Check out the new design

《古兰经》译解 - 契瓦语翻译 - 哈利德·伊布拉欣·比德拉。 * - 译解目录


含义的翻译 章: 穆扎底拉   段:
أَلَمۡ تَرَ أَنَّ ٱللَّهَ يَعۡلَمُ مَا فِي ٱلسَّمَٰوَٰتِ وَمَا فِي ٱلۡأَرۡضِۖ مَا يَكُونُ مِن نَّجۡوَىٰ ثَلَٰثَةٍ إِلَّا هُوَ رَابِعُهُمۡ وَلَا خَمۡسَةٍ إِلَّا هُوَ سَادِسُهُمۡ وَلَآ أَدۡنَىٰ مِن ذَٰلِكَ وَلَآ أَكۡثَرَ إِلَّا هُوَ مَعَهُمۡ أَيۡنَ مَا كَانُواْۖ ثُمَّ يُنَبِّئُهُم بِمَا عَمِلُواْ يَوۡمَ ٱلۡقِيَٰمَةِۚ إِنَّ ٱللَّهَ بِكُلِّ شَيۡءٍ عَلِيمٌ
Kodi sukudziwa (iwe, womvera wanzeru) kuti Allah akudziwa zakumwamba ndi zam’dziko lapansi? Sipakhala manong’onong’o a (anthu) atatu koma Iye Ngwachinayi wawo (ndi kudziwa kwake kosabisika chilichonse cha kumwamba ndi m’dziko), ngakhale a (anthu) asanu koma Iye Ngwachisanu ndi chimodzi wawo (mkudziwa Kwake), ngakhale ali ochepera kuposera pamenepa kapena ochulukira koma Iye ali nawo paliponse pomwe ati akhale (Allah ali nawo pamodzi mukudziwa Kwake kosabisika chilichonse), kenako adzawafotokozera pa tsiku la chiweruziro zimene adachita; ndithu Allah Ngodziwa chilichonse (mokwanira).[348]
[348] M’ndime iyi, Allah akutichenjeza kuti pamene tikuchita kalikonse tisamaganizire kuti Allah sakutiona. Palibe chimene chingabisike kwa Allah cha m’dziko lapansi kapena kumwamba; m’zoyankhula kapena m’zochitachita.
阿拉伯语经注:
أَلَمۡ تَرَ إِلَى ٱلَّذِينَ نُهُواْ عَنِ ٱلنَّجۡوَىٰ ثُمَّ يَعُودُونَ لِمَا نُهُواْ عَنۡهُ وَيَتَنَٰجَوۡنَ بِٱلۡإِثۡمِ وَٱلۡعُدۡوَٰنِ وَمَعۡصِيَتِ ٱلرَّسُولِۖ وَإِذَا جَآءُوكَ حَيَّوۡكَ بِمَا لَمۡ يُحَيِّكَ بِهِ ٱللَّهُ وَيَقُولُونَ فِيٓ أَنفُسِهِمۡ لَوۡلَا يُعَذِّبُنَا ٱللَّهُ بِمَا نَقُولُۚ حَسۡبُهُمۡ جَهَنَّمُ يَصۡلَوۡنَهَاۖ فَبِئۡسَ ٱلۡمَصِيرُ
Kodi siudaone! Kwa amene aletsedwa kunong’onezana zoipa pakati pawo, kenako akubwereza zimene adaletsedwa? Akunong’onezana za machimo, mtopola ndi kunyoza Mtumiki. Akakudzera akukulonjera (ndi malonje achinyengo) amene Allah sadakulonjerepo nawo ndipo akunena m’mitima mwawo: “Kodi nchifukwa chiyani Allah sakutilanga ndi mawu tikunenawa (ngati iyeyu ndi Mtumikidi wa Allah?” Jahannam ikuwakwanira: adzailowa. Ndipo taonani kuipa malo (awo) wobwerera! [349]
[349] Ayuda amamlonjera Mtumiki ndi mawu akuti: “Saamu alayikumu” kutanthauza kuti: Imfa ikhale pa inu. Amayankhula mokhotetsa lirime kuti ampusitse Mtumiki kuti aganizire kuti akumlonjera moyenera kuti: “Asalamu alayikumu.”
阿拉伯语经注:
يَٰٓأَيُّهَا ٱلَّذِينَ ءَامَنُوٓاْ إِذَا تَنَٰجَيۡتُمۡ فَلَا تَتَنَٰجَوۡاْ بِٱلۡإِثۡمِ وَٱلۡعُدۡوَٰنِ وَمَعۡصِيَتِ ٱلرَّسُولِ وَتَنَٰجَوۡاْ بِٱلۡبِرِّ وَٱلتَّقۡوَىٰۖ وَٱتَّقُواْ ٱللَّهَ ٱلَّذِيٓ إِلَيۡهِ تُحۡشَرُونَ
