Check out the new design

Traduction des sens du Noble Coran - La traduction tchétchène - Khâlid Ibrâhîm Bîtâlâ * - Lexique des traductions


Traduction des sens Sourate: Al Mâ'idah   Verset:
وَلَوۡ أَنَّ أَهۡلَ ٱلۡكِتَٰبِ ءَامَنُواْ وَٱتَّقَوۡاْ لَكَفَّرۡنَا عَنۡهُمۡ سَيِّـَٔاتِهِمۡ وَلَأَدۡخَلۡنَٰهُمۡ جَنَّٰتِ ٱلنَّعِيمِ
Ndipo kukadakhala kuti awa anthu a buku adakhulupirira ndi kumuopa Allah, tikadawafafanizira zolakwa zawo, ndi kuwalowetsa m’minda ya mtendere.
Les exégèses en arabe:
وَلَوۡ أَنَّهُمۡ أَقَامُواْ ٱلتَّوۡرَىٰةَ وَٱلۡإِنجِيلَ وَمَآ أُنزِلَ إِلَيۡهِم مِّن رَّبِّهِمۡ لَأَكَلُواْ مِن فَوۡقِهِمۡ وَمِن تَحۡتِ أَرۡجُلِهِمۚ مِّنۡهُمۡ أُمَّةٞ مُّقۡتَصِدَةٞۖ وَكَثِيرٞ مِّنۡهُمۡ سَآءَ مَا يَعۡمَلُونَ
Akadakhala kuti iwo adaigwiritsa ntchito Taurat ndi Injili, ndi zomwe zidavumbulutsidwa kwa iwo kuchokera kwa Mbuye wawo (monga Qurani), ndithudi akanadya za kumwamba ndi za pansi pa myendo yawo. Mwa iwo alipo amene akutsatira njira yabwino. Komanso ambiri mwa iwo nzoipa zedi zomwe akuchita.
Les exégèses en arabe:
۞ يَٰٓأَيُّهَا ٱلرَّسُولُ بَلِّغۡ مَآ أُنزِلَ إِلَيۡكَ مِن رَّبِّكَۖ وَإِن لَّمۡ تَفۡعَلۡ فَمَا بَلَّغۡتَ رِسَالَتَهُۥۚ وَٱللَّهُ يَعۡصِمُكَ مِنَ ٱلنَّاسِۗ إِنَّ ٱللَّهَ لَا يَهۡدِي ٱلۡقَوۡمَ ٱلۡكَٰفِرِينَ
E iwe Mtumiki! Fikitsa (kwa anthu) zomwe zavumbulutsidwa kwa iwe kuchokera kwa Mbuye wako. Ngati suchita, ndiye kuti sudafikitse uthenga Wake. Ndipo Allah akuteteza kwa anthu; (usaope aliyense). Ndithudi, Allah satsogolera anthu osakhulupirira.
Les exégèses en arabe:
قُلۡ يَٰٓأَهۡلَ ٱلۡكِتَٰبِ لَسۡتُمۡ عَلَىٰ شَيۡءٍ حَتَّىٰ تُقِيمُواْ ٱلتَّوۡرَىٰةَ وَٱلۡإِنجِيلَ وَمَآ أُنزِلَ إِلَيۡكُم مِّن رَّبِّكُمۡۗ وَلَيَزِيدَنَّ كَثِيرٗا مِّنۡهُم مَّآ أُنزِلَ إِلَيۡكَ مِن رَّبِّكَ طُغۡيَٰنٗا وَكُفۡرٗاۖ فَلَا تَأۡسَ عَلَى ٱلۡقَوۡمِ ٱلۡكَٰفِرِينَ
Nena: “E inu anthu a buku! Simuli kanthu (pa chipembedzo chanu) mpaka muimilire (kutsatira malamulo) a Taurat ndi Injili ndi zomwe zavumbulutsidwa kwa inu kuchokera kwa Mbuye wanu, ziwaonjezera kulakwa ndi kusakhulupirira ambiri a iwo zomwe zavumbulutsidwa kwa iwe kuchokera kwa Mbuye wako, choncho usadandaule za anthu osakhulupirira.
Les exégèses en arabe:
إِنَّ ٱلَّذِينَ ءَامَنُواْ وَٱلَّذِينَ هَادُواْ وَٱلصَّٰبِـُٔونَ وَٱلنَّصَٰرَىٰ مَنۡ ءَامَنَ بِٱللَّهِ وَٱلۡيَوۡمِ ٱلۡأٓخِرِ وَعَمِلَ صَٰلِحٗا فَلَا خَوۡفٌ عَلَيۡهِمۡ وَلَا هُمۡ يَحۡزَنُونَ
Ndithudi, amene akhulupirira ndi amene ali m’chipembedzo cha Chiyuda, ndi Asabayi, ndi Akhrisitu, - amene akhulupirire Allah ndi tsiku lachimaliziro, (monga momwe akulangizira Mtumiki Muhammad {s.a.w}) nachita zabwino, - palibe mantha kwa iwo ndiponso sadzadandaula.
Les exégèses en arabe:
لَقَدۡ أَخَذۡنَا مِيثَٰقَ بَنِيٓ إِسۡرَٰٓءِيلَ وَأَرۡسَلۡنَآ إِلَيۡهِمۡ رُسُلٗاۖ كُلَّمَا جَآءَهُمۡ رَسُولُۢ بِمَا لَا تَهۡوَىٰٓ أَنفُسُهُمۡ فَرِيقٗا كَذَّبُواْ وَفَرِيقٗا يَقۡتُلُونَ
Ndithudi, tidalandira pangano kwa ana a Israyeli (kuti adzamvera Allah) ndipo tidawatumizira atumiki. Nthawi iliyonse akawadzera mtumiki ndi chomwe mitima yawo siinkafuna, adawatsutsa ena (mwa atumikiwo), ndipo ena ankawapha kumene.
Les exégèses en arabe:
 
Traduction des sens Sourate: Al Mâ'idah
Lexique des sourates Numéro de la page
 
Traduction des sens du Noble Coran - La traduction tchétchène - Khâlid Ibrâhîm Bîtâlâ - Lexique des traductions

Traduit par Khâlid Ibrâhîm Bîtâlâ.

Fermeture