwa kwabasi (kotero kuti adzampambana Mûsa).”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
فَجُمِعَ ٱلسَّحَرَةُ لِمِيقَٰتِ يَوۡمٖ مَّعۡلُومٖ
Choncho amatsenga adasonkhanitsidwa mu nthawi ya tsiku lodziwika.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَقِيلَ لِلنَّاسِ هَلۡ أَنتُم مُّجۡتَمِعُونَ
Ndipo anthu adauzidwa: “Kodi inu musonkhana? (Choncho, sonkhanani).”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
لَعَلَّنَا نَتَّبِعُ ٱلسَّحَرَةَ إِن كَانُواْ هُمُ ٱلۡغَٰلِبِينَ
“Mwina tingawatsatire amatsenga ngati iwo ndiamene apambane.”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
فَلَمَّا جَآءَ ٱلسَّحَرَةُ قَالُواْ لِفِرۡعَوۡنَ أَئِنَّ لَنَا لَأَجۡرًا إِن كُنَّا نَحۡنُ ٱلۡغَٰلِبِينَ
Ndipo pamene amatsenga adadza, adati kwa Farawo: “Kodi tidzakhala ndi mphoto ngati ife ndife tipambane?”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
قَالَ نَعَمۡ وَإِنَّكُمۡ إِذٗا لَّمِنَ ٱلۡمُقَرَّبِينَ
(Farawo) adati: “Inde, (ndipo kuonjezera apo) ndithu inu mudzakhala mwa amene amakhala pafupi (ndi ine, monga nduna zanga).”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
قَالَ لَهُم مُّوسَىٰٓ أَلۡقُواْ مَآ أَنتُم مُّلۡقُونَ
Mûsa adati kwa iwo: “Ponyani zimene mufuna kuponya (zosonyeza kuya kwa matsenga anu).”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
فَأَلۡقَوۡاْ حِبَالَهُمۡ وَعِصِيَّهُمۡ وَقَالُواْ بِعِزَّةِ فِرۡعَوۡنَ إِنَّا لَنَحۡنُ ٱلۡغَٰلِبُونَ
Choncho adaponya zingwe zawo ndi ndodo zawo, ndipo adati: “Kupyolera mu mphamvu za Farawo, ndithu ife ndife opambana.”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
فَأَلۡقَىٰ مُوسَىٰ عَصَاهُ فَإِذَا هِيَ تَلۡقَفُ مَا يَأۡفِكُونَ
Kenako Mûsa adaponya ndodo yake; mwadzidzidzi iyo idameza zabodza zomwe iwo adakonza.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
فَأُلۡقِيَ ٱلسَّحَرَةُ سَٰجِدِينَ
Pamenepo amatsenga adadzigwetsa pansi molambira.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
قَالُوٓاْ ءَامَنَّا بِرَبِّ ٱلۡعَٰلَمِينَ
Adati: “Tamkhulupirira Mbuye wa zolengedwa.”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
رَبِّ مُوسَىٰ وَهَٰرُونَ
“Mbuye wa Mûsa ndi Harun.”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
قَالَ ءَامَنتُمۡ لَهُۥ قَبۡلَ أَنۡ ءَاذَنَ لَكُمۡۖ إِنَّهُۥ لَكَبِيرُكُمُ ٱلَّذِي عَلَّمَكُمُ ٱلسِّحۡرَ فَلَسَوۡفَ تَعۡلَمُونَۚ لَأُقَطِّعَنَّ أَيۡدِيَكُمۡ وَأَرۡجُلَكُم مِّنۡ خِلَٰفٖ وَلَأُصَلِّبَنَّكُمۡ أَجۡمَعِينَ
(Farawo) adati: “Ha! Mwamkhulupirira chotani ndisanakulolezeni? Ndithu iyeyu ndimkulu wanu amene adakuphunzitsani matsenga. Choncho posachedwa mudziwa (chimene ndikuchiteni) ndithu ndidula manja anu ndi miyendo yanu mosinthanitsa (podula mkono wakumanja ndi mwendo wakumanzere; kapena kudula mkono wakumanzere ndi mwendo wakumanja), ndipo kenako ndikupachikani nonsenu.”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
قَالُواْ لَا ضَيۡرَۖ إِنَّآ إِلَىٰ رَبِّنَا مُنقَلِبُونَ
(Amatsenga) adati: “Palibe vuto, ndithu ife (tonse) tibwerera kwa Mbuye wathu.”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
إِنَّا نَطۡمَعُ أَن يَغۡفِرَ لَنَا رَبُّنَا خَطَٰيَٰنَآ أَن كُنَّآ أَوَّلَ ٱلۡمُؤۡمِنِينَ
“Ndithu ife tikuyembekezera kuti Mbuye wathu atikhululukire zolakwa zathu; pokhala oyamba mwa okhulupirira.”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
۞ وَأَوۡحَيۡنَآ إِلَىٰ مُوسَىٰٓ أَنۡ أَسۡرِ بِعِبَادِيٓ إِنَّكُم مُّتَّبَعُونَ
Ndipo tidamvumbulutsira Mûsa (kuti): “Pita ndi anthu anga m’nthawi yausiku (musamuke m’dziko la Iguputo); ndithu inu mutsatidwa.”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
فَأَرۡسَلَ فِرۡعَوۡنُ فِي ٱلۡمَدَآئِنِ حَٰشِرِينَ
Choncho Farawo adatuma (owatuma) kuti asonkhanitse anthu m’mizinda (kuti aletse ana a Israyeli kutuluka).
