แปล​ความหมาย​อัลกุรอาน​ - คำแปลภาษาชิเชวา * - สารบัญ​คำแปล


แปลความหมาย​ สูเราะฮ์: An-Najm   อายะฮ์:

An-Najm

وَٱلنَّجۡمِ إِذَا هَوَىٰ
Ndikulumbira nyenyezi pamene zikulowa.
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
مَا ضَلَّ صَاحِبُكُمۡ وَمَا غَوَىٰ
Sadasokere m’bale wanu (Mtumiki panjira ya choonadi) ndipo sadakhulupirire zonama.
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
وَمَا يَنطِقُ عَنِ ٱلۡهَوَىٰٓ
Ndipo sayankhula zofuna za mtima wake.
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
إِنۡ هُوَ إِلَّا وَحۡيٞ يُوحَىٰ
Iyoyi (Qur’an imene akuinena), sichina, koma ndichivumbulutso chovumbulutsidwa.
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
عَلَّمَهُۥ شَدِيدُ ٱلۡقُوَىٰ
Adamphunzitsa (chivumbulutsochi) (Jibril) wanyonga zambiri.
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
ذُو مِرَّةٖ فَٱسۡتَوَىٰ
Wanzeru zakuya; ndipo adakhazikika (m’maonekedwe ake).
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
وَهُوَ بِٱلۡأُفُقِ ٱلۡأَعۡلَىٰ
Ali m’chizimezime kumwamba.
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
ثُمَّ دَنَا فَتَدَلَّىٰ
Kenako (Jibril) adamuyandikira (Mtumiki {s.a.w}) ndikuonjezera kumuyandikira.
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
فَكَانَ قَابَ قَوۡسَيۡنِ أَوۡ أَدۡنَىٰ
(Kumuyandikira kwake) kudali ngati (mpata wa) nsonga ziwiri za uta, kapena kuyandikira kuposa apo.
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
فَأَوۡحَىٰٓ إِلَىٰ عَبۡدِهِۦ مَآ أَوۡحَىٰ
(Choncho Jibril) adavumbulutsira kapolo wake (wa Allah) zimene adazivumbulutsa.
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
مَا كَذَبَ ٱلۡفُؤَادُ مَا رَأَىٰٓ
Sudaname mtima (wa Mtumiki) pazimene adaziona.
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
أَفَتُمَٰرُونَهُۥ عَلَىٰ مَا يَرَىٰ
Kodi mukutsutsana naye (Mthenga wa Allah) pazimene adaziona?
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
وَلَقَدۡ رَءَاهُ نَزۡلَةً أُخۡرَىٰ
Ndipo ndithu adamuona (Jibril) m’kuona kachiwiri mkaonekedwe kake.
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
عِندَ سِدۡرَةِ ٱلۡمُنتَهَىٰ
Pa ‘Sidratil Muntaha’ (mtengo wamasawu pothera zinthu zonse).
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
عِندَهَا جَنَّةُ ٱلۡمَأۡوَىٰٓ
Pafupi pake pali Janatu Ma’awa, (munda wokhalamo).
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
إِذۡ يَغۡشَى ٱلسِّدۡرَةَ مَا يَغۡشَىٰ
Pomwe chophimba chidaphimba msawuwo.
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
مَا زَاغَ ٱلۡبَصَرُ وَمَا طَغَىٰ
Maso ake sadaphonye kapena kupyola malire (oikidwa).
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
لَقَدۡ رَأَىٰ مِنۡ ءَايَٰتِ رَبِّهِ ٱلۡكُبۡرَىٰٓ
Ndithu (Mneneri Muhammad {s.a.w}) adaona zina mwa zizindikiro zikuluzikulu za Mbuye wake (zosonyeza mphamvu Zake)
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
أَفَرَءَيۡتُمُ ٱللَّٰتَ وَٱلۡعُزَّىٰ
Kodi mwamuona Laat ndi Uzza?
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
وَمَنَوٰةَ ٱلثَّالِثَةَ ٱلۡأُخۡرَىٰٓ
