Ibisobanuro bya qoran ntagatifu - Ibisobanuro mu rurimi rw''urushiishiyu * - Ishakiro ry'ibisobanuro


Ibisobanuro by'amagambo Isura: Annajmi (Inyenyeri)   Umurongo:

Annajmi (Inyenyeri)

وَٱلنَّجۡمِ إِذَا هَوَىٰ
Ndikulumbira nyenyezi pamene zikulowa.
Ibisobanuro by'icyarabu:
مَا ضَلَّ صَاحِبُكُمۡ وَمَا غَوَىٰ
Sadasokere m’bale wanu (Mtumiki panjira ya choonadi) ndipo sadakhulupirire zonama.
Ibisobanuro by'icyarabu:
وَمَا يَنطِقُ عَنِ ٱلۡهَوَىٰٓ
Ndipo sayankhula zofuna za mtima wake.
Ibisobanuro by'icyarabu:
إِنۡ هُوَ إِلَّا وَحۡيٞ يُوحَىٰ
Iyoyi (Qur’an imene akuinena), sichina, koma ndichivumbulutso chovumbulutsidwa.
Ibisobanuro by'icyarabu:
عَلَّمَهُۥ شَدِيدُ ٱلۡقُوَىٰ
Adamphunzitsa (chivumbulutsochi) (Jibril) wanyonga zambiri.
Ibisobanuro by'icyarabu:
ذُو مِرَّةٖ فَٱسۡتَوَىٰ
Wanzeru zakuya; ndipo adakhazikika (m’maonekedwe ake).
Ibisobanuro by'icyarabu:
وَهُوَ بِٱلۡأُفُقِ ٱلۡأَعۡلَىٰ
Ali m’chizimezime kumwamba.
Ibisobanuro by'icyarabu:
ثُمَّ دَنَا فَتَدَلَّىٰ
Kenako (Jibril) adamuyandikira (Mtumiki {s.a.w}) ndikuonjezera kumuyandikira.
Ibisobanuro by'icyarabu:
فَكَانَ قَابَ قَوۡسَيۡنِ أَوۡ أَدۡنَىٰ
(Kumuyandikira kwake) kudali ngati (mpata wa) nsonga ziwiri za uta, kapena kuyandikira kuposa apo.
Ibisobanuro by'icyarabu:
فَأَوۡحَىٰٓ إِلَىٰ عَبۡدِهِۦ مَآ أَوۡحَىٰ
(Choncho Jibril) adavumbulutsira kapolo wake (wa Allah) zimene adazivumbulutsa.
Ibisobanuro by'icyarabu:
مَا كَذَبَ ٱلۡفُؤَادُ مَا رَأَىٰٓ
Sudaname mtima (wa Mtumiki) pazimene adaziona.
Ibisobanuro by'icyarabu:
أَفَتُمَٰرُونَهُۥ عَلَىٰ مَا يَرَىٰ
Kodi mukutsutsana naye (Mthenga wa Allah) pazimene adaziona?
Ibisobanuro by'icyarabu:
وَلَقَدۡ رَءَاهُ نَزۡلَةً أُخۡرَىٰ
Ndipo ndithu adamuona (Jibril) m’kuona kachiwiri mkaonekedwe kake.
Ibisobanuro by'icyarabu:
عِندَ سِدۡرَةِ ٱلۡمُنتَهَىٰ
Pa ‘Sidratil Muntaha’ (mtengo wamasawu pothera zinthu zonse).
Ibisobanuro by'icyarabu:
عِندَهَا جَنَّةُ ٱلۡمَأۡوَىٰٓ
Pafupi pake pali Janatu Ma’awa, (munda wokhalamo).
Ibisobanuro by'icyarabu:
إِذۡ يَغۡشَى ٱلسِّدۡرَةَ مَا يَغۡشَىٰ
Pomwe chophimba chidaphimba msawuwo.
Ibisobanuro by'icyarabu:
مَا زَاغَ ٱلۡبَصَرُ وَمَا طَغَىٰ
Maso ake sadaphonye kapena kupyola malire (oikidwa).