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
إِنَّ هَٰٓؤُلَآءِ لَشِرۡذِمَةٞ قَلِيلُونَ
(Adawauza otumidwa aja kuti auze anthu kuti): “Ndithu awa (ana a Israyeli) ndikagulu kochepa.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَإِنَّهُمۡ لَنَا لَغَآئِظُونَ
Ndipo ndithu iwo akutikwiitsa.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَإِنَّا لَجَمِيعٌ حَٰذِرُونَ
Koma ndithu ife tonse (ndife ochuluka komabe ngakhale zili choncho) tikuwaopa.”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
فَأَخۡرَجۡنَٰهُم مِّن جَنَّٰتٖ وَعُيُونٖ
Choncho tidawatulutsa m’minda ndi mwa akasupe.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَكُنُوزٖ وَمَقَامٖ كَرِيمٖ
Ndi m’nkhokwe za chuma ndi m’malo okongola.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
كَذَٰلِكَۖ وَأَوۡرَثۡنَٰهَا بَنِيٓ إِسۡرَٰٓءِيلَ
Momwemo ndi mmene tidawachitira ndipo tidawalowetsera chokolo zinthu zawo zonse kwa ana a Israyeli.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
فَأَتۡبَعُوهُم مُّشۡرِقِينَ
Choncho (anthu a Farawo ndi iye mwini) adawatsatira (ana a Israyeli) dzuwa litatuluka.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
فَلَمَّا تَرَٰٓءَا ٱلۡجَمۡعَانِ قَالَ أَصۡحَٰبُ مُوسَىٰٓ إِنَّا لَمُدۡرَكُونَ
Ndipo pamene magulu awiri adaonana (anthu a Farawo ndi anthu a Mûsa), anthu a Mûsa adati: “Ndithu ife tigwidwa.”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
قَالَ كَلَّآۖ إِنَّ مَعِيَ رَبِّي سَيَهۡدِينِ
(Mûsa) adati: “Iyayi! Ndithu Mbuye wanga ali nane pamodzi. Andiongolera (kuti ife tonse tipulumuke).”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
فَأَوۡحَيۡنَآ إِلَىٰ مُوسَىٰٓ أَنِ ٱضۡرِب بِّعَصَاكَ ٱلۡبَحۡرَۖ فَٱنفَلَقَ فَكَانَ كُلُّ فِرۡقٖ كَٱلطَّوۡدِ ٱلۡعَظِيمِ
Ndipo tidam’vumbulutsira mawu Mûsa (akuti): “Menya nyanja ndi ndodo yako.” Ndipo idagawikana, mbali iliyonse idali ngati phiri lalikulu.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَأَزۡلَفۡنَا ثَمَّ ٱلۡأٓخَرِينَ
Ndipo tidawayandikitsa pamenepo anthu enawo, (Farawo ndi anthu ake nalowa pa njira yomweyo pambuyo pa Mûsa ndi anthu ake).
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَأَنجَيۡنَا مُوسَىٰ وَمَن مَّعَهُۥٓ أَجۡمَعِينَ
Ndipo tidapulumutsa Mûsa ndi onse amene adali nawo (mpaka adaoloka nyanjayo, madzi ali chiimire mbali iyi ndi iyi).
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
ثُمَّ أَغۡرَقۡنَا ٱلۡأٓخَرِينَ
Kenako tidawamiza enawo, (Farawo ndi anthu ake).
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
إِنَّ فِي ذَٰلِكَ لَأٓيَةٗۖ وَمَا كَانَ أَكۡثَرُهُم مُّؤۡمِنِينَ
Ndithu pa zimenezi pali lingaliro. Koma ambiri a iwo sali okhulupirira.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَإِنَّ رَبَّكَ لَهُوَ ٱلۡعَزِيزُ ٱلرَّحِيمُ
Ndipo, ndithu Mbuye wako ndi Mwini mphamvu zoposa (amalanga ndi chilango choopsa omwe amunyoza); Wachisoni (kwa omkhulupirira ndi kumumvera).
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَٱتۡلُ عَلَيۡهِمۡ نَبَأَ إِبۡرَٰهِيمَ
Ndipo awerengere (osakhulupirira) nkhani ya (M’neneri) Ibrahim.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
إِذۡ قَالَ لِأَبِيهِ وَقَوۡمِهِۦ مَا تَعۡبُدُونَ
Pamene adafunsa bambo wake ndi anthu ake (kuti); “Kodi mukupembedza chiyani?”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
قَالُواْ نَعۡبُدُ أَصۡنَامٗا فَنَظَلُّ لَهَا عَٰكِفِينَ
Adati: “Tikupembedza mafano; ndipo tipitiriza kuwapembedza.”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
قَالَ هَلۡ يَسۡمَعُونَكُمۡ إِذۡ تَدۡعُونَ
(Ibrahim) adati: “Kodi amakumvani mukawaitana?”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
أَوۡ يَنفَعُونَكُمۡ أَوۡ يَضُرُّونَ
“Kapena amakuthandizani (mukawapembedza) kapena amapereka masautso kwa inu (mukasiya kuwapembedza)?”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
قَالُواْ بَلۡ وَجَدۡنَآ ءَابَآءَنَا كَذَٰلِكَ يَفۡعَلُونَ
(Iwo) adati: “Koma tidapeza makolo athu akuchita zimenezi.”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
قَالَ أَفَرَءَيۡتُم مَّا كُنتُمۡ تَعۡبُدُونَ
(Ibrahim) adati: “Kodi mukuwaona awa amene mwakhala mukuwapembedza,”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