Ndi Manata; (fano lanu) lina lachitatu, (kuti iwowa ndi milungu)?
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
أَلَكُمُ ٱلذَّكَرُ وَلَهُ ٱلۡأُنثَىٰ
Kodi mwadzisankhira ana aamuna (kukhala anu), ndi aakazi nkukhala a Iye (Allah)?
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
تِلۡكَ إِذٗا قِسۡمَةٞ ضِيزَىٰٓ
Choncho kugawa kumeneko nkopanda chilungamo (pompatsa Allah zimene mumazida).
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
إِنۡ هِيَ إِلَّآ أَسۡمَآءٞ سَمَّيۡتُمُوهَآ أَنتُمۡ وَءَابَآؤُكُم مَّآ أَنزَلَ ٱللَّهُ بِهَا مِن سُلۡطَٰنٍۚ إِن يَتَّبِعُونَ إِلَّا ٱلظَّنَّ وَمَا تَهۡوَى ٱلۡأَنفُسُۖ وَلَقَدۡ جَآءَهُم مِّن رَّبِّهِمُ ٱلۡهُدَىٰٓ
Sali (mafanowo) chilichonse koma ndi maina basi omwe mudawatcha inu ndi makolo anu, (molingana ndi zilakolako zanu zachabe); Allah sadatsitse umboni pazimenezo (wotsimikiza pamawu anuwo). Sakutsatira koma zoganizira basi ndi zimene ikufuna mitima (yawo yopotoka). Ndithu chidawadzera chiongoko kuchokera kwa Mbuye wawo (chomwe m’kati mwake mudali kuongoka kwawo akadachitsatira).
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
أَمۡ لِلۡإِنسَٰنِ مَا تَمَنَّىٰ
Kodi munthu akuganiza kuti adzapeza chilichonse chimene akuchilakalaka?
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
فَلِلَّهِ ٱلۡأٓخِرَةُ وَٱلۡأُولَىٰ
Moyo wa tsiku lachimaliziro ndi wadziko lapansi ngwa Allah Yekha.
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
۞ وَكَم مِّن مَّلَكٖ فِي ٱلسَّمَٰوَٰتِ لَا تُغۡنِي شَفَٰعَتُهُمۡ شَيۡـًٔا إِلَّا مِنۢ بَعۡدِ أَن يَأۡذَنَ ٱللَّهُ لِمَن يَشَآءُ وَيَرۡضَىٰٓ
Ndipo kuli angelo ambiri kumwamba omwe kuchondelera kwawo sikungathandize china chilichonse pokhapokha Allah ataloleza kwa amene wamfuna ndi kumuyanja.
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
إِنَّ ٱلَّذِينَ لَا يُؤۡمِنُونَ بِٱلۡأٓخِرَةِ لَيُسَمُّونَ ٱلۡمَلَٰٓئِكَةَ تَسۡمِيَةَ ٱلۡأُنثَىٰ
Ndithu amene sakhulupirira za (Moyo wa) tsiku lachimaliziro, amawatcha angelo kuti ndiakazi.
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
وَمَا لَهُم بِهِۦ مِنۡ عِلۡمٍۖ إِن يَتَّبِعُونَ إِلَّا ٱلظَّنَّۖ وَإِنَّ ٱلظَّنَّ لَا يُغۡنِي مِنَ ٱلۡحَقِّ شَيۡـٔٗا
Ndipo alibe kudziwa kulikonse pa zimenezo sakutsata china koma maganizo. Ndipo ndithu kuganizira sikuthandiza chilichonse pofuna kupeza choonadi.
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
فَأَعۡرِضۡ عَن مَّن تَوَلَّىٰ عَن ذِكۡرِنَا وَلَمۡ يُرِدۡ إِلَّا ٱلۡحَيَوٰةَ ٱلدُّنۡيَا
Choncho apewe (osakhulupirirawa) amene anyozera chikumbutso Chathu (Qur’an); ndipo palibe chimene akufuna koma moyo wa padziko lapansi basi.
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
ذَٰلِكَ مَبۡلَغُهُم مِّنَ ٱلۡعِلۡمِۚ إِنَّ رَبَّكَ هُوَ أَعۡلَمُ بِمَن ضَلَّ عَن سَبِيلِهِۦ وَهُوَ أَعۡلَمُ بِمَنِ ٱهۡتَدَىٰ
Zimenezo ndiwo mapeto a kudziwa kwawo. Ndithu Mbuye wako Ngodziwa kwambiri za amene akusokera njira Yake ndiponso akudziwa bwino za yemwe wawongoka.
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
وَلِلَّهِ مَا فِي ٱلسَّمَٰوَٰتِ وَمَا فِي ٱلۡأَرۡضِ لِيَجۡزِيَ ٱلَّذِينَ أَسَٰٓـُٔواْ بِمَا عَمِلُواْ وَيَجۡزِيَ ٱلَّذِينَ أَحۡسَنُواْ بِٱلۡحُسۡنَى
