Qurani Kərimin mənaca tərcüməsi - Şişyo dilinə tərcümə * - Tərcumənin mündəricatı


Mənaların tərcüməsi Surə: ən-Nəbə   Ayə:

ən-Nəbə

عَمَّ يَتَسَآءَلُونَ
۞ Kodi akufunsana zachiyani?
Ərəbcə təfsirlər:
عَنِ ٱلنَّبَإِ ٱلۡعَظِيمِ
Za nkhani yayikulu ija.
Ərəbcə təfsirlər:
ٱلَّذِي هُمۡ فِيهِ مُخۡتَلِفُونَ
Imene iwo akusiyana (maganizo).[372]
[372] Nkhani yaikulu imene akafiri (anthu osakhulupilira Allah) adali kufunsana wina ndi mnzake ndi nkhani yakuuka tsiku la Qiyâma ndi uneneri wa Mtumiki Muhammad. Amafunsana kuti, “Kodi nzoona tidzauka m’manda, nanga nzoona kuti Muhammad ndi Mneneri?” Adali kufunsananso kuti, “Kodi zakuti Allah ndi Mmodzi ndi zoona?”
Ərəbcə təfsirlər:
كَلَّا سَيَعۡلَمُونَ
Aleke (zimenezo) adzadziwa posachedwapa.[373]
[373] Kuyankhula koti: “Kallaa” kwanenedwa kwambiri m’Qur’an. Tanthauzo lake nthawi zina ndikuletsa, nthawi zina ndikutsimikiza. Choncho mawuwa amatanthauzidwa malinga ndi momwe chiganizocho chilili.
Ərəbcə təfsirlər:
ثُمَّ كَلَّا سَيَعۡلَمُونَ
Ayi, ndithu aleke (zimenezo); posachedwapa adzadziwa zoona zake (pamene chilango chidzawatsikira).[374]
[374] Allah, apa, akuwauza kuti asiye kuganizira zinthu zopanda pake. Kodi sadadziwebe mpaka pano kuti Muhammad ndi Mneneri wa Allah, ndikuti Allah ndi Mmodzi yekha? Ndikutinso kuli tsiku lachimaliziro; pamene munthu aliyense adzalipidwa pa zimene adachita? Basi tsiku lachimaliziro likadzawafikira adzadziwa kuti zimene adali kuwauza Mneneri nzoona.
Ərəbcə təfsirlər:
أَلَمۡ نَجۡعَلِ ٱلۡأَرۡضَ مِهَٰدٗا
Kodi sitidachite nthaka kukhala ngati choyala?[375]
[375] Kuyambira Ayah iyi, kudzafika Ayah 16, Allah akusonyeza anthu Ake madalitso ambiri omwe wawadalitsa nawo kuti azindikire kuti Mwini kupereka madalitso amenewa m’dziko sangawasiye anthu Ake m’kusokera popanda kuwatumizira munthu wowaongolera ku njira yabwino, ndikuwadziwitsa zamtendere wapadziko ndi tsiku lachimaliziro. Ndikuti Allah amene adapanga zonsezi palibe chimene angachilephere. Ndipo tanthauzo la choyala, apa, ndi pamalo poti nkutheka munthu kuchita chimene akufuna pa moyo wake. Tanthauzo lake sikuti dothi lakhala ngati mkeka wa pabedi ayi.
Ərəbcə təfsirlər:
وَٱلۡجِبَالَ أَوۡتَادٗا
Ndi mapiri ngati zichiri (zolimbitsa nthaka)?
Ərəbcə təfsirlər:
وَخَلَقۡنَٰكُمۡ أَزۡوَٰجٗا
Ndipo takulengani mitundu iwiri (amuna ndi akazi).
Ərəbcə təfsirlər:
وَجَعَلۡنَا نَوۡمَكُمۡ سُبَاتٗا
Ndipo tidachita tulo tanu kukhala mpumulo (ku mavuto a ntchito).
Ərəbcə təfsirlər:
وَجَعَلۡنَا ٱلَّيۡلَ لِبَاسٗا
Ndipo taupanga usiku kukhala ngati chovala (pokuvindikirani ndi mdima wake).
Ərəbcə təfsirlər:
وَجَعَلۡنَا ٱلنَّهَارَ مَعَاشٗا
Ndipo tapanga masana kukhala nthawi yopezera zofunika pa moyo;
Ərəbcə təfsirlər:
وَبَنَيۡنَا فَوۡقَكُمۡ سَبۡعٗا شِدَادٗا
Ndipo tamanga pamwamba panu thambo zisanu ndi ziwiri zolimba;
