Check out the new design

《古兰经》译解 - 契瓦语翻译 - 哈利德·伊布拉欣·比德拉。 * - 译解目录


含义的翻译 章: 开海菲   段:
وَدَخَلَ جَنَّتَهُۥ وَهُوَ ظَالِمٞ لِّنَفۡسِهِۦ قَالَ مَآ أَظُنُّ أَن تَبِيدَ هَٰذِهِۦٓ أَبَدٗا
Ndipo adalowa m’munda mwake uku akudzichitira yekha zoipa. Adati: “Sindiganiza ngakhale mpang’ono pomwe kuti (munda) uwu udzaonongeka.”
阿拉伯语经注:
وَمَآ أَظُنُّ ٱلسَّاعَةَ قَآئِمَةٗ وَلَئِن رُّدِدتُّ إِلَىٰ رَبِّي لَأَجِدَنَّ خَيۡرٗا مِّنۡهَا مُنقَلَبٗا
“Ndiponso sindiganiza kuti Qiyâma (chimaliziro) idzachitikadi. Ngati (itapezekadi Kiyamayo), ine nkubwezedwa kwa Mbuye wanga, ndithu ndikapeza malo abwino wobwererako kuposa awa. (Monga momwe ndapezera mwayi kuno, ukonso ndikapeza, ngati Kiyamayo ilikodi).”
阿拉伯语经注:
قَالَ لَهُۥ صَاحِبُهُۥ وَهُوَ يُحَاوِرُهُۥٓ أَكَفَرۡتَ بِٱلَّذِي خَلَقَكَ مِن تُرَابٖ ثُمَّ مِن نُّطۡفَةٖ ثُمَّ سَوَّىٰكَ رَجُلٗا
Mnzake adanena kwa iye mokambirana naye: “Kodi ukumukana yemwe adakulenga ndi dongo, kenako ndi dontho lamadzi a umuna ndiponso adakupanga kukhala munthu wolingana?”
阿拉伯语经注:
لَّٰكِنَّا۠ هُوَ ٱللَّهُ رَبِّي وَلَآ أُشۡرِكُ بِرَبِّيٓ أَحَدٗا
“Koma ine ndikukhulupirira kuti Iye ndi Mulungu Mbuye wanga, ndipo sindiphatikiza aliyense ndi Mbuye wanga.”
阿拉伯语经注:
وَلَوۡلَآ إِذۡ دَخَلۡتَ جَنَّتَكَ قُلۡتَ مَا شَآءَ ٱللَّهُ لَا قُوَّةَ إِلَّا بِٱللَّهِۚ إِن تَرَنِ أَنَا۠ أَقَلَّ مِنكَ مَالٗا وَوَلَدٗا
“Ndipo pamene umalowa m’munda wako ukadanena kuti izi ndi zimene wandifunira Allah, mphamvu sizikadapezeka koma kupyolera mwa Allah (zikadakhala zabwino kwa iwe). Ngati ukundiona ine kuti ndili ndi chuma chochepa ndi ana ochepa kuposa iwe (koma sindisiya kutamanda Allah).”
阿拉伯语经注:
فَعَسَىٰ رَبِّيٓ أَن يُؤۡتِيَنِ خَيۡرٗا مِّن جَنَّتِكَ وَيُرۡسِلَ عَلَيۡهَا حُسۡبَانٗا مِّنَ ٱلسَّمَآءِ فَتُصۡبِحَ صَعِيدٗا زَلَقًا
“Mwina Mbuye wanga angandipatse zabwino kuposa munda wakowo ndi kuutumizira mliri wachiphaliwali kuchokera kumwamba, ndipo ndikusanduka nthaka yotelera (yoguga).”
阿拉伯语经注:
أَوۡ يُصۡبِحَ مَآؤُهَا غَوۡرٗا فَلَن تَسۡتَطِيعَ لَهُۥ طَلَبٗا
“Kapena madzi ake nkumangophwa kotero kuti sungathe kuwapeza.”
阿拉伯语经注:
وَأُحِيطَ بِثَمَرِهِۦ فَأَصۡبَحَ يُقَلِّبُ كَفَّيۡهِ عَلَىٰ مَآ أَنفَقَ فِيهَا وَهِيَ خَاوِيَةٌ عَلَىٰ عُرُوشِهَا وَيَقُولُ يَٰلَيۡتَنِي لَمۡ أُشۡرِكۡ بِرَبِّيٓ أَحَدٗا
Tsono mliri unagwa pa zipatso zakezo (ndikuziononga motheratu), ndipo adayamba kutembenuza manja modandaulira zomwe adaonongera m’menemo; (mindayo) mitengo yake itagwera pansi. Ndipo adati: “Kalanga ine! Ndikadapanda kumphatikiza Mbuye wanga ndi aliyense (zoterezi sizikadachitika.)”
阿拉伯语经注:
وَلَمۡ تَكُن لَّهُۥ فِئَةٞ يَنصُرُونَهُۥ مِن دُونِ ٱللَّهِ وَمَا كَانَ مُنتَصِرًا
Ndipo sadakhale ndi anthu omthangata pamene Allah adamtaya, ngakhale iye mwini sadadzithandize.
阿拉伯语经注:
هُنَالِكَ ٱلۡوَلَٰيَةُ لِلَّهِ ٱلۡحَقِّۚ هُوَ خَيۡرٞ ثَوَابٗا وَخَيۡرٌ عُقۡبٗا
Pamalo potere chitetezo chimakhala cha Allah Yekha Woona. Iye Ngolipira bwino, ndiponso Wabwino (pakudza) ndi malekezero abwino.
阿拉伯语经注:
وَٱضۡرِبۡ لَهُم مَّثَلَ ٱلۡحَيَوٰةِ ٱلدُّنۡيَا كَمَآءٍ أَنزَلۡنَٰهُ مِنَ ٱلسَّمَآءِ فَٱخۡتَلَطَ بِهِۦ نَبَاتُ ٱلۡأَرۡضِ فَأَصۡبَحَ هَشِيمٗا تَذۡرُوهُ ٱلرِّيَٰحُۗ وَكَانَ ٱللَّهُ عَلَىٰ كُلِّ شَيۡءٖ مُّقۡتَدِرًا
Ndipo apatse fanizo la moyo wadziko lapansi, uli ngati madzi amene tikutsitsa kuchokera kumitambo kenako (madziwo) amasakanikirana ndi mmera wa m’nthaka (ndikuyamba kumera mokongola), kenako (mmerawo) nkukhala masamba ouma odukaduka omwe mphepo ikuwaulutsa uku ndi uku. Ndipo Allah ali ndi mphamvu pachilichonse.
阿拉伯语经注:
 
含义的翻译 章: 开海菲
章节目录 页码
 
《古兰经》译解 - 契瓦语翻译 - 哈利德·伊布拉欣·比德拉。 - 译解目录

由哈利德·伊布拉欣·白塔拉翻译。

关闭