Ibisobanuro bya qoran ntagatifu - Ibisobanuro mu rurimi rw''urushiishiyu * - Ishakiro ry'ibisobanuro


Ibisobanuro by'amagambo Isura: Al_Ma’uun (Ibikoresho byo mu rugo)   Umurongo:

Al_Ma’uun (Ibikoresho byo mu rugo)

أَرَءَيۡتَ ٱلَّذِي يُكَذِّبُ بِٱلدِّينِ
Kodi wamuona yemwe akutsutsa za mphoto (ndi chiwerengero cha tsiku lachimaliziro)?[487]
[487] Sura imeneyi ikufotokoza m’mene alili makhalidwe a anthu ambiri, ngakhale amene amadzitcha kuti ndi Asilamu. Aliyense amene ali ndi makhalidwe otere ndiye kuti sakhulupilira za tsiku la chiweruziro. Akadakhala kuti akukhulupilira za tsikuli, sibwenzi akusiya kuwachitira za chifundo osauka ndi amasiye. Sapereka chithandizo ngakhale kulimbikitsa ena ngati iye alibe.
Ibisobanuro by'icyarabu:
فَذَٰلِكَ ٱلَّذِي يَدُعُّ ٱلۡيَتِيمَ
Iye ndi yemwe akukankha wamasiye (mwankhanza).
Ibisobanuro by'icyarabu:
وَلَا يَحُضُّ عَلَىٰ طَعَامِ ٱلۡمِسۡكِينِ
Ndipo salimbikitsa (ena pamodzi ndi iye mwini) kudyetsa osauka.
Ibisobanuro by'icyarabu:
فَوَيۡلٞ لِّلۡمُصَلِّينَ
Choncho kuonongeka kuli pa ena mwa opemphera swala (amene ali ndi mbiri izi);
Ibisobanuro by'icyarabu:
ٱلَّذِينَ هُمۡ عَن صَلَاتِهِمۡ سَاهُونَ
Omwe amachitira mphwayi mapemphero awo.[488]
[488] Kuchitira mphwayi mapemphero (Swala), kumeneku ndiko kupemphera modukizadukiza. Tsiku lina nkupempherapo, tsiku lina ayi. Kapenanso kupemphera modzionetsera kwa anthu (riyaa).
Ibisobanuro by'icyarabu:
ٱلَّذِينَ هُمۡ يُرَآءُونَ
Amenenso (akamachita mapemphero awo) amadzionetsera (kwa anthu mwachipha maso kuti apeze ulemelero ndi kutamandidwa mmitima mwa anthu).[489]
[489] Riyaa ndiko kuchita ntchito yabwino ndicholinga choonetsa anthu, kuti akuone kuti ndiwe wabwino, mwina kuti ukhale wokondedwa ndi anthu. Kapenanso kuti upeze za m’matumba mwawo. Amenewa ndi machitidwe a “Shiriki” (kum’phatikiza Allah ndi zolengedwa Zake pa mapemphero) ndiponso ndi njira yobera anthu.
Ibisobanuro by'icyarabu:
وَيَمۡنَعُونَ ٱلۡمَاعُونَ
Ndipo amamana ziwiya (zawo posabwereka anzawo zinthu zofunika pa moyo wa aliyense monga nkhwangwa, mpeni, mtondo ndi zina zotere).
Ibisobanuro by'icyarabu:
 
Ibisobanuro by'amagambo Isura: Al_Ma’uun (Ibikoresho byo mu rugo)
Urutonde rw'amasura numero y'urupapuro
 
Ibisobanuro bya qoran ntagatifu - Ibisobanuro mu rurimi rw''urushiishiyu - Ishakiro ry'ibisobanuro

Ibisobanuro bya qor'an ntagatifu mu rurimi rw'urushiishiyu, byasobanuwe na KHALID IBAHIIM BIITALA kopi ya 2020

Gufunga