أَنتُمۡ وَءَابَآؤُكُمُ ٱلۡأَقۡدَمُونَ
“Inu ndi makolo anu amene adatsogola?”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
فَإِنَّهُمۡ عَدُوّٞ لِّيٓ إِلَّا رَبَّ ٱلۡعَٰلَمِينَ
“Ndithu iwo ndiadani anga, kupatula Mbuye wa zolengedwa zonse;”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
ٱلَّذِي خَلَقَنِي فَهُوَ يَهۡدِينِ
“Yemwe adandilenga, ndiponso Yemwe akundiongolera (kunjira yolungama);”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَٱلَّذِي هُوَ يُطۡعِمُنِي وَيَسۡقِينِ
“Ndiyemwe akundidyetsa ndi kundimwetsa.”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَإِذَا مَرِضۡتُ فَهُوَ يَشۡفِينِ
“Ndipo ndikadwala ndiyemwe amandichiritsa.”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَٱلَّذِي يُمِيتُنِي ثُمَّ يُحۡيِينِ
“Ndi Amene adzandipatsa imfa, ndipo (tsiku la Qiyâma) adzandidzutsa;”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَٱلَّذِيٓ أَطۡمَعُ أَن يَغۡفِرَ لِي خَطِيٓـَٔتِي يَوۡمَ ٱلدِّينِ
“Ndi Yemwe ndikuyembekezera kuti adzandikhululukira zolakwa zanga tsiku la malipiro.”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
رَبِّ هَبۡ لِي حُكۡمٗا وَأَلۡحِقۡنِي بِٱلصَّٰلِحِينَ
“E Mbuye wanga! Ndipatseni nzeru zoweruzira (zinthu), ndikundilumikiza ndi anthu abwino;”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَٱجۡعَل لِّي لِسَانَ صِدۡقٖ فِي ٱلۡأٓخِرِينَ
“Ndipatseni kutchulidwa kwabwino kwa anthu ena odza pambuyo;”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَٱجۡعَلۡنِي مِن وَرَثَةِ جَنَّةِ ٱلنَّعِيمِ
“Ndichiteni kukhala mmodzi mwa olandira Munda wamtendere;”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَٱغۡفِرۡ لِأَبِيٓ إِنَّهُۥ كَانَ مِنَ ٱلضَّآلِّينَ
“Ndipo khululukirani bambo wanga; ndithu iye adali mmodzi wa osokera;”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَلَا تُخۡزِنِي يَوۡمَ يُبۡعَثُونَ
“Ndipo musadzandiyalutse pa tsiku loukitsidwa anthu (ku imfa);”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
يَوۡمَ لَا يَنفَعُ مَالٞ وَلَا بَنُونَ
“Tsiku lomwe chuma ndi ana sizidzathandiza (aliyense).”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
إِلَّا مَنۡ أَتَى ٱللَّهَ بِقَلۡبٖ سَلِيمٖ
“Kupatula yemwe adzadza kwa Allah ndi mtima woyera (iye ndiamene adzathandizidwa patsikulo).”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَأُزۡلِفَتِ ٱلۡجَنَّةُ لِلۡمُتَّقِينَ
Ndipo Munda wamtendere udzayandikitsidwa kwa oopa (Allah),
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَبُرِّزَتِ ٱلۡجَحِيمُ لِلۡغَاوِينَ
Ndipo Jahannam idzaonetsedwa kwa opotoka;
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَقِيلَ لَهُمۡ أَيۡنَ مَا كُنتُمۡ تَعۡبُدُونَ
Ndipo kudzanenedwa kwa iwo: “Ali kuti amene mudali kuwapembedza aja,
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
مِن دُونِ ٱللَّهِ هَلۡ يَنصُرُونَكُمۡ أَوۡ يَنتَصِرُونَ
M’malo mwa Allah? Kodi angathe kukuthandizani kapena kudzithandiza okha?”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
فَكُبۡكِبُواْ فِيهَا هُمۡ وَٱلۡغَاوُۥنَ
Ndipo iwo ndi opotoka ena adzaponyedwa ndi nkhope zawo m’menemo (mu Jahannam).
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَجُنُودُ إِبۡلِيسَ أَجۡمَعُونَ
Ndi magulu onse ankhondo a Iblis (omwe adali kukometsa kwa anthu zoipa ndi machimo).
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
قَالُواْ وَهُمۡ فِيهَا يَخۡتَصِمُونَ
Adzanena (movomereza kulakwa kwawo) uku naonso ali m’menemo, akukangana (ndi anzawo omwe adawasokeretsa):
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
تَٱللَّهِ إِن كُنَّا لَفِي ضَلَٰلٖ مُّبِينٍ
“Ndikulumbira Allah, ndithu tidali m’kusokera kowonekera.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
إِذۡ نُسَوِّيكُم بِرَبِّ ٱلۡعَٰلَمِينَ
Pamene timakufananitsani ndi Mbuye wa zolengedwa.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَمَآ أَضَلَّنَآ إِلَّا ٱلۡمُجۡرِمُونَ
Ndipo sadatisokeretse, koma oipa okha basi.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
فَمَا لَنَا مِن شَٰفِعِينَ
Choncho ife tilibe aomboli (otiombola),
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَلَا صَدِيقٍ حَمِيمٖ
Ngakhalenso bwenzi wapamtima (woti angatipulumutse kumasautsowa).