Ibisobanuro by'icyarabu:
لَقَدۡ رَأَىٰ مِنۡ ءَايَٰتِ رَبِّهِ ٱلۡكُبۡرَىٰٓ
Ndithu (Mneneri Muhammad {s.a.w}) adaona zina mwa zizindikiro zikuluzikulu za Mbuye wake (zosonyeza mphamvu Zake)
Ibisobanuro by'icyarabu:
أَفَرَءَيۡتُمُ ٱللَّٰتَ وَٱلۡعُزَّىٰ
Kodi mwamuona Laat ndi Uzza?
Ibisobanuro by'icyarabu:
وَمَنَوٰةَ ٱلثَّالِثَةَ ٱلۡأُخۡرَىٰٓ
Ndi Manata; (fano lanu) lina lachitatu, (kuti iwowa ndi milungu)?
Ibisobanuro by'icyarabu:
أَلَكُمُ ٱلذَّكَرُ وَلَهُ ٱلۡأُنثَىٰ
Kodi mwadzisankhira ana aamuna (kukhala anu), ndi aakazi nkukhala a Iye (Allah)?
Ibisobanuro by'icyarabu:
تِلۡكَ إِذٗا قِسۡمَةٞ ضِيزَىٰٓ
Choncho kugawa kumeneko nkopanda chilungamo (pompatsa Allah zimene mumazida).
Ibisobanuro by'icyarabu:
إِنۡ هِيَ إِلَّآ أَسۡمَآءٞ سَمَّيۡتُمُوهَآ أَنتُمۡ وَءَابَآؤُكُم مَّآ أَنزَلَ ٱللَّهُ بِهَا مِن سُلۡطَٰنٍۚ إِن يَتَّبِعُونَ إِلَّا ٱلظَّنَّ وَمَا تَهۡوَى ٱلۡأَنفُسُۖ وَلَقَدۡ جَآءَهُم مِّن رَّبِّهِمُ ٱلۡهُدَىٰٓ
Sali (mafanowo) chilichonse koma ndi maina basi omwe mudawatcha inu ndi makolo anu, (molingana ndi zilakolako zanu zachabe); Allah sadatsitse umboni pazimenezo (wotsimikiza pamawu anuwo). Sakutsatira koma zoganizira basi ndi zimene ikufuna mitima (yawo yopotoka). Ndithu chidawadzera chiongoko kuchokera kwa Mbuye wawo (chomwe m’kati mwake mudali kuongoka kwawo akadachitsatira).
Ibisobanuro by'icyarabu:
أَمۡ لِلۡإِنسَٰنِ مَا تَمَنَّىٰ
Kodi munthu akuganiza kuti adzapeza chilichonse chimene akuchilakalaka?
Ibisobanuro by'icyarabu:
فَلِلَّهِ ٱلۡأٓخِرَةُ وَٱلۡأُولَىٰ
Moyo wa tsiku lachimaliziro ndi wadziko lapansi ngwa Allah Yekha.
Ibisobanuro by'icyarabu:
۞ وَكَم مِّن مَّلَكٖ فِي ٱلسَّمَٰوَٰتِ لَا تُغۡنِي شَفَٰعَتُهُمۡ شَيۡـًٔا إِلَّا مِنۢ بَعۡدِ أَن يَأۡذَنَ ٱللَّهُ لِمَن يَشَآءُ وَيَرۡضَىٰٓ
Ndipo kuli angelo ambiri kumwamba omwe kuchondelera kwawo sikungathandize china chilichonse pokhapokha Allah ataloleza kwa amene wamfuna ndi kumuyanja.
Ibisobanuro by'icyarabu:
إِنَّ ٱلَّذِينَ لَا يُؤۡمِنُونَ بِٱلۡأٓخِرَةِ لَيُسَمُّونَ ٱلۡمَلَٰٓئِكَةَ تَسۡمِيَةَ ٱلۡأُنثَىٰ
Ndithu amene sakhulupirira za (Moyo wa) tsiku lachimaliziro, amawatcha angelo kuti ndiakazi.
