Tradução dos significados do Nobre Qur’an. - Tradução para a língua chachio * - Índice de tradução


Tradução dos significados Surah: Suratu Al-Qalam   Versículo:

Suratu Al-Qalam

نٓۚ وَٱلۡقَلَمِ وَمَا يَسۡطُرُونَ
Nûn. Ndikulumbilira cholembera (chimene akulembera angelo), ndi zimene amalemba.
Os Tafssir em língua árabe:
مَآ أَنتَ بِنِعۡمَةِ رَبِّكَ بِمَجۡنُونٖ
Pa chisomo cha Mbuye wako iwe sindiwe wamisala (pokupatsa uneneri).
Os Tafssir em língua árabe:
وَإِنَّ لَكَ لَأَجۡرًا غَيۡرَ مَمۡنُونٖ
Ndipo ndithu udzakhala ndi malipiro akulu osaduka, (onkerankera mtsogolo chifukwa cha mavuto amene ukukumana nawo pofikitsa uthenga).
Os Tafssir em língua árabe:
وَإِنَّكَ لَعَلَىٰ خُلُقٍ عَظِيمٖ
Ndipo ndithu uli nawo makhalidwe abwino kwambiri (omwe Allah adakulenga nawo).
Os Tafssir em língua árabe:
فَسَتُبۡصِرُ وَيُبۡصِرُونَ
Basi, posachedwapa uona, iwonso aona.
Os Tafssir em língua árabe:
بِأَييِّكُمُ ٱلۡمَفۡتُونُ
Kuti ndani mwa inu wamisala (iwe kapena iwo)?
Os Tafssir em língua árabe:
إِنَّ رَبَّكَ هُوَ أَعۡلَمُ بِمَن ضَلَّ عَن سَبِيلِهِۦ وَهُوَ أَعۡلَمُ بِٱلۡمُهۡتَدِينَ
Ndithu Mbuye wako akum’dziwa bwino amene wasokera panjira yake. Ndiponso akuwadziwa bwino amene ali oongoka.
Os Tafssir em língua árabe:
فَلَا تُطِعِ ٱلۡمُكَذِّبِينَ
Choncho, usawamvere otsutsa; (usasiye zimene uli nazo ngakhale sakugwirizana nazo).
Os Tafssir em língua árabe:
وَدُّواْ لَوۡ تُدۡهِنُ فَيُدۡهِنُونَ
Akufuna kuti ukadakhala wofewa kwa iwo (pa zinthu zina) nawo akadakhala ofewa (kwa iwe).
Os Tafssir em língua árabe:
وَلَا تُطِعۡ كُلَّ حَلَّافٖ مَّهِينٍ
Ndipo usamumvere aliyense wochulukitsa kulumbira, woyaluka.
Os Tafssir em língua árabe:
هَمَّازٖ مَّشَّآءِۭ بِنَمِيمٖ
Wojeda, woyenda ndi ukazitape (ndi cholinga choononga umodzi wawo).
Os Tafssir em língua árabe:
مَّنَّاعٖ لِّلۡخَيۡرِ مُعۡتَدٍ أَثِيمٍ
Wotsekereza zabwino, wamtopola, wamachimo ambiri.
Os Tafssir em língua árabe:
عُتُلِّۭ بَعۡدَ ذَٰلِكَ زَنِيمٍ
Wouma mtima; pamwamba pa izi ndi wodzipachika mu mtundu wa ena (pomwe iye sali m’menemo).
Os Tafssir em língua árabe:
أَن كَانَ ذَا مَالٖ وَبَنِينَ
Chifukwa choti iye ndi mwini chuma ndi ana (ndi zimene ali kunyadira).
Os Tafssir em língua árabe:
إِذَا تُتۡلَىٰ عَلَيۡهِ ءَايَٰتُنَا قَالَ أَسَٰطِيرُ ٱلۡأَوَّلِينَ
Zikawerengedwa kwa iye Ayah Zathu amanena: “Izi ndi nthano za akale (ndi zabodza zawo, zopeka).”
Os Tafssir em língua árabe:
سَنَسِمُهُۥ عَلَى ٱلۡخُرۡطُومِ
Timuika pamphuno pake chizindikiro (chosasiyana nacho kuti ayaluke nacho pamaso pa anthu).
