《古兰经》译解 - 契瓦语翻译 * - 译解目录


含义的翻译 段: (14) 章: 赛拜艾
فَلَمَّا قَضَيۡنَا عَلَيۡهِ ٱلۡمَوۡتَ مَا دَلَّهُمۡ عَلَىٰ مَوۡتِهِۦٓ إِلَّا دَآبَّةُ ٱلۡأَرۡضِ تَأۡكُلُ مِنسَأَتَهُۥۖ فَلَمَّا خَرَّ تَبَيَّنَتِ ٱلۡجِنُّ أَن لَّوۡ كَانُواْ يَعۡلَمُونَ ٱلۡغَيۡبَ مَا لَبِثُواْ فِي ٱلۡعَذَابِ ٱلۡمُهِينِ
Pamene tidalamula imfa yake (Sulaiman), palibe chimene chidawasonyeza za imfa yake koma kachirombo ka m’nthaka (chiswe) kamene kadadya ndodo yake. Choncho pamene adagwa, ziwanda zidazindikira kuti zikadakhala zikudziwa zobisika sizidakakhala m’chilango chosambulacho.[334]
[334] Kalelo anthu adali ndi chikhulupiliro chakuti ziwanda zimadziwa zamseri; monga kudziwa zam’tsogolo. Ndipo kudapezeka kuti Sulaiman adaimilira kupemphera ku chipinda chake chopemphelera uku atatsamira ndodo yake, imfa niimpeza ali chiimilire, choncho adakhala chaka chathunthu ali chomwecho uku atafa kale. Mmenemo nkuti ziwanda zikugwira ntchito yotopetsa, osadziwa kuti Sulaiman adafa, mpaka pamene chiswe chidadya ndodo imene adatsamira, nagwa pansi. Apo mpomwe imfa yake idadziwika. Potero anthu adadziwa tsopano kuti ziwanda sizidziwa zam’tsogolo.
阿拉伯语经注:
 
含义的翻译 段: (14) 章: 赛拜艾
章节目录 页码
 
《古兰经》译解 - 契瓦语翻译 - 译解目录

古兰经契瓦文译解,哈利德·伊布拉欣·比德拉翻译,2020年版

关闭