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
فَلَوۡ أَنَّ لَنَا كَرَّةٗ فَنَكُونَ مِنَ ٱلۡمُؤۡمِنِينَ
Tikadapeza mwayi wobwerera (ku moyo wa padziko), tikadakhala mwa okhulupirira.”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
إِنَّ فِي ذَٰلِكَ لَأٓيَةٗۖ وَمَا كَانَ أَكۡثَرُهُم مُّؤۡمِنِينَ
Ndithu m’zimenezi, muli malingaliro akulu, koma ambiri a iwo sali okhulupirira.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَإِنَّ رَبَّكَ لَهُوَ ٱلۡعَزِيزُ ٱلرَّحِيمُ
Ndipo ndithu Mbuye wako, ndiye Mwini mphamvu zoposa; Wachisoni chosatha.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
كَذَّبَتۡ قَوۡمُ نُوحٍ ٱلۡمُرۡسَلِينَ
Anthu a Nuh adatsutsa atumiki.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
إِذۡ قَالَ لَهُمۡ أَخُوهُمۡ نُوحٌ أَلَا تَتَّقُونَ
Pamene adawauza Nuh m’bale wawo kuti: “Kodi simukuopa (Allah ngakhale nditakuuzani zoopsa zimene zikukudikirani)?”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
إِنِّي لَكُمۡ رَسُولٌ أَمِينٞ
“Ndithu ine kwa inu ndine Mtumiki wokhulupirika;”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
فَٱتَّقُواْ ٱللَّهَ وَأَطِيعُونِ
“Choncho muopeni Allah ndipo ndimvereni.”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَمَآ أَسۡـَٔلُكُمۡ عَلَيۡهِ مِنۡ أَجۡرٍۖ إِنۡ أَجۡرِيَ إِلَّا عَلَىٰ رَبِّ ٱلۡعَٰلَمِينَ
“Ndipo sindikupemphani malipiro pa zimenezi; malipiro anga ali kwa (Allah) Mbuye wa zolengedwa.”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
فَٱتَّقُواْ ٱللَّهَ وَأَطِيعُونِ
“Choncho muopeni Allah ndipo ndimvereni.”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
۞ قَالُوٓاْ أَنُؤۡمِنُ لَكَ وَٱتَّبَعَكَ ٱلۡأَرۡذَلُونَ
(Iwo) adati: “Nchotani kuti tikukhulupirire iwe chikhalirecho anthu wamba ndi amene akukutsatira?”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
قَالَ وَمَا عِلۡمِي بِمَا كَانُواْ يَعۡمَلُونَ
(Nuh) adati: “Sindikudziwa zimene adali kuchita (zomwe zachititsa kuti Allah awaongolere kunjira yoongoka).”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
إِنۡ حِسَابُهُمۡ إِلَّا عَلَىٰ رَبِّيۖ لَوۡ تَشۡعُرُونَ
“Chiwerengero chawo sichili kwina koma kwa Mbuye wanga, mukadakhala mukuzindikira.”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَمَآ أَنَا۠ بِطَارِدِ ٱلۡمُؤۡمِنِينَ
“Ndipo sindine wopirikitsa okhulupirira (ku chipembedzo cha Allah kuti inu olemekezeka muchikhulupirire).”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
إِنۡ أَنَا۠ إِلَّا نَذِيرٞ مُّبِينٞ
“Ine sikanthu , koma ndine mchenjezi woonekera.”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
قَالُواْ لَئِن لَّمۡ تَنتَهِ يَٰنُوحُ لَتَكُونَنَّ مِنَ ٱلۡمَرۡجُومِينَ
(Iwo) adati: “Ngati susiya, iwe Nuh, (zonena zakozi) ndithu ukhala mmodzi mwa ogendedwa (miyala mpaka ufe).”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
قَالَ رَبِّ إِنَّ قَوۡمِي كَذَّبُونِ
(Nuh) adati (kwa Allah): “Mbuye wanga! Ndithu anthu anga anditsutsa.”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
فَٱفۡتَحۡ بَيۡنِي وَبَيۡنَهُمۡ فَتۡحٗا وَنَجِّنِي وَمَن مَّعِيَ مِنَ ٱلۡمُؤۡمِنِينَ
Choncho weruzani pakati panga ndi pakati pa iwo (chiweruzo chabwino), ndipo ndipulumutseni pamodzi ndi amene alinane mwa okhulupirira.”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
فَأَنجَيۡنَٰهُ وَمَن مَّعَهُۥ فِي ٱلۡفُلۡكِ ٱلۡمَشۡحُونِ
Choncho, tidampulumutsa pamodzi ndi omwe adali naye m’chombo chodzadza (ndi chilichonse chamoyo chomwe chidalipo m’dziko, chachimuna ndi chachikazi chidaikidwa m’menemo).
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
ثُمَّ أَغۡرَقۡنَا بَعۡدُ ٱلۡبَاقِينَ
Pambuyo pake tidawamiza otsalawo.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
إِنَّ فِي ذَٰلِكَ لَأٓيَةٗۖ وَمَا كَانَ أَكۡثَرُهُم مُّؤۡمِنِينَ
Ndithu m’zimenezi muli malingaliro; koma ambiri a iwo sadali okhulupirira.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَإِنَّ رَبَّكَ لَهُوَ ٱلۡعَزِيزُ ٱلرَّحِيمُ
Ndipo ndithu Mbuye wako, Iye Ngwamphamvu zoposa; Ngwachisoni chosatha.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
كَذَّبَتۡ عَادٌ ٱلۡمُرۡسَلِينَ
Naonso Âdi adatsutsa atumiki.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
إِذۡ قَالَ لَهُمۡ أَخُوهُمۡ هُودٌ أَلَا تَتَّقُونَ
Pamene m’bale wawo (Mneneri) Hûd adawafunsa kuti: “Kodi simuopa (Allah)?”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
إِنِّي لَكُمۡ رَسُولٌ أَمِينٞ
“Ndithu ine ndine Mtumiki wokhulupirika kwa inu;”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
فَٱتَّقُواْ ٱللَّهَ وَأَطِيعُونِ
“Choncho, muopeni Allah ndipo mverani ine.”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَمَآ أَسۡـَٔلُكُمۡ عَلَيۡهِ مِنۡ أَجۡرٍۖ إِنۡ أَجۡرِيَ إِلَّا عَلَىٰ رَبِّ ٱلۡعَٰلَمِينَ
“Ndipo pazimenezi sindikukupemphani malipiro; ndithu malipiro anga ali kwa (Allah) Mbuye wa zolengedwa.”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
أَتَبۡنُونَ بِكُلِّ رِيعٍ ءَايَةٗ تَعۡبَثُونَ
