Check out the new design

Salin ng mga Kahulugan ng Marangal na Qur'an - Salin sa Wikang Chichewa ni Khalid Ibrahim Bityala * - Indise ng mga Salin


Salin ng mga Kahulugan Surah: At-Tawbah   Ayah:
يُرِيدُونَ أَن يُطۡفِـُٔواْ نُورَ ٱللَّهِ بِأَفۡوَٰهِهِمۡ وَيَأۡبَى ٱللَّهُ إِلَّآ أَن يُتِمَّ نُورَهُۥ وَلَوۡ كَرِهَ ٱلۡكَٰفِرُونَ
Akufuna kuzimitsa kuunika kwa Allah (Chisilamu) ndi pakamwa pawo; ndipo Allah sadzalola koma kukwaniritsa kuunika kwake ngakhale kuti osakhulupirira zikuwanyansa.
Ang mga Tafsir na Arabe:
هُوَ ٱلَّذِيٓ أَرۡسَلَ رَسُولَهُۥ بِٱلۡهُدَىٰ وَدِينِ ٱلۡحَقِّ لِيُظۡهِرَهُۥ عَلَى ٱلدِّينِ كُلِّهِۦ وَلَوۡ كَرِهَ ٱلۡمُشۡرِكُونَ
Iye ndi Yemwe adatuma Mtumiki Wake ndi ulangizi ndiponso chipembedzo choona kuti achiwonetsere pa zipembedzo zonse, ngakhale atanyansidwa nazo Amushirikina.
Ang mga Tafsir na Arabe:
۞ يَٰٓأَيُّهَا ٱلَّذِينَ ءَامَنُوٓاْ إِنَّ كَثِيرٗا مِّنَ ٱلۡأَحۡبَارِ وَٱلرُّهۡبَانِ لَيَأۡكُلُونَ أَمۡوَٰلَ ٱلنَّاسِ بِٱلۡبَٰطِلِ وَيَصُدُّونَ عَن سَبِيلِ ٱللَّهِۗ وَٱلَّذِينَ يَكۡنِزُونَ ٱلذَّهَبَ وَٱلۡفِضَّةَ وَلَا يُنفِقُونَهَا فِي سَبِيلِ ٱللَّهِ فَبَشِّرۡهُم بِعَذَابٍ أَلِيمٖ
E inu amene mwakhulupirira! Ndithu ambiri ophunzira a za chipembedzo cha Chiyuda ndi cha Chikhristu, akudya chuma cha anthu mwachinyengo ndi kusekeleza anthu ku njira ya Allah. Ndipo amene akusonkhanitsa golide ndi siliva popanda kuzipereka pa njira ya Allah, auze nkhani ya chilango chowawa.
Ang mga Tafsir na Arabe:
يَوۡمَ يُحۡمَىٰ عَلَيۡهَا فِي نَارِ جَهَنَّمَ فَتُكۡوَىٰ بِهَا جِبَاهُهُمۡ وَجُنُوبُهُمۡ وَظُهُورُهُمۡۖ هَٰذَا مَا كَنَزۡتُمۡ لِأَنفُسِكُمۡ فَذُوقُواْ مَا كُنتُمۡ تَكۡنِزُونَ
Pa tsiku lomwe (chuma chawo) chidzatenthedwa ku moto wa Jahannam, ndipo ndi chumacho zidzatenthedwa nkhope zawo, nthiti zawo ndi misana yawo (ali kuwuzidwa kuti): “Izi ndi zija zomwe mudadzisungira nokha. Choncho lawani (chilango) cha zomwe mudali kuzisunga.[207]
[207] Mu Ayah iyi, Allah akuchenjeza amene akusonkhanitsa chumacho nkumangochiunjika m’nkhokwe popanda kutulutsamo chopereka (Zakaat). Akawalanga nacho pa tsiku la chimaliziro ndi chilango cha moto. Tero, tulutsamoni Zakaat m’chuma chanu. Musanyozere lamulo la Allah.
Ang mga Tafsir na Arabe:
إِنَّ عِدَّةَ ٱلشُّهُورِ عِندَ ٱللَّهِ ٱثۡنَا عَشَرَ شَهۡرٗا فِي كِتَٰبِ ٱللَّهِ يَوۡمَ خَلَقَ ٱلسَّمَٰوَٰتِ وَٱلۡأَرۡضَ مِنۡهَآ أَرۡبَعَةٌ حُرُمٞۚ ذَٰلِكَ ٱلدِّينُ ٱلۡقَيِّمُۚ فَلَا تَظۡلِمُواْ فِيهِنَّ أَنفُسَكُمۡۚ وَقَٰتِلُواْ ٱلۡمُشۡرِكِينَ كَآفَّةٗ كَمَا يُقَٰتِلُونَكُمۡ كَآفَّةٗۚ وَٱعۡلَمُوٓاْ أَنَّ ٱللَّهَ مَعَ ٱلۡمُتَّقِينَ
Ndithu chiwerengero cha miyezi kwa Allah (pa chaka), ndi miyezi khumi ndi iwiri m’chilamulo cha Allah kuyambira tsiku lomwe adalenga thambo ndi nthaka. M’menemo muli miyezi inayi yopatulika. Ichi ndicho chipembedzo cha Allah cholunjika, choncho musadzichitire nokha zoipa m’menemo. Ndipo menyanani ndi Amshrikina nonse pamodzi monga momwe akumenyana nanu onse pamodzi. Ndipo dziwani kuti Allah ali pamodzi ndi oopa.[208]
[208] Chiwerengero chamiyezi m’chaka, ndi khumi ndi iwiri monga mwalamulo la Allah. M’miyeziyi muli miyezi inayi yopatulika yomwe ndi Rajabu, Thul Qa’da, Thul Hijja ndi Muharamu. M’miyeziyi nkosaloledwa kuchita nkhondo pokhapokha mutaputidwa ndi adani.
Ang mga Tafsir na Arabe:
 
Salin ng mga Kahulugan Surah: At-Tawbah
Indise ng mga Surah Numero ng Pahina
 
Salin ng mga Kahulugan ng Marangal na Qur'an - Salin sa Wikang Chichewa ni Khalid Ibrahim Bityala - Indise ng mga Salin

Isinalin ni Khalid Ibrahim Bitala.

Isara