Ibisobanuro by'icyarabu:
وَمَا لَهُم بِهِۦ مِنۡ عِلۡمٍۖ إِن يَتَّبِعُونَ إِلَّا ٱلظَّنَّۖ وَإِنَّ ٱلظَّنَّ لَا يُغۡنِي مِنَ ٱلۡحَقِّ شَيۡـٔٗا
Ndipo alibe kudziwa kulikonse pa zimenezo sakutsata china koma maganizo. Ndipo ndithu kuganizira sikuthandiza chilichonse pofuna kupeza choonadi.
Ibisobanuro by'icyarabu:
فَأَعۡرِضۡ عَن مَّن تَوَلَّىٰ عَن ذِكۡرِنَا وَلَمۡ يُرِدۡ إِلَّا ٱلۡحَيَوٰةَ ٱلدُّنۡيَا
Choncho apewe (osakhulupirirawa) amene anyozera chikumbutso Chathu (Qur’an); ndipo palibe chimene akufuna koma moyo wa padziko lapansi basi.
Ibisobanuro by'icyarabu:
ذَٰلِكَ مَبۡلَغُهُم مِّنَ ٱلۡعِلۡمِۚ إِنَّ رَبَّكَ هُوَ أَعۡلَمُ بِمَن ضَلَّ عَن سَبِيلِهِۦ وَهُوَ أَعۡلَمُ بِمَنِ ٱهۡتَدَىٰ
Zimenezo ndiwo mapeto a kudziwa kwawo. Ndithu Mbuye wako Ngodziwa kwambiri za amene akusokera njira Yake ndiponso akudziwa bwino za yemwe wawongoka.
Ibisobanuro by'icyarabu:
وَلِلَّهِ مَا فِي ٱلسَّمَٰوَٰتِ وَمَا فِي ٱلۡأَرۡضِ لِيَجۡزِيَ ٱلَّذِينَ أَسَٰٓـُٔواْ بِمَا عَمِلُواْ وَيَجۡزِيَ ٱلَّذِينَ أَحۡسَنُواْ بِٱلۡحُسۡنَى
Ndipo zonse za kumwamba ndi zadziko lapansi nza Allah Yekha, (pozilenga ndi kuziyang’anira), kuti adzawalipire amene adaipitsa pa zimene adachita ndi kutinso adzawalipire zabwino amene adachita zabwino.
Ibisobanuro by'icyarabu:
ٱلَّذِينَ يَجۡتَنِبُونَ كَبَٰٓئِرَ ٱلۡإِثۡمِ وَٱلۡفَوَٰحِشَ إِلَّا ٱللَّمَمَۚ إِنَّ رَبَّكَ وَٰسِعُ ٱلۡمَغۡفِرَةِۚ هُوَ أَعۡلَمُ بِكُمۡ إِذۡ أَنشَأَكُم مِّنَ ٱلۡأَرۡضِ وَإِذۡ أَنتُمۡ أَجِنَّةٞ فِي بُطُونِ أُمَّهَٰتِكُمۡۖ فَلَا تُزَكُّوٓاْ أَنفُسَكُمۡۖ هُوَ أَعۡلَمُ بِمَنِ ٱتَّقَىٰٓ
Amene akuwapewa machimo akuluakulu ndi zadama, kupatula timachimo tating’onoting’ono (timene Allah amatikhululuka); ndithu Mbuye wako ndiwokhululuka kwakukulu. Iye akudziwa chikhalidwe chanu kuyambira pomwe adakulengani kuchokera m’nthaka ndi pamene inu mudali makanda m’mimba mwa amayi anu (mosinthasintha; mosiyanasiyana). Choncho musadzitame nokha kuyera mtima; Iye Ngodziwa kwambiri za yemwe akumuopa (Allah).
