Check out the new design

அல்குர்ஆன் மொழிபெயர்ப்பு - ஷேவா(Chewa) மொழிபெயர்ப்பு - காலித் இப்ராஹிம் பேடாலா * - மொழிபெயர்ப்பு அட்டவணை


மொழிபெயர்ப்பு அத்தியாயம்: அத்தவ்பா   வசனம்:
يَحۡلِفُونَ بِٱللَّهِ لَكُمۡ لِيُرۡضُوكُمۡ وَٱللَّهُ وَرَسُولُهُۥٓ أَحَقُّ أَن يُرۡضُوهُ إِن كَانُواْ مُؤۡمِنِينَ
Akulumbira kwa inu potchula dzina la Allah kuti akukondweretseni (chikhalirecho akunyoza Allah ndi Mtumiki Wake), pomwe Allah ndi Mtumiki Wake ndiye wofunika kuti amkondweretse ngati iwo ngokhulupiriradi (mwachoonadi).
அரபு விரிவுரைகள்:
أَلَمۡ يَعۡلَمُوٓاْ أَنَّهُۥ مَن يُحَادِدِ ٱللَّهَ وَرَسُولَهُۥ فَأَنَّ لَهُۥ نَارَ جَهَنَّمَ خَٰلِدٗا فِيهَاۚ ذَٰلِكَ ٱلۡخِزۡيُ ٱلۡعَظِيمُ
Kodi sadziwa kuti amene akulimbana ndi Allah ndi Mtumiki Wake, adzapeza moto wa Jahannam ndi kukhalamo nthawi yaitali? Kumeneko ndikuyaluka kwakukulu.
அரபு விரிவுரைகள்:
يَحۡذَرُ ٱلۡمُنَٰفِقُونَ أَن تُنَزَّلَ عَلَيۡهِمۡ سُورَةٞ تُنَبِّئُهُم بِمَا فِي قُلُوبِهِمۡۚ قُلِ ٱسۡتَهۡزِءُوٓاْ إِنَّ ٱللَّهَ مُخۡرِجٞ مَّا تَحۡذَرُونَ
Achiphamaso akuopa kuwatsikira Sura yomwe ingawafotokozere (zachinyengo chawo) chomwe chili m’mitima mwawo. Nena: “Chitani zachipongwe. Ndithu Allah atulutsira poyera zomwe mukuziopazo (kuti Asilamu asazidziwe).”
அரபு விரிவுரைகள்:
وَلَئِن سَأَلۡتَهُمۡ لَيَقُولُنَّ إِنَّمَا كُنَّا نَخُوضُ وَنَلۡعَبُۚ قُلۡ أَبِٱللَّهِ وَءَايَٰتِهِۦ وَرَسُولِهِۦ كُنتُمۡ تَسۡتَهۡزِءُونَ
Ndipo utawafunsa (chifukwa ninji chipembedzo akuchichitira chipongwe)? Anena: “Ife timangosereula ndi kusewera basi (palibe china).” Nena: “Mumachitira Allah ndi Ayah (ndime) Zake ndi Mtumiki Wake zachipongwe?”
அரபு விரிவுரைகள்:
لَا تَعۡتَذِرُواْ قَدۡ كَفَرۡتُم بَعۡدَ إِيمَٰنِكُمۡۚ إِن نَّعۡفُ عَن طَآئِفَةٖ مِّنكُمۡ نُعَذِّبۡ طَآئِفَةَۢ بِأَنَّهُمۡ كَانُواْ مُجۡرِمِينَ
Musapereke madandaulo (abodza), ndithu mwaonetsera ukafiri wanu poyera, pambuyo pa kukhulupirira kwanu (kwabodza). Ngati gulu lina mwa inu tilikhululukira (litalapa), gulu lina tililanga chifukwa cha kupitiriza kulakwa kwawo.
அரபு விரிவுரைகள்:
ٱلۡمُنَٰفِقُونَ وَٱلۡمُنَٰفِقَٰتُ بَعۡضُهُم مِّنۢ بَعۡضٖۚ يَأۡمُرُونَ بِٱلۡمُنكَرِ وَيَنۡهَوۡنَ عَنِ ٱلۡمَعۡرُوفِ وَيَقۡبِضُونَ أَيۡدِيَهُمۡۚ نَسُواْ ٱللَّهَ فَنَسِيَهُمۡۚ إِنَّ ٱلۡمُنَٰفِقِينَ هُمُ ٱلۡفَٰسِقُونَ
Achiphamaso aamuna ndi achiphamaso aakazi onse khalidwe lawo ndi limodzi. Amalamulira zoipa ndikuletsa zabwino, ndipo amafumbata manja awo (sathandiza pa zabwino). Amuiwala Allah (ponyozera malamulo Ake). Iyenso wawaiwala (powanyozera). Ndithu achiphamaso ngotuluka mchilamulo (cha Allah).
அரபு விரிவுரைகள்:
وَعَدَ ٱللَّهُ ٱلۡمُنَٰفِقِينَ وَٱلۡمُنَٰفِقَٰتِ وَٱلۡكُفَّارَ نَارَ جَهَنَّمَ خَٰلِدِينَ فِيهَاۚ هِيَ حَسۡبُهُمۡۚ وَلَعَنَهُمُ ٱللَّهُۖ وَلَهُمۡ عَذَابٞ مُّقِيمٞ
Allah walonjeza achiphamaso aamuna ndi achiphamaso aakazi ndi akafiri moto wa Jahannam, akakhala m’menemo nthawi yaitali. Umenewo ukukwanira kwa iwo (kuwalanga). Ndipo Allah wawatembelera, ndipo iwo adzapeza chilango cha nthawi zonse.
அரபு விரிவுரைகள்:
 
மொழிபெயர்ப்பு அத்தியாயம்: அத்தவ்பா
அத்தியாயங்களின் அட்டவணை பக்க எண்
 
அல்குர்ஆன் மொழிபெயர்ப்பு - ஷேவா(Chewa) மொழிபெயர்ப்பு - காலித் இப்ராஹிம் பேடாலா - மொழிபெயர்ப்பு அட்டவணை

மொழிபெயர்த்தது காலித் இப்ராஹீம் பைதாலா.

மூடுக