クルアーンの対訳 - チェワ語対訳 * - 対訳の目次


対訳 節: (6) 章: 至高章
سَنُقۡرِئُكَ فَلَا تَنسَىٰٓ
Tikulakatulira (chivumbulutso Chathu) ndipo siuyiwala.[419]
[419] Mneneri Muhammad (s.a.w) adali munthu monga anthu ena ndipo adali ndi mbiri zonga anthu adalinazo, monga: kukonda ndi kusakonda, kuiwala ndi kukumbukira. Padapezeka kuti nthawi ina adaiwala ndi kupemphera maraka atatu m’Swala ya maraka anayi. Pachifukwa ichi pa nthawi yovumbulutsidwa Qur’an ndi Jibril, adali akubwereza bwereza mawu ovumbulutsidwawo kuopa kuti angaiwale. Choncho, apa Allah akumuletsa kuti asadzivutitse kumabwerezabwereza mawuwo pamene akuvumbulutsidwa ndipo adamupatsa lonjezo nthawi yomweyo kuti sadzaiwala. Ndipo adakwaniritsa lonjezo Lake. Mtumiki (s.a.w) adali kumtsikira ma surah aataliatali ndipo amatha kuwawerenga (molakatula) popanda kuonjezera kanthu kapena kuchepetsa, ngakhale kuti iye sadali kudziwa kuwerenga ndi kulemba. Kuwerenga kwake kudali kwakungolakatula pa mtima.
アラビア語 クルアーン注釈:
 
対訳 節: (6) 章: 至高章
章名の目次 ページ番号
 
クルアーンの対訳 - チェワ語対訳 - 対訳の目次

クルアーン・チェワ語対訳 - Khalid Ibrahim

閉じる