আল-কোৰআনুল কাৰীমৰ অৰ্থানুবাদ - চেৱা অনুবাদ * - অনুবাদসমূহৰ সূচীপত্ৰ


অৰ্থানুবাদ ছুৰা: ছুৰা আন-নাজম   আয়াত:

ছুৰা আন-নাজম

وَٱلنَّجۡمِ إِذَا هَوَىٰ
Ndikulumbira nyenyezi pamene zikulowa.
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
مَا ضَلَّ صَاحِبُكُمۡ وَمَا غَوَىٰ
Sadasokere m’bale wanu (Mtumiki panjira ya choonadi) ndipo sadakhulupirire zonama.
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
وَمَا يَنطِقُ عَنِ ٱلۡهَوَىٰٓ
Ndipo sayankhula zofuna za mtima wake.
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
إِنۡ هُوَ إِلَّا وَحۡيٞ يُوحَىٰ
Iyoyi (Qur’an imene akuinena), sichina, koma ndichivumbulutso chovumbulutsidwa.
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
عَلَّمَهُۥ شَدِيدُ ٱلۡقُوَىٰ
Adamphunzitsa (chivumbulutsochi) (Jibril) wanyonga zambiri.
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
ذُو مِرَّةٖ فَٱسۡتَوَىٰ
Wanzeru zakuya; ndipo adakhazikika (m’maonekedwe ake).
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
وَهُوَ بِٱلۡأُفُقِ ٱلۡأَعۡلَىٰ
Ali m’chizimezime kumwamba.
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
ثُمَّ دَنَا فَتَدَلَّىٰ
Kenako (Jibril) adamuyandikira (Mtumiki {s.a.w}) ndikuonjezera kumuyandikira.
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
فَكَانَ قَابَ قَوۡسَيۡنِ أَوۡ أَدۡنَىٰ
(Kumuyandikira kwake) kudali ngati (mpata wa) nsonga ziwiri za uta, kapena kuyandikira kuposa apo.
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
فَأَوۡحَىٰٓ إِلَىٰ عَبۡدِهِۦ مَآ أَوۡحَىٰ
(Choncho Jibril) adavumbulutsira kapolo wake (wa Allah) zimene adazivumbulutsa.
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
مَا كَذَبَ ٱلۡفُؤَادُ مَا رَأَىٰٓ
Sudaname mtima (wa Mtumiki) pazimene adaziona.
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
أَفَتُمَٰرُونَهُۥ عَلَىٰ مَا يَرَىٰ
Kodi mukutsutsana naye (Mthenga wa Allah) pazimene adaziona?
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
وَلَقَدۡ رَءَاهُ نَزۡلَةً أُخۡرَىٰ
Ndipo ndithu adamuona (Jibril) m’kuona kachiwiri mkaonekedwe kake.
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
عِندَ سِدۡرَةِ ٱلۡمُنتَهَىٰ
Pa ‘Sidratil Muntaha’ (mtengo wamasawu pothera zinthu zonse).
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
عِندَهَا جَنَّةُ ٱلۡمَأۡوَىٰٓ
Pafupi pake pali Janatu Ma’awa, (munda wokhalamo).
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
إِذۡ يَغۡشَى ٱلسِّدۡرَةَ مَا يَغۡشَىٰ
Pomwe chophimba chidaphimba msawuwo.
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
مَا زَاغَ ٱلۡبَصَرُ وَمَا طَغَىٰ
Maso ake sadaphonye kapena kupyola malire (oikidwa).
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
لَقَدۡ رَأَىٰ مِنۡ ءَايَٰتِ رَبِّهِ ٱلۡكُبۡرَىٰٓ
Ndithu (Mneneri Muhammad {s.a.w}) adaona zina mwa zizindikiro zikuluzikulu za Mbuye wake (zosonyeza mphamvu Zake)
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
أَفَرَءَيۡتُمُ ٱللَّٰتَ وَٱلۡعُزَّىٰ
Kodi mwamuona Laat ndi Uzza?
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
وَمَنَوٰةَ ٱلثَّالِثَةَ ٱلۡأُخۡرَىٰٓ
