ការបកប្រែអត្ថន័យគួរអាន - ការបកប្រែជាភាសាឆេវ៉ា * - សន្ទស្សន៍នៃការបកប្រែ


ការបកប្រែអត្ថន័យ ជំពូក​: សូរ៉ោះអាន់ណាហ្ពាក   អាយ៉ាត់:

សូរ៉ោះអាន់ណាហ្ពាក

عَمَّ يَتَسَآءَلُونَ
۞ Kodi akufunsana zachiyani?
តាហ្វសៀរជាភាសា​អារ៉ាប់ជាច្រេីន:
عَنِ ٱلنَّبَإِ ٱلۡعَظِيمِ
Za nkhani yayikulu ija.
តាហ្វសៀរជាភាសា​អារ៉ាប់ជាច្រេីន:
ٱلَّذِي هُمۡ فِيهِ مُخۡتَلِفُونَ
Imene iwo akusiyana (maganizo).[372]
[372] Nkhani yaikulu imene akafiri (anthu osakhulupilira Allah) adali kufunsana wina ndi mnzake ndi nkhani yakuuka tsiku la Qiyâma ndi uneneri wa Mtumiki Muhammad. Amafunsana kuti, “Kodi nzoona tidzauka m’manda, nanga nzoona kuti Muhammad ndi Mneneri?” Adali kufunsananso kuti, “Kodi zakuti Allah ndi Mmodzi ndi zoona?”
តាហ្វសៀរជាភាសា​អារ៉ាប់ជាច្រេីន:
كَلَّا سَيَعۡلَمُونَ
Aleke (zimenezo) adzadziwa posachedwapa.[373]
[373] Kuyankhula koti: “Kallaa” kwanenedwa kwambiri m’Qur’an. Tanthauzo lake nthawi zina ndikuletsa, nthawi zina ndikutsimikiza. Choncho mawuwa amatanthauzidwa malinga ndi momwe chiganizocho chilili.
តាហ្វសៀរជាភាសា​អារ៉ាប់ជាច្រេីន:
ثُمَّ كَلَّا سَيَعۡلَمُونَ
Ayi, ndithu aleke (zimenezo); posachedwapa adzadziwa zoona zake (pamene chilango chidzawatsikira).[374]
[374] Allah, apa, akuwauza kuti asiye kuganizira zinthu zopanda pake. Kodi sadadziwebe mpaka pano kuti Muhammad ndi Mneneri wa Allah, ndikuti Allah ndi Mmodzi yekha? Ndikutinso kuli tsiku lachimaliziro; pamene munthu aliyense adzalipidwa pa zimene adachita? Basi tsiku lachimaliziro likadzawafikira adzadziwa kuti zimene adali kuwauza Mneneri nzoona.
តាហ្វសៀរជាភាសា​អារ៉ាប់ជាច្រេីន:
أَلَمۡ نَجۡعَلِ ٱلۡأَرۡضَ مِهَٰدٗا
Kodi sitidachite nthaka kukhala ngati choyala?[375]
[375] Kuyambira Ayah iyi, kudzafika Ayah 16, Allah akusonyeza anthu Ake madalitso ambiri omwe wawadalitsa nawo kuti azindikire kuti Mwini kupereka madalitso amenewa m’dziko sangawasiye anthu Ake m’kusokera popanda kuwatumizira munthu wowaongolera ku njira yabwino, ndikuwadziwitsa zamtendere wapadziko ndi tsiku lachimaliziro. Ndikuti Allah amene adapanga zonsezi palibe chimene angachilephere. Ndipo tanthauzo la choyala, apa, ndi pamalo poti nkutheka munthu kuchita chimene akufuna pa moyo wake. Tanthauzo lake sikuti dothi lakhala ngati mkeka wa pabedi ayi.
តាហ្វសៀរជាភាសា​អារ៉ាប់ជាច្រេីន:
وَٱلۡجِبَالَ أَوۡتَادٗا
Ndi mapiri ngati zichiri (zolimbitsa nthaka)?
តាហ្វសៀរជាភាសា​អារ៉ាប់ជាច្រេីន:
وَخَلَقۡنَٰكُمۡ أَزۡوَٰجٗا
Ndipo takulengani mitundu iwiri (amuna ndi akazi).
តាហ្វសៀរជាភាសា​អារ៉ាប់ជាច្រេីន:
وَجَعَلۡنَا نَوۡمَكُمۡ سُبَاتٗا
Ndipo tidachita tulo tanu kukhala mpumulo (ku mavuto a ntchito).
តាហ្វសៀរជាភាសា​អារ៉ាប់ជាច្រេីន:
وَجَعَلۡنَا ٱلَّيۡلَ لِبَاسٗا
Ndipo taupanga usiku kukhala ngati chovala (pokuvindikirani ndi mdima wake).
តាហ្វសៀរជាភាសា​អារ៉ាប់ជាច្រេីន:
وَجَعَلۡنَا ٱلنَّهَارَ مَعَاشٗا
Ndipo tapanga masana kukhala nthawi yopezera zofunika pa moyo;
តាហ្វសៀរជាភាសា​អារ៉ាប់ជាច្រេីន:
وَبَنَيۡنَا فَوۡقَكُمۡ سَبۡعٗا شِدَادٗا
Ndipo tamanga pamwamba panu thambo zisanu ndi ziwiri zolimba;
តាហ្វសៀរជាភាសា​អារ៉ាប់ជាច្រេីន:
وَجَعَلۡنَا سِرَاجٗا وَهَّاجٗا
Ndipo tidapanga nyali yowala ndi yotentha kwambiri (dzuwa);
តាហ្វសៀរជាភាសា​អារ៉ាប់ជាច្រេីន:
وَأَنزَلۡنَا مِنَ ٱلۡمُعۡصِرَٰتِ مَآءٗ ثَجَّاجٗا
Ndipo tawatsitsa madzi otsika mwamphamvu kuchokera ku mitambo, ya mvula;
តាហ្វសៀរជាភាសា​អារ៉ាប់ជាច្រេីន:
لِّنُخۡرِجَ بِهِۦ حَبّٗا وَنَبَاتٗا
Kuti titulutse ndi madziwo mbewu ndi m’mera, (chomwe ndi chakudya cha anthu ndi nyama).
តាហ្វសៀរជាភាសា​អារ៉ាប់ជាច្រេីន:
وَجَنَّٰتٍ أَلۡفَافًا
Ndi minda yothothana nthambi za mitengo.
តាហ្វសៀរជាភាសា​អារ៉ាប់ជាច្រេីន:
إِنَّ يَوۡمَ ٱلۡفَصۡلِ كَانَ مِيقَٰتٗا
Ndithu tsiku la chiweruziro ndinthawi imene idakhazikitsidwa kale.
តាហ្វសៀរជាភាសា​អារ៉ាប់ជាច្រេីន:
يَوۡمَ يُنفَخُ فِي ٱلصُّورِ فَتَأۡتُونَ أَفۡوَاجٗا
Tsiku limene lipenga (lakuuka) lidzaimbidwa ndipo inu mudzabwera (kubwalo losonkhanirana) muli magulumagulu.
តាហ្វសៀរជាភាសា​អារ៉ាប់ជាច្រេីន:
وَفُتِحَتِ ٱلسَّمَآءُ فَكَانَتۡ أَبۡوَٰبٗا
Ndipo thambo lidzatsegulidwa (mbali zonse): choncho lidzakhala makomomakomo.
តាហ្វសៀរជាភាសា​អារ៉ាប់ជាច្រេីន:
وَسُيِّرَتِ ٱلۡجِبَالُ فَكَانَتۡ سَرَابًا
Ndipo mapiri adzachotsedwa m’malo mwake, adzakhala ngati zideruderu.[376]
[376] Apa, ndikuti zimene munthu amaziona patsogolo pake nkumaziganizira ngati madzi pomwe sali madzi. Choncho pa tsiku limenelo mapiri adzaoneka ngati akhazikika monga m’mene adalili pomwe sichoncho, adzakhala ngati thonje louluka ndi mphepo.
តាហ្វសៀរជាភាសា​អារ៉ាប់ជាច្រេីន:
إِنَّ جَهَنَّمَ كَانَتۡ مِرۡصَادٗا
Ndithu moto wa Jahannam ukuwadikilira (oipa).