“Kodi mukudzimangira nyumba pamalo paliponse pachitunda pokongola, moseweretsa?”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَتَتَّخِذُونَ مَصَانِعَ لَعَلَّكُمۡ تَخۡلُدُونَ
“Ndipo mukudzimangira (nyumba zonga) linga ngati kuti mukuona kuti mudzakhala muyaya?”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَإِذَا بَطَشۡتُم بَطَشۡتُمۡ جَبَّارِينَ
“Ndipo mukamamenya nkhondo mumamenya modzitukumula.”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
فَٱتَّقُواْ ٱللَّهَ وَأَطِيعُونِ
“Choncho muopeni Allah ndipo ndimvereni.”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَٱتَّقُواْ ٱلَّذِيٓ أَمَدَّكُم بِمَا تَعۡلَمُونَ
“Ndipo muopeni Yemwe adakupatsani zimene mukuzidziwa.”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
أَمَدَّكُم بِأَنۡعَٰمٖ وَبَنِينَ
“Adakupatsani ziweto ndi ana.”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَجَنَّٰتٖ وَعُيُونٍ
“Ndi minda ndi akasupe.”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
إِنِّيٓ أَخَافُ عَلَيۡكُمۡ عَذَابَ يَوۡمٍ عَظِيمٖ
“Ndithu ine ndikukuoperani chilango cha tsiku lalikulu.”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
قَالُواْ سَوَآءٌ عَلَيۡنَآ أَوَعَظۡتَ أَمۡ لَمۡ تَكُن مِّنَ ٱلۡوَٰعِظِينَ
Iwo adati: “Kwa ife nchimodzimodzi, utichenjeze kapena iwe usakhale mmodzi mwa ochenjeza.”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
إِنۡ هَٰذَآ إِلَّا خُلُقُ ٱلۡأَوَّلِينَ
“Ndithu kutero (anthu ena kudzitcha atumiki a Allah), sikanthu koma ndi machitidwe a anthu akale.”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَمَا نَحۡنُ بِمُعَذَّبِينَ
“Ndipo ife sitidzalangidwa (monga momwe ukunenera).”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
فَكَذَّبُوهُ فَأَهۡلَكۡنَٰهُمۡۚ إِنَّ فِي ذَٰلِكَ لَأٓيَةٗۖ وَمَا كَانَ أَكۡثَرُهُم مُّؤۡمِنِينَ
Choncho adamtsutsa, ndipo tidawaononga. Ndithu m’zimenezi muli malingaliro; koma ambiri a iwo sadali okhulupirira.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَإِنَّ رَبَّكَ لَهُوَ ٱلۡعَزِيزُ ٱلرَّحِيمُ
Ndipo ndithu Mbuye wako ndiye Wamphamvu zoposa; Wachisoni chosatha.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
كَذَّبَتۡ ثَمُودُ ٱلۡمُرۡسَلِينَ
A Samudu (naonso) adatsutsa atumiki.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
إِذۡ قَالَ لَهُمۡ أَخُوهُمۡ صَٰلِحٌ أَلَا تَتَّقُونَ
Pamene m’bale wawo Swalih adawauza kuti: “Kodi simuopa (Allah)?”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
إِنِّي لَكُمۡ رَسُولٌ أَمِينٞ
“Ndithu ine ndimtumiki wokhulupirika kwa inu.”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
فَٱتَّقُواْ ٱللَّهَ وَأَطِيعُونِ
“Choncho muopeni Allah ndipo mverani ine.”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَمَآ أَسۡـَٔلُكُمۡ عَلَيۡهِ مِنۡ أَجۡرٍۖ إِنۡ أَجۡرِيَ إِلَّا عَلَىٰ رَبِّ ٱلۡعَٰلَمِينَ
“Ndipo sindikupemphani malipiro pa zimenezi. Palibe kumene kuli malipiro anga koma kwa Mbuye wa zolengedwa.”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
أَتُتۡرَكُونَ فِي مَا هَٰهُنَآ ءَامِنِينَ
“Kodi (mukuganizira kuti) mudzasiidwa mwamtendere pa izi zili pano (popanda imfa kukudzerani?)”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
فِي جَنَّٰتٖ وَعُيُونٖ
“M’minda ndi mu akasupe?”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَزُرُوعٖ وَنَخۡلٖ طَلۡعُهَا هَضِيمٞ
“Ndi (m’minda) yammera ndi mitengo yakanjedza yamikoko yakupsa yofewa?”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَتَنۡحِتُونَ مِنَ ٱلۡجِبَالِ بُيُوتٗا فَٰرِهِينَ
“Ndipo mukugoba nyumba m’mapiri mwaluso.”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
فَٱتَّقُواْ ٱللَّهَ وَأَطِيعُونِ
“Choncho muopeni Allah ndipo ndimvereni.”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَلَا تُطِيعُوٓاْ أَمۡرَ ٱلۡمُسۡرِفِينَ
“Ndipo musamvere za awo opyola malire.”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
ٱلَّذِينَ يُفۡسِدُونَ فِي ٱلۡأَرۡضِ وَلَا يُصۡلِحُونَ
“Amene akuononga pa dziko, ndipo sakonza.”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
قَالُوٓاْ إِنَّمَآ أَنتَ مِنَ ٱلۡمُسَحَّرِينَ
Iwo adati: “Ndithu iwe ndi mmodzi wa olodzedwa.”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
مَآ أَنتَ إِلَّا بَشَرٞ مِّثۡلُنَا فَأۡتِ بِـَٔايَةٍ إِن كُنتَ مِنَ ٱلصَّٰدِقِينَ
“Iwe suli kanthu, koma munthu ngati ife; tabwera ndi chozizwitsa, ngati ndiwedi mmodzi wa onena zoona!”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
قَالَ هَٰذِهِۦ نَاقَةٞ لَّهَا شِرۡبٞ وَلَكُمۡ شِرۡبُ يَوۡمٖ مَّعۡلُومٖ
Iye adati: “(Ndakubweretserani) ngamira iyi yaikazi; (koma) ili ndi gawo lake lakumwa, ndipo inu muli ndi gawo lanu lakutunga (madzi) patsiku lodziwika. (Tsiku lina lotunga rnadzi anthu).”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَلَا تَمَسُّوهَا بِسُوٓءٖ فَيَأۡخُذَكُمۡ عَذَابُ يَوۡمٍ عَظِيمٖ
“Ndipo musaikhudze ndi choipa chilichonse kuopera kuti chingakupezeni chilango cha tsiku lalikulu.”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
فَعَقَرُوهَا فَأَصۡبَحُواْ نَٰدِمِينَ
Koma iwo adaipha; ndipo adali odzinena (pamene chidadza chilango cha Allah).
