ಪವಿತ್ರ ಕುರ್‌ಆನ್ ಅರ್ಥಾನುವಾದ - ಚೇವಾ ಅನುವಾದ * - ಅನುವಾದಗಳ ವಿಷಯಸೂಚಿ


ಅರ್ಥಗಳ ಅನುವಾದ ಅಧ್ಯಾಯ: ಸೂರ ಅಝ್ಝಲ್ ಝಲ   ಶ್ಲೋಕ:

ಸೂರ ಅಝ್ಝಲ್ ಝಲ

إِذَا زُلۡزِلَتِ ٱلۡأَرۡضُ زِلۡزَالَهَا
Likadzagwedezedwa dziko lapansi kugwedezeka kwake kwamphamvu,
ಅರಬ್ಬಿ ವ್ಯಾಖ್ಯಾನಗಳು:
وَأَخۡرَجَتِ ٱلۡأَرۡضُ أَثۡقَالَهَا
Ndipo nthaka idzatulutsa mitolo yake (zinthu zomwe zidali mkati mwake, monga akufa ndi miyala ya mtengo wapatali),
ಅರಬ್ಬಿ ವ್ಯಾಖ್ಯಾನಗಳು:
وَقَالَ ٱلۡإِنسَٰنُ مَا لَهَا
Ndipo munthu adzanena (mwa mantha, ndikudabwa nthawi imeneyo). Ha! Yatani nthaka, (kodi Qiyâma yafika)?
ಅರಬ್ಬಿ ವ್ಯಾಖ್ಯಾನಗಳು:
يَوۡمَئِذٖ تُحَدِّثُ أَخۡبَارَهَا
Tsiku limenelo idzanena nkhani zake zonse, (zabwino kapena zoipa).[470]
[470] Idzanena nthaka pa tsiku limenelo pamene Allah adzaiuza kuti inene monga momwe amazinenetsera zinthu zimene chikhalire sizilankhula, pakuti Allah ndi Wamphamvu zonse. Kapena m’mene iti idzakhalire nthaka kudzakwanira munthu kudziwa kuti ikutanthauza chakuti, popanda kutulutsa mawu monga momwe timadziwira munthu wosangalala ndi wachisoni; wanjala ndi wokhuta popanda kuyankhula. Nkhani zomwe idzafotokoza nthaka pa tsiku limenelo, monga momwe adanenera Mneneri Muhammad (s.a.w), ndi izi:- Tsiku la chiweruziro nthaka idzamuikira umboni munthu aliyense kapena m’badwo uliwonse pa chimene adachita pamwamba pake (pamwamba pa nthaka). Limeneli ndilo tanthauzo la mawu aja oti “ Nthaka idzanena nkhani zake.”
ಅರಬ್ಬಿ ವ್ಯಾಖ್ಯಾನಗಳು:
بِأَنَّ رَبَّكَ أَوۡحَىٰ لَهَا
Pakuti Mbuye wako adzailamula kutero (kuti igwedezeke ndikunena zimene zinkachitika pamwamba pake).
ಅರಬ್ಬಿ ವ್ಯಾಖ್ಯಾನಗಳು:
يَوۡمَئِذٖ يَصۡدُرُ ٱلنَّاسُ أَشۡتَاتٗا لِّيُرَوۡاْ أَعۡمَٰلَهُمۡ
Tsiku limenelo anthu adzachoka (m’manda) ali m’magulu obalalika kuti akasonyezedwe ntchito zawo (ndikudziwa chiwerengero chawo chimene chili kwa Allah).
ಅರಬ್ಬಿ ವ್ಯಾಖ್ಯಾನಗಳು:
فَمَن يَعۡمَلۡ مِثۡقَالَ ذَرَّةٍ خَيۡرٗا يَرَهُۥ
Choncho, amene angachite chabwino cholemera ngati kanjere kakang’ono, adzaona malipiro ake.[471]
[471] (Ndime 7-8) Ma Ayah awiriwa akutidziwitsa kuti munthu adzalipidwa pa chilichonse chimene akuchita, chabwino kapena choipa, ngakhale chikhale chochepa monga kulemera kwa kanjere kochepa kwambiri.
ಅರಬ್ಬಿ ವ್ಯಾಖ್ಯಾನಗಳು:
وَمَن يَعۡمَلۡ مِثۡقَالَ ذَرَّةٖ شَرّٗا يَرَهُۥ
Ndipo amene angachite choipa cholemera ngati kanjere kakang’ono, adzaona malipiro ake. (Allah sachitira chinyengo aliyense).
ಅರಬ್ಬಿ ವ್ಯಾಖ್ಯಾನಗಳು:
 
ಅರ್ಥಗಳ ಅನುವಾದ ಅಧ್ಯಾಯ: ಸೂರ ಅಝ್ಝಲ್ ಝಲ
ಅಧ್ಯಾಯಗಳ ವಿಷಯಸೂಚಿ ಪುಟ ಸಂಖ್ಯೆ
 
ಪವಿತ್ರ ಕುರ್‌ಆನ್ ಅರ್ಥಾನುವಾದ - ಚೇವಾ ಅನುವಾದ - ಅನುವಾದಗಳ ವಿಷಯಸೂಚಿ

ಪವಿತ್ರ ಕುರ್‌ಆನ್ ಚೇವಾ ಅರ್ಥಾನುವಾದ - ಖಾಲಿದ್ ಇಬ್ರಾಹೀಂ ಬೀತಾಲಾ - ಮುದ್ರಣ: 2020

ಮುಚ್ಚಿ