Tradução dos significados do Nobre Qur’an. - Tradução para a língua chachio * - Índice de tradução


Tradução dos significados Surah: Suratu Al-Maa'un   Versículo:

Suratu Al-Maa'un

أَرَءَيۡتَ ٱلَّذِي يُكَذِّبُ بِٱلدِّينِ
Kodi wamuona yemwe akutsutsa za mphoto (ndi chiwerengero cha tsiku lachimaliziro)?[487]
[487] Sura imeneyi ikufotokoza m’mene alili makhalidwe a anthu ambiri, ngakhale amene amadzitcha kuti ndi Asilamu. Aliyense amene ali ndi makhalidwe otere ndiye kuti sakhulupilira za tsiku la chiweruziro. Akadakhala kuti akukhulupilira za tsikuli, sibwenzi akusiya kuwachitira za chifundo osauka ndi amasiye. Sapereka chithandizo ngakhale kulimbikitsa ena ngati iye alibe.
Os Tafssir em língua árabe:
فَذَٰلِكَ ٱلَّذِي يَدُعُّ ٱلۡيَتِيمَ
Iye ndi yemwe akukankha wamasiye (mwankhanza).
Os Tafssir em língua árabe:
وَلَا يَحُضُّ عَلَىٰ طَعَامِ ٱلۡمِسۡكِينِ
Ndipo salimbikitsa (ena pamodzi ndi iye mwini) kudyetsa osauka.
Os Tafssir em língua árabe:
فَوَيۡلٞ لِّلۡمُصَلِّينَ
Choncho kuonongeka kuli pa ena mwa opemphera swala (amene ali ndi mbiri izi);
Os Tafssir em língua árabe:
ٱلَّذِينَ هُمۡ عَن صَلَاتِهِمۡ سَاهُونَ
Omwe amachitira mphwayi mapemphero awo.[488]
[488] Kuchitira mphwayi mapemphero (Swala), kumeneku ndiko kupemphera modukizadukiza. Tsiku lina nkupempherapo, tsiku lina ayi. Kapenanso kupemphera modzionetsera kwa anthu (riyaa).
Os Tafssir em língua árabe:
ٱلَّذِينَ هُمۡ يُرَآءُونَ
Amenenso (akamachita mapemphero awo) amadzionetsera (kwa anthu mwachipha maso kuti apeze ulemelero ndi kutamandidwa mmitima mwa anthu).[489]
[489] Riyaa ndiko kuchita ntchito yabwino ndicholinga choonetsa anthu, kuti akuone kuti ndiwe wabwino, mwina kuti ukhale wokondedwa ndi anthu. Kapenanso kuti upeze za m’matumba mwawo. Amenewa ndi machitidwe a “Shiriki” (kum’phatikiza Allah ndi zolengedwa Zake pa mapemphero) ndiponso ndi njira yobera anthu.
Os Tafssir em língua árabe:
وَيَمۡنَعُونَ ٱلۡمَاعُونَ
Ndipo amamana ziwiya (zawo posabwereka anzawo zinthu zofunika pa moyo wa aliyense monga nkhwangwa, mpeni, mtondo ndi zina zotere).
Os Tafssir em língua árabe:
 
Tradução dos significados Surah: Suratu Al-Maa'un
Índice de capítulos Número de página
 
Tradução dos significados do Nobre Qur’an. - Tradução para a língua chachio - Índice de tradução

Tradução de significados do Nobre Al-Qur'án para a língua Chichio, traduzido por Khalid Ibrahim Bitálá. Edição do ano 2020

Fechar