Ibisobanuro bya qoran ntagatifu - Ibisobanuro mu rurimi rw''urushiishiyu * - Ishakiro ry'ibisobanuro


Ibisobanuro by'amagambo Isura: Alkawthar (Ibyiza byinshi)   Umurongo:

Alkawthar (Ibyiza byinshi)

إِنَّآ أَعۡطَيۡنَٰكَ ٱلۡكَوۡثَرَ
Ndithu takupatsa zabwino zambiri (zina mwa izo ndi mtsinje wotchedwa Kauthar).[490]
[490] Tanthauzo la “zabwino zambiri” apa, ndi uneneri, maphunziro, ntchito zabwino, ulemelero, kupambana pakukhala ndi omutsatira ambiri ndi zabwino zina zam’dziko lino lapansi ndi tsiku lachimaliziro, zosawerengeka zomwe sadapatsidwe aliyense pambuyo pa iye ngakhale mtsogolo mwake. Ndithu zimenezi, popanda chikaiko, ndizabwino kwambiri kuposa chuma ndi ana.
Ibisobanuro by'icyarabu:
فَصَلِّ لِرَبِّكَ وَٱنۡحَرۡ
(Pakuti ndakupatsa zimenezo), pitiriza kupembedza Mbuye wako (moyera mtima) ndipo ipha nsembe yako (chifukwa chakuthokoza Allah pa zimene wakupatsa, monga ulemelero ndikukusankhira zabwino zambiri).[491]
[491] Tanthauzo loti “Mbuye wako yekha umupembedze” nkuti amupembedze Allah Yekha, asachite chiphamaso, asakhale monga amene amachita mapemphero ndi cholinga choti adzionetsere kwa anthu. Ndikutinso apereke nsembe m’dzina Lake, osati azimu ndi zina zotero.
Ibisobanuro by'icyarabu:
إِنَّ شَانِئَكَ هُوَ ٱلۡأَبۡتَرُ
Ndithu mdani wako ndiye ali wopanda mwawi. [492]
[492] Adani a Mtumiki (s.a.w) adali kukondwera kwambiri pamene ankaona kuti ana ake onse achimuna atha kumwalira, iwo ankaona kuti palibe ubwino uli onse kwa munthu pano pa dziko ngati sadapatsidwe ana achimuna ndi chuma. Pa chifukwa ichi, adali kumutcha “Abtar,” wopanda madalitso. Msura imeneyi Allah akumtonthoza Mneneriyo ndiponso akuyankha adani ake.
Ibisobanuro by'icyarabu:
 
Ibisobanuro by'amagambo Isura: Alkawthar (Ibyiza byinshi)
Urutonde rw'amasura numero y'urupapuro
 
Ibisobanuro bya qoran ntagatifu - Ibisobanuro mu rurimi rw''urushiishiyu - Ishakiro ry'ibisobanuro

Ibisobanuro bya qor'an ntagatifu mu rurimi rw'urushiishiyu, byasobanuwe na KHALID IBAHIIM BIITALA kopi ya 2020

Gufunga