Check out the new design

《古兰经》译解 - 契瓦语翻译 - 哈利德·伊布拉欣·比德拉。 * - 译解目录


含义的翻译 章: 赛拜艾   段:
قَالَ ٱلَّذِينَ ٱسۡتَكۡبَرُواْ لِلَّذِينَ ٱسۡتُضۡعِفُوٓاْ أَنَحۡنُ صَدَدۡنَٰكُمۡ عَنِ ٱلۡهُدَىٰ بَعۡدَ إِذۡ جَآءَكُمۖ بَلۡ كُنتُم مُّجۡرِمِينَ
Amene adadzikweza adzanena kwa amene adaponderezedwa: “Ha, kodi ife tidakutsekerezani ku chiongoko chitakudzerani? Iyayi, koma mudali oipa.”
阿拉伯语经注:
وَقَالَ ٱلَّذِينَ ٱسۡتُضۡعِفُواْ لِلَّذِينَ ٱسۡتَكۡبَرُواْ بَلۡ مَكۡرُ ٱلَّيۡلِ وَٱلنَّهَارِ إِذۡ تَأۡمُرُونَنَآ أَن نَّكۡفُرَ بِٱللَّهِ وَنَجۡعَلَ لَهُۥٓ أَندَادٗاۚ وَأَسَرُّواْ ٱلنَّدَامَةَ لَمَّا رَأَوُاْ ٱلۡعَذَابَۚ وَجَعَلۡنَا ٱلۡأَغۡلَٰلَ فِيٓ أَعۡنَاقِ ٱلَّذِينَ كَفَرُواْۖ هَلۡ يُجۡزَوۡنَ إِلَّا مَا كَانُواْ يَعۡمَلُونَ
Ndipo amene adaponderezedwa adzanena kwa amene adadzikweza: “Iyayi, koma (mumachita) ndale za usiku ndi usana (zotitsekereza nazo ku chikhulupiliro) pamene mumatilamula kuti tinkanire Allah ndikumpangira Iye milungu inzake.” Iwo adzabisa madandaulo pamene adzaona chilango. Ndipo tidzaika magoli m’makosi mwa amene sadakhulupirire; kodi angalipidwe china, osati zija ankachita?[337]
[337] M’ndime iyi, Allah akutifotokozera kuti pa tsiku la chimaliziro padzakhala kukangana pakati pa atsogeleri ndi anthu otsogoleredwa. Izi zidzachitika pamene otsogoleredwa adzatsimikiza kuti atsogoleri awo amawasokeza; ankangowalangiza zachabe. Potero adzakhala ndi madandaulo aakulu chifukwa chotsatira anthu osokera. Komatu madandaulo oterewa sadzawapindulira chilichonse popeza mwayi udzakhala utatha kale. Choncho nkofunika kuti potsata mtsogoleri aliyense tiyambe taganizira komwe akunka nafe; tisangokokedwa ngati nyama pakuti Allah adatipatsa dalitso lanzeru. Choncho tigwiritse ntchito bwino nzeru tsoka lisanatigwere.
阿拉伯语经注:
وَمَآ أَرۡسَلۡنَا فِي قَرۡيَةٖ مِّن نَّذِيرٍ إِلَّا قَالَ مُتۡرَفُوهَآ إِنَّا بِمَآ أُرۡسِلۡتُم بِهِۦ كَٰفِرُونَ
Palibe pamene tidatuma mchenjezi m’mudzi uliwonse koma opeza bwino a m’mudzimo ankanena: “Ndithu ife tikuzikana zimene mwatumidwa nazozi.”
阿拉伯语经注:
وَقَالُواْ نَحۡنُ أَكۡثَرُ أَمۡوَٰلٗا وَأَوۡلَٰدٗا وَمَا نَحۡنُ بِمُعَذَّبِينَ
Ndipo ankanena (monyada): “Ife tili ndi chuma chambiri ndi ana (amhiri); choncho ife sitidzalangidwa (pa tsiku la chimaliziro).”
阿拉伯语经注:
قُلۡ إِنَّ رَبِّي يَبۡسُطُ ٱلرِّزۡقَ لِمَن يَشَآءُ وَيَقۡدِرُ وَلَٰكِنَّ أَكۡثَرَ ٱلنَّاسِ لَا يَعۡلَمُونَ
Nena: “Ndithu Mbuye wanga amamchulukitsira rizq (zopatsa) laulere amene wamfuna (ngakhale ali woipa), ndipo amamchepetsera (amene wamfuna ngakhale kuti ndi munthu wabwino). Koma anthu ambiri sazindikira (zimenezi).”
阿拉伯语经注:
وَمَآ أَمۡوَٰلُكُمۡ وَلَآ أَوۡلَٰدُكُم بِٱلَّتِي تُقَرِّبُكُمۡ عِندَنَا زُلۡفَىٰٓ إِلَّا مَنۡ ءَامَنَ وَعَمِلَ صَٰلِحٗا فَأُوْلَٰٓئِكَ لَهُمۡ جَزَآءُ ٱلضِّعۡفِ بِمَا عَمِلُواْ وَهُمۡ فِي ٱلۡغُرُفَٰتِ ءَامِنُونَ
Ndipo sichuma chanu ndi ana anu zomwe zingakuyandikitseni kwa Ife ulemelero, koma (chikhulupiliro cha) amene wakhulupirira ndi kuchita zabwino. Iwo adzapeza malipiro owonjezeka kwambiri pa zomwe adachita. Iwo adzakhala mwamtendere m’zipinda za ku Minda ya mtendere.
阿拉伯语经注:
وَٱلَّذِينَ يَسۡعَوۡنَ فِيٓ ءَايَٰتِنَا مُعَٰجِزِينَ أُوْلَٰٓئِكَ فِي ٱلۡعَذَابِ مُحۡضَرُونَ
Ndipo amene akuchita khama kulimbana ndi zizindikiro Zathu ndi cholinga choti alepheretse (zofuna Zathu,) iwowo adzabweretsedwa ku chilango (cha Moto).
阿拉伯语经注:
قُلۡ إِنَّ رَبِّي يَبۡسُطُ ٱلرِّزۡقَ لِمَن يَشَآءُ مِنۡ عِبَادِهِۦ وَيَقۡدِرُ لَهُۥۚ وَمَآ أَنفَقۡتُم مِّن شَيۡءٖ فَهُوَ يُخۡلِفُهُۥۖ وَهُوَ خَيۡرُ ٱلرَّٰزِقِينَ
Nena (iwe Mneneri): “Ndithu Mbuye wanga amamchulukitsira rizq (zaulere) amene wamfuna mwa akapolo Ake; ndiponso amamchepetsera (amene wamfuna). Ndipo chilichonse chimene mupereka, Iye adzakupatsani china m’malo mwake; Iye Ngwabwino popatsa zaulere, kuposa opatsa.
阿拉伯语经注:
 
含义的翻译 章: 赛拜艾
章节目录 页码
 
《古兰经》译解 - 契瓦语翻译 - 哈利德·伊布拉欣·比德拉。 - 译解目录

由哈利德·伊布拉欣·白塔拉翻译。

关闭