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
فَأَخَذَهُمُ ٱلۡعَذَابُۚ إِنَّ فِي ذَٰلِكَ لَأٓيَةٗۖ وَمَا كَانَ أَكۡثَرُهُم مُّؤۡمِنِينَ
Choncho chilango (cha Allah) chidawaononga, ndithu pa zimenezi pali phunziro; koma ambiri a iwo sadali okhulupirira.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَإِنَّ رَبَّكَ لَهُوَ ٱلۡعَزِيزُ ٱلرَّحِيمُ
Ndipo, ndithu Mbuye wako, Iye Ngwamphamvu zoposa; wachisoni chosatha.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
كَذَّبَتۡ قَوۡمُ لُوطٍ ٱلۡمُرۡسَلِينَ
Anthu a Luti adatsutsa atumiki.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
إِذۡ قَالَ لَهُمۡ أَخُوهُمۡ لُوطٌ أَلَا تَتَّقُونَ
Pamene m’bale wawo Luti adanena kwa iwo (kuti): “Kodi simuopa (Allah)?”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
إِنِّي لَكُمۡ رَسُولٌ أَمِينٞ
“Ndithu ine ndine Mtumiki wokhulupirika kwa inu.”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
فَٱتَّقُواْ ٱللَّهَ وَأَطِيعُونِ
“Choncho muopeni Allah ndipo ndimvereni.”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَمَآ أَسۡـَٔلُكُمۡ عَلَيۡهِ مِنۡ أَجۡرٍۖ إِنۡ أَجۡرِيَ إِلَّا عَلَىٰ رَبِّ ٱلۡعَٰلَمِينَ
“Ndipo sindikupemphani malipiro pa zimenezi; palibe komwe kuli malipiro anga koma kwa Mbuye wazolengedwa.”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
أَتَأۡتُونَ ٱلذُّكۡرَانَ مِنَ ٱلۡعَٰلَمِينَ
“Kodi mukugonana ndi amuna (anzanu) muzolengedwa (za Allah),
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَتَذَرُونَ مَا خَلَقَ لَكُمۡ رَبُّكُم مِّنۡ أَزۡوَٰجِكُمۚ بَلۡ أَنتُمۡ قَوۡمٌ عَادُونَ
“Ndikusiya amene Mbuye wanu adakulengerani kuti akhale akazi anu? Ndithu inu ndinu anthu olumpha malire.”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
قَالُواْ لَئِن لَّمۡ تَنتَهِ يَٰلُوطُ لَتَكُونَنَّ مِنَ ٱلۡمُخۡرَجِينَ
Iwo adati: “Ngati susiya (izi), E iwe Luti! ndithu ukhala mmodzi wa opirikitsidwa.”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
قَالَ إِنِّي لِعَمَلِكُم مِّنَ ٱلۡقَالِينَ
Iye adati: “Ndithu ine ndine m’modzi wakuzida izi zochita zanu (choncho Sindisiya kuzidzudzula).”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
رَبِّ نَجِّنِي وَأَهۡلِي مِمَّا يَعۡمَلُونَ
“E Mbuye wanga! Ndipulumutseni ine ndi banja langa ku (matsoka a) zimene akuchita.”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
فَنَجَّيۡنَٰهُ وَأَهۡلَهُۥٓ أَجۡمَعِينَ
Ndipo tidampulumutsa iye ndi onse a pa banja lake,
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
إِلَّا عَجُوزٗا فِي ٱلۡغَٰبِرِينَ
Kupatula nkhalamba yaikazi idali mwa otsalira m’mbuyo.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
ثُمَّ دَمَّرۡنَا ٱلۡأٓخَرِينَ
Titatero tidawaononga enawo.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَأَمۡطَرۡنَا عَلَيۡهِم مَّطَرٗاۖ فَسَآءَ مَطَرُ ٱلۡمُنذَرِينَ
Ndipo tidawavumbwitsira mvula (yamiyala); iyipirenji, mvula ya ochenjezedwa!
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
إِنَّ فِي ذَٰلِكَ لَأٓيَةٗۖ وَمَا كَانَ أَكۡثَرُهُم مُّؤۡمِنِينَ
Ndithu pazimenezi pali malingaliro. Koma ambiri a iwo sadali okhulupirira.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَإِنَّ رَبَّكَ لَهُوَ ٱلۡعَزِيزُ ٱلرَّحِيمُ
Ndipo, ndithu Mbuye wako, Ngwamphamvu kwambiri; Ngwachisoni chosatha.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
كَذَّبَ أَصۡحَٰبُ لۡـَٔيۡكَةِ ٱلۡمُرۡسَلِينَ
Anthu a m’dziko lamitengo yambiri (Madiana) adatsutsa atumiki.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
إِذۡ قَالَ لَهُمۡ شُعَيۡبٌ أَلَا تَتَّقُونَ
(Akumbutse) pamene (Mneneri) Shuaib adati kwa iwo: “Kodi simuopa (Allah)?”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
إِنِّي لَكُمۡ رَسُولٌ أَمِينٞ
“Ndithu ndine Mtumiki wokhulupirika kwa inu.”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
فَٱتَّقُواْ ٱللَّهَ وَأَطِيعُونِ
“Choncho muopeni Allah ndipo ndimvereni.”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَمَآ أَسۡـَٔلُكُمۡ عَلَيۡهِ مِنۡ أَجۡرٍۖ إِنۡ أَجۡرِيَ إِلَّا عَلَىٰ رَبِّ ٱلۡعَٰلَمِينَ
“Ndipo sindikupemphani malipiro pa zimenezi; kulibe malipiro anga koma kwa (Allah) Mbuye wa zolengedwa.”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
۞ أَوۡفُواْ ٱلۡكَيۡلَ وَلَا تَكُونُواْ مِنَ ٱلۡمُخۡسِرِينَ
