Check out the new design

《古兰经》译解 - 契瓦语翻译 - 哈利德·伊布拉欣·比德拉。 * - 译解目录


含义的翻译 章: 穆扎底拉   段:
يَٰٓأَيُّهَا ٱلَّذِينَ ءَامَنُوٓاْ إِذَا نَٰجَيۡتُمُ ٱلرَّسُولَ فَقَدِّمُواْ بَيۡنَ يَدَيۡ نَجۡوَىٰكُمۡ صَدَقَةٗۚ ذَٰلِكَ خَيۡرٞ لَّكُمۡ وَأَطۡهَرُۚ فَإِن لَّمۡ تَجِدُواْ فَإِنَّ ٱللَّهَ غَفُورٞ رَّحِيمٌ
12 . E inu amene mwakhulupirira! Mukafuna kuyankhula ndi Mtumiki (s.a.w) tsogozani pa zoyankhula zanuzo, sadaka: kutero ndibwino kwa inu ndiponso ndichoyeretsa (mitima yanu). Koma ngati simudapeze (sadakayo) ndithu Allah Ngokhululuka, Ngwachisoni.
阿拉伯语经注:
ءَأَشۡفَقۡتُمۡ أَن تُقَدِّمُواْ بَيۡنَ يَدَيۡ نَجۡوَىٰكُمۡ صَدَقَٰتٖۚ فَإِذۡ لَمۡ تَفۡعَلُواْ وَتَابَ ٱللَّهُ عَلَيۡكُمۡ فَأَقِيمُواْ ٱلصَّلَوٰةَ وَءَاتُواْ ٱلزَّكَوٰةَ وَأَطِيعُواْ ٱللَّهَ وَرَسُولَهُۥۚ وَٱللَّهُ خَبِيرُۢ بِمَا تَعۡمَلُونَ
Kodi mwaopa kutsogoza sadaka pakunena naye (Mtumiki)? Ngati simudachite zimenezi basi Allah wakukhululukirani; choncho pempherani Swala moyenera ndipo perekani Zakaat ndiponso mverani Allah pamodzi ndi Mtumiki Wake. Ndipo Allah akudziwa zonse zimene mukuchita.
阿拉伯语经注:
۞ أَلَمۡ تَرَ إِلَى ٱلَّذِينَ تَوَلَّوۡاْ قَوۡمًا غَضِبَ ٱللَّهُ عَلَيۡهِم مَّا هُم مِّنكُمۡ وَلَا مِنۡهُمۡ وَيَحۡلِفُونَ عَلَى ٱلۡكَذِبِ وَهُمۡ يَعۡلَمُونَ
Kodi sukuwaona amene apalana ubwenzi ndi anthu amene Allah wawakwiira; iwo sali mwa inu ndiponso sali mwa iwo. Ndipo akulumbira zabodza uku akudziwa (kuti limeneli ndibodza).
阿拉伯语经注:
أَعَدَّ ٱللَّهُ لَهُمۡ عَذَابٗا شَدِيدًاۖ إِنَّهُمۡ سَآءَ مَا كَانُواْ يَعۡمَلُونَ
Allah wawakonzera chilango chaukali, ndithudi nzoipa zimene amachita.
阿拉伯语经注:
ٱتَّخَذُوٓاْ أَيۡمَٰنَهُمۡ جُنَّةٗ فَصَدُّواْ عَن سَبِيلِ ٱللَّهِ فَلَهُمۡ عَذَابٞ مُّهِينٞ
Kulumbira kwawo adakuchita kukhala chodzitetezera (iwo, ana awo ndi chuma chawo); choncho adatsekereza (anthu) ku njira ya Allah; choncho chilango choyalutsa chili pa iwo.[351]
[351] Tanthauzo la “Kulumbira kwawo adakuchita chodzitetezera” ndiko kuti achiphamaso amadziteteza kwa Asilamu pakungosonyeza Chisilamu chachiphamaso, chapakamwa pokha pomwe mitima yawo siimakhulupilira. Amatero pakuopa kuti Asilamu angawachitire zimene amawachitira anthu osakhulupilira monga kuwathira nkhondo akaputidwa.
阿拉伯语经注:
لَّن تُغۡنِيَ عَنۡهُمۡ أَمۡوَٰلُهُمۡ وَلَآ أَوۡلَٰدُهُم مِّنَ ٱللَّهِ شَيۡـًٔاۚ أُوْلَٰٓئِكَ أَصۡحَٰبُ ٱلنَّارِۖ هُمۡ فِيهَا خَٰلِدُونَ
Chuma chawo, ngakhale ana awo, sizidzawathandiza konse ku chilango cha Allah. Iwowo ndi anthu a ku Moto m’menemo iwo adzakhala nthawi yaitali.
阿拉伯语经注:
يَوۡمَ يَبۡعَثُهُمُ ٱللَّهُ جَمِيعٗا فَيَحۡلِفُونَ لَهُۥ كَمَا يَحۡلِفُونَ لَكُمۡ وَيَحۡسَبُونَ أَنَّهُمۡ عَلَىٰ شَيۡءٍۚ أَلَآ إِنَّهُمۡ هُمُ ٱلۡكَٰذِبُونَ
(Alikumbukire) tsiku limene Allah adzawaukitsa (ku imfa) onse, adzayamba kulumbira kwa Iye (zabodza) monga akulumbira (zabodza) kwa inu. Ndipo akuganiza kuti apezapo kanthu (pakulumbira kwawo). Dziwani, ndithudi, iwo ndi abodza.
阿拉伯语经注:
ٱسۡتَحۡوَذَ عَلَيۡهِمُ ٱلشَّيۡطَٰنُ فَأَنسَىٰهُمۡ ذِكۡرَ ٱللَّهِۚ أُوْلَٰٓئِكَ حِزۡبُ ٱلشَّيۡطَٰنِۚ أَلَآ إِنَّ حِزۡبَ ٱلشَّيۡطَٰنِ هُمُ ٱلۡخَٰسِرُونَ
Satana wawapambana ndipo wawaiwalitsa kukumbukira Allah. Iwowa ndiachipani cha satana. Dziwani kuti chipani cha satana nchotayika, (choonongeka).
阿拉伯语经注:
إِنَّ ٱلَّذِينَ يُحَآدُّونَ ٱللَّهَ وَرَسُولَهُۥٓ أُوْلَٰٓئِكَ فِي ٱلۡأَذَلِّينَ
Ndithudi amene akutsutsana ndi Allah ndi Mthenga Wake, iwowo adzakhala m’gulu la onyozeka.
阿拉伯语经注:
كَتَبَ ٱللَّهُ لَأَغۡلِبَنَّ أَنَا۠ وَرُسُلِيٓۚ إِنَّ ٱللَّهَ قَوِيٌّ عَزِيزٞ
Allah adalamula (kuti): “Ndithu ndipambana Ine ndi atumiki Anga.” Ndithu Allah ndiwanyonga zokwana, Wopambana (sapambanidwa ndi aliyense).
阿拉伯语经注:
 
含义的翻译 章: 穆扎底拉
章节目录 页码
 
《古兰经》译解 - 契瓦语翻译 - 哈利德·伊布拉欣·比德拉。 - 译解目录

由哈利德·伊布拉欣·白塔拉翻译。

关闭