Naonso aja amene akuti: “Ife ndife Akhrisitu,” tidalandira pangano lawo koma adasiya gawo lalikulu la zomwe adakumbutsidwa. Tero tidabzala pakati pawo chidani ndi kusakondana mpaka tsiku lachimaliziro. Ndipo Allah adzawawuza zimene adali kuchita.[160]
[160] Ndime iyi ikusonyeza kupatukana komwe kuli pakati pawo kotero kuti mpingo wina umayesa unzake monga wakunja. Monga mpingo wa Roman Catholic umaiona mipingo ina monga ya Protestant, Orthodox ndi yambiri ngati mipingo ya chikunja. Zonsezi nchifukwa cha kusatsatira zophunzitsa zenizeni za Chikhrisitu.
E inu anthu a buku! Ndithudi wakufikani Mtumiki Wathu yemwe akukufotokozerani poyera zambiri zomwe munkabisa za m’buku. Koma akusiya zambiri (posazilongosola). Ndithudi kwakudzerani kuunika kochokera kwa Allah ndi buku lomwe likufotokoza mwatchutchutchu (chinthu chilichonse).
Ndi bukulo Allah akuwatsogolera kunjira zamtendere amene akutsata chiyanjano chake ndikuwatulutsa mu m’dima ndi kuwaika m’kuunika mwa lamulo Lake, ndi kuwatsogolera kunjira yoongoka.
Ndithudi, amukana (Allah) amene akunena kuti Mulungu ndiye Mesiya Mwana wa Mariya. Nena: “Ndani akadatha kuletsa chilichonse kwa Allah ngati Iye akadafuna kuononga Mesiya mwana wa Mariya ndi mayi wakeyo, ndi onse omwe ali m’dziko lapansi? Ndipo ufumu wa kumwamba ndi pansi ndi zapakati pake ngwa Allah. Amalenga chimene wafuna. Ndipo Allah Ngokhoza chilichonse.”[161]
[161] Mndime iyi atchula zoyankhula zawo za machimo zoti Isa (Yesu) ndi mwana wa Mulungu, kapena ndi Mulungu amene, kapena ndi mmodzi mmilungu itatu. Ndipo akunenetsa za kufooka kwa mneneri Isa (Yesu) pamaso pa Allah monga kulili kufookanso kwa zolengedwa zina.
Ndimeyi ikunenetsanso kuti Allah monga amalenga mkalengedwe kamene Iye wafuna, mchosadabwitsa kwa Iye kulenga Isa (Yesu) popanda tate. Ndipo nchosadabwitsanso kwa Iye kulenga Adam popanda tate ndi mayi. Nanga nchotani kuti Akhrisitu azimuyesa Mneneri Isa (Yesu) kuti ndi mwana wa Mulungu kamba koti alibe tate? Bwanji nanga Adam naye sakumuyesa mwana wa Mulungu poti nayenso alibe tate ndi mayi? Ndibwino kutsata choonadi ngakhale choonadicho chikuchokera kwa mdani. Choonadi ndi choonadi.
Contents of the translations can be downloaded and re-published, with the following terms and conditions:
1. No modification, addition, or deletion of the content.
2. Clearly referring to the publisher and the source (QuranEnc.com).
3. Mentioning the version number when re-publishing the translation.
4. Keeping the transcript information inside the document.
5. Notifying the source (QuranEnc.com) of any note on the translation.
6. Updating the translation according to the latest version issued from the source (QuranEnc.com).
7. Inappropriate advertisements must not be included when displaying translations of the meanings of the Noble Quran.
Résultats de la recherche:
API specs
Endpoints:
Sura translation
GET / https://quranenc.com/api/v1/translation/sura/{translation_key}/{sura_number} description: get the specified translation (by its translation_key) for the speicified sura (by its number)
Parameters: translation_key: (the key of the currently selected translation) sura_number: [1-114] (Sura number in the mosshaf which should be between 1 and 114)
Returns:
json object containing array of objects, each object contains the "sura", "aya", "translation" and "footnotes".
GET / https://quranenc.com/api/v1/translation/aya/{translation_key}/{sura_number}/{aya_number} description: get the specified translation (by its translation_key) for the speicified aya (by its number sura_number and aya_number)
Parameters: translation_key: (the key of the currently selected translation) sura_number: [1-114] (Sura number in the mosshaf which should be between 1 and 114) aya_number: [1-...] (Aya number in the sura)
Returns:
json object containing the "sura", "aya", "translation" and "footnotes".