Ndi Manata; (fano lanu) lina lachitatu, (kuti iwowa ndi milungu)?
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
أَلَكُمُ ٱلذَّكَرُ وَلَهُ ٱلۡأُنثَىٰ
Kodi mwadzisankhira ana aamuna (kukhala anu), ndi aakazi nkukhala a Iye (Allah)?
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
تِلۡكَ إِذٗا قِسۡمَةٞ ضِيزَىٰٓ
Choncho kugawa kumeneko nkopanda chilungamo (pompatsa Allah zimene mumazida).
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
إِنۡ هِيَ إِلَّآ أَسۡمَآءٞ سَمَّيۡتُمُوهَآ أَنتُمۡ وَءَابَآؤُكُم مَّآ أَنزَلَ ٱللَّهُ بِهَا مِن سُلۡطَٰنٍۚ إِن يَتَّبِعُونَ إِلَّا ٱلظَّنَّ وَمَا تَهۡوَى ٱلۡأَنفُسُۖ وَلَقَدۡ جَآءَهُم مِّن رَّبِّهِمُ ٱلۡهُدَىٰٓ
Sali (mafanowo) chilichonse koma ndi maina basi omwe mudawatcha inu ndi makolo anu, (molingana ndi zilakolako zanu zachabe); Allah sadatsitse umboni pazimenezo (wotsimikiza pamawu anuwo). Sakutsatira koma zoganizira basi ndi zimene ikufuna mitima (yawo yopotoka). Ndithu chidawadzera chiongoko kuchokera kwa Mbuye wawo (chomwe m’kati mwake mudali kuongoka kwawo akadachitsatira).
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
أَمۡ لِلۡإِنسَٰنِ مَا تَمَنَّىٰ
Kodi munthu akuganiza kuti adzapeza chilichonse chimene akuchilakalaka?
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
فَلِلَّهِ ٱلۡأٓخِرَةُ وَٱلۡأُولَىٰ
Moyo wa tsiku lachimaliziro ndi wadziko lapansi ngwa Allah Yekha.
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
۞ وَكَم مِّن مَّلَكٖ فِي ٱلسَّمَٰوَٰتِ لَا تُغۡنِي شَفَٰعَتُهُمۡ شَيۡـًٔا إِلَّا مِنۢ بَعۡدِ أَن يَأۡذَنَ ٱللَّهُ لِمَن يَشَآءُ وَيَرۡضَىٰٓ
Ndipo kuli angelo ambiri kumwamba omwe kuchondelera kwawo sikungathandize china chilichonse pokhapokha Allah ataloleza kwa amene wamfuna ndi kumuyanja.
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
إِنَّ ٱلَّذِينَ لَا يُؤۡمِنُونَ بِٱلۡأٓخِرَةِ لَيُسَمُّونَ ٱلۡمَلَٰٓئِكَةَ تَسۡمِيَةَ ٱلۡأُنثَىٰ
Ndithu amene sakhulupirira za (Moyo wa) tsiku lachimaliziro, amawatcha angelo kuti ndiakazi.
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
وَمَا لَهُم بِهِۦ مِنۡ عِلۡمٍۖ إِن يَتَّبِعُونَ إِلَّا ٱلظَّنَّۖ وَإِنَّ ٱلظَّنَّ لَا يُغۡنِي مِنَ ٱلۡحَقِّ شَيۡـٔٗا
Ndipo alibe kudziwa kulikonse pa zimenezo sakutsata china koma maganizo. Ndipo ndithu kuganizira sikuthandiza chilichonse pofuna kupeza choonadi.
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
فَأَعۡرِضۡ عَن مَّن تَوَلَّىٰ عَن ذِكۡرِنَا وَلَمۡ يُرِدۡ إِلَّا ٱلۡحَيَوٰةَ ٱلدُّنۡيَا
Choncho apewe (osakhulupirirawa) amene anyozera chikumbutso Chathu (Qur’an); ndipo palibe chimene akufuna koma moyo wa padziko lapansi basi.
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
ذَٰلِكَ مَبۡلَغُهُم مِّنَ ٱلۡعِلۡمِۚ إِنَّ رَبَّكَ هُوَ أَعۡلَمُ بِمَن ضَلَّ عَن سَبِيلِهِۦ وَهُوَ أَعۡلَمُ بِمَنِ ٱهۡتَدَىٰ
Zimenezo ndiwo mapeto a kudziwa kwawo. Ndithu Mbuye wako Ngodziwa kwambiri za amene akusokera njira Yake ndiponso akudziwa bwino za yemwe wawongoka.
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
وَلِلَّهِ مَا فِي ٱلسَّمَٰوَٰتِ وَمَا فِي ٱلۡأَرۡضِ لِيَجۡزِيَ ٱلَّذِينَ أَسَٰٓـُٔواْ بِمَا عَمِلُواْ وَيَجۡزِيَ ٱلَّذِينَ أَحۡسَنُواْ بِٱلۡحُسۡنَى