“Kwaniritsani mulingo (pamalonda pamene mukupima), ndipo musakhale mwaopungula (mulingo).”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَزِنُواْ بِٱلۡقِسۡطَاسِ ٱلۡمُسۡتَقِيمِ
“Ndipo yesani ndi sikelo yolungama (yolondola).”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَلَا تَبۡخَسُواْ ٱلنَّاسَ أَشۡيَآءَهُمۡ وَلَا تَعۡثَوۡاْ فِي ٱلۡأَرۡضِ مُفۡسِدِينَ
“Ndipo musawachepetsere anthu zinthu zawo, ndiponso musayende padziko uku mukuononga.”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَٱتَّقُواْ ٱلَّذِي خَلَقَكُمۡ وَٱلۡجِبِلَّةَ ٱلۡأَوَّلِينَ
“Ndipo muopeni amene adalenga inu ndiponso zolengedwa zoyamba (zimene zidanka kale).”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
قَالُوٓاْ إِنَّمَآ أَنتَ مِنَ ٱلۡمُسَحَّرِينَ
Iwo adati: “Ndithu iwe ndi mmodzi wa olodzedwa.”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَمَآ أَنتَ إِلَّا بَشَرٞ مِّثۡلُنَا وَإِن نَّظُنُّكَ لَمِنَ ٱلۡكَٰذِبِينَ
“Ndipo iwe suli kanthu koma munthu ngati ife, ndipo ndithu tikukutsimikizira kuti ndiwe mmodzi wa abodza.”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
فَأَسۡقِطۡ عَلَيۡنَا كِسَفٗا مِّنَ ٱلسَّمَآءِ إِن كُنتَ مِنَ ٱلصَّٰدِقِينَ
“Choncho tigwetsere zidutswa za thambo (kuti zitiononge) ngati uli mmodzi wa onena zoona.”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
قَالَ رَبِّيٓ أَعۡلَمُ بِمَا تَعۡمَلُونَ
(Shuaib) adati: “Mbuye wanga Ngodziwa kwambiri zimene mukuchita. (Akadzaona kuti inu ngoyenera kulangidwa ndizidutswa za thambo, adzakulangani).”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
فَكَذَّبُوهُ فَأَخَذَهُمۡ عَذَابُ يَوۡمِ ٱلظُّلَّةِۚ إِنَّهُۥ كَانَ عَذَابَ يَوۡمٍ عَظِيمٍ
Koma adamutsutsa. Ndipo chidawagwera chilango chatsiku la mthunzi; ndithu chimenecho chidali chilango cha tsiku lalikulu.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
إِنَّ فِي ذَٰلِكَ لَأٓيَةٗۖ وَمَا كَانَ أَكۡثَرُهُم مُّؤۡمِنِينَ
Ndithu pa zimenezi pali lingaliro; koma ambiri a iwo sadali okhulupirira.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَإِنَّ رَبَّكَ لَهُوَ ٱلۡعَزِيزُ ٱلرَّحِيمُ
Ndipo, ndithu Mbuye wako Ngwamphamvu kwambiri; Ngwachisoni chosatha.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَإِنَّهُۥ لَتَنزِيلُ رَبِّ ٱلۡعَٰلَمِينَ
Ndipo, ndithu iyi (Qur’an) ndiyo chivumbulutso cha Mbuye wazolengedwa zonse.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
نَزَلَ بِهِ ٱلرُّوحُ ٱلۡأَمِينُ
Mzimu Wokhulupirika (Jiburil) udaivumbulutsa.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
عَلَىٰ قَلۡبِكَ لِتَكُونَ مِنَ ٱلۡمُنذِرِينَ
Pa mtima wako kuti ukhale mmodzi wa achenjezi,
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
بِلِسَانٍ عَرَبِيّٖ مُّبِينٖ
M’chiyankhulo cha Chiarabu chomveka bwino.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَإِنَّهُۥ لَفِي زُبُرِ ٱلۡأَوَّلِينَ
Ndipo ndithu izi (zomwe zili m’Qur’an) zilipo m’mabuku akale.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
أَوَلَمۡ يَكُن لَّهُمۡ ءَايَةً أَن يَعۡلَمَهُۥ عُلَمَٰٓؤُاْ بَنِيٓ إِسۡرَٰٓءِيلَ
Kodi sipadapezeke chisonyezo kwa iwo kuti akuidziwa (Qur’an) odziwa mwa ana a Israyeli (kotero kuti ena alowa m’Chisilamu)?
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَلَوۡ نَزَّلۡنَٰهُ عَلَىٰ بَعۡضِ ٱلۡأَعۡجَمِينَ
Ndipo tikadaivumbulutsa kwa wina amene sali Muarabu,
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
فَقَرَأَهُۥ عَلَيۡهِم مَّا كَانُواْ بِهِۦ مُؤۡمِنِينَ
Kotero kuti nkuwawerengera momveka bwino, sakadaikhulupirira.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
كَذَٰلِكَ سَلَكۡنَٰهُ فِي قُلُوبِ ٱلۡمُجۡرِمِينَ
Momwemo ndimo tidalowetsera kuitsutsa (Qur’an) m’mitima ya oipa.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
لَا يُؤۡمِنُونَ بِهِۦ حَتَّىٰ يَرَوُاْ ٱلۡعَذَابَ ٱلۡأَلِيمَ
Sangaikhulupirire kufikira ataona chilango chowawa.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
فَيَأۡتِيَهُم بَغۡتَةٗ وَهُمۡ لَا يَشۡعُرُونَ
Choncho chidzawadzera mwadzidzidzi pomwe iwo sakuzindikira.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
فَيَقُولُواْ هَلۡ نَحۡنُ مُنظَرُونَ
Tero adzayamba kunena: “Kodi ife tipatsidwa nthawi (yoti tilape)?”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
أَفَبِعَذَابِنَا يَسۡتَعۡجِلُونَ
Kodi akuchifulumizitsa chilango Chathu?