Ndipo zonse za kumwamba ndi zadziko lapansi nza Allah Yekha, (pozilenga ndi kuziyang’anira), kuti adzawalipire amene adaipitsa pa zimene adachita ndi kutinso adzawalipire zabwino amene adachita zabwino.
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
ٱلَّذِينَ يَجۡتَنِبُونَ كَبَٰٓئِرَ ٱلۡإِثۡمِ وَٱلۡفَوَٰحِشَ إِلَّا ٱللَّمَمَۚ إِنَّ رَبَّكَ وَٰسِعُ ٱلۡمَغۡفِرَةِۚ هُوَ أَعۡلَمُ بِكُمۡ إِذۡ أَنشَأَكُم مِّنَ ٱلۡأَرۡضِ وَإِذۡ أَنتُمۡ أَجِنَّةٞ فِي بُطُونِ أُمَّهَٰتِكُمۡۖ فَلَا تُزَكُّوٓاْ أَنفُسَكُمۡۖ هُوَ أَعۡلَمُ بِمَنِ ٱتَّقَىٰٓ
Amene akuwapewa machimo akuluakulu ndi zadama, kupatula timachimo tating’onoting’ono (timene Allah amatikhululuka); ndithu Mbuye wako ndiwokhululuka kwakukulu. Iye akudziwa chikhalidwe chanu kuyambira pomwe adakulengani kuchokera m’nthaka ndi pamene inu mudali makanda m’mimba mwa amayi anu (mosinthasintha; mosiyanasiyana). Choncho musadzitame nokha kuyera mtima; Iye Ngodziwa kwambiri za yemwe akumuopa (Allah).
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
أَفَرَءَيۡتَ ٱلَّذِي تَوَلَّىٰ
Kodi wamuona yemwe wadzipatula (pakusiya kutsatira choonadi)?
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
وَأَعۡطَىٰ قَلِيلٗا وَأَكۡدَىٰٓ
Ndipo wapereka (chuma) chochepa nasiyanso kuperekako.
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
أَعِندَهُۥ عِلۡمُ ٱلۡغَيۡبِ فَهُوَ يَرَىٰٓ
Kodi akudziwa zamseri, kotero kuti akuziwona (zomwe wadza nazo (Mtumiki {s.a.w) kuti sizoona)?
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
أَمۡ لَمۡ يُنَبَّأۡ بِمَا فِي صُحُفِ مُوسَىٰ
Kapena sadauzidwe zomwe zidali m’mabuku a Mûsa.
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
وَإِبۡرَٰهِيمَ ٱلَّذِي وَفَّىٰٓ
Ndi Ibrahim amene adakwaniritsa (lonjezo la Allah)?
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
أَلَّا تَزِرُ وَازِرَةٞ وِزۡرَ أُخۡرَىٰ
Kuti mzimu wamachimo sungasenze machimo a mzimu wina.
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
وَأَن لَّيۡسَ لِلۡإِنسَٰنِ إِلَّا مَا سَعَىٰ
Ndi kutinso munthu sakalipidwa koma zimene adachita.
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
وَأَنَّ سَعۡيَهُۥ سَوۡفَ يُرَىٰ
Ndipo ndithu ntchito zake zidzaonekera.
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
ثُمَّ يُجۡزَىٰهُ ٱلۡجَزَآءَ ٱلۡأَوۡفَىٰ
Kenako (munthu) adzalipidwa malipiro okwanira (pa ntchito zake zimene amachita).
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
وَأَنَّ إِلَىٰ رَبِّكَ ٱلۡمُنتَهَىٰ
Ndipo ndithu kwa Mbuye wako yekha ndiwo malekezero (a chilichonse).
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
وَأَنَّهُۥ هُوَ أَضۡحَكَ وَأَبۡكَىٰ
Ndithu Iye ndiAmene amapereka chisangalalo ndi zoliritsa.
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
وَأَنَّهُۥ هُوَ أَمَاتَ وَأَحۡيَا
Ndipo Iye yekha ndi Amene amapereka imfa ndi moyo.
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
وَأَنَّهُۥ خَلَقَ ٱلزَّوۡجَيۡنِ ٱلذَّكَرَ وَٱلۡأُنثَىٰ
Ndipo Iye ndiAmene adalenga mitundu iwiri: chachimuna ndi chachikazi, (anthu ndi zamoyo zina).