Ndipo zonse za kumwamba ndi zadziko lapansi nza Allah Yekha, (pozilenga ndi kuziyang’anira), kuti adzawalipire amene adaipitsa pa zimene adachita ndi kutinso adzawalipire zabwino amene adachita zabwino.
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
ٱلَّذِينَ يَجۡتَنِبُونَ كَبَٰٓئِرَ ٱلۡإِثۡمِ وَٱلۡفَوَٰحِشَ إِلَّا ٱللَّمَمَۚ إِنَّ رَبَّكَ وَٰسِعُ ٱلۡمَغۡفِرَةِۚ هُوَ أَعۡلَمُ بِكُمۡ إِذۡ أَنشَأَكُم مِّنَ ٱلۡأَرۡضِ وَإِذۡ أَنتُمۡ أَجِنَّةٞ فِي بُطُونِ أُمَّهَٰتِكُمۡۖ فَلَا تُزَكُّوٓاْ أَنفُسَكُمۡۖ هُوَ أَعۡلَمُ بِمَنِ ٱتَّقَىٰٓ
Amene akuwapewa machimo akuluakulu ndi zadama, kupatula timachimo tating’onoting’ono (timene Allah amatikhululuka); ndithu Mbuye wako ndiwokhululuka kwakukulu. Iye akudziwa chikhalidwe chanu kuyambira pomwe adakulengani kuchokera m’nthaka ndi pamene inu mudali makanda m’mimba mwa amayi anu (mosinthasintha; mosiyanasiyana). Choncho musadzitame nokha kuyera mtima; Iye Ngodziwa kwambiri za yemwe akumuopa (Allah).
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
أَفَرَءَيۡتَ ٱلَّذِي تَوَلَّىٰ
Kodi wamuona yemwe wadzipatula (pakusiya kutsatira choonadi)?
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
وَأَعۡطَىٰ قَلِيلٗا وَأَكۡدَىٰٓ
Ndipo wapereka (chuma) chochepa nasiyanso kuperekako.
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
أَعِندَهُۥ عِلۡمُ ٱلۡغَيۡبِ فَهُوَ يَرَىٰٓ
Kodi akudziwa zamseri, kotero kuti akuziwona (zomwe wadza nazo (Mtumiki {s.a.w) kuti sizoona)?
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
أَمۡ لَمۡ يُنَبَّأۡ بِمَا فِي صُحُفِ مُوسَىٰ
Kapena sadauzidwe zomwe zidali m’mabuku a Mûsa.
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
وَإِبۡرَٰهِيمَ ٱلَّذِي وَفَّىٰٓ
Ndi Ibrahim amene adakwaniritsa (lonjezo la Allah)?
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
أَلَّا تَزِرُ وَازِرَةٞ وِزۡرَ أُخۡرَىٰ
Kuti mzimu wamachimo sungasenze machimo a mzimu wina.
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
وَأَن لَّيۡسَ لِلۡإِنسَٰنِ إِلَّا مَا سَعَىٰ
Ndi kutinso munthu sakalipidwa koma zimene adachita.
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
وَأَنَّ سَعۡيَهُۥ سَوۡفَ يُرَىٰ
Ndipo ndithu ntchito zake zidzaonekera.
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
ثُمَّ يُجۡزَىٰهُ ٱلۡجَزَآءَ ٱلۡأَوۡفَىٰ
Kenako (munthu) adzalipidwa malipiro okwanira (pa ntchito zake zimene amachita).
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
وَأَنَّ إِلَىٰ رَبِّكَ ٱلۡمُنتَهَىٰ
Ndipo ndithu kwa Mbuye wako yekha ndiwo malekezero (a chilichonse).
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
وَأَنَّهُۥ هُوَ أَضۡحَكَ وَأَبۡكَىٰ
Ndithu Iye ndiAmene amapereka chisangalalo ndi zoliritsa.
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
وَأَنَّهُۥ هُوَ أَمَاتَ وَأَحۡيَا
Ndipo Iye yekha ndi Amene amapereka imfa ndi moyo.
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
وَأَنَّهُۥ خَلَقَ ٱلزَّوۡجَيۡنِ ٱلذَّكَرَ وَٱلۡأُنثَىٰ
Ndipo Iye ndiAmene adalenga mitundu iwiri: chachimuna ndi chachikazi, (anthu ndi zamoyo zina).