តាហ្វសៀរជាភាសា​អារ៉ាប់ជាច្រេីន:
لِّلطَّٰغِينَ مَـَٔابٗا
Mbuto ya opyola malire.[377]
[377] Jahannam ndi dzina lamoto wodziwika wa tsiku lachimaliziro. Apa Allah akutidziwitsa kuti Jahannam ndi malo amene akudikira akafiri kuti m’menemo akalipidwe malipiro awo chifukwa chokanira aneneri pambuyo powasonyeza zizindikiro zoti iwo ndi aneneri a Allah. Ndiponso kumulakwira Allah pochita zimene adaletsa monga; kukana umodzi wa Allah, kukana utumiki wa Mahammad (s.a.w) ndi kukana uthenga wa Qur’an. Komanso kugwa mmachimo osiyanasiyana.
តាហ្វសៀរជាភាសា​អារ៉ាប់ជាច្រេីន:
لَّٰبِثِينَ فِيهَآ أَحۡقَابٗا
Adzakhala m’menemo muyaya.
តាហ្វសៀរជាភាសា​អារ៉ាប់ជាច្រេីន:
لَّا يَذُوقُونَ فِيهَا بَرۡدٗا وَلَا شَرَابًا
Sadzalawa m’menemo kuzizira (kowachotsera kutentha), kapena chakumwa (chowachotsera ludzu lawo);
តាហ្វសៀរជាភាសា​អារ៉ាប់ជាច្រេីន:
إِلَّا حَمِيمٗا وَغَسَّاقٗا
Kupatula madzi otentha kwambiri ndi mafinya (otuluka mmatupi a anthu a ku Moto);
តាហ្វសៀរជាភាសា​អារ៉ាប់ជាច្រេីន:
جَزَآءٗ وِفَاقًا
Kukhala malipiro olingana ndi ntchito zawo.
តាហ្វសៀរជាភាសា​អារ៉ាប់ជាច្រេីន:
إِنَّهُمۡ كَانُواْ لَا يَرۡجُونَ حِسَابٗا
Ndithu iwo sadali kuyembekezera chiwerengero (cha Allah);
តាហ្វសៀរជាភាសា​អារ៉ាប់ជាច្រេីន:
وَكَذَّبُواْ بِـَٔايَٰتِنَا كِذَّابٗا
Adatsutsa zizindikiro Zathu (zosonyeza kuuka kwa akufa) ndi mtsutso waukulu.
តាហ្វសៀរជាភាសា​អារ៉ាប់ជាច្រេីន:
وَكُلَّ شَيۡءٍ أَحۡصَيۡنَٰهُ كِتَٰبٗا
Ndipo chinthu chilichonse tachisunga mochilemba.
តាហ្វសៀរជាភាសា​អារ៉ាប់ជាច្រេីន:
فَذُوقُواْ فَلَن نَّزِيدَكُمۡ إِلَّا عَذَابًا
Basi, lawani (lero chilango Changa); sitikuonjezerani chinthu china koma chilango pamwamba pa chilango.
តាហ្វសៀរជាភាសា​អារ៉ាប់ជាច្រេីន:
إِنَّ لِلۡمُتَّقِينَ مَفَازًا
Ndithu anthu oopa Allah adzakhala ndi malo wopambana.
តាហ្វសៀរជាភាសា​អារ៉ាប់ជាច្រេីន:
حَدَآئِقَ وَأَعۡنَٰبٗا
Minda ndi zipatso za mphesa.
តាហ្វសៀរជាភាសា​អារ៉ាប់ជាច្រេីន:
وَكَوَاعِبَ أَتۡرَابٗا
Ndi mabuthu (anamwali) ofanana misinkhu.
តាហ្វសៀរជាភាសា​អារ៉ាប់ជាច្រេីន:
وَكَأۡسٗا دِهَاقٗا
Ndi zipanda zodzaza ndi zakumwa.
តាហ្វសៀរជាភាសា​អារ៉ាប់ជាច្រេីន:
لَّا يَسۡمَعُونَ فِيهَا لَغۡوٗا وَلَا كِذَّٰبٗا
Sakamva m’menemo mawu opanda pake kapena bodza.
តាហ្វសៀរជាភាសា​អារ៉ាប់ជាច្រេីន:
جَزَآءٗ مِّن رَّبِّكَ عَطَآءً حِسَابٗا
