Check out the new design

《古兰经》译解 - 契瓦语翻译 - 哈利德·伊布拉欣·比德拉。 * - 译解目录


含义的翻译 章: 开海菲   段:
ٱلۡمَالُ وَٱلۡبَنُونَ زِينَةُ ٱلۡحَيَوٰةِ ٱلدُّنۡيَاۖ وَٱلۡبَٰقِيَٰتُ ٱلصَّٰلِحَٰتُ خَيۡرٌ عِندَ رَبِّكَ ثَوَابٗا وَخَيۡرٌ أَمَلٗا
Chuma ndi ana ndizokometsera za moyo wa dziko lapansi, koma ntchito zabwino zopitirira ndizo zabwino kwa Mbuye wako, monga mphoto ndi chiyembekezo chabwino.
阿拉伯语经注:
وَيَوۡمَ نُسَيِّرُ ٱلۡجِبَالَ وَتَرَى ٱلۡأَرۡضَ بَارِزَةٗ وَحَشَرۡنَٰهُمۡ فَلَمۡ نُغَادِرۡ مِنۡهُمۡ أَحَدٗا
Ndipo (akumbutse) tsiku lomwe tidzayendetsa mapiri (powaulutsa ngati ubweya mu mlengalenga), ndipo udzaiona nthaka ili tetetee, (itatambasuka yosakhwinyata ndi mapiri kapena zitunda), ndipo tidzawasonkhanitsa (tsiku limenelo), ndipo sitidzasiya aliyense mwa iwo (oyamba ndi omaliza).
阿拉伯语经注:
وَعُرِضُواْ عَلَىٰ رَبِّكَ صَفّٗا لَّقَدۡ جِئۡتُمُونَا كَمَا خَلَقۡنَٰكُمۡ أَوَّلَ مَرَّةِۭۚ بَلۡ زَعَمۡتُمۡ أَلَّن نَّجۡعَلَ لَكُم مَّوۡعِدٗا
Ndipo adzabwera nawo kwa Mbuye wako atandanda m’mizere (ndikuuzidwa): “Ndithu mwatidzera monga tidakulengerani pachiyambi (opanda nsapato, amaliseche ndiponso opanda chilichonse chuma ndi ana). Koma mumaganiza kuti sitikuikirani lonjezo (ili louka ku imfa ndi kuweruzidwa).”
阿拉伯语经注:
وَوُضِعَ ٱلۡكِتَٰبُ فَتَرَى ٱلۡمُجۡرِمِينَ مُشۡفِقِينَ مِمَّا فِيهِ وَيَقُولُونَ يَٰوَيۡلَتَنَا مَالِ هَٰذَا ٱلۡكِتَٰبِ لَا يُغَادِرُ صَغِيرَةٗ وَلَا كَبِيرَةً إِلَّآ أَحۡصَىٰهَاۚ وَوَجَدُواْ مَا عَمِلُواْ حَاضِرٗاۗ وَلَا يَظۡلِمُ رَبُّكَ أَحَدٗا
Ndipo kaundula adzaikidwa (pamaso pawo), ndipo udzaaona oipa ali oopa chifukwa cha zomwe zili m’menemo, ndipo adzanena: “Kalanga ife taonongeka! Ngotani kaundula uyu, sasiya chaching’ono ngakhale chachikulu, koma zonse kuzilemba.” Ndipo adzapeza zonse zimene adazichita zitalembedwa m’menemo. Ndipo Mbuye wako sapondereza aliyense (pomusenzetsa zomwe sizake, kapena kumchitira zomwe sizikumuyenera).
阿拉伯语经注:
وَإِذۡ قُلۡنَا لِلۡمَلَٰٓئِكَةِ ٱسۡجُدُواْ لِأٓدَمَ فَسَجَدُوٓاْ إِلَّآ إِبۡلِيسَ كَانَ مِنَ ٱلۡجِنِّ فَفَسَقَ عَنۡ أَمۡرِ رَبِّهِۦٓۗ أَفَتَتَّخِذُونَهُۥ وَذُرِّيَّتَهُۥٓ أَوۡلِيَآءَ مِن دُونِي وَهُمۡ لَكُمۡ عَدُوُّۢۚ بِئۡسَ لِلظَّٰلِمِينَ بَدَلٗا
Ndipo (kumbuka) pamene tidawauza angelo: “Mchitireni sijida Adam (mugwadireni momulemekeza).” Onse adachitadi sijida kupatula Iblis. Iye adali mmodzi wa ziwanda, ndipo adatuluka m’chilamulo cha Mbuye wake. Kodi iye ndi mbumba yake mukuwalola kukhala abwenzi (anu) kusiya Ine, pomwe iwo ndiadani anu? Taonani kuipa kusintha kwa anthu oipa!
阿拉伯语经注:
۞ مَّآ أَشۡهَدتُّهُمۡ خَلۡقَ ٱلسَّمَٰوَٰتِ وَٱلۡأَرۡضِ وَلَا خَلۡقَ أَنفُسِهِمۡ وَمَا كُنتُ مُتَّخِذَ ٱلۡمُضِلِّينَ عَضُدٗا
Sindidawachite (iwo) kukhala mboni nkulenga kwa thambo ndi nthaka, ngakhale kuwalenga kwawo ndipo sindidawalole osokeretsa kukhala athandizi (Anga).
阿拉伯语经注:
وَيَوۡمَ يَقُولُ نَادُواْ شُرَكَآءِيَ ٱلَّذِينَ زَعَمۡتُمۡ فَدَعَوۡهُمۡ فَلَمۡ يَسۡتَجِيبُواْ لَهُمۡ وَجَعَلۡنَا بَيۡنَهُم مَّوۡبِقٗا
Ndipo (kumbukani) tsiku lomwe (Allah) adzanena: “Aitaneni aja omwe munkandiphatikiza nawo omwe munkati (ndi milungu inzanga).” Choncho, adzaiitana koma siidzawayankha; ndipo tidzaika chionongeko pakati pawo (ndipo sadzakumananso).
阿拉伯语经注:
وَرَءَا ٱلۡمُجۡرِمُونَ ٱلنَّارَ فَظَنُّوٓاْ أَنَّهُم مُّوَاقِعُوهَا وَلَمۡ يَجِدُواْ عَنۡهَا مَصۡرِفٗا
Ndipo woipa adzauona moto (panthawi imeneyo) ndikutsimikiza kuti iwo alowa m’menemo. Ndipo sadzapeza pouzembera.
阿拉伯语经注:
 
含义的翻译 章: 开海菲
章节目录 页码
 
《古兰经》译解 - 契瓦语翻译 - 哈利德·伊布拉欣·比德拉。 - 译解目录

由哈利德·伊布拉欣·白塔拉翻译。

关闭