Terjemahan makna Alquran Alkarim - Terjemahan Berbahasa Chichewa * - Daftar isi terjemahan


Terjemahan makna Surah: Surah Al-Qalam   Ayah:

Surah Al-Qalam

نٓۚ وَٱلۡقَلَمِ وَمَا يَسۡطُرُونَ
Nûn. Ndikulumbilira cholembera (chimene akulembera angelo), ndi zimene amalemba.
Tafsir berbahasa Arab:
مَآ أَنتَ بِنِعۡمَةِ رَبِّكَ بِمَجۡنُونٖ
Pa chisomo cha Mbuye wako iwe sindiwe wamisala (pokupatsa uneneri).
Tafsir berbahasa Arab:
وَإِنَّ لَكَ لَأَجۡرًا غَيۡرَ مَمۡنُونٖ
Ndipo ndithu udzakhala ndi malipiro akulu osaduka, (onkerankera mtsogolo chifukwa cha mavuto amene ukukumana nawo pofikitsa uthenga).
Tafsir berbahasa Arab:
وَإِنَّكَ لَعَلَىٰ خُلُقٍ عَظِيمٖ
Ndipo ndithu uli nawo makhalidwe abwino kwambiri (omwe Allah adakulenga nawo).
Tafsir berbahasa Arab:
فَسَتُبۡصِرُ وَيُبۡصِرُونَ
Basi, posachedwapa uona, iwonso aona.
Tafsir berbahasa Arab:
بِأَييِّكُمُ ٱلۡمَفۡتُونُ
Kuti ndani mwa inu wamisala (iwe kapena iwo)?
Tafsir berbahasa Arab:
إِنَّ رَبَّكَ هُوَ أَعۡلَمُ بِمَن ضَلَّ عَن سَبِيلِهِۦ وَهُوَ أَعۡلَمُ بِٱلۡمُهۡتَدِينَ
Ndithu Mbuye wako akum’dziwa bwino amene wasokera panjira yake. Ndiponso akuwadziwa bwino amene ali oongoka.
Tafsir berbahasa Arab:
فَلَا تُطِعِ ٱلۡمُكَذِّبِينَ
Choncho, usawamvere otsutsa; (usasiye zimene uli nazo ngakhale sakugwirizana nazo).
Tafsir berbahasa Arab:
وَدُّواْ لَوۡ تُدۡهِنُ فَيُدۡهِنُونَ
Akufuna kuti ukadakhala wofewa kwa iwo (pa zinthu zina) nawo akadakhala ofewa (kwa iwe).
Tafsir berbahasa Arab:
وَلَا تُطِعۡ كُلَّ حَلَّافٖ مَّهِينٍ
Ndipo usamumvere aliyense wochulukitsa kulumbira, woyaluka.
Tafsir berbahasa Arab:
هَمَّازٖ مَّشَّآءِۭ بِنَمِيمٖ
Wojeda, woyenda ndi ukazitape (ndi cholinga choononga umodzi wawo).
Tafsir berbahasa Arab:
مَّنَّاعٖ لِّلۡخَيۡرِ مُعۡتَدٍ أَثِيمٍ
Wotsekereza zabwino, wamtopola, wamachimo ambiri.
Tafsir berbahasa Arab:
عُتُلِّۭ بَعۡدَ ذَٰلِكَ زَنِيمٍ
Wouma mtima; pamwamba pa izi ndi wodzipachika mu mtundu wa ena (pomwe iye sali m’menemo).
Tafsir berbahasa Arab:
أَن كَانَ ذَا مَالٖ وَبَنِينَ
Chifukwa choti iye ndi mwini chuma ndi ana (ndi zimene ali kunyadira).
Tafsir berbahasa Arab:
إِذَا تُتۡلَىٰ عَلَيۡهِ ءَايَٰتُنَا قَالَ أَسَٰطِيرُ ٱلۡأَوَّلِينَ
Zikawerengedwa kwa iye Ayah Zathu amanena: “Izi ndi nthano za akale (ndi zabodza zawo, zopeka).”
Tafsir berbahasa Arab:
سَنَسِمُهُۥ عَلَى ٱلۡخُرۡطُومِ
Timuika pamphuno pake chizindikiro (chosasiyana nacho kuti ayaluke nacho pamaso pa anthu).
