የቅዱስ ቁርዓን ይዘት ትርጉም - ቸዋኛ ትርጉም * - የትርጉሞች ማዉጫ


የይዘት ትርጉም ምዕራፍ: ሱረቱ አል ኢንፊጣር   አንቀጽ:

ሱረቱ አል ኢንፊጣር

إِذَا ٱلسَّمَآءُ ٱنفَطَرَتۡ
Pamene thambo lidzasweke,[397]
[397] Kuyambira pa Ayah 1 mpaka 4, Allah akutisonyeza zododometsa zina za tsiku lachimaliziro.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
وَإِذَا ٱلۡكَوَاكِبُ ٱنتَثَرَتۡ
Ndi pamene nyenyezi zidzayoyoke (ndi kumwazikana),
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
وَإِذَا ٱلۡبِحَارُ فُجِّرَتۡ
Pamenenso nyanja zikuluzikulu zidzaphwasulidwe.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
وَإِذَا ٱلۡقُبُورُ بُعۡثِرَتۡ
Ndiponso pamene manda adzafukulidwe (ndikutuluka akufa omwe adali mmenemo),
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
عَلِمَتۡ نَفۡسٞ مَّا قَدَّمَتۡ وَأَخَّرَتۡ
(Panthawiyo) mzimu uliwonse udzadziwa zimene udatsogoza (zabwino ndi zoipa) ndi zimene udasiya m’mbuyo.[398]
[398] Munthu aliyense pa tsiku limenelo adzadziwa zimene adachita, zabwino ndi zoipa.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
يَٰٓأَيُّهَا ٱلۡإِنسَٰنُ مَا غَرَّكَ بِرَبِّكَ ٱلۡكَرِيمِ
E iwe munthu! Nchiani chakunyenga kumsiya Mbuye wako wa ufulu (kufikira pomnyoza)?
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
ٱلَّذِي خَلَقَكَ فَسَوَّىٰكَ فَعَدَلَكَ
Amene adalenga iwe nakulinganiza (ziwalo zako) ndi kukulongosola (moyenera);
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
فِيٓ أَيِّ صُورَةٖ مَّا شَآءَ رَكَّبَكَ
Ndipo maonekedwe amtundu uliwonse omwe adawafuna adakuveka (popanda chifuniro chako).
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
كَلَّا بَلۡ تُكَذِّبُونَ بِٱلدِّينِ
Ayi, sichoncho! Koma inu mukutsutsa za (tsiku) lamalipiro.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
وَإِنَّ عَلَيۡكُمۡ لَحَٰفِظِينَ
Ndithu pa inu alipo okuyang’ anirani,[399]
[399] Munthu aliyense ali nawo angelo awiri, Rakibu ndi Atidu. Ntchito zawo ndi kulemba ntchito za munthu, zabwino ndi zoipa zomwe.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
كِرَامٗا كَٰتِبِينَ
Olemekezeka, olemba (zochita zanu.)
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
يَعۡلَمُونَ مَا تَفۡعَلُونَ
Akudziwa (zonse) zimene mukuchita (zabwino ndi zoipa).
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
إِنَّ ٱلۡأَبۡرَارَ لَفِي نَعِيمٖ
Ndithudi ochita zabwino adzakhala mu mtendere.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
وَإِنَّ ٱلۡفُجَّارَ لَفِي جَحِيمٖ
Ndipo ndithu amene ali olakwira malamulo a Allah adzakhala ku Moto wopsereza.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
يَصۡلَوۡنَهَا يَوۡمَ ٱلدِّينِ
Adzaulowa tsiku la malipiro.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
وَمَا هُمۡ عَنۡهَا بِغَآئِبِينَ
Ndipo iwo kumeneko sadzachokako.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
وَمَآ أَدۡرَىٰكَ مَا يَوۡمُ ٱلدِّينِ
Kodi nchiyani chingakudziwitse za tsiku la malipiro?
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
ثُمَّ مَآ أَدۡرَىٰكَ مَا يَوۡمُ ٱلدِّينِ
Ndipo nchiyani chingakudziwitse za tsiku lamalipiro?
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
يَوۡمَ لَا تَمۡلِكُ نَفۡسٞ لِّنَفۡسٖ شَيۡـٔٗاۖ وَٱلۡأَمۡرُ يَوۡمَئِذٖ لِّلَّهِ
Limeneli ndi tsiku limene mzimu uliwonse sudzakhala ndi mphamvu (yodzetsa mtendere kapena yochotsa chovuta) pa mzimu wina. Ndipo lamulo pa tsiku limeneli ndi la Allah yekha.[400]
[400] Tanthauzo lake ndikuti tsiku limenelo sipadzakhala munthu wotha kumthandiza mnzake pa chilichonse ndiponso palibe adzakhale ndi mphamvu zolamula kupatula Allah yekha.
የአረብኛ ቁርኣን ማብራሪያ:
 
የይዘት ትርጉም ምዕራፍ: ሱረቱ አል ኢንፊጣር
የምዕራፎች ማውጫ የገፅ ቁጥር
 
የቅዱስ ቁርዓን ይዘት ትርጉም - ቸዋኛ ትርጉም - የትርጉሞች ማዉጫ

የተከበረው ቁርአን ቸዋኛ መልዕክተ ትርጉም፤ በኻሊድ ኢብራሂም ቢታላ የ 2020 ቅጅ

መዝጋት