Amenewa ndi malipiro ochokera kwa Mbuye wako zopereka zokwanira.[378]
[378] Chipembedzo cha Chisilamu chikuphunzitsa kuti pali zisangalalo ziwiri: Chisangalalo cha mzimu ndi chisangalalo cha thupi. Tsono chisangalalo cha mzimu ndiko kuyanjana kochokera kwa Allah kumene anthu Ake abwino adzakupeza. Chisangalalo cha thupi ndi monga m’mene afotokozera mu Ayah iyi ndi msura zina. Zokondweretsa monga minda, akazi okongola, mowa (osaledzeretsa) ndiponso sikudzakhala kumva chilichonse chokhumudwitsa.
Taonani, zoledzeretsa ndi zoletsedwa padziko lino lapansi chifukwa cha zoipa zake. Koma mowa wa patsiku la Qiyâma udzakhala wopanda zoipa.
តាហ្វសៀរជាភាសា​អារ៉ាប់ជាច្រេីន:
رَّبِّ ٱلسَّمَٰوَٰتِ وَٱلۡأَرۡضِ وَمَا بَيۡنَهُمَا ٱلرَّحۡمَٰنِۖ لَا يَمۡلِكُونَ مِنۡهُ خِطَابٗا
Mbuye wa kumwamba ndi pansi ndi zimene zili pakati pake; Wachifundo chambiri. Palibe amene adzakhala ndi mphamvu yolankhulana naye (pa tsiku limenero);
តាហ្វសៀរជាភាសា​អារ៉ាប់ជាច្រេីន:
يَوۡمَ يَقُومُ ٱلرُّوحُ وَٱلۡمَلَٰٓئِكَةُ صَفّٗاۖ لَّا يَتَكَلَّمُونَ إِلَّا مَنۡ أَذِنَ لَهُ ٱلرَّحۡمَٰنُ وَقَالَ صَوَابٗا
Tsiku limene adzaima Jibril ndi angelo pa mzere (ali odzichepetsa); sadzayankhula aliyense mwa iwo kupatula yekhayo amene adzaloledwa ndi (Allah) Wachifundo chambiri (kuyankhula) ndipo adzanena zolondola.
តាហ្វសៀរជាភាសា​អារ៉ាប់ជាច្រេីន:
ذَٰلِكَ ٱلۡيَوۡمُ ٱلۡحَقُّۖ فَمَن شَآءَ ٱتَّخَذَ إِلَىٰ رَبِّهِۦ مَـَٔابًا
Limenelo ndi tsiku loona, (lopanda chikaiko); choncho amene akufuna adzipezere malo (njira yonkera) kwa Mbuye wake. (Pomugonjera Iye pa moyo uno wadziko lapansi).
តាហ្វសៀរជាភាសា​អារ៉ាប់ជាច្រេីន:
إِنَّآ أَنذَرۡنَٰكُمۡ عَذَابٗا قَرِيبٗا يَوۡمَ يَنظُرُ ٱلۡمَرۡءُ مَا قَدَّمَتۡ يَدَاهُ وَيَقُولُ ٱلۡكَافِرُ يَٰلَيۡتَنِي كُنتُ تُرَٰبَۢا
Ndithu tikukuchenjezani zachilango chomwe chili pafupi kudza; tsiku limene munthu adzayang’ana zimene adatsogoza manja ake, ndipo wosakhulupirira adzanena: Kalanga ine! Ndikadakhala dothi, (kuti ndisalangidwe chilango chikundiyembekezachi).
តាហ្វសៀរជាភាសា​អារ៉ាប់ជាច្រេីន:
 
ការបកប្រែអត្ថន័យ ជំពូក​: សូរ៉ោះអាន់ណាហ្ពាក
សន្ទស្សន៍នៃជំពូក លេខ​ទំព័រ
 
ការបកប្រែអត្ថន័យគួរអាន - ការបកប្រែជាភាសាឆេវ៉ា - សន្ទស្សន៍នៃការបកប្រែ

ការបកប្រែអត្ថន័យគម្ពីគួរអានជាភាសាឆេវ៉ា ដោយលោកខលីទ អុីប្រហុីម ប៊ីតាឡា ក្នុងឆ្នាំ2020

បិទ