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
مِن نُّطۡفَةٍ إِذَا تُمۡنَىٰ
Kuchokera m’mbewu ya moyo pamene imafwamphukira (m’chiberekero).
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
وَأَنَّ عَلَيۡهِ ٱلنَّشۡأَةَ ٱلۡأُخۡرَىٰ
Ndipo ndithu ndi udindo Wake kuukitsa kwina (pambuyo pa imfa).
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
وَأَنَّهُۥ هُوَ أَغۡنَىٰ وَأَقۡنَىٰ
Ndipo Iye ndiAmene amapatsa chokwanira ndipo ndi amene amapatsa chosunga.
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
وَأَنَّهُۥ هُوَ رَبُّ ٱلشِّعۡرَىٰ
Ndipo ndithu Iye ndi Mbuye wa nyenyezi yotchedwa Shiira;
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
وَأَنَّهُۥٓ أَهۡلَكَ عَادًا ٱلۡأُولَىٰ
Ndipo Iye ndi amene adaononga Âdi oyamba; (anthu a Mneneri Hûd).
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
وَثَمُودَاْ فَمَآ أَبۡقَىٰ
Ndi Samudu; (anthu a Mneneri Swaleh;) choncho sadasiye (ndi mmodzi yemwe wa iwo).
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
وَقَوۡمَ نُوحٖ مِّن قَبۡلُۖ إِنَّهُمۡ كَانُواْ هُمۡ أَظۡلَمَ وَأَطۡغَىٰ
Ndipo (adawaononganso) anthu a Nuh, kale (asadaononge Âdi ndi Samudu). Ndithu iwo adali osalungama ndi olumpha malire kwambiri (kuposa Âdi ndi Samudu).
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
وَٱلۡمُؤۡتَفِكَةَ أَهۡوَىٰ
Ndi midzi yotembenuzidwa kumwamba kukhala pansi, pansi kukhala kumwamba, (ya anthu a Luti) adaigwetsa.
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
فَغَشَّىٰهَا مَا غَشَّىٰ
Tero chidaivindikira (midziyo) chomwe chidaivindikira (chilango).
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
فَبِأَيِّ ءَالَآءِ رَبِّكَ تَتَمَارَىٰ
Kodi ndimtendere uti (mumtendere) wa Mbuye wako umene ukuukaikira?
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
هَٰذَا نَذِيرٞ مِّنَ ٱلنُّذُرِ ٱلۡأُولَىٰٓ
Uyu (Mtumiki) ndimchenjezi mwa achenjezi oyamba (amene adachenjezedwa nawo anthu a mibadwo yakale)
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
أَزِفَتِ ٱلۡأٓزِفَةُ
Chayandikira choyandikira (Qiyâma).
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
لَيۡسَ لَهَا مِن دُونِ ٱللَّهِ كَاشِفَةٌ
Palibe amene angachionetse koma Allah Yekha.
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
أَفَمِنۡ هَٰذَا ٱلۡحَدِيثِ تَعۡجَبُونَ
Kodi mukuidabwa nkhaniyi (ya Qur’an moikana)?
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
وَتَضۡحَكُونَ وَلَا تَبۡكُونَ
Mungoseka (mwachipongwe) ndipo simukulira (pamene mukuimva monga momwe akuchitira okhulupirira).
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
وَأَنتُمۡ سَٰمِدُونَ
Ndipo mukunyozera?
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
فَٱسۡجُدُواْۤ لِلَّهِۤ وَٱعۡبُدُواْ۩
Mlambireni ndi kumpembedza Allah (amene wavumbulutsa Qur’an kuti ikhale chiongoko cha anthu).
আৰবী তাফছীৰসমূহ:
 
অৰ্থানুবাদ ছুৰা: ছুৰা আন-নাজম
ছুৰাৰ তালিকা পৃষ্ঠা নং
 
আল-কোৰআনুল কাৰীমৰ অৰ্থানুবাদ - চেৱা অনুবাদ - অনুবাদসমূহৰ সূচীপত্ৰ

চেৱা ভাষাত কোৰআনুল কাৰীমৰ অৰ্থানুবাদ- অনুবাদ কৰিছে খালিদ ইব্ৰাহীম বেতালা। ২০২০ চন।

বন্ধ