Ibisobanuro by'icyarabu:
أَفَرَءَيۡتَ ٱلَّذِي تَوَلَّىٰ
Kodi wamuona yemwe wadzipatula (pakusiya kutsatira choonadi)?
Ibisobanuro by'icyarabu:
وَأَعۡطَىٰ قَلِيلٗا وَأَكۡدَىٰٓ
Ndipo wapereka (chuma) chochepa nasiyanso kuperekako.
Ibisobanuro by'icyarabu:
أَعِندَهُۥ عِلۡمُ ٱلۡغَيۡبِ فَهُوَ يَرَىٰٓ
Kodi akudziwa zamseri, kotero kuti akuziwona (zomwe wadza nazo (Mtumiki {s.a.w) kuti sizoona)?
Ibisobanuro by'icyarabu:
أَمۡ لَمۡ يُنَبَّأۡ بِمَا فِي صُحُفِ مُوسَىٰ
Kapena sadauzidwe zomwe zidali m’mabuku a Mûsa.
Ibisobanuro by'icyarabu:
وَإِبۡرَٰهِيمَ ٱلَّذِي وَفَّىٰٓ
Ndi Ibrahim amene adakwaniritsa (lonjezo la Allah)?
Ibisobanuro by'icyarabu:
أَلَّا تَزِرُ وَازِرَةٞ وِزۡرَ أُخۡرَىٰ
Kuti mzimu wamachimo sungasenze machimo a mzimu wina.
Ibisobanuro by'icyarabu:
وَأَن لَّيۡسَ لِلۡإِنسَٰنِ إِلَّا مَا سَعَىٰ
Ndi kutinso munthu sakalipidwa koma zimene adachita.
Ibisobanuro by'icyarabu:
وَأَنَّ سَعۡيَهُۥ سَوۡفَ يُرَىٰ
Ndipo ndithu ntchito zake zidzaonekera.
Ibisobanuro by'icyarabu:
ثُمَّ يُجۡزَىٰهُ ٱلۡجَزَآءَ ٱلۡأَوۡفَىٰ
Kenako (munthu) adzalipidwa malipiro okwanira (pa ntchito zake zimene amachita).
Ibisobanuro by'icyarabu:
وَأَنَّ إِلَىٰ رَبِّكَ ٱلۡمُنتَهَىٰ
Ndipo ndithu kwa Mbuye wako yekha ndiwo malekezero (a chilichonse).
Ibisobanuro by'icyarabu:
وَأَنَّهُۥ هُوَ أَضۡحَكَ وَأَبۡكَىٰ
Ndithu Iye ndiAmene amapereka chisangalalo ndi zoliritsa.
Ibisobanuro by'icyarabu:
وَأَنَّهُۥ هُوَ أَمَاتَ وَأَحۡيَا
Ndipo Iye yekha ndi Amene amapereka imfa ndi moyo.
Ibisobanuro by'icyarabu:
وَأَنَّهُۥ خَلَقَ ٱلزَّوۡجَيۡنِ ٱلذَّكَرَ وَٱلۡأُنثَىٰ
Ndipo Iye ndiAmene adalenga mitundu iwiri: chachimuna ndi chachikazi, (anthu ndi zamoyo zina).
Ibisobanuro by'icyarabu:
مِن نُّطۡفَةٍ إِذَا تُمۡنَىٰ
Kuchokera m’mbewu ya moyo pamene imafwamphukira (m’chiberekero).
Ibisobanuro by'icyarabu:
وَأَنَّ عَلَيۡهِ ٱلنَّشۡأَةَ ٱلۡأُخۡرَىٰ
Ndipo ndithu ndi udindo Wake kuukitsa kwina (pambuyo pa imfa).
Ibisobanuro by'icyarabu:
وَأَنَّهُۥ هُوَ أَغۡنَىٰ وَأَقۡنَىٰ
Ndipo Iye ndiAmene amapatsa chokwanira ndipo ndi amene amapatsa chosunga.
