Check out the new design

Traduction des sens du Noble Coran - La traduction tchétchène - Khâlid Ibrâhîm Bîtâlâ * - Lexique des traductions


Traduction des sens Sourate: Al Mâ'idah   Verset:
وَقَفَّيۡنَا عَلَىٰٓ ءَاثَٰرِهِم بِعِيسَى ٱبۡنِ مَرۡيَمَ مُصَدِّقٗا لِّمَا بَيۡنَ يَدَيۡهِ مِنَ ٱلتَّوۡرَىٰةِۖ وَءَاتَيۡنَٰهُ ٱلۡإِنجِيلَ فِيهِ هُدٗى وَنُورٞ وَمُصَدِّقٗا لِّمَا بَيۡنَ يَدَيۡهِ مِنَ ٱلتَّوۡرَىٰةِ وَهُدٗى وَمَوۡعِظَةٗ لِّلۡمُتَّقِينَ
Ndipo tidatsatiza pa mapazi a aneneriwo, Isa (Yesu) mwana wa Mariya kudzatsimikizira zomwe zidali patsogolo pake m’buku la Taurat. Ndipo tidampatsa Injili yomwe m’kati mwake muli chiongoko ndi kuunika; ndikutsimikizira zomwe zidali patsogolo pake za m’buku la Taurat. Ndipo ndi chiongoko ndi ulaliki wabwino kwa oopa (Allah).
Les exégèses en arabe:
وَلۡيَحۡكُمۡ أَهۡلُ ٱلۡإِنجِيلِ بِمَآ أَنزَلَ ٱللَّهُ فِيهِۚ وَمَن لَّمۡ يَحۡكُم بِمَآ أَنزَلَ ٱللَّهُ فَأُوْلَٰٓئِكَ هُمُ ٱلۡفَٰسِقُونَ
Anthu abuku la Injili alamulire potsatira zimene Allah adavumbulutsa mmenemo. Ndipo amene asiya kulamulira ndi zomwe Allah wavumbulutsa iwo ndiwo opandukira malamulo (a Allah).
Les exégèses en arabe:
وَأَنزَلۡنَآ إِلَيۡكَ ٱلۡكِتَٰبَ بِٱلۡحَقِّ مُصَدِّقٗا لِّمَا بَيۡنَ يَدَيۡهِ مِنَ ٱلۡكِتَٰبِ وَمُهَيۡمِنًا عَلَيۡهِۖ فَٱحۡكُم بَيۡنَهُم بِمَآ أَنزَلَ ٱللَّهُۖ وَلَا تَتَّبِعۡ أَهۡوَآءَهُمۡ عَمَّا جَآءَكَ مِنَ ٱلۡحَقِّۚ لِكُلّٖ جَعَلۡنَا مِنكُمۡ شِرۡعَةٗ وَمِنۡهَاجٗاۚ وَلَوۡ شَآءَ ٱللَّهُ لَجَعَلَكُمۡ أُمَّةٗ وَٰحِدَةٗ وَلَٰكِن لِّيَبۡلُوَكُمۡ فِي مَآ ءَاتَىٰكُمۡۖ فَٱسۡتَبِقُواْ ٱلۡخَيۡرَٰتِۚ إِلَى ٱللَّهِ مَرۡجِعُكُمۡ جَمِيعٗا فَيُنَبِّئُكُم بِمَا كُنتُمۡ فِيهِ تَخۡتَلِفُونَ
Ndipo takuvumbulutsira buku mwa choonadi, lomwe likuikira umboni mabuku omwe adalipo patsogolo pake, ndi kuwateteza, (monga ponena kuti: “Lamulo ili ndiloona; ili iyayi.”) Choncho weruza pakati pawo ndi zomwe Allah wavumbulutsa, ndipo usatsate zofuna zawo kusiya choona chomwe chakufika. Ndipo m’badwo uliwonse mwa inu tidaupangira shariya (malamulo) yake ndi njira yake. Allah akadafuna, akadakuikani kukhala mpingo umodzi (wotsata chilamulo chofanana). Koma akufuna kukuyesani pa zomwe wakupatsani. Choncho pikisanani pa zinthu zabwino. Inu nonse kobwerera kwanu nkwa Allah. Naye adzakuuzani (nonsenu) mu zomwe mudali kusiyana;
Les exégèses en arabe:
وَأَنِ ٱحۡكُم بَيۡنَهُم بِمَآ أَنزَلَ ٱللَّهُ وَلَا تَتَّبِعۡ أَهۡوَآءَهُمۡ وَٱحۡذَرۡهُمۡ أَن يَفۡتِنُوكَ عَنۢ بَعۡضِ مَآ أَنزَلَ ٱللَّهُ إِلَيۡكَۖ فَإِن تَوَلَّوۡاْ فَٱعۡلَمۡ أَنَّمَا يُرِيدُ ٱللَّهُ أَن يُصِيبَهُم بِبَعۡضِ ذُنُوبِهِمۡۗ وَإِنَّ كَثِيرٗا مِّنَ ٱلنَّاسِ لَفَٰسِقُونَ
Weruza pakati pawo ndi chimene Allah wavumbulutsa, ndipo usatsate zofuna zawo, koma chenjera nawo kuti angakusokoneze nkusiya zina mwa zimene Allah wavumbulutsa kwa iwe. Ndipo ngati anyozera dziwa kuti Allah afuna kuwapatsa chilango cha ena mwa machimo awo. Ndithudi, anthu ambiri ngopandukira (malamulo a Allah).
Les exégèses en arabe:
أَفَحُكۡمَ ٱلۡجَٰهِلِيَّةِ يَبۡغُونَۚ وَمَنۡ أَحۡسَنُ مِنَ ٱللَّهِ حُكۡمٗا لِّقَوۡمٖ يُوقِنُونَ
Kodi iwo akufuna chiweruzo cha nthawi yaumbuli (chamasiku aumbuli, Chisilamu chisanadze)? Kodi ndani ali wabwino poweruza kuposa Allah kwa anthu otsimikiza (kuti Allah alipo)?
Les exégèses en arabe:
 
Traduction des sens Sourate: Al Mâ'idah
Lexique des sourates Numéro de la page
 
Traduction des sens du Noble Coran - La traduction tchétchène - Khâlid Ibrâhîm Bîtâlâ - Lexique des traductions

Traduit par Khâlid Ibrâhîm Bîtâlâ.

Fermeture