Ərəbcə təfsirlər:
وَجَعَلۡنَا سِرَاجٗا وَهَّاجٗا
Ndipo tidapanga nyali yowala ndi yotentha kwambiri (dzuwa);
Ərəbcə təfsirlər:
وَأَنزَلۡنَا مِنَ ٱلۡمُعۡصِرَٰتِ مَآءٗ ثَجَّاجٗا
Ndipo tawatsitsa madzi otsika mwamphamvu kuchokera ku mitambo, ya mvula;
Ərəbcə təfsirlər:
لِّنُخۡرِجَ بِهِۦ حَبّٗا وَنَبَاتٗا
Kuti titulutse ndi madziwo mbewu ndi m’mera, (chomwe ndi chakudya cha anthu ndi nyama).
Ərəbcə təfsirlər:
وَجَنَّٰتٍ أَلۡفَافًا
Ndi minda yothothana nthambi za mitengo.
Ərəbcə təfsirlər:
إِنَّ يَوۡمَ ٱلۡفَصۡلِ كَانَ مِيقَٰتٗا
Ndithu tsiku la chiweruziro ndinthawi imene idakhazikitsidwa kale.
Ərəbcə təfsirlər:
يَوۡمَ يُنفَخُ فِي ٱلصُّورِ فَتَأۡتُونَ أَفۡوَاجٗا
Tsiku limene lipenga (lakuuka) lidzaimbidwa ndipo inu mudzabwera (kubwalo losonkhanirana) muli magulumagulu.
Ərəbcə təfsirlər:
وَفُتِحَتِ ٱلسَّمَآءُ فَكَانَتۡ أَبۡوَٰبٗا
Ndipo thambo lidzatsegulidwa (mbali zonse): choncho lidzakhala makomomakomo.
Ərəbcə təfsirlər:
وَسُيِّرَتِ ٱلۡجِبَالُ فَكَانَتۡ سَرَابًا
Ndipo mapiri adzachotsedwa m’malo mwake, adzakhala ngati zideruderu.[376]
[376] Apa, ndikuti zimene munthu amaziona patsogolo pake nkumaziganizira ngati madzi pomwe sali madzi. Choncho pa tsiku limenelo mapiri adzaoneka ngati akhazikika monga m’mene adalili pomwe sichoncho, adzakhala ngati thonje louluka ndi mphepo.
Ərəbcə təfsirlər:
إِنَّ جَهَنَّمَ كَانَتۡ مِرۡصَادٗا
Ndithu moto wa Jahannam ukuwadikilira (oipa).
Ərəbcə təfsirlər:
لِّلطَّٰغِينَ مَـَٔابٗا
Mbuto ya opyola malire.[377]
[377] Jahannam ndi dzina lamoto wodziwika wa tsiku lachimaliziro. Apa Allah akutidziwitsa kuti Jahannam ndi malo amene akudikira akafiri kuti m’menemo akalipidwe malipiro awo chifukwa chokanira aneneri pambuyo powasonyeza zizindikiro zoti iwo ndi aneneri a Allah. Ndiponso kumulakwira Allah pochita zimene adaletsa monga; kukana umodzi wa Allah, kukana utumiki wa Mahammad (s.a.w) ndi kukana uthenga wa Qur’an. Komanso kugwa mmachimo osiyanasiyana.
Ərəbcə təfsirlər:
لَّٰبِثِينَ فِيهَآ أَحۡقَابٗا
Adzakhala m’menemo muyaya.
Ərəbcə təfsirlər:
لَّا يَذُوقُونَ فِيهَا بَرۡدٗا وَلَا شَرَابًا
Sadzalawa m’menemo kuzizira (kowachotsera kutentha), kapena chakumwa (chowachotsera ludzu lawo);
Ərəbcə təfsirlər:
إِلَّا حَمِيمٗا وَغَسَّاقٗا
Kupatula madzi otentha kwambiri ndi mafinya (otuluka mmatupi a anthu a ku Moto);
Ərəbcə təfsirlər:
جَزَآءٗ وِفَاقًا
Kukhala malipiro olingana ndi ntchito zawo.
Ərəbcə təfsirlər:
إِنَّهُمۡ كَانُواْ لَا يَرۡجُونَ حِسَابٗا
Ndithu iwo sadali kuyembekezera chiwerengero (cha Allah);
Ərəbcə təfsirlər:
وَكَذَّبُواْ بِـَٔايَٰتِنَا كِذَّابٗا
Adatsutsa zizindikiro Zathu (zosonyeza kuuka kwa akufa) ndi mtsutso waukulu.
Ərəbcə təfsirlər:
وَكُلَّ شَيۡءٍ أَحۡصَيۡنَٰهُ كِتَٰبٗا
Ndipo chinthu chilichonse tachisunga mochilemba.
Ərəbcə təfsirlər:
فَذُوقُواْ فَلَن نَّزِيدَكُمۡ إِلَّا عَذَابًا