Os Tafssir em língua árabe:
إِنَّا بَلَوۡنَٰهُمۡ كَمَا بَلَوۡنَآ أَصۡحَٰبَ ٱلۡجَنَّةِ إِذۡ أَقۡسَمُواْ لَيَصۡرِمُنَّهَا مُصۡبِحِينَ
Ndithu ife tidawayesa (eni mzinda wa Makka ndi mtendere omwe udali pa iwo, koma adakana monga) momwe tidawayesera eni munda, pamene adalumbira kuti akathyola (zipatso za m’munda wawozo) mbandakucha (kuti osauka asawaone angawapemphe).
Os Tafssir em língua árabe:
وَلَا يَسۡتَثۡنُونَ
Ndipo sadapatule (ngakhale wosauka ndi m’modzi yemwe ponena kuti uje timpatse, uje tisampatse, kapena sadanene kuti: “Ngati Allah afuna).”
Os Tafssir em língua árabe:
فَطَافَ عَلَيۡهَا طَآئِفٞ مِّن رَّبِّكَ وَهُمۡ نَآئِمُونَ
Mliri woopsa wochokera kwa Mbuye wako udauzinga (mundawo nthawi yausiku) iwo ali mtulo.
Os Tafssir em língua árabe:
فَأَصۡبَحَتۡ كَٱلصَّرِيمِ
Choncho udakhala ngati wokololedwa (chifukwa cha mliri uja).
Os Tafssir em língua árabe:
فَتَنَادَوۡاْ مُصۡبِحِينَ
Tero adaitanizana nthawi ya mbandakucha.
Os Tafssir em língua árabe:
أَنِ ٱغۡدُواْ عَلَىٰ حَرۡثِكُمۡ إِن كُنتُمۡ صَٰرِمِينَ
“Lawilirani kumunda wanu kuja ngati mukufuna kukolola (kuopera kuti angakuoneni osauka).”
Os Tafssir em língua árabe:
فَٱنطَلَقُواْ وَهُمۡ يَتَخَٰفَتُونَ
Adanyamuka uku akunong’ onezana.
Os Tafssir em língua árabe:
أَن لَّا يَدۡخُلَنَّهَا ٱلۡيَوۡمَ عَلَيۡكُم مِّسۡكِينٞ
(Akunena kuti): “Asakulowelereni wosauka lero mmenemo.”
Os Tafssir em língua árabe:
وَغَدَوۡاْ عَلَىٰ حَرۡدٖ قَٰدِرِينَ
Ndipo adalawilira ali ndi chitsimikizo choti atha kuwamana (osauka).
Os Tafssir em língua árabe:
فَلَمَّا رَأَوۡهَا قَالُوٓاْ إِنَّا لَضَآلُّونَ
Choncho pamene adauona, adanena (uku akunjenjemera): “Ndithu ife tasokera (sikuno ayi, munda wathu uja siuno).”
Os Tafssir em língua árabe:
بَلۡ نَحۡنُ مَحۡرُومُونَ
“Iyayi, ndiwomwewu; koma tamanidwa zinthu zake.”
Os Tafssir em língua árabe:
قَالَ أَوۡسَطُهُمۡ أَلَمۡ أَقُل لَّكُمۡ لَوۡلَا تُسَبِّحُونَ
Wolungama mwa iwo adanena: “Kodi sindinakuuzeni (pamene mudali kulangizana zomana osowa) kuti bwanji osamkumbukira Allah (ndi kusintha cholinga chanu)?”
Os Tafssir em língua árabe:
قَالُواْ سُبۡحَٰنَ رَبِّنَآ إِنَّا كُنَّا ظَٰلِمِينَ
(Iwo) adanena: “Alemekezeke Mbuye wathu ndithu ife tidali achinyengo (chifukwa cha kuipa kwa cholinga chathu).”
Os Tafssir em língua árabe:
فَأَقۡبَلَ بَعۡضُهُمۡ عَلَىٰ بَعۡضٖ يَتَلَٰوَمُونَ
Ndipo adatembenukirana ndikuyamba kudzudzulana.
Os Tafssir em língua árabe:
قَالُواْ يَٰوَيۡلَنَآ إِنَّا كُنَّا طَٰغِينَ
Adati: “E chionongeko chathu! Ndithu Ife tidapyola malire (m’chinyengo chathu).”
Os Tafssir em língua árabe:
عَسَىٰ رَبُّنَآ أَن يُبۡدِلَنَا خَيۡرٗا مِّنۡهَآ إِنَّآ إِلَىٰ رَبِّنَا رَٰغِبُونَ
“Mwina Mbuye wathu angatipatse zabwino m’malo mwa munda wathuwu. Ndithu ife tikufunitsitsa kwa Mbuye wathu (chikhululuko Chake).”
Os Tafssir em língua árabe:
كَذَٰلِكَ ٱلۡعَذَابُۖ وَلَعَذَابُ ٱلۡأٓخِرَةِ أَكۡبَرُۚ لَوۡ كَانُواْ يَعۡلَمُونَ
Umo ndi mmene chimakhalira chilango (Changa chomwe ndimachitsitsa pa dziko lapansi kwa amene chamuyenera); koma chilango cha tsiku lachimaliziro nchachikulu zedi, akadakhala akudziwa.
Os Tafssir em língua árabe:
إِنَّ لِلۡمُتَّقِينَ عِندَ رَبِّهِمۡ جَنَّٰتِ ٱلنَّعِيمِ
Ndithu oopa Allah adzakhala ndi Minda ya mtendere kwa Mbuye wawo.
Os Tafssir em língua árabe:
أَفَنَجۡعَلُ ٱلۡمُسۡلِمِينَ كَٱلۡمُجۡرِمِينَ
Kodi tiwachite Asilamu monga ochimwa.
Os Tafssir em língua árabe:
مَا لَكُمۡ كَيۡفَ تَحۡكُمُونَ
Kodi nchiyani chakupezani! Nanga mukuweruza bwanji (maweruzo opanda chilungamo)?
Os Tafssir em língua árabe:
أَمۡ لَكُمۡ كِتَٰبٞ فِيهِ تَدۡرُسُونَ
Kapena muli ndi buku limene mukuwerenga.
Os Tafssir em língua árabe:
إِنَّ لَكُمۡ فِيهِ لَمَا تَخَيَّرُونَ
Kuti ndithu mulinazo mmenemo zomwe mukudzisankhira.
Os Tafssir em língua árabe:
أَمۡ لَكُمۡ أَيۡمَٰنٌ عَلَيۡنَا بَٰلِغَةٌ إِلَىٰ يَوۡمِ ٱلۡقِيَٰمَةِ إِنَّ لَكُمۡ لَمَا تَحۡكُمُونَ
Kapena muli nawo mapangano ndi Ife okafika mpaka tsiku lachimaliziro akuti inu mudzapeza zimene mukudziweruzira?
Os Tafssir em língua árabe:
سَلۡهُمۡ أَيُّهُم بِذَٰلِكَ زَعِيمٌ
Afunse (iwe Mtumiki) ndani mwa iwo amene ali mtsogoleri (pa malamulo amenewa)?
Os Tafssir em língua árabe:
أَمۡ لَهُمۡ شُرَكَآءُ فَلۡيَأۡتُواْ بِشُرَكَآئِهِمۡ إِن كَانُواْ صَٰدِقِينَ
Kapena iwo ali nawo othandidzana nawo (pa mau awa)? Chomwecho atabweretsa othandizana nawo ngati akunena zowona!
Os Tafssir em língua árabe:
يَوۡمَ يُكۡشَفُ عَن سَاقٖ وَيُدۡعَوۡنَ إِلَى ٱلسُّجُودِ فَلَا يَسۡتَطِيعُونَ
(Akumbukire) tsiku la mavuto okhwima, ndipo adzaitanidwa (akafiri) kuti achite sijida (polambira Allah) koma sadzatha.
Os Tafssir em língua árabe:
خَٰشِعَةً أَبۡصَٰرُهُمۡ تَرۡهَقُهُمۡ ذِلَّةٞۖ وَقَدۡ كَانُواْ يُدۡعَوۡنَ إِلَى ٱلسُّجُودِ وَهُمۡ سَٰلِمُونَ
Maso awo adzangoti pansi zyoli, manyazi ndi kunyozeka kudzawaphimba; chikhalirecho adali kuitanidwa (pa dziko lapansi) kuti agwetse nkhope pansi pomwe iwo adali ndi moyo wa ngwiro (koma ankakana).
Os Tafssir em língua árabe:
فَذَرۡنِي وَمَن يُكَذِّبُ بِهَٰذَا ٱلۡحَدِيثِۖ سَنَسۡتَدۡرِجُهُم مِّنۡ حَيۡثُ لَا يَعۡلَمُونَ