E inu amene mwakhulupirira! Ngati mukunong’onezana, musamanong’onezane za machimo ndi mtopola ndi kunyoza Mtumiki; koma nong’onezanani za kulungama ndi kuopa Allah ndipo muopeni Allah, kwa Iye nkumene mudzasonkhanitsidwe (ndi kuweruzidwa).
阿拉伯语经注:
إِنَّمَا ٱلنَّجۡوَىٰ مِنَ ٱلشَّيۡطَٰنِ لِيَحۡزُنَ ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ وَلَيۡسَ بِضَآرِّهِمۡ شَيۡـًٔا إِلَّا بِإِذۡنِ ٱللَّهِۚ وَعَلَى ٱللَّهِ فَلۡيَتَوَكَّلِ ٱلۡمُؤۡمِنُونَ
Ndithu manong’onong’o oipa amachokera kwa satana kuti adandaulitse amene akhulupirira; koma sangawapweteke nawo chilichonse kupatula Allah atafuna ndipo okhulupirira atsamire kwa Allah Yekha, (asalabadire zonong’onezana zawo).
阿拉伯语经注:
يَٰٓأَيُّهَا ٱلَّذِينَ ءَامَنُوٓاْ إِذَا قِيلَ لَكُمۡ تَفَسَّحُواْ فِي ٱلۡمَجَٰلِسِ فَٱفۡسَحُواْ يَفۡسَحِ ٱللَّهُ لَكُمۡۖ وَإِذَا قِيلَ ٱنشُزُواْ فَٱنشُزُواْ يَرۡفَعِ ٱللَّهُ ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ مِنكُمۡ وَٱلَّذِينَ أُوتُواْ ٱلۡعِلۡمَ دَرَجَٰتٖۚ وَٱللَّهُ بِمَا تَعۡمَلُونَ خَبِيرٞ
E inu amene mwakhulupirira! Kukapemphedwa kwa inu kuti perekani malo pabwalo (pokhala), perekani malowo (kuti anzanu apeze pokhala; mukatero) Allah akuphanulirani (chifundo Chake pano pa dziko ndi kumwamba). Ndipo kukanenedwa kuti imilirani, muimilire (musanyozere, apatseni ena malo); Allah awakwezera (ulemelero) mwa inu amene akhulupirira ndi amene apatsidwa nzeru. Ndipo Allah akudziwa bwino zimene mukuchita.[350]
[350] Kuvumbulutsidwa kwa ndime iyi pali mawu akuti: Mtumiki (s.a.w) amaikira mtima kwambiri pa anthu amene adamenya nkhondo ya Badir; amgulu la Amuhajirina ndi Answari. Ndipo ena mwa iwowa adadza pa bwalo la Mtumiki ndi kupeza anthu ena atakhala kale adakhala chiimire chifukwa chosowa pokhala uku akuyembekezera kuti anzawo aja awapatseko pokhala; koma anthu adakhala kale aja sadalabadireko chilichonse. Mtumiki ataona izi zidamuwawa mu mtima ndipo adawauza omwe adakhala kale aja kuti aimilire apereke malo kwa anzawo. Achiphamaso adayamba kum’dzudzula Mtumiki (s.a.w) kuti bwanji akuchotsa anthu okhalakhala pamalo chifukwa cha anthu obwera mochedwa; sikupanda chilungamo kumeneko? Adatero achiphamaso aja. Ndipo poyankha zimenezi Allah adati: “E inu okhulupilira! Mukauzidwa kuti perekani malo kwa anzanu mupereke.” Ndipo mukauzidwa kuti imilirani, muimilire.”
M’ndime imeneyi Allah akutiphunzitsa kuti timvere Mtumiki (s.a.w) pa chilichonse chimene watilangiza popanda kuwiringula.
阿拉伯语经注:
 
含义的翻译 章: 穆扎底拉
章节目录 页码
 
《古兰经》译解 - 契瓦语翻译 - 哈利德·伊布拉欣·比德拉。 - 译解目录

由哈利德·伊布拉欣·白塔拉翻译。

关闭