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
مِن نُّطۡفَةٍ إِذَا تُمۡنَىٰ
Kuchokera m’mbewu ya moyo pamene imafwamphukira (m’chiberekero).
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
وَأَنَّ عَلَيۡهِ ٱلنَّشۡأَةَ ٱلۡأُخۡرَىٰ
Ndipo ndithu ndi udindo Wake kuukitsa kwina (pambuyo pa imfa).
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
وَأَنَّهُۥ هُوَ أَغۡنَىٰ وَأَقۡنَىٰ
Ndipo Iye ndiAmene amapatsa chokwanira ndipo ndi amene amapatsa chosunga.
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
وَأَنَّهُۥ هُوَ رَبُّ ٱلشِّعۡرَىٰ
Ndipo ndithu Iye ndi Mbuye wa nyenyezi yotchedwa Shiira;
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
وَأَنَّهُۥٓ أَهۡلَكَ عَادًا ٱلۡأُولَىٰ
Ndipo Iye ndi amene adaononga Âdi oyamba; (anthu a Mneneri Hûd).
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
وَثَمُودَاْ فَمَآ أَبۡقَىٰ
Ndi Samudu; (anthu a Mneneri Swaleh;) choncho sadasiye (ndi mmodzi yemwe wa iwo).
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
وَقَوۡمَ نُوحٖ مِّن قَبۡلُۖ إِنَّهُمۡ كَانُواْ هُمۡ أَظۡلَمَ وَأَطۡغَىٰ
Ndipo (adawaononganso) anthu a Nuh, kale (asadaononge Âdi ndi Samudu). Ndithu iwo adali osalungama ndi olumpha malire kwambiri (kuposa Âdi ndi Samudu).
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
وَٱلۡمُؤۡتَفِكَةَ أَهۡوَىٰ
Ndi midzi yotembenuzidwa kumwamba kukhala pansi, pansi kukhala kumwamba, (ya anthu a Luti) adaigwetsa.
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
فَغَشَّىٰهَا مَا غَشَّىٰ
Tero chidaivindikira (midziyo) chomwe chidaivindikira (chilango).
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
فَبِأَيِّ ءَالَآءِ رَبِّكَ تَتَمَارَىٰ
Kodi ndimtendere uti (mumtendere) wa Mbuye wako umene ukuukaikira?
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
هَٰذَا نَذِيرٞ مِّنَ ٱلنُّذُرِ ٱلۡأُولَىٰٓ
Uyu (Mtumiki) ndimchenjezi mwa achenjezi oyamba (amene adachenjezedwa nawo anthu a mibadwo yakale)
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
أَزِفَتِ ٱلۡأٓزِفَةُ
Chayandikira choyandikira (Qiyâma).
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
لَيۡسَ لَهَا مِن دُونِ ٱللَّهِ كَاشِفَةٌ
Palibe amene angachionetse koma Allah Yekha.
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
أَفَمِنۡ هَٰذَا ٱلۡحَدِيثِ تَعۡجَبُونَ
Kodi mukuidabwa nkhaniyi (ya Qur’an moikana)?
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
وَتَضۡحَكُونَ وَلَا تَبۡكُونَ
Mungoseka (mwachipongwe) ndipo simukulira (pamene mukuimva monga momwe akuchitira okhulupirira).
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
وَأَنتُمۡ سَٰمِدُونَ
Ndipo mukunyozera?
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
فَٱسۡجُدُواْۤ لِلَّهِۤ وَٱعۡبُدُواْ۩
Mlambireni ndi kumpembedza Allah (amene wavumbulutsa Qur’an kuti ikhale chiongoko cha anthu).
ตัฟสีรต่างๆ​ ภาษาอาหรับ:
 
แปลความหมาย​ สูเราะฮ์: An-Najm
สารบัญสูเราะฮ์ หมายเลข​หน้า​
 
แปล​ความหมาย​อัลกุรอาน​ - คำแปลภาษาชิเชวา - สารบัญ​คำแปล

การแปลความหมายอัลกุรอานเป็นภาษาชิเชวา แปลโดย คอลิด อิบรอฮีม เบตาลา (ed. 2020)

ปิด