Choncho ndisiye, (iwe Mtumiki), ndi amene akukanira nkhani iyi tiwakokera kuchilango pang’onopang’ono pamene iwo sakudziwa (mmene chiti chiwadzere chilangochi).
Os Tafssir em língua árabe:
وَأُمۡلِي لَهُمۡۚ إِنَّ كَيۡدِي مَتِينٌ
Ndipo ndikuwalekelera (pochedwetsa chilango); ndithudi makonzedwe Anga ngokhwima, (palibe angapulumuke mmenemo).
Os Tafssir em língua árabe:
أَمۡ تَسۡـَٔلُهُمۡ أَجۡرٗا فَهُم مِّن مَّغۡرَمٖ مُّثۡقَلُونَ
Kapena ukuwapempha malipiro (pofikitsa uthenga) kotero kuti iwo akulemedwa ndi kulipira?
Os Tafssir em língua árabe:
أَمۡ عِندَهُمُ ٱلۡغَيۡبُ فَهُمۡ يَكۡتُبُونَ
Kapena ali nazo (nzeru) zobisika kotero kuti iwo akulemba (zimene akuweruzazo)!
Os Tafssir em língua árabe:
فَٱصۡبِرۡ لِحُكۡمِ رَبِّكَ وَلَا تَكُن كَصَاحِبِ ٱلۡحُوتِ إِذۡ نَادَىٰ وَهُوَ مَكۡظُومٞ
Choncho pirira ndi lamulo la Mbuye wako (chifukwa chowalekelera ndi kuchedwetsa chipulumutso chako); ndipo usakhale ngati mwini nsomba (Yunusu pa changu ndi mkwiyo kwa anthu ake) pamene adaitana (Mbuye wake) uku ali wodzazidwa ndi mkwiyo (kupempha kuti chidze mwachangu chilango kwa anthu ake).
Os Tafssir em língua árabe:
لَّوۡلَآ أَن تَدَٰرَكَهُۥ نِعۡمَةٞ مِّن رَّبِّهِۦ لَنُبِذَ بِٱلۡعَرَآءِ وَهُوَ مَذۡمُومٞ
Chikadapanda kumfikira chisomo chochokera kwa Mbuye wake (ndi kuvomera kulapa kwake), akadaponyedwa (kuchokera m’mimba mwa chinsomba chija) pagombe (popanda kanthu) ali wodzudzulidwa.
Os Tafssir em língua árabe:
فَٱجۡتَبَٰهُ رَبُّهُۥ فَجَعَلَهُۥ مِنَ ٱلصَّٰلِحِينَ
Koma adamsankha Mbuye wake (povomera kulapa kwake) ndipo adamchita kukhala mmodzi wa anthu abwino.
Os Tafssir em língua árabe:
وَإِن يَكَادُ ٱلَّذِينَ كَفَرُواْ لَيُزۡلِقُونَكَ بِأَبۡصَٰرِهِمۡ لَمَّا سَمِعُواْ ٱلذِّكۡرَ وَيَقُولُونَ إِنَّهُۥ لَمَجۡنُونٞ
Ndithudi anthu amene sadakhulupirire adayandikira kukuteleretsa ndi kunyogodola kwa maso awo (chifukwa chachidani ndi mkwiyo) pamene adamva chikumbutso (Qur’an), ndipo akunena kuti iyeyo ngwamisala.
Os Tafssir em língua árabe:
وَمَا هُوَ إِلَّا ذِكۡرٞ لِّلۡعَٰلَمِينَ
Ndipo ichi sichina, koma (ndi phunziro, ndi nzeru) ndi chikumbutso kwa zolengedwa zonse.
Os Tafssir em língua árabe:
 
Tradução dos significados Surah: Suratu Al-Qalam
Índice de capítulos Número de página
 
Tradução dos significados do Nobre Qur’an. - Tradução para a língua chachio - Índice de tradução

Tradução de significados do Nobre Al-Qur'án para a língua Chichio, traduzido por Khalid Ibrahim Bitálá. Edição do ano 2020

Fechar