Akufuna kuzimitsa kuunika kwa Allah (Chisilamu) ndi pakamwa pawo; ndipo Allah sadzalola koma kukwaniritsa kuunika kwake ngakhale kuti osakhulupirira zikuwanyansa.
Iye ndi Yemwe adatuma Mtumiki Wake ndi ulangizi ndiponso chipembedzo choona kuti achiwonetsere pa zipembedzo zonse, ngakhale atanyansidwa nazo Amushirikina.
E inu amene mwakhulupirira! Ndithu ambiri ophunzira a za chipembedzo cha Chiyuda ndi cha Chikhristu, akudya chuma cha anthu mwachinyengo ndi kusekeleza anthu ku njira ya Allah. Ndipo amene akusonkhanitsa golide ndi siliva popanda kuzipereka pa njira ya Allah, auze nkhani ya chilango chowawa.
Pa tsiku lomwe (chuma chawo) chidzatenthedwa ku moto wa Jahannam, ndipo ndi chumacho zidzatenthedwa nkhope zawo, nthiti zawo ndi misana yawo (ali kuwuzidwa kuti): “Izi ndi zija zomwe mudadzisungira nokha. Choncho lawani (chilango) cha zomwe mudali kuzisunga.[207]
[207] Mu Ayah iyi, Allah akuchenjeza amene akusonkhanitsa chumacho nkumangochiunjika m’nkhokwe popanda kutulutsamo chopereka (Zakaat). Akawalanga nacho pa tsiku la chimaliziro ndi chilango cha moto. Tero, tulutsamoni Zakaat m’chuma chanu. Musanyozere lamulo la Allah.
Ndithu chiwerengero cha miyezi kwa Allah (pa chaka), ndi miyezi khumi ndi iwiri m’chilamulo cha Allah kuyambira tsiku lomwe adalenga thambo ndi nthaka. M’menemo muli miyezi inayi yopatulika. Ichi ndicho chipembedzo cha Allah cholunjika, choncho musadzichitire nokha zoipa m’menemo. Ndipo menyanani ndi Amshrikina nonse pamodzi monga momwe akumenyana nanu onse pamodzi. Ndipo dziwani kuti Allah ali pamodzi ndi oopa.[208]
[208] Chiwerengero chamiyezi m’chaka, ndi khumi ndi iwiri monga mwalamulo la Allah. M’miyeziyi muli miyezi inayi yopatulika yomwe ndi Rajabu, Thul Qa’da, Thul Hijja ndi Muharamu. M’miyeziyi nkosaloledwa kuchita nkhondo pokhapokha mutaputidwa ndi adani.
Contents of the translations can be downloaded and re-published, with the following terms and conditions:
1. No modification, addition, or deletion of the content.
2. Clearly referring to the publisher and the source (QuranEnc.com).
3. Mentioning the version number when re-publishing the translation.
4. Keeping the transcript information inside the document.
5. Notifying the source (QuranEnc.com) of any note on the translation.
6. Updating the translation according to the latest version issued from the source (QuranEnc.com).
7. Inappropriate advertisements must not be included when displaying translations of the meanings of the Noble Quran.
Mga Resulta ng Paghahanap:
API specs
Endpoints:
Sura translation
GET / https://quranenc.com/api/v1/translation/sura/{translation_key}/{sura_number} description: get the specified translation (by its translation_key) for the speicified sura (by its number)
Parameters: translation_key: (the key of the currently selected translation) sura_number: [1-114] (Sura number in the mosshaf which should be between 1 and 114)
Returns:
json object containing array of objects, each object contains the "sura", "aya", "translation" and "footnotes".
GET / https://quranenc.com/api/v1/translation/aya/{translation_key}/{sura_number}/{aya_number} description: get the specified translation (by its translation_key) for the speicified aya (by its number sura_number and aya_number)
Parameters: translation_key: (the key of the currently selected translation) sura_number: [1-114] (Sura number in the mosshaf which should be between 1 and 114) aya_number: [1-...] (Aya number in the sura)
Returns:
json object containing the "sura", "aya", "translation" and "footnotes".