Basi, lawani (lero chilango Changa); sitikuonjezerani chinthu china koma chilango pamwamba pa chilango.
Ərəbcə təfsirlər:
إِنَّ لِلۡمُتَّقِينَ مَفَازًا
Ndithu anthu oopa Allah adzakhala ndi malo wopambana.
Ərəbcə təfsirlər:
حَدَآئِقَ وَأَعۡنَٰبٗا
Minda ndi zipatso za mphesa.
Ərəbcə təfsirlər:
وَكَوَاعِبَ أَتۡرَابٗا
Ndi mabuthu (anamwali) ofanana misinkhu.
Ərəbcə təfsirlər:
وَكَأۡسٗا دِهَاقٗا
Ndi zipanda zodzaza ndi zakumwa.
Ərəbcə təfsirlər:
لَّا يَسۡمَعُونَ فِيهَا لَغۡوٗا وَلَا كِذَّٰبٗا
Sakamva m’menemo mawu opanda pake kapena bodza.
Ərəbcə təfsirlər:
جَزَآءٗ مِّن رَّبِّكَ عَطَآءً حِسَابٗا
Amenewa ndi malipiro ochokera kwa Mbuye wako zopereka zokwanira.[378]
[378] Chipembedzo cha Chisilamu chikuphunzitsa kuti pali zisangalalo ziwiri: Chisangalalo cha mzimu ndi chisangalalo cha thupi. Tsono chisangalalo cha mzimu ndiko kuyanjana kochokera kwa Allah kumene anthu Ake abwino adzakupeza. Chisangalalo cha thupi ndi monga m’mene afotokozera mu Ayah iyi ndi msura zina. Zokondweretsa monga minda, akazi okongola, mowa (osaledzeretsa) ndiponso sikudzakhala kumva chilichonse chokhumudwitsa.
Taonani, zoledzeretsa ndi zoletsedwa padziko lino lapansi chifukwa cha zoipa zake. Koma mowa wa patsiku la Qiyâma udzakhala wopanda zoipa.
Ərəbcə təfsirlər:
رَّبِّ ٱلسَّمَٰوَٰتِ وَٱلۡأَرۡضِ وَمَا بَيۡنَهُمَا ٱلرَّحۡمَٰنِۖ لَا يَمۡلِكُونَ مِنۡهُ خِطَابٗا
Mbuye wa kumwamba ndi pansi ndi zimene zili pakati pake; Wachifundo chambiri. Palibe amene adzakhala ndi mphamvu yolankhulana naye (pa tsiku limenero);
Ərəbcə təfsirlər:
يَوۡمَ يَقُومُ ٱلرُّوحُ وَٱلۡمَلَٰٓئِكَةُ صَفّٗاۖ لَّا يَتَكَلَّمُونَ إِلَّا مَنۡ أَذِنَ لَهُ ٱلرَّحۡمَٰنُ وَقَالَ صَوَابٗا
Tsiku limene adzaima Jibril ndi angelo pa mzere (ali odzichepetsa); sadzayankhula aliyense mwa iwo kupatula yekhayo amene adzaloledwa ndi (Allah) Wachifundo chambiri (kuyankhula) ndipo adzanena zolondola.
Ərəbcə təfsirlər:
ذَٰلِكَ ٱلۡيَوۡمُ ٱلۡحَقُّۖ فَمَن شَآءَ ٱتَّخَذَ إِلَىٰ رَبِّهِۦ مَـَٔابًا
Limenelo ndi tsiku loona, (lopanda chikaiko); choncho amene akufuna adzipezere malo (njira yonkera) kwa Mbuye wake. (Pomugonjera Iye pa moyo uno wadziko lapansi).
Ərəbcə təfsirlər:
إِنَّآ أَنذَرۡنَٰكُمۡ عَذَابٗا قَرِيبٗا يَوۡمَ يَنظُرُ ٱلۡمَرۡءُ مَا قَدَّمَتۡ يَدَاهُ وَيَقُولُ ٱلۡكَافِرُ يَٰلَيۡتَنِي كُنتُ تُرَٰبَۢا
Ndithu tikukuchenjezani zachilango chomwe chili pafupi kudza; tsiku limene munthu adzayang’ana zimene adatsogoza manja ake, ndipo wosakhulupirira adzanena: Kalanga ine! Ndikadakhala dothi, (kuti ndisalangidwe chilango chikundiyembekezachi).
Ərəbcə təfsirlər:
 
Mənaların tərcüməsi Surə: ən-Nəbə
Surələrin mündəricatı Səhifənin rəqəmi
 
Qurani Kərimin mənaca tərcüməsi - Şişyo dilinə tərcümə - Tərcumənin mündəricatı

Qurani Kərimin şişyo dilinə mənaca tərcüməsi. Tərcüməçi:

Bağlamaq