Ibisobanuro by'icyarabu:
وَأَنَّهُۥ هُوَ رَبُّ ٱلشِّعۡرَىٰ
Ndipo ndithu Iye ndi Mbuye wa nyenyezi yotchedwa Shiira;
Ibisobanuro by'icyarabu:
وَأَنَّهُۥٓ أَهۡلَكَ عَادًا ٱلۡأُولَىٰ
Ndipo Iye ndi amene adaononga Âdi oyamba; (anthu a Mneneri Hûd).
Ibisobanuro by'icyarabu:
وَثَمُودَاْ فَمَآ أَبۡقَىٰ
Ndi Samudu; (anthu a Mneneri Swaleh;) choncho sadasiye (ndi mmodzi yemwe wa iwo).
Ibisobanuro by'icyarabu:
وَقَوۡمَ نُوحٖ مِّن قَبۡلُۖ إِنَّهُمۡ كَانُواْ هُمۡ أَظۡلَمَ وَأَطۡغَىٰ
Ndipo (adawaononganso) anthu a Nuh, kale (asadaononge Âdi ndi Samudu). Ndithu iwo adali osalungama ndi olumpha malire kwambiri (kuposa Âdi ndi Samudu).
Ibisobanuro by'icyarabu:
وَٱلۡمُؤۡتَفِكَةَ أَهۡوَىٰ
Ndi midzi yotembenuzidwa kumwamba kukhala pansi, pansi kukhala kumwamba, (ya anthu a Luti) adaigwetsa.
Ibisobanuro by'icyarabu:
فَغَشَّىٰهَا مَا غَشَّىٰ
Tero chidaivindikira (midziyo) chomwe chidaivindikira (chilango).
Ibisobanuro by'icyarabu:
فَبِأَيِّ ءَالَآءِ رَبِّكَ تَتَمَارَىٰ
Kodi ndimtendere uti (mumtendere) wa Mbuye wako umene ukuukaikira?
Ibisobanuro by'icyarabu:
هَٰذَا نَذِيرٞ مِّنَ ٱلنُّذُرِ ٱلۡأُولَىٰٓ
Uyu (Mtumiki) ndimchenjezi mwa achenjezi oyamba (amene adachenjezedwa nawo anthu a mibadwo yakale)
Ibisobanuro by'icyarabu:
أَزِفَتِ ٱلۡأٓزِفَةُ
Chayandikira choyandikira (Qiyâma).
Ibisobanuro by'icyarabu:
لَيۡسَ لَهَا مِن دُونِ ٱللَّهِ كَاشِفَةٌ
Palibe amene angachionetse koma Allah Yekha.
Ibisobanuro by'icyarabu:
أَفَمِنۡ هَٰذَا ٱلۡحَدِيثِ تَعۡجَبُونَ
Kodi mukuidabwa nkhaniyi (ya Qur’an moikana)?
Ibisobanuro by'icyarabu:
وَتَضۡحَكُونَ وَلَا تَبۡكُونَ
Mungoseka (mwachipongwe) ndipo simukulira (pamene mukuimva monga momwe akuchitira okhulupirira).
Ibisobanuro by'icyarabu:
وَأَنتُمۡ سَٰمِدُونَ
Ndipo mukunyozera?
Ibisobanuro by'icyarabu:
فَٱسۡجُدُواْۤ لِلَّهِۤ وَٱعۡبُدُواْ۩
Mlambireni ndi kumpembedza Allah (amene wavumbulutsa Qur’an kuti ikhale chiongoko cha anthu).
Ibisobanuro by'icyarabu:
 
Ibisobanuro by'amagambo Isura: Annajmi (Inyenyeri)
Urutonde rw'amasura numero y'urupapuro
 
Ibisobanuro bya qoran ntagatifu - Ibisobanuro mu rurimi rw''urushiishiyu - Ishakiro ry'ibisobanuro

Ibisobanuro bya qor'an ntagatifu mu rurimi rw'urushiishiyu, byasobanuwe na KHALID IBAHIIM BIITALA kopi ya 2020

Gufunga