Check out the new design

Salin ng mga Kahulugan ng Marangal na Qur'an - Salin sa Wikang Chichewa ni Khalid Ibrahim Bityala * - Indise ng mga Salin


Salin ng mga Kahulugan Surah: At-Tawbah   Ayah:
ٱنفِرُواْ خِفَافٗا وَثِقَالٗا وَجَٰهِدُواْ بِأَمۡوَٰلِكُمۡ وَأَنفُسِكُمۡ فِي سَبِيلِ ٱللَّهِۚ ذَٰلِكُمۡ خَيۡرٞ لَّكُمۡ إِن كُنتُمۡ تَعۡلَمُونَ
Pitani (mukamenyane) muli opepukidwa ndi olemedwa; ndipo menyerani njira ya Allah nchuma chanu ndi inu nomwe. Zimenezi nzabwino kwa inu ngati muli anthu odziwa.
Ang mga Tafsir na Arabe:
لَوۡ كَانَ عَرَضٗا قَرِيبٗا وَسَفَرٗا قَاصِدٗا لَّٱتَّبَعُوكَ وَلَٰكِنۢ بَعُدَتۡ عَلَيۡهِمُ ٱلشُّقَّةُۚ وَسَيَحۡلِفُونَ بِٱللَّهِ لَوِ ٱسۡتَطَعۡنَا لَخَرَجۡنَا مَعَكُمۡ يُهۡلِكُونَ أَنفُسَهُمۡ وَٱللَّهُ يَعۡلَمُ إِنَّهُمۡ لَكَٰذِبُونَ
Ukadakhala ulendo wokafuna za m’dziko zopepuka kuzipeza, ndi ulendo wofupika, ndithu akadakutsata (achiphamaso). Koma ulendo wamavutowu wakhala wautali kwa iwo. Ndipo iwo alumbilira Allah (ponena kuti): “Kukadakhala kotheka kwa ife, tikadapita nanu.” (Pa mawu awa), akudziononga okha. Ndipo Allah akudziwa kuti iwo Ngabodza.
Ang mga Tafsir na Arabe:
عَفَا ٱللَّهُ عَنكَ لِمَ أَذِنتَ لَهُمۡ حَتَّىٰ يَتَبَيَّنَ لَكَ ٱلَّذِينَ صَدَقُواْ وَتَعۡلَمَ ٱلۡكَٰذِبِينَ
Allah wakukhululukira. Bwanji wawaloleza kutsalira? (Ukadayembekeza) kufikira adziwike kwa iwe amene akunena zoona, ndikuti uwadziwe abodza.
Ang mga Tafsir na Arabe:
لَا يَسۡتَـٔۡذِنُكَ ٱلَّذِينَ يُؤۡمِنُونَ بِٱللَّهِ وَٱلۡيَوۡمِ ٱلۡأٓخِرِ أَن يُجَٰهِدُواْ بِأَمۡوَٰلِهِمۡ وَأَنفُسِهِمۡۗ وَٱللَّهُ عَلِيمُۢ بِٱلۡمُتَّقِينَ
Sangakupemphe chilolezo (chotsala ku nkhondo) amene akhulupirira Allah ndi tsiku lachimaliziro kuti asapite kukamenyera (chipembedzo cha Allah) ndi chuma chawo ndi Matupi awo. Ndipo Allah akuwadziwa amene akumuopa.
Ang mga Tafsir na Arabe:
إِنَّمَا يَسۡتَـٔۡذِنُكَ ٱلَّذِينَ لَا يُؤۡمِنُونَ بِٱللَّهِ وَٱلۡيَوۡمِ ٱلۡأٓخِرِ وَٱرۡتَابَتۡ قُلُوبُهُمۡ فَهُمۡ فِي رَيۡبِهِمۡ يَتَرَدَّدُونَ
Ndithu amakupempha chilolezo aja amene sakhulupirira Allah ndi tsiku la chimaliziro, ndipo mitima yawo yakaikira, ndipo iwo, chifukwa cha kukaika kwawo akungotekeseka.
Ang mga Tafsir na Arabe:
۞ وَلَوۡ أَرَادُواْ ٱلۡخُرُوجَ لَأَعَدُّواْ لَهُۥ عُدَّةٗ وَلَٰكِن كَرِهَ ٱللَّهُ ٱنۢبِعَاثَهُمۡ فَثَبَّطَهُمۡ وَقِيلَ ٱقۡعُدُواْ مَعَ ٱلۡقَٰعِدِينَ
Akadafunadi kuti atuluke (kupita ku nkhondo) akadakonzekera zokonzekera za ku nkhondo; koma Allah sadafune kuti iwo apiteko; choncho adawatsekereza, ndipo kudanenedwa: “Khalani pamodzi ndi Otsalira.”
Ang mga Tafsir na Arabe:
لَوۡ خَرَجُواْ فِيكُم مَّا زَادُوكُمۡ إِلَّا خَبَالٗا وَلَأَوۡضَعُواْ خِلَٰلَكُمۡ يَبۡغُونَكُمُ ٱلۡفِتۡنَةَ وَفِيكُمۡ سَمَّٰعُونَ لَهُمۡۗ وَٱللَّهُ عَلِيمُۢ بِٱلظَّٰلِمِينَ
Ngati akadatuluka nanu pamodzi, sakadakuonjezerani chilichonse koma chisokonezo ndi kuyenda mwa ukazitape pakati panu ndicholinga chokufunirani chisokonezo, ndipo mwa inu alipo akuwamvelera, ndipo Allah Ngodziwa za oipa.
Ang mga Tafsir na Arabe:
 
Salin ng mga Kahulugan Surah: At-Tawbah
Indise ng mga Surah Numero ng Pahina
 
Salin ng mga Kahulugan ng Marangal na Qur'an - Salin sa Wikang Chichewa ni Khalid Ibrahim Bityala - Indise ng mga Salin

Isinalin ni Khalid Ibrahim Bitala.

Isara