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
أَفَرَءَيۡتَ إِن مَّتَّعۡنَٰهُمۡ سِنِينَ
Kodi ukuona bwanji, ngati titawasangalatsa zaka (zankhaninkhani).
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
ثُمَّ جَآءَهُم مَّا كَانُواْ يُوعَدُونَ
Kenako nkuwadzera (chilango) chomwe adalonjezedwa,
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
مَآ أَغۡنَىٰ عَنۡهُم مَّا كَانُواْ يُمَتَّعُونَ
Sizidawathandize zomwe adali kusangalatsidwa nazozo.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَمَآ أَهۡلَكۡنَا مِن قَرۡيَةٍ إِلَّا لَهَا مُنذِرُونَ
Ndipo sitidauononge mudzi uliwonse koma udali ndi achenjezi.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
ذِكۡرَىٰ وَمَا كُنَّا ظَٰلِمِينَ
(Kuti akhale) chikumbutso. Ndipo sitidali osalungama (powaononga popanda kuwachenjeza).
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَمَا تَنَزَّلَتۡ بِهِ ٱلشَّيَٰطِينُ
Ndipo asatana sadaivumbulutse (iyi Qur’an monga osakhulupirira akunenera monyoza).
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَمَا يَنۢبَغِي لَهُمۡ وَمَا يَسۡتَطِيعُونَ
Ndipo sikoyenera kwa iwo (kuivumbulutsa Qur’an) ndiponso sangathe.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
إِنَّهُمۡ عَنِ ٱلسَّمۡعِ لَمَعۡزُولُونَ
Ndithu iwo ngotsekerezedwa kumvetsera (zimene angelo amalankhula kumwamba).
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
فَلَا تَدۡعُ مَعَ ٱللَّهِ إِلَٰهًا ءَاخَرَ فَتَكُونَ مِنَ ٱلۡمُعَذَّبِينَ
Choncho usapembedze mulungu wina pamodzi ndi Allah, kuti ungakhale mwa olangidwa.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَأَنذِرۡ عَشِيرَتَكَ ٱلۡأَقۡرَبِينَ
Ndipo achenjeze abale ako a pafupi.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَٱخۡفِضۡ جَنَاحَكَ لِمَنِ ٱتَّبَعَكَ مِنَ ٱلۡمُؤۡمِنِينَ
Ndipo fungatira ndi phiko lako amene akutsata mwa okhulupirira. (Ukhale wachifundo kwa iwo).
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
فَإِنۡ عَصَوۡكَ فَقُلۡ إِنِّي بَرِيٓءٞ مِّمَّا تَعۡمَلُونَ
Ngati atakunyoza, nena: “Ine ndili kutali ndi zimene mukuchitazo.”
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَتَوَكَّلۡ عَلَى ٱلۡعَزِيزِ ٱلرَّحِيمِ
Ndipo tsamira kwa (Mbuye wako) Mwini mphamvu zoposa; Wachisoni chosatha.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
ٱلَّذِي يَرَىٰكَ حِينَ تَقُومُ
Yemwe akukuona pamene ukuimilira (pamapemphero).
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَتَقَلُّبَكَ فِي ٱلسَّٰجِدِينَ
Ndikutembenukatembenuka kwako (pogwetsa mphumi yako pansi ndi kudzuka ndi kuimilira) pamodzi ndi ogwetsa mphumi pansi (polambira Allah).
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
إِنَّهُۥ هُوَ ٱلسَّمِيعُ ٱلۡعَلِيمُ
Ndithu Iye Ngwakumva; Ngodziwa chilichonse.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
هَلۡ أُنَبِّئُكُمۡ عَلَىٰ مَن تَنَزَّلُ ٱلشَّيَٰطِينُ
Kodi ndikuuzeni amene asatana amawatsikira?
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
تَنَزَّلُ عَلَىٰ كُلِّ أَفَّاكٍ أَثِيمٖ
Amamtsikira yense wabodza lamkunkhuniza; wamachimo.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
يُلۡقُونَ ٱلسَّمۡعَ وَأَكۡثَرُهُمۡ كَٰذِبُونَ
Amawaponyera (asatana anzawo a mu anthu) zimene azimva. Koma ambiri a iwo ngabodza.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَٱلشُّعَرَآءُ يَتَّبِعُهُمُ ٱلۡغَاوُۥنَ
Ndipo alakatuli (olakatula zopanda phindu) amatsatidwa ndi (anthu) opotoka.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
أَلَمۡ تَرَ أَنَّهُمۡ فِي كُلِّ وَادٖ يَهِيمُونَ
Kodi suona kuti iwo akungoyumbayumba m’chigwa chilichonse (chamawu)?
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
وَأَنَّهُمۡ يَقُولُونَ مَا لَا يَفۡعَلُونَ
Ndithunso iwo akunena zomwe sachita.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
إِلَّا ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ وَعَمِلُواْ ٱلصَّٰلِحَٰتِ وَذَكَرُواْ ٱللَّهَ كَثِيرٗا وَٱنتَصَرُواْ مِنۢ بَعۡدِ مَا ظُلِمُواْۗ وَسَيَعۡلَمُ ٱلَّذِينَ ظَلَمُوٓاْ أَيَّ مُنقَلَبٖ يَنقَلِبُونَ
Kupatula amene akhulupirira ndikumachita zabwino, ndikumamtchula Allah mowirikiza, ndikuzipulumutsa okha pambuyo pochitiridwa zoipa. Ndipo posachedwa amene adzichitira okha zoipa adziwa kotembenukira komwe adzatembenukire.
Các Tafsir tiếng Ả-rập:
 
Ý nghĩa nội dung Chương: Chương Al-Shu-'ara'
Mục lục các chương Kinh Số trang
 
Bản dịch ý nghĩa nội dung Qur'an - Dịch thuật tiếng Chichio - Mục lục các bản dịch

Bản dịch ý nghĩa nội dung Kinh Qur'an bằng tiếng Chichio, do Khalid Ibrahim Petala dịch thuật, bản dịch năm 2020.

Đóng lại