Salin ng mga Kahulugan ng Marangal na Qur'an - الترجمة الشيشيوا * - Indise ng mga Salin


Salin ng mga Kahulugan Surah: Al-Kawthar   Ayah:

Al-Kawthar

إِنَّآ أَعۡطَيۡنَٰكَ ٱلۡكَوۡثَرَ
Ndithu takupatsa zabwino zambiri (zina mwa izo ndi mtsinje wotchedwa Kauthar).[490]
[490] Tanthauzo la “zabwino zambiri” apa, ndi uneneri, maphunziro, ntchito zabwino, ulemelero, kupambana pakukhala ndi omutsatira ambiri ndi zabwino zina zam’dziko lino lapansi ndi tsiku lachimaliziro, zosawerengeka zomwe sadapatsidwe aliyense pambuyo pa iye ngakhale mtsogolo mwake. Ndithu zimenezi, popanda chikaiko, ndizabwino kwambiri kuposa chuma ndi ana.
Ang mga Tafsir na Arabe:
فَصَلِّ لِرَبِّكَ وَٱنۡحَرۡ
(Pakuti ndakupatsa zimenezo), pitiriza kupembedza Mbuye wako (moyera mtima) ndipo ipha nsembe yako (chifukwa chakuthokoza Allah pa zimene wakupatsa, monga ulemelero ndikukusankhira zabwino zambiri).[491]
[491] Tanthauzo loti “Mbuye wako yekha umupembedze” nkuti amupembedze Allah Yekha, asachite chiphamaso, asakhale monga amene amachita mapemphero ndi cholinga choti adzionetsere kwa anthu. Ndikutinso apereke nsembe m’dzina Lake, osati azimu ndi zina zotero.
Ang mga Tafsir na Arabe:
إِنَّ شَانِئَكَ هُوَ ٱلۡأَبۡتَرُ
Ndithu mdani wako ndiye ali wopanda mwawi. [492]
[492] Adani a Mtumiki (s.a.w) adali kukondwera kwambiri pamene ankaona kuti ana ake onse achimuna atha kumwalira, iwo ankaona kuti palibe ubwino uli onse kwa munthu pano pa dziko ngati sadapatsidwe ana achimuna ndi chuma. Pa chifukwa ichi, adali kumutcha “Abtar,” wopanda madalitso. Msura imeneyi Allah akumtonthoza Mneneriyo ndiponso akuyankha adani ake.
Ang mga Tafsir na Arabe:
 
Salin ng mga Kahulugan Surah: Al-Kawthar
Indise ng mga Surah Numero ng Pahina
 
Salin ng mga Kahulugan ng Marangal na Qur'an - الترجمة الشيشيوا - Indise ng mga Salin

ترجمة معاني القرآن الكريم إلى اللغة الشيشيوا، ترجمها خالد إبراهيم بيتالا. نسخة عام 2020م.

Isara