Terjemahan makna Alquran Alkarim - Terjemahan Berbahasa Chichewa * - Daftar isi terjemahan


Terjemahan makna Surah: Surah Az-Zalzalah   Ayah:

Surah Az-Zalzalah

إِذَا زُلۡزِلَتِ ٱلۡأَرۡضُ زِلۡزَالَهَا
Likadzagwedezedwa dziko lapansi kugwedezeka kwake kwamphamvu,
Tafsir berbahasa Arab:
وَأَخۡرَجَتِ ٱلۡأَرۡضُ أَثۡقَالَهَا
Ndipo nthaka idzatulutsa mitolo yake (zinthu zomwe zidali mkati mwake, monga akufa ndi miyala ya mtengo wapatali),
Tafsir berbahasa Arab:
وَقَالَ ٱلۡإِنسَٰنُ مَا لَهَا
Ndipo munthu adzanena (mwa mantha, ndikudabwa nthawi imeneyo). Ha! Yatani nthaka, (kodi Qiyâma yafika)?
Tafsir berbahasa Arab:
يَوۡمَئِذٖ تُحَدِّثُ أَخۡبَارَهَا
Tsiku limenelo idzanena nkhani zake zonse, (zabwino kapena zoipa).[470]
[470] Idzanena nthaka pa tsiku limenelo pamene Allah adzaiuza kuti inene monga momwe amazinenetsera zinthu zimene chikhalire sizilankhula, pakuti Allah ndi Wamphamvu zonse. Kapena m’mene iti idzakhalire nthaka kudzakwanira munthu kudziwa kuti ikutanthauza chakuti, popanda kutulutsa mawu monga momwe timadziwira munthu wosangalala ndi wachisoni; wanjala ndi wokhuta popanda kuyankhula. Nkhani zomwe idzafotokoza nthaka pa tsiku limenelo, monga momwe adanenera Mneneri Muhammad (s.a.w), ndi izi:- Tsiku la chiweruziro nthaka idzamuikira umboni munthu aliyense kapena m’badwo uliwonse pa chimene adachita pamwamba pake (pamwamba pa nthaka). Limeneli ndilo tanthauzo la mawu aja oti “ Nthaka idzanena nkhani zake.”
Tafsir berbahasa Arab:
بِأَنَّ رَبَّكَ أَوۡحَىٰ لَهَا
Pakuti Mbuye wako adzailamula kutero (kuti igwedezeke ndikunena zimene zinkachitika pamwamba pake).
Tafsir berbahasa Arab:
يَوۡمَئِذٖ يَصۡدُرُ ٱلنَّاسُ أَشۡتَاتٗا لِّيُرَوۡاْ أَعۡمَٰلَهُمۡ
Tsiku limenelo anthu adzachoka (m’manda) ali m’magulu obalalika kuti akasonyezedwe ntchito zawo (ndikudziwa chiwerengero chawo chimene chili kwa Allah).
Tafsir berbahasa Arab:
فَمَن يَعۡمَلۡ مِثۡقَالَ ذَرَّةٍ خَيۡرٗا يَرَهُۥ
Choncho, amene angachite chabwino cholemera ngati kanjere kakang’ono, adzaona malipiro ake.[471]
[471] (Ndime 7-8) Ma Ayah awiriwa akutidziwitsa kuti munthu adzalipidwa pa chilichonse chimene akuchita, chabwino kapena choipa, ngakhale chikhale chochepa monga kulemera kwa kanjere kochepa kwambiri.
Tafsir berbahasa Arab:
وَمَن يَعۡمَلۡ مِثۡقَالَ ذَرَّةٖ شَرّٗا يَرَهُۥ
Ndipo amene angachite choipa cholemera ngati kanjere kakang’ono, adzaona malipiro ake. (Allah sachitira chinyengo aliyense).
Tafsir berbahasa Arab:
 
Terjemahan makna Surah: Surah Az-Zalzalah
Daftar surah Nomor Halaman
 
Terjemahan makna Alquran Alkarim - Terjemahan Berbahasa Chichewa - Daftar isi terjemahan

Terjemahan Makna Al-Qur`ān Al-Karīm ke Bahasa Chichewa oleh Khalid Ibrahim Betala. Edisi 2020 M

Tutup