Check out the new design

அல்குர்ஆன் மொழிபெயர்ப்பு - ஷேவா(Chewa) மொழிபெயர்ப்பு - காலித் இப்ராஹிம் பேடாலா * - மொழிபெயர்ப்பு அட்டவணை


மொழிபெயர்ப்பு அத்தியாயம்: அத்தவ்பா   வசனம்:
لَقَدِ ٱبۡتَغَوُاْ ٱلۡفِتۡنَةَ مِن قَبۡلُ وَقَلَّبُواْ لَكَ ٱلۡأُمُورَ حَتَّىٰ جَآءَ ٱلۡحَقُّ وَظَهَرَ أَمۡرُ ٱللَّهِ وَهُمۡ كَٰرِهُونَ
Ndithudi, akhala akukufunirani chisokonezo kuyambira kale, akusanthulirasanthulira zinthu (n’cholinga choti athane nawe) kufikira choonadi chadza ndi kuonekera poyera lamulo la Allah (lowakhaulitsa Ayuda) iwo asakufuna.
அரபு விரிவுரைகள்:
وَمِنۡهُم مَّن يَقُولُ ٱئۡذَن لِّي وَلَا تَفۡتِنِّيٓۚ أَلَا فِي ٱلۡفِتۡنَةِ سَقَطُواْۗ وَإِنَّ جَهَنَّمَ لَمُحِيطَةُۢ بِٱلۡكَٰفِرِينَ
Ndipo mwa iwo pali yemwe akuti: “Ndiloreni ine (kuti nditsale ku nkhondo) ndipo musandiponye m’mayeso (kuopa kuti ndingalakwe ndikaona akazi akumeneko).” Dziwani kuti iwo agwera kale m’mayesero. Ndipo, ndithu Jahannam ikawazinga mbali zonse osakhulupirira.
அரபு விரிவுரைகள்:
إِن تُصِبۡكَ حَسَنَةٞ تَسُؤۡهُمۡۖ وَإِن تُصِبۡكَ مُصِيبَةٞ يَقُولُواْ قَدۡ أَخَذۡنَآ أَمۡرَنَا مِن قَبۡلُ وَيَتَوَلَّواْ وَّهُمۡ فَرِحُونَ
Chikakupeza chabwino, (iwe Mtumiki Muhammad (s.a.w) ndi okutsatira) zimawanyansa, ndipo vuto likakupeza amanena: “Tidalingalira zinthu zathu kale. (Nchifukwa chake mavuto atizemba).” Ndipo amatembenuka nkupita uku akukondwa.[210]
[210] Achinyengo sadali kufunira zabwino Asilamu ngakhale kuti adali kudzipachika m’gulu la Asilamu mwachinyengo. Ankati vuto likawagwera Asilamu amasangalala. Koma chikawadzera chabwino amadandaula.
அரபு விரிவுரைகள்:
قُل لَّن يُصِيبَنَآ إِلَّا مَا كَتَبَ ٱللَّهُ لَنَا هُوَ مَوۡلَىٰنَاۚ وَعَلَى ٱللَّهِ فَلۡيَتَوَكَّلِ ٱلۡمُؤۡمِنُونَ
Nena: “Palibe chomwe chitipeze koma chimene Allah watilembera. Iye ndi Mbuye wathu.” Choncho, Asilamu ayadzamire kwa Allah Yekha.
அரபு விரிவுரைகள்:
قُلۡ هَلۡ تَرَبَّصُونَ بِنَآ إِلَّآ إِحۡدَى ٱلۡحُسۡنَيَيۡنِۖ وَنَحۡنُ نَتَرَبَّصُ بِكُمۡ أَن يُصِيبَكُمُ ٱللَّهُ بِعَذَابٖ مِّنۡ عِندِهِۦٓ أَوۡ بِأَيۡدِينَاۖ فَتَرَبَّصُوٓاْ إِنَّا مَعَكُم مُّتَرَبِّصُونَ
Nena: “Kodi chilipo chimene mukuyembekezera mwa ife posakhala chimodzi mwa zinthu ziwiri zabwino, (kupambana pa nkhondo ndi kupeza zotolatola zake, kapena kufa ndikukalowa ku Munda wamtendere)? Ndipo nafe tikukuyembekezerani kuti Allah akupatsani chilango chochokera kwa Iye, kapena kupyolera m’manja mwathu. Choncho bayembekezerani; nafenso tikuyembekezera nanu limodzi.”
அரபு விரிவுரைகள்:
قُلۡ أَنفِقُواْ طَوۡعًا أَوۡ كَرۡهٗا لَّن يُتَقَبَّلَ مِنكُمۡ إِنَّكُمۡ كُنتُمۡ قَوۡمٗا فَٰسِقِينَ
Nena (kwa achiphamaso): “Perekani (chuma chanu) mwa chifuniro kapena mosafuna sichizalandiridwa kwa inu. Ndithu inu ndinu anthu otuluka m’chilamulo cha Allah.”
அரபு விரிவுரைகள்:
وَمَا مَنَعَهُمۡ أَن تُقۡبَلَ مِنۡهُمۡ نَفَقَٰتُهُمۡ إِلَّآ أَنَّهُمۡ كَفَرُواْ بِٱللَّهِ وَبِرَسُولِهِۦ وَلَا يَأۡتُونَ ٱلصَّلَوٰةَ إِلَّا وَهُمۡ كُسَالَىٰ وَلَا يُنفِقُونَ إِلَّا وَهُمۡ كَٰرِهُونَ
Palibe chomwe chidaletsa kulandiridwa kwa zopereka zawo koma chifukwa chakuti iwo sadakhulupirire Allah ndi Mtumiki Wake; ndiponso sapita kopemphera koma mwaulesi; ndipo sapereka chopereka koma monyinyirika.
அரபு விரிவுரைகள்:
 
மொழிபெயர்ப்பு அத்தியாயம்: அத்தவ்பா
அத்தியாயங்களின் அட்டவணை பக்க எண்
 
அல்குர்ஆன் மொழிபெயர்ப்பு - ஷேவா(Chewa) மொழிபெயர்ப்பு - காலித் இப்ராஹிம் பேடாலா - மொழிபெயர்ப்பு அட்டவணை

மொழிபெயர்த்தது காலித் இப்ராஹீம் பைதாலா.

மூடுக