Tafsir berbahasa Arab:
إِنَّا بَلَوۡنَٰهُمۡ كَمَا بَلَوۡنَآ أَصۡحَٰبَ ٱلۡجَنَّةِ إِذۡ أَقۡسَمُواْ لَيَصۡرِمُنَّهَا مُصۡبِحِينَ
Ndithu ife tidawayesa (eni mzinda wa Makka ndi mtendere omwe udali pa iwo, koma adakana monga) momwe tidawayesera eni munda, pamene adalumbira kuti akathyola (zipatso za m’munda wawozo) mbandakucha (kuti osauka asawaone angawapemphe).
Tafsir berbahasa Arab:
وَلَا يَسۡتَثۡنُونَ
Ndipo sadapatule (ngakhale wosauka ndi m’modzi yemwe ponena kuti uje timpatse, uje tisampatse, kapena sadanene kuti: “Ngati Allah afuna).”
Tafsir berbahasa Arab:
فَطَافَ عَلَيۡهَا طَآئِفٞ مِّن رَّبِّكَ وَهُمۡ نَآئِمُونَ
Mliri woopsa wochokera kwa Mbuye wako udauzinga (mundawo nthawi yausiku) iwo ali mtulo.
Tafsir berbahasa Arab:
فَأَصۡبَحَتۡ كَٱلصَّرِيمِ
Choncho udakhala ngati wokololedwa (chifukwa cha mliri uja).
Tafsir berbahasa Arab:
فَتَنَادَوۡاْ مُصۡبِحِينَ
Tero adaitanizana nthawi ya mbandakucha.
Tafsir berbahasa Arab:
أَنِ ٱغۡدُواْ عَلَىٰ حَرۡثِكُمۡ إِن كُنتُمۡ صَٰرِمِينَ
“Lawilirani kumunda wanu kuja ngati mukufuna kukolola (kuopera kuti angakuoneni osauka).”
Tafsir berbahasa Arab:
فَٱنطَلَقُواْ وَهُمۡ يَتَخَٰفَتُونَ
Adanyamuka uku akunong’ onezana.
Tafsir berbahasa Arab:
أَن لَّا يَدۡخُلَنَّهَا ٱلۡيَوۡمَ عَلَيۡكُم مِّسۡكِينٞ
(Akunena kuti): “Asakulowelereni wosauka lero mmenemo.”
Tafsir berbahasa Arab:
وَغَدَوۡاْ عَلَىٰ حَرۡدٖ قَٰدِرِينَ
Ndipo adalawilira ali ndi chitsimikizo choti atha kuwamana (osauka).
Tafsir berbahasa Arab:
فَلَمَّا رَأَوۡهَا قَالُوٓاْ إِنَّا لَضَآلُّونَ
Choncho pamene adauona, adanena (uku akunjenjemera): “Ndithu ife tasokera (sikuno ayi, munda wathu uja siuno).”
Tafsir berbahasa Arab:
بَلۡ نَحۡنُ مَحۡرُومُونَ
“Iyayi, ndiwomwewu; koma tamanidwa zinthu zake.”
Tafsir berbahasa Arab:
قَالَ أَوۡسَطُهُمۡ أَلَمۡ أَقُل لَّكُمۡ لَوۡلَا تُسَبِّحُونَ
Wolungama mwa iwo adanena: “Kodi sindinakuuzeni (pamene mudali kulangizana zomana osowa) kuti bwanji osamkumbukira Allah (ndi kusintha cholinga chanu)?”
Tafsir berbahasa Arab:
قَالُواْ سُبۡحَٰنَ رَبِّنَآ إِنَّا كُنَّا ظَٰلِمِينَ
(Iwo) adanena: “Alemekezeke Mbuye wathu ndithu ife tidali achinyengo (chifukwa cha kuipa kwa cholinga chathu).”
Tafsir berbahasa Arab:
فَأَقۡبَلَ بَعۡضُهُمۡ عَلَىٰ بَعۡضٖ يَتَلَٰوَمُونَ
Ndipo adatembenukirana ndikuyamba kudzudzulana.
Tafsir berbahasa Arab:
قَالُواْ يَٰوَيۡلَنَآ إِنَّا كُنَّا طَٰغِينَ
Adati: “E chionongeko chathu! Ndithu Ife tidapyola malire (m’chinyengo chathu).”
Tafsir berbahasa Arab:
عَسَىٰ رَبُّنَآ أَن يُبۡدِلَنَا خَيۡرٗا مِّنۡهَآ إِنَّآ إِلَىٰ رَبِّنَا رَٰغِبُونَ
“Mwina Mbuye wathu angatipatse zabwino m’malo mwa munda wathuwu. Ndithu ife tikufunitsitsa kwa Mbuye wathu (chikhululuko Chake).”
Tafsir berbahasa Arab:
كَذَٰلِكَ ٱلۡعَذَابُۖ وَلَعَذَابُ ٱلۡأٓخِرَةِ أَكۡبَرُۚ لَوۡ كَانُواْ يَعۡلَمُونَ
Umo ndi mmene chimakhalira chilango (Changa chomwe ndimachitsitsa pa dziko lapansi kwa amene chamuyenera); koma chilango cha tsiku lachimaliziro nchachikulu zedi, akadakhala akudziwa.
Tafsir berbahasa Arab:
إِنَّ لِلۡمُتَّقِينَ عِندَ رَبِّهِمۡ جَنَّٰتِ ٱلنَّعِيمِ
Ndithu oopa Allah adzakhala ndi Minda ya mtendere kwa Mbuye wawo.
Tafsir berbahasa Arab:
أَفَنَجۡعَلُ ٱلۡمُسۡلِمِينَ كَٱلۡمُجۡرِمِينَ
Kodi tiwachite Asilamu monga ochimwa.
Tafsir berbahasa Arab:
مَا لَكُمۡ كَيۡفَ تَحۡكُمُونَ
Kodi nchiyani chakupezani! Nanga mukuweruza bwanji (maweruzo opanda chilungamo)?
Tafsir berbahasa Arab:
أَمۡ لَكُمۡ كِتَٰبٞ فِيهِ تَدۡرُسُونَ
Kapena muli ndi buku limene mukuwerenga.
Tafsir berbahasa Arab:
إِنَّ لَكُمۡ فِيهِ لَمَا تَخَيَّرُونَ
Kuti ndithu mulinazo mmenemo zomwe mukudzisankhira.
Tafsir berbahasa Arab:
أَمۡ لَكُمۡ أَيۡمَٰنٌ عَلَيۡنَا بَٰلِغَةٌ إِلَىٰ يَوۡمِ ٱلۡقِيَٰمَةِ إِنَّ لَكُمۡ لَمَا تَحۡكُمُونَ
Kapena muli nawo mapangano ndi Ife okafika mpaka tsiku lachimaliziro akuti inu mudzapeza zimene mukudziweruzira?
Tafsir berbahasa Arab:
سَلۡهُمۡ أَيُّهُم بِذَٰلِكَ زَعِيمٌ
Afunse (iwe Mtumiki) ndani mwa iwo amene ali mtsogoleri (pa malamulo amenewa)?
Tafsir berbahasa Arab:
أَمۡ لَهُمۡ شُرَكَآءُ فَلۡيَأۡتُواْ بِشُرَكَآئِهِمۡ إِن كَانُواْ صَٰدِقِينَ
Kapena iwo ali nawo othandidzana nawo (pa mau awa)? Chomwecho atabweretsa othandizana nawo ngati akunena zowona!
Tafsir berbahasa Arab:
يَوۡمَ يُكۡشَفُ عَن سَاقٖ وَيُدۡعَوۡنَ إِلَى ٱلسُّجُودِ فَلَا يَسۡتَطِيعُونَ
(Akumbukire) tsiku la mavuto okhwima, ndipo adzaitanidwa (akafiri) kuti achite sijida (polambira Allah) koma sadzatha.
Tafsir berbahasa Arab:
خَٰشِعَةً أَبۡصَٰرُهُمۡ تَرۡهَقُهُمۡ ذِلَّةٞۖ وَقَدۡ كَانُواْ يُدۡعَوۡنَ إِلَى ٱلسُّجُودِ وَهُمۡ سَٰلِمُونَ
Maso awo adzangoti pansi zyoli, manyazi ndi kunyozeka kudzawaphimba; chikhalirecho adali kuitanidwa (pa dziko lapansi) kuti agwetse nkhope pansi pomwe iwo adali ndi moyo wa ngwiro (koma ankakana).
Tafsir berbahasa Arab:
فَذَرۡنِي وَمَن يُكَذِّبُ بِهَٰذَا ٱلۡحَدِيثِۖ سَنَسۡتَدۡرِجُهُم مِّنۡ حَيۡثُ لَا يَعۡلَمُونَ
Choncho ndisiye, (iwe Mtumiki), ndi amene akukanira nkhani iyi tiwakokera kuchilango pang’onopang’ono pamene iwo sakudziwa (mmene chiti chiwadzere chilangochi).
Tafsir berbahasa Arab:
وَأُمۡلِي لَهُمۡۚ إِنَّ كَيۡدِي مَتِينٌ
Ndipo ndikuwalekelera (pochedwetsa chilango); ndithudi makonzedwe Anga ngokhwima, (palibe angapulumuke mmenemo).
Tafsir berbahasa Arab:
أَمۡ تَسۡـَٔلُهُمۡ أَجۡرٗا فَهُم مِّن مَّغۡرَمٖ مُّثۡقَلُونَ
Kapena ukuwapempha malipiro (pofikitsa uthenga) kotero kuti iwo akulemedwa ndi kulipira?
Tafsir berbahasa Arab:
أَمۡ عِندَهُمُ ٱلۡغَيۡبُ فَهُمۡ يَكۡتُبُونَ
Kapena ali nazo (nzeru) zobisika kotero kuti iwo akulemba (zimene akuweruzazo)!
Tafsir berbahasa Arab:
فَٱصۡبِرۡ لِحُكۡمِ رَبِّكَ وَلَا تَكُن كَصَاحِبِ ٱلۡحُوتِ إِذۡ نَادَىٰ وَهُوَ مَكۡظُومٞ
Choncho pirira ndi lamulo la Mbuye wako (chifukwa chowalekelera ndi kuchedwetsa chipulumutso chako); ndipo usakhale ngati mwini nsomba (Yunusu pa changu ndi mkwiyo kwa anthu ake) pamene adaitana (Mbuye wake) uku ali wodzazidwa ndi mkwiyo (kupempha kuti chidze mwachangu chilango kwa anthu ake).
Tafsir berbahasa Arab:
لَّوۡلَآ أَن تَدَٰرَكَهُۥ نِعۡمَةٞ مِّن رَّبِّهِۦ لَنُبِذَ بِٱلۡعَرَآءِ وَهُوَ مَذۡمُومٞ
Chikadapanda kumfikira chisomo chochokera kwa Mbuye wake (ndi kuvomera kulapa kwake), akadaponyedwa (kuchokera m’mimba mwa chinsomba chija) pagombe (popanda kanthu) ali wodzudzulidwa.
Tafsir berbahasa Arab:
فَٱجۡتَبَٰهُ رَبُّهُۥ فَجَعَلَهُۥ مِنَ ٱلصَّٰلِحِينَ
Koma adamsankha Mbuye wake (povomera kulapa kwake) ndipo adamchita kukhala mmodzi wa anthu abwino.
Tafsir berbahasa Arab:
وَإِن يَكَادُ ٱلَّذِينَ كَفَرُواْ لَيُزۡلِقُونَكَ بِأَبۡصَٰرِهِمۡ لَمَّا سَمِعُواْ ٱلذِّكۡرَ وَيَقُولُونَ إِنَّهُۥ لَمَجۡنُونٞ
Ndithudi anthu amene sadakhulupirire adayandikira kukuteleretsa ndi kunyogodola kwa maso awo (chifukwa chachidani ndi mkwiyo) pamene adamva chikumbutso (Qur’an), ndipo akunena kuti iyeyo ngwamisala.
Tafsir berbahasa Arab:
وَمَا هُوَ إِلَّا ذِكۡرٞ لِّلۡعَٰلَمِينَ
Ndipo ichi sichina, koma (ndi phunziro, ndi nzeru) ndi chikumbutso kwa zolengedwa zonse.
Tafsir berbahasa Arab:
 
Terjemahan makna Surah: Surah Al-Qalam
Daftar surah Nomor Halaman
 
Terjemahan makna Alquran Alkarim - Terjemahan Berbahasa Chichewa - Daftar isi terjemahan

Terjemahan Makna Al-Qur`ān Al-Karīm ke Bahasa Chichewa oleh Khalid Ibrahim Betala